< Numeri 25 >

1 Aisraeli akukhala ku Sitimu, anayamba kuchita chigololo ndi akazi a ku Mowabu,
I življaše Izrailj u Sitimu, i narod stade èiniti preljubu sa kæerima Moavskim.
2 amene ankawayitana ku nsembe za milungu yawo. Anthuwo anadya chakudya chopereka kwa milungu ndi kupembedza milunguyo.
One pozivahu narod na žrtve svojih bogova, i narod jeðaše, i klanjaše se bogovima njihovijem.
3 Motero Aisraeli anapembedza nawo Baala-Peori ndipo Yehova anawapsera mtima kwambiri.
I Izrailj prionu uz Velfegora; i razgnjevi se Gospod na Izrailja.
4 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga atsogoleri onse a anthu awa, uwaphe poyera, pamaso pa Yehova kuti mkwiyo waukulu wa Yehova uchoke pa Israeli.”
I reèe Gospod Mojsiju: uzmi sve knezove narodne, i objesi ih Gospodu prema suncu, da se odvrati gnjev Gospodnji od Izrailja.
5 Choncho Mose anawuza oweruza a Israeli kuti, “Aliyense wa inu ayenera kupha anthu ake amene anapembedza nawo Baala-Peori.”
I reèe Mojsije sudijama Izrailjevijem: pobijte svaki svoje koji su prionuli uz Velfegora.
6 Kenaka mwamuna wina wa ku Israeli anabweretsa ku banja lake mkazi wa Chimidiyani pamaso pa Mose ndi anthu onse a Israeli pamene ankalira pa khomo la tenti ya msonkhano.
I gle, jedan izmeðu sinova Izrailjevijeh doðe i dovede k braæi svojoj jednu Madijanku na oèi Mojsiju i na oèi svemu zboru sinova Izrailjevijeh; a oni zaplakaše na vratima šatora od sastanka.
7 Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni ataona izi, anachoka pa msonkhanowo, natenga mkondo mʼdzanja lake.
A kad to vidje Fines sin Eleazara sina Arona sveštenika, usta isred zbora i uze koplje u ruku;
8 Ndipo anatsatira Mwisraeliyu mpaka mʼtenti yake. Anasolola mkondowo ndi kubaya awiriwo kupyola Mwisraeliyo mpaka mʼthupi la mkaziyo. Pamenepo mliri unaleka pakati pa Aisraeli.
I uðe za èovjekom Izrailjcem u šator, i probode ih oboje, èovjeka Izrailjca i onu ženu, kroz trbuh, i presta pogibija meðu sinovima Izrailjevijem.
9 Pa mliriwo, anthu okwana 24,000 anafa.
I izgibe ih od te pogibije dvadeset i èetiri tisuæe.
10 Yehova anawuza Mose kuti,
Tada reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
11 “Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni wabweza mkwiyo wanga pa Aisraeli chifukwa sanalole kuti wina aliyense apembedze mulungu wina koma Ine ndekha. Nʼchifukwa chake sindinawawononge mu mkwiyo wanga.
Fines sin Eleazara sina Arona sveštenika odvrati gnjev moj od sinova Izrailjevijeh otvorivši revnost za me meðu njima, da ne bih istrijebio sinove Izrailjeve u revnosti svojoj.
12 Tsono muwuze kuti ndikhazikitsa pangano langa la mtendere ndi iye.
Zato mu kaži: evo dajem mu svoj zavjet mirni.
13 Ndikupangana naye pangano la unsembe wosatha, iyeyo pamodzi ndi zidzukulu zake zonse, chifukwa sanalole kuti anthu awukire Ine Mulungu, ndipo anachita ntchito yopepesera machimo Aisraeli.”
I imaæe on i sjeme njegovo nakon njega zavjet sveštenstva vjeènoga, jer revnova za Boga svojega i oèisti sinove Izrailjeve.
14 Dzina la Mwisraeli yemwe anaphedwa ndi mkazi wa Chimidiyani anali Zimuri mwana wa Salu, mtsogoleri wa banja la Simeoni.
A èovjeku Izrailjcu ubijenome, koji bi ubijen s Madijankom, bješe ime Zamrije sin Salmonov, knez od doma oca svojega od plemena Simeunova.
15 Ndipo dzina la mkazi wa Chimidiyani, yemwe anaphedwayo, linali Kozibi mwana wa Zuri, mtsogoleri wa fuko la ku Midiyaniko.
A ubijenoj ženi Madijanci bješe ime Hazvija kæi Sura kneza narodnoga u domu oca svojega meðu Madijancima.
16 Yehova anawuza Mose kuti,
I reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
17 “Amidiyani ndi adani anu ndipo uwaphe,
Zavojštite na Madijance, i bijte ih;
18 chifukwa ankakuonani inu ngati adani awo pamene anakupusitsani pa nkhani ya ku Peori, ndiponso za mlongo wawo Kozibi, mwana wamkazi wa mtsogoleri wa Amidiyani, mkazi yemwe anaphedwa pamene mliri unabwera chifukwa cha zimene zinachitika ku Peori.”
Jer oni zavojštiše na vas prijevarama svojim, i prevariše vas Velfegorom i Hazvijom kæerju kneza Madijanskoga, sestrom svojom, koja bi ubijena u dan pogibije koja doðe s Fegora.

< Numeri 25 >