< Numeri 23 >

1 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano, ndipo mukonzenso ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
I reèe Valam Valaku: naèini mi ovdje sedam oltara, i pripravi mi ovdje sedam telaca i sedam ovnova.
2 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo awiriwo anapereka ngʼombe imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
I uèini Valak kako mu reèe Valam; i prinese Valak s Valamom na svakom oltaru po jedno tele i ovna.
3 Kenaka Balaamu anati kwa Balaki, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu ineyo ndipite pambali. Mwina Yehova adzabwera kuti akumane nane. Chilichonse chimene akandionetse ndidzakuwuzani” Choncho anapita ku malo okwera a chipululu.
Pa reèe Valam Valaku: stoj kod svoje žrtve paljenice; a ja idem eda bih se sreo s Gospodom, pa što mi javi kazaæu ti. I on otide sam.
4 Mulungu anakumana naye ndipo Balaamu anati, “Ndakonza maguwa asanu ndi awiri ndipo pa guwa lililonse ndaperekapo nsembe ya ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzinso.”
I srete Bog Valama, a on mu reèe: sedam oltara spremih, i prinesoh po tele i ovna na svakom oltaru.
5 Yehova anawuza Balaamu kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
A Gospod metnu rijeèi u usta Valamu, i reèe: vrati se k Valaku i tako mu reci.
6 Ndipo anabwerera kwa iye namupeza atayima pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu onse a Mowabu.
I vrati se k njemu, a on stajaše kod žrtve svoje paljenice i svi knezovi Moavski.
7 Ndipo Balaamu ananena uthenga wake: “Balaki ananditenga kuchoka ku Aramu, mfumu ya ku Mowabu kuchokera ku mapiri a kummawa. Iye anati, ‘Bwera, temberera Yakobo mʼmalo mwanga, pita nyoza Israeli.’
A on otvori prièu svoju, i reèe: iz Arama dovede me Valak car Moavski s planine istoène, govoreæi: hodi, prokuni mi Jakova, hodi, naruži Izrailja.
8 Ndingatemberere bwanji amene Mulungu sanawatemberere? Ndinganyoze bwanji amene Yehova sanawanyoze?
Kako bih kleo onoga koga ne kune Bog? ili kako bih ružio onoga koga Gospod ne ruži?
9 Kuchokera pamwamba pa mapiri ndikuona anthu, ndikuwaona kuchokera pa zitunda. Ndikuona anthu okhala pawokha, osakhala mʼgulu limodzi ndi mitundu ina.
Jer svrh stijena vidim ga, i s humova gledam ga. Gle, ovaj æe narod nastavati sam, i s drugim narodima neæe se pomiješati.
10 Ndani angawerenge zidzukulu za Yakobo zochuluka ngati fumbi, kapena chimodzi mwa zigawo zinayi za Israeli? Lekeni ndife imfa ya oyera mtima, ndi chimaliziro changa chikhale ngati chawo!”
Ko æe izbrojiti prah Jakovljev i broj od èetvrti Izrailja? Da bih ja umro smræu pravednièkom, i kraj moj da bi bio kao njihov!
11 Balaki anati kwa Balaamu, “Wandichitira chiyani? Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, ndipo taona, sunachite chilichonse koma kuwadalitsa!”
Tada reèe Valak Valamu: šta to radiš od mene? Ja te dozvah da prokuneš neprijatelje moje, a gle, ti blagosiljaš jednako.
12 Iye anayankha kuti, “Kodi sindinayenera kuyankhula zimene Yehova anandiwuza?”
A on odgovori i reèe: zar neæu paziti i govoriti ono što mi je Gospod metnuo u usta?
13 Kenaka Balaki anawuza Balaamu kuti, “Tiye tipite limodzi ku malo ena komwe ungawaone. Udzangoona gulu limodzi osati onsewo. Ndipo pamenepo, ukawatemberere mʼmalo mwanga.”
Tada mu reèe Valak: hodi sa mnom na drugo mjesto, odakle æeš ga vidjeti; samo mu kraj vidiš, a svega ga ne vidiš; prokuni mi ga odande.
14 Tsono anamutengera ku munda wa Zofimu pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo kumeneko anamanga maguwa ansembe asanu ndi awiri ndipo anapereka nsembe ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
I dovede ga u polje Zofim, navrh Fazge, i naèini sedam oltara, i prinese na svakom oltaru po jedno tele i ovna.
15 Balaamu anawuza Balaki kuti, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu pamene ine ndikukakumana ndi Mulungu cha uko.”
Tada Valam reèe Valaku: stoj tu kod žrtve svoje paljenice, a ja idem onamo na susret Gospodu.
16 Yehova anakumana ndi Balaamu ndipo anamuyankhula kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
I srete Gospod Valama, i metnu mu rijeè u usta, i reèe: vrati se k Valaku, i tako govori.
17 Ndipo anapita kwa iye ndipo anamupeza atayimirira pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu a ku Mowabu. Balaki anafunsa Balaamu kuti, “Yehova wayankhula chiyani?”
I doðe k njemu, a on stajaše kod žrtve svoje paljenice i s njim knezovi Moavski; i reèe Valak: šta veli Gospod?
18 Pamenepo Balaamu ananena uthenga wake: “Nyamuka Balaki ndipo tamvera; Undimvere iwe mwana wa Zipori.
A on otvori prièu svoju, i reèe: ustani Valaèe, i poslušaj, èuj me sine Seforov!
19 Mulungu si munthu kuti aname, kapena mwana wa munthu kuti asinthe maganizo ake. Kodi amayankhula koma osachita? Kodi amalonjeza koma osakwaniritsa?
Bog nije èovjek da laže, ni sin èovjeèji da se pokaje. Što kaže neæe li uèiniti, i što reèe neæe li izvršiti?
20 Wandilamula kuti ndidalitse, Iyeyo wadalitsa ndipo sindingasinthe.
Gle, primih da blagoslovim; jer je on blagoslovio, a ja neæu poreæi.
21 “Palibe kuwukira kulikonse kumene wakuona mwa Yakobo, sanaone chovuta mu Israeli. Yehova Mulungu wawo ali nawo: mfuwu wa mfumu uli pakati pawo.
Ne gleda na bezakonje u Jakovu ni na nevaljalstvo u Izrailju; Gospod je njegov s njim, i graja u njemu kao car kad nadvlada.
22 Mulungu wowatulutsa mʼdziko la Igupto, ali ndi mphamvu ngati za njati.
Bog ga je izveo iz Misira, on mu je kao snaga jednorogova.
23 Palibe matsenga amene angalimbane ndi Yakobo, palibe mawula amene angalimbane ndi Israeli. Tsopano za Yakobo ndi Israeli adzanena kuti, ‘Onani zimene Mulungu wachita!’
Jer nema èini na Jakova ni vraèanja na Izrailja; u ovo doba govoriæe se o Jakovu i o Izrailju, što je uèinio Bog.
24 Taonani, anthu anyamuka ngati mkango waukazi; adzuka okha ngati mkango waumuna umene supuma mpaka utadya nyama imene wagwira ndi kumwa magazi a nyama yogwidwayo.”
Evo, narod æe ustati kao silan lav, i kao laviæ skoèiæe; neæe leæi dokle ne pojede lova i popije krvi pobijenijeh.
25 Ndipo Balaki anati kwa Balaamu, “Usawatemberere ndi pangʼono pomwe kapena kuwadalitsa!
Tada reèe Valak Valamu: nemoj ga ni kleti ni blagosiljati.
26 “Balaamu anayankha Balaki kuti, ‘Kodi sindinakuwuzeni kuti ndiyenera kuchita zimene Yehova wanena?’”
A Valam odgovori Valaku: nijesam li ti kazao da æu èiniti što mi god Gospod kaže?
27 Kenaka Balaki anati kwa Balaamu, “Bwera ndikutengere ku malo ena. Mwina chidzamukondweretsa Mulungu kuti uwatemberere kumeneko mʼmalo mwanga.”
A Valak reèe Valamu: hodi, odvešæu te na drugo mjesto; da ako Bogu bude volja da mi ga odande prokuneš.
28 Ndipo Balaki anamutengera Balaamu pamwamba pa Peori, poyangʼanana ndi chipululu.
I odvede Valak Valama navrh Fegora, koji gleda u pustinju.
29 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano ndipo mundikonzere ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
I reèe Valam Valaku: naèini mi ovdje sedam oltara, i pripravi mi ovdje sedam telaca i sedam ovnova.
30 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo anapereka nsembe ngʼombe imodzi yayimuna ndi nkhosa imodzi yayimuna pa guwa lililonse.
I uèini Valak kako reèe Valam i prinese žrtvu po tele i ovna na svakom oltaru.

< Numeri 23 >