< Numeri 31 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Opet reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
2 “Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
Osveti sinove Izrailjeve na Madijancima, pak æeš se onda pribrati k rodu svojemu.
3 Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
I Mojsije reèe narodu govoreæi: opremite izmeðu sebe ljude na vojsku da idu na Madijance da uèine osvetu Gospodnju na Madijancima,
4 Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
Po tisuæu od plemena, od svakoga plemena Izrailjeva opremite na vojsku.
5 Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
I dadoše od tisuæa Izrailjevijeh po tisuæu od svakoga plemena, dvanaest tisuæa opremiše na vojsku.
6 Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
I posla Mojsije po tisuæu od svakoga plemena na vojsku, i s njima Finesa sina Eleazara sveštenika, i u njega bjehu sudi sveti i trube.
7 Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
I zavojštiše na Madijance, kako zapovjedi Gospod Mojsiju, i pobiše sve muškinje.
8 Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
Pobiše i careve Madijanske, s drugima koje im pobiše, Evina i Rokoma i Sura i Ura i Rovoka, pet careva Madijanskih, i Valama sina Veorova ubiše maèem.
9 Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
I zarobiše sinovi Izrailjevi žene Madijanke i djecu njihovu, i zaplijeniše svu stoku njihovu, krupnu i sitnu, i sve blago njihovo.
10 Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
A mjesta njihova u kojima življahu i gradove njihove sve popališe ognjem.
11 Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
I sve roblje i sav plijen, ljude i stoku, uzeše;
12 Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
I povedoše k Mojsiju i Eleazaru svešteniku i ka zboru sinova Izrailjevijeh, i roblje i ostali plijen i dobit u oko na polju Moavskom, koje je na Jordanu prema Jerihonu.
13 Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
A Mojsije i Eleazar sveštenik i svi knezovi od zbora izidoše im na susret iz okola.
14 Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
I Mojsije se razgnjevi na vojvode, na tisuænike i stotinare, koji se vraæahu s vojske;
15 Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
I reèe im Mojsije: a što ostaviste u životu sve žene?
16 Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
Ta one po rijeèi Valamovoj navratiše sinove Izrailjeve da zgriješe Gospodu s Fegora, te doðe ona pogibija na narod Gospodnji.
17 Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
Zato sada pobijte svu djecu mušku, i sve žene pobijte, koje su poznale èovjeka.
18 koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
A djevojke, koje ne poznaše èovjeka, ostavite u životu.
19 “Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
A vi ostanite izvan okola sedam dana; svaki koji je ubio koga i koji se dotakao ubijenoga, oèistite se treæi dan i sedmi dan, sebe i roblje svoje.
20 Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
I sve haljine i sve stvari kožne i sve što je od kostrijeti i sve sudove drvene oèistite.
21 Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
I reèe Eleazar sveštenik vojnicima, koji bijahu išli na vojsku: ovo je naredba i zakon što je Gospod zapovjedio Mojsiju:
22 Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
Zlato, srebro, mjed, gvožðe, kositer i olovo,
23 ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
Što god podnosi vatru, propustite kroz vatru, i oèistiæe se, ali pošto se oèisti vodom oèišæenja; a što god ne podnosi vatre, propustite kroz vodu.
24 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
I operite haljine svoje sedmi dan, i biæete èisti; i onda æete uæi u oko.
25 Yehova anawuza Mose kuti,
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
26 “Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
Izbroj sve što je zaplijenjeno, ljude i stoku, ti i Eleazar sveštenik i poglavari od plemena narodnijeh.
27 Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
I razdijeli sve zaplijenjeno na dvoje: na vojnike koji su išli na vojsku i na sav zbor.
28 Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
I uzmi dio za Gospoda od vojnika koji su išli na vojsku, po jednu dušu od pedeset, i od ljudi i od goveda i od magaraca i od ovaca.
29 Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
Od njihove polovine to uzmite, i podajte Eleazaru svešteniku za prinos Gospodu.
30 Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
I od polovine koja dopade sinovima Izrailjevijem uzmi po jedno od pedeset, i od ljudi i od goveda i od magaraca i od ovaca i od svake stoke, i to podaj Levitima koji rade što treba za šator Gospodnji.
31 Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
I uèini Mojsije i Eleazar sveštenik kako zapovjedi Gospod Mojsiju.
32 Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
I bješe plijena, što osta od plijena koji zaplijeni vojska: šest stotina i sedamdeset i pet tisuæa ovaca,
33 Ngʼombe 72,000,
I sedamdeset i dvije tisuæe goveda,
34 abulu 61,000,
I šezdeset i jedna tisuæa magaraca,
35 ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
I ženskinja što ne bješe poznalo èovjeka, svega trideset i dvije tisuæe duša.
36 Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
A u polovini, u dijelu onijeh koji bijahu išli na vojsku, bješe na broj tri stotine i trideset i sedam tisuæa i pet stotina ovaca,
37 mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
A od toga dio Gospodu bješe šest stotina i sedamdeset i pet ovaca;
38 ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
I trideset i šest tisuæa goveda, a od toga dio Gospodu sedamdeset i dva;
39 abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
I trideset tisuæa i pet stotina magaraca, a od toga dio Gospodu šezdeset i jedan;
40 anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
I šesnaest tisuæa duša ljudskih, a od toga dio Gospodu trideset i dvije duše.
41 Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
I dade Mojsije Eleazaru svešteniku dio za prinos Gospodu, kao što mu zapovjedi Gospod.
42 Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
A od druge polovine, koja dopade sinovima Izrailjevijem, koju uze Mojsije od ljudi koji bjehu išli na vojsku,
43 Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
A i u toj polovini, koja dopade zboru, bješe tri stotine i trideset i sedam tisuæa i pet stotina ovaca,
44 ngʼombe 36,000,
Trideset i šest tisuæa goveda,
45 abulu 30,500,
Trideset tisuæa i pet stotina magaraca,
46 anthu 16,000.
I šesnaest tisuæa duša ljudskih)
47 Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
Od te polovine, koja dopade sinovima Izrailjevijem, uze Mojsije po jedno od pedeset, i od ljudi i od stoke, i dade Levitima koji rade što treba za šator Gospodnji, kao što mu Gospod zapovjedi.
48 Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
I pristupiše k Mojsiju vojvode, tisuænici i stotinari,
49 iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
I rekoše mu: sluge tvoje prebrojiše vojnike koji bijahu pod našom rukom, i nijednoga nije manje.
50 Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
Zato prinosimo Gospodu prinos, svaki što je ko zadobio, zlatnijeh zaklada, kopaèa, narukvica, prstena, obodaca i lanèiæa, da bi se oèistile duše naše pred Gospodom.
51 Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
I uze Mojsije i Eleazar sveštenik od njih zlato, svakojake zaklade.
52 Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
A bješe svega zlata prinesenoga, što prinesoše Mojsiju tisuænici i stotinari, šesnaest tisuæa i sedam stotina i pedeset sikala.
53 Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
A vojnici zadržaše sebi što koji bješe zaplijenio.
54 Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.
I uzevši Mojsije i Eleazar zlato od tisuænika i stotinara, unesoše ga u šator od sastanka za spomen sinovima Izrailjevijem pred Gospodom.

< Numeri 31 >