< Numeri 16 >

1 Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
And Korah, son of Izhar, son of Kohath, son of Levi, taketh both Dathan and Abiram sons of Eliab, and On son of Peleth, sons of Reuben,
2 ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
and they rise up before Moses, with men of the sons of Israel, two hundred and fifty, princes of the company, called of the convention, men of name,
3 Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
and they are assembled against Moses and against Aaron, and say unto them, 'Enough of you! for all the company — all of them [are] holy, and in their midst [is] Jehovah; and wherefore do ye lift yourselves up above the assembly of Jehovah?'
4 Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
And Moses heareth, and falleth on his face,
5 Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
and he speaketh unto Korah, and unto all his company, saying, 'Morning! — and Jehovah is knowing those who are his, and him who is holy, and hath brought near unto Him; even him whom He doth fix on He bringeth near unto Him.
6 Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
This do: take to yourselves censers, Korah, and all his company,
7 ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
and put in them fire, and put on them perfume, before Jehovah to-morrow, and it hath been, the man whom Jehovah chooseth, he [is] the holy one; — enough of you, sons of Levi.'
8 Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
And Moses saith unto Korah, 'Hear ye, I pray you, sons of Levi;
9 Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
is it little to you that the God of Israel hath separated you from the company of Israel to bring you near unto Himself, to do the service of the tabernacle of Jehovah, and to stand before the company to serve them? —
10 Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
yea, He doth bring thee near, and all thy brethren the sons of Levi with thee — and ye have sought also the priesthood!
11 Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
Therefore, thou and all thy company who are met [are] against Jehovah; and Aaron, what [is] he, that ye murmur against him?'
12 Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
And Moses sendeth to call for Dathan and for Abiram sons of Eliab, and they say, 'We do not come up;
13 Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
is it little that thou hast brought us up out of a land flowing with milk and honey to put us to death in a wilderness that thou also certainly makest thyself prince over us?
14 Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
Yea, unto a land flowing with milk and honey thou hast not brought us in, nor dost thou give to us an inheritance of field and vineyard; the eyes of these men dost thou pick out? we do not come up.'
15 Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
And it is very displeasing to Moses, and he saith unto Jehovah, 'Turn not Thou unto their present; not one ass from them have I taken, nor have I afflicted one of them.'
16 Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
And Moses saith unto Korah, 'Thou and all thy company, be ye before Jehovah, thou, and they, and Aaron, to-morrow;
17 Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
and take ye each his censer, and ye have put on them perfume, and brought near before Jehovah, each his censer, two hundred and fifty censers; and thou and Aaron, each his censer.'
18 Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
And they take each his censer, and put on them fire, and lay on them perfume, and they stand at the opening of the tent of meeting, with Moses and Aaron.
19 Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
And Korah assembleth against them all the company unto the opening of the tent of meeting, and the honour of Jehovah is seen by all the company.
20 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
And Jehovah speaketh unto Moses and unto Aaron, saying,
21 “Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
'Be ye separated from the midst of this company, and I consume them in a moment;'
22 Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
and they fall on their faces, and say, 'God, God of the spirits of all flesh — the one man sinneth, and against all the company Thou art wroth!'
23 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah speaketh unto Moses, saying,
24 “Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
'Speak unto the company, saying, Go ye up from round about the tabernacle of Korah, Dathan, and Abiram.'
25 Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
And Moses riseth, and goeth unto Dathan and Abiram, and the elders of Israel go after him,
26 Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
and he speaketh unto the company, saying, 'Turn aside, I pray you, from the tents of these wicked men, and come not against anything that they have, lest ye be consumed in all their sins.'
27 Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
And they go up from the tabernacle of Korah, Dathan and Abiram, from round about, and Dathan, and Abiram have come out, standing at the opening of their tents, and their wives, and their sons, and their infants.
28 Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
And Moses saith, 'By this ye do know that Jehovah hath sent me to do all these works, that [they are] not from my own heart;
29 Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
if according to the death of all men these die — or the charge of all men is charged upon them — Jehovah hath not sent me;
30 Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol h7585)
and if a strange thing Jehovah do, and the ground hath opened her mouth and swallowed them, and all that they have, and they have gone down alive to Sheol — then ye have known that these men have despised Jehovah.' (Sheol h7585)
31 Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
And it cometh to pass at his finishing speaking all these words, that the ground which [is] under them cleaveth,
32 ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
and the earth openeth her mouth, and swalloweth them, and their houses, and all the men who [are] for Korah, and all the goods,
33 Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol h7585)
and they go down, they, and all that they have, alive to Sheol, and the earth closeth over them, and they perish from the midst of the assembly; (Sheol h7585)
34 Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
and all Israel who [are] round about them have fled at their voice, for they said, 'Lest the earth swallow us;'
35 Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
and fire hath come out from Jehovah, and consumeth the two hundred and fifty men bringing near the perfume.
36 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah speaketh unto Moses, saying,
37 “Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
'Say unto Eleazar son of Aaron the priest, and he lifteth up the censers from the midst of the burning, and the fire scatter thou yonder, for they have been hallowed,
38 Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
[even] the censers of these sinners against their own souls; and they have made them spread-out plates, a covering for the altar, for they have brought them near before Jehovah, and they are hallowed; and they are become a sign to the sons of Israel.'
39 Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
And Eleazar the priest taketh the brazen censers which they who are burnt had brought near, and they spread them out, a covering for the altar —
40 monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
a memorial to the sons of Israel, so that a stranger who is not of the seed of Aaron doth not draw near to make a perfume before Jehovah, and is not as Korah, and as his company, — as Jehovah hath spoken by the hand of Moses to him.
41 Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
And all the company of the sons of Israel murmur, on the morrow, against Moses and against Aaron, saying, 'Ye — ye have put to death the people of Jehovah.'
42 Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
And it cometh to pass, in the company being assembled against Moses and against Aaron, that they turn towards the tent of meeting, and lo, the cloud hath covered it, and the honour of Jehovah is seen;
43 Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
and Moses cometh — Aaron also — unto the front of the tent of meeting.
44 ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah speaketh unto Moses, saying,
45 “Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
'Get you up from the midst of this company, and I consume them in a moment;' and they fall on their faces,
46 Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
and Moses saith unto Aaron, 'Take the censer, and put on it fire from off the altar, and place perfume, and go, hasten unto the company, and make atonement for them, for the wrath hath gone out from the presence of Jehovah — the plague hath begun.'
47 Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
And Aaron taketh as Moses hath spoken, and runneth unto the midst of the assembly, and lo, the plague hath begun among the people; and he giveth the perfume, and maketh atonement for the people,
48 Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
and standeth between the dead and the living, and the plague is restrained;
49 Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
and those who die by the plague are fourteen thousand and seven hundred, apart from those who die for the matter of Korah;
50 Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.
and Aaron turneth back unto Moses, unto the opening of the tent of meeting, and the plague hath been restrained.

< Numeri 16 >