< Numeri 28 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Also the Lord seide to Moises, Comaunde thou to the sones of Israel, and thou schalt seie to hem,
2 “Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
Offre ye bi her tymes myn offryng, and looues, and encense of swettist odour.
3 Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
These ben the sacrificis whiche ye owen to offre; twey lambren of o yeer, with out wem, ech dai in to euerlastynge brent sacrifice.
4 Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
Ye schulen offre oon eerli, and the tother at euentid.
5 Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
`Ye schulen offre the tenthe part of ephi `of floure, `which be spreynt with pureste oile, and haue the fourthe part of hyn.
6 Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
It is continuel brent sacrifice, which ye offriden in the hil of Synai, in to `odour of swettiste encense to the Lord.
7 Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
And ye schulen offre the fourthe part of hyn of wyn, bi ech lomb, in the seyntuarie of the Lord.
8 Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
And ye schulen offre in lijk maner the tother lomb at euentid, bi al the custom of the morewe sacrifice, and of moist sacrifices therof, an offryng of swettist odour to the Lord.
9 “‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
Forsothe in the `dai of sabat ye schulen offre twey lambren of o yeer, without wem, and twei tenthe partis of flour spreynt togidere with oile, in sacrifice, `and ye schulen offre moiste sacrificis that ben sched bi custom,
10 Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
bi alle sabatis, in to euerlastynge brent sacrifice.
11 “Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
Forsothe in calendis, that is, in the bigynnyngis of monethis, ye schulen offre brent sacrifice to the Lord, tweyne calues of the droue, o ram, seuene lambren of o yeer, without wem,
12 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
and thre tenthe partis of flour spreynt to gidere with oile, in sacrifice, bi ech calf, and twey tenthe partis of flour spreynt to gidere with oile, bi ech ram;
13 ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
and the tenthe part of `a dyme of flour of oile in sacrifice, bi ech lomb; it is brent sacrifice of `swetist odour, and of encense to the Lord.
14 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
Forsothe the moiste sacrifices of wyn, that schulen be sched bi alle slayn sacrificis, schulen be these; the half part of hyn bi ech calf, the thridde part bi a ram, the fourthe part bi a lomb; this schal be brent sacrifices bi ech monethe, that comen oon aftir anothir while the yeer turneth.
15 Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
Also a `buc of geet schal be offrid to the Lord for synnes, in to euerlastynge brent sacrifice, with his moiste offryngis.
16 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
Forsothe in the firste monethe, in the fouretenthe dai of the monethe, schal be phase, `that is, pask `ethir passyng, of the Lord;
17 Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
and in the fiftenthe day schal be the solempnyte of the therf looues. Bi seuene daies ye schulen ete therf looues;
18 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
of whiche the firste dai schal be worschipful and hooli; ye schulen not do ony seruyle werk therynne.
19 Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
And ye schulen offre brent sacrifice to the Lord, twey calues, o ram, seuene lambren of o yeer, without wem;
20 Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
and the sacrifices of ech bi itsilf of flour, which be spreynt to gidere with oile, thre tenthe partis bi ech calf,
21 Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
and twey tenthe partis bi a ram, and the tenthe part of `a dyme bi ech lomb, that is, bi seuene lambren.
22 Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
`And ye schulen offre o `buc of geet for synne, that clensyng be maad for you,
23 Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
outakun the brent sacrifice of the morewtid, which ye schulen offre euere.
24 Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
So ye schulen do bi ech dai of seuene daies, into the nurschyng of fier, and in to swettist odour to the Lord, that schal rise of the brent sacrifice, and of moiste sacrifices of ech.
25 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Also the seuenthe day schal be moost solempne and hooli to you; ye schulen not do ony seruyle werk ther ynne.
26 “‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
Also the dai of the firste fruytis, whanne ye schulen offre newe fruitis to the Lord, whanne the wokis schulen be fillyd, schal be worschipful and hooli; ye schulen not do ony seruyle werk ther ynne.
27 Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
And ye schulen offre brent sacrifice to the Lord, in to `swettiste odour; twey calues of the droue, o ram, and seuene lambren of o yeer, with out wem;
28 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
and in the sacrifices of tho ye schulen offre thre tenthe partis of flour spreynt togidere with oile, bi ech calf, twei tenthe partis bi rammes,
29 Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
the tenthe parte of `a dyme bi the lambren, whiche ben to gidere, seuene lambren.
30 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
`And ye schulen offre a `buc of geet, which is offrid for clensyng, outakun brent sacrifice euerlastynge, and the moiste sacrifices therof;
31 Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.
ye schulen offre alle thingis with out wem, with her moyste sacrifices.

< Numeri 28 >