< Numeri 26 >

1 Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni,
Und es geschah nach der Plage, daß Jehovah sprach zu Mose und zu Eleasar, dem Sohne Aharons, des Priesters; und Er sprach:
2 “Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.”
Nehmet auf die Kopfzahl der ganzen Gemeinde der Söhne Israels vom zwanzigsten Jahre und aufwärts nach dem Hause ihrer Väter, alle, die im Heer ausziehen in Israel.
3 Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti,
Und Mose und Eleasar, der Priester, redete mit ihnen in Arboth Moab am Jordan, bei Jericho und sprachen:
4 “Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.” Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:
Vom zwanzigsten Jahre an und aufwärts, wie Jehovah dem Mose und den Söhnen Israels, die aus Ägyptenland auszogen, geboten hat.
5 Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi: kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki; kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;
Ruben, Israels Erstgeborener: Söhne Rubens waren Chanoch, die Familie der Chanochiten; von Phallu die Familie der Phalluiten;
6 kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.
Von Chezron die Familie der Chezroniten, von Charmi die Familie der Charmiten;
7 Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.
Dies sind die Familien der Rubeniten. Ihrer Gemusterten aber waren es dreiundvierzigtausendsiebenhundertdreißig;
8 Mwana wa Palu anali Eliabu,
Und die Söhne Phallus Eliab.
9 ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova.
Und die Söhne Eliabs Nemuel und Dathan und Abiram - das waren Dathan und Abiram, Berufene der Gemeinde, die zankten mit Mose und mit Aharon in der Gemeinde Korachs, als sie wider Jehovah zankten.
10 Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo.
Und die Erde öffnete ihren Mund und verschlang sie und Korach, da die Gemeinde starb, indem das Feuer die zweihundertfünfzig Männer auffraß und sie zum Zeichen wurden.
11 Koma ana a Kora sanafe nawo.
Korachs Söhne waren aber nicht gestorben.
12 Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele; kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini; kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;
Die Söhne Simeons nach ihren Familien: Von Nemuel die Familie der Nemueliten, von Jamin die Familie der Jaminiten, von Jachin die Familie der Jachiniten;
13 kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera; kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.
Von Serach die Familie der Serachiten, von Schaul die Familie der Schauliten.
14 Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.
Dies sind die Familien der Simeoniten: Zweiundzwanzigtausendzweihundert.
15 Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi: kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni; kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi; kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;
Die Söhne Gads nach ihren Familien: Von Zephon die Familie der Zephoniten, von Chaggi die Familie der Chaggiten, von Schuni die Familie der Schuniten;
16 kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini; kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;
Von Osni die Familie der Osniten, von Eri die Familie der Eriten;
17 kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi; kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.
Von Arod die Familie der Aroditen; von Areli die Familie der Areliten.
18 Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.
Dies sind die Familien der Söhne Gads nach ihren Gemusterten: vierzigtausendfünfhundert.
19 Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.
Die Söhne Judahs: Er und Onan. Und Er und Onan starben im Lande Kanaan.
20 Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Sela, fuko la Asera; kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi; kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.
Und die Söhne Judahs waren nach ihren Familien: Von Schelah die Familie der Schelaniten, von Perez die Familie der Parziten, von Serach die Familie der Sarchiten.
21 Zidzukulu za Perezi zinali izi: kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.
Und die Söhne des Perez waren: Von Chezron die Familie der Chezroniten, von Chamul die Familie der Chamuliten.
22 Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.
Dies sind die Familien Judahs nach ihren Gemusterten: sechsundsiebzigtausendfünfhundert.
23 Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Tola, fuko la Atola; kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;
Die Söhne Issaschars nach ihren Familien: Von Thola die Familie der Tholaiten; von Puvah die Familie der Puniten.
24 kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu. Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.
Von Jaschub die Familie der Jaschubiten; von Schimron die Familie der Schimroniten.
25 Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.
Das sind die Familien Issaschars nach ihren Gemusterten: vierundsechzigtausenddreihundert.
26 Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi; kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni; kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.
Die Söhne Sebuluns nach ihren Familien: Von Sared die Familie der Sarditen; von Elon die Familie der Eloniten; von Jachleel die Familie der Jachleeliten;
27 Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.
Dies sind die Familien der Sebuluniten nach ihren Gemusterten: sechzigtausendfünfhundert.
28 Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:
Die Söhne Josephs nach ihren Familien sind Menascheh und Ephraim.
29 Zidzukulu za Manase: kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi); kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.
Die Söhne Menaschehs: Von Machir die Familie der Machiriten. Und Machir zeugte Gilead. Von Gilead die Familie der Gileaditen.
30 Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi; kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri; kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;
Das sind die Söhne Gileads: Jeser, die Familie der Jesriten; von Chelek, die Familie der Chelekiten.
31 kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli; kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;
Und Asriel, die Familie der Asrieliten; und Schechem, die Familie der Schichmiten.
32 kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida; kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.
Und Schemidah, die Familie der Schemidaiten, und Chepher, die Familie der Chephriten.
33 (Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)
Und Zelaphechad, Chephers Sohn, hatte keine Söhne, nur Töchter. Und die Namen von Zelaphechads Töchtern waren Machlah und Noah, Choglah, Milkah und Thirzah.
34 Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.
Das sind die Familien Menaschehs; und ihrer Gemusterten sind zweiundfünfzigtausendsiebenhundert.
35 Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi; kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela; kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri; kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.
Das sind die Söhne Ephraims nach ihren Familien: Von Schuthelach die Familie der Schuthalchiten; von Becher die Familie der Bachriten; von Thachan die Familie der Thachaniten.
36 Zidzukulu za Sutela zinali izi: kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.
Und dies sind die Söhne Schuthelachs: Von Eran die Familie der Eraniten.
37 Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500. Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.
Dies sind die Familien der Söhne Ephraims nach ihren Gemusterten: zweiundreißigtausendfünfhundert. Das sind die Söhne Josephs nach ihren Familien.
38 Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Bela, fuko la Abela; kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli; kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;
Die Söhne Benjamins nach ihren Familien: Von Bela die Familie der Baliten; von Aschbel die Familie der Aschbeliten; von Achiram die Familie der Achiramiten;
39 kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu; kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;
Von Schephupham die Familie der Schuphamiten; von Chupham die Familie der Chuphamiten.
40 Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi: kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi; kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;
Und die Söhne Belahs sind Ard und Naaman; die Familie der Arditen, von Naaman die Familie der Naamiten.
41 Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.
Dies sind die Söhne Benjamins nach ihren Familien; und ihrer Gemusterten waren es fünfundvierzigtausendsechshundert.
42 Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu. Izi zinali zidzukulu za Dani.
Das sind die Söhne Dans nach ihren Familien: Von Schucham die Familie der Schuchamiten. Dies die Familien Dans nach ihren Familien.
43 Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.
Alle Familien der Schuchaniten nach ihren Gemusterten waren vierundsechzigtausendvierhundert.
44 Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna; kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi; kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;
Die Söhne Aschers nach ihren Familien sind: Von Jimmah die Familie der Jimniten; von Jischvi die Familie der Jischviten; von Beriah die Familie der Beriiten.
45 ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya: kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi; kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;
Von den Söhnen Beriah, von Cheber die Familie der Chebriten; von Malkiel die Familie der Malkieliten.
46 (Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)
Und der Name der Tochter Aschers war Serach.
47 Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.
Dies sind die Familien der Söhne Aschers nach ihren Gemusterten: dreiundfünfzigtausendvierhundert.
48 Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli; kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;
Die Söhne Naphthalis nach ihren Familien: Von Jachzeel die Familie der Jachzeeliten; von Guni die Familie der Guniten.
49 kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri; kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.
Von Jezer die Familie der Jizriten; von Schillem die Familie der Schillemiten.
50 Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.
Das sind die Familien Naphthalis nach ihren Familien; und ihrer Gemusterten waren es fünfundvierzigtausendvierhundert.
51 Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.
Dies sind die Gemusterten der Söhne Israels sechshunderttausend und tausendsiebenhundertdreißig.
52 Yehova anawuza Mose kuti,
Und Jehovah redete zu Mose und sprach:
53 “Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo.
An diese soll das Land verteilt werden zum Erbe nach der Zahl der Namen.
54 Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa.
Dem Vielen werde viel zu seinem Erbe und dem Wenigen wenig zu seinem Erbe. Jeglichem Manne werde sein Erbe gegeben nach dem Verhältnis seiner Gemusterten.
55 Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo.
Man verteile jedoch das Land durch das Los; nach den Namen der Stämme ihrer Väter sollen sie es erben.
56 Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”
Nach dem Los soll man sein Erbe verteilen, zwischen viel oder wenig.
57 Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa: kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni; kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati; kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.
Und das sind die gemusterten der Leviten nach ihren Familien: Von Gerschon die Familie der Gerschoniten; von Kohath die Familie der Kohathiten; von Merari die Familie der Merariten.
58 Awanso anali mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, fuko la Kora banja la Akohati, (Kohati anali abambo a Amramu.
Dies sind die Familien Levis, die Familien der Libniten, der Familien der Chebroniten, die Familie der Machliten, die Familie der Muschiten, die Familie der Korchiten, und Kohath zeugte den Amram.
59 Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo.
Und der Name von Amrams Weib war Jochebet, eine Tochter Levis, die dem Levi in Ägypten geboren ward. Und sie gebar dem Amram den Aharon und den Mose und Mirjam, ihre Schwester.
60 Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Und dem Aharon wurden geboren Nadab und Abihu, Eleasar und Ithamar.
61 Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).
Und Nadab und Abihu waren gestorben, da sie fremdes Feuer vor Jehovah darbrachten.
62 Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.
Und ihrer Gemusterten waren es dreiundzwanzigtausend, alles Männliche von einem Monat und aufwärts: denn sie wurden nicht inmitten der Söhne Israels gemustert, weil ihnen kein Erbe inmitten der Söhne Israels gegeben ward.
63 Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko.
Dies sind die von Mose und dem Priester Eleasar Gemusterten, da sie die Söhne Israels in Arboth Moab am Jordan, bei Jericho, musterten.
64 Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai;
Und unter ihnen war kein Mann, der von Mose und Aharon, dem Priester, Gemusterten, da sie die Söhne Israels in der Wüste Sinai musterten.
65 Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
Denn Jehovah hatte von ihnen gesprochen, daß sie in der Wüste des Todes sterben sollten. Und kein Mann blieb von ihnen übrig außer Kaleb, der Sohn Jephunnehs und Joschua, der Sohn Nuns.

< Numeri 26 >