< Numeri 15 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Opet reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo,
Reci sinovima Izrailjevijem i kaži im: kad doðete u zemlju gdje æete nastavati, koju æu vam ja dati,
3 ndipo mukamadzapereka kwa Yehova, nsembe yotentha pa moto ya ngʼombe kapena nkhosa monga fungo lokoma kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena nsembe zina, nsembe yapadera chifukwa cha lumbiro kapena nsembe yoperekedwa mwaufulu kapenanso yoperekedwa pa chikondwerero,
I stanete prinositi žrtvu ognjenu Gospodu, žrtvu paljenicu ili žrtvu zavjeta radi ili od drage volje, ili o praznicima svojim, gotoveæi miris ugodni Gospodu od krupne ili od sitne stoke,
4 munthu amene akubweretsa zopereka zake, azikapereka kwa Yehova chopereka chachakudya cholemera kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta wokwana lita imodzi.
Tada ko prinese prinos svoj Gospodu, neka donese uza nj dar, desetinu efe bijeloga brašna pomiješana s èetvrtinom ina ulja.
5 Pamodzi ndi mwana wankhosa aliyense wa nsembe yopsereza kapena nsembe ina, muzikakonzanso lita imodzi la vinyo ngati chopereka cha chakumwa.’”
I vina èetvrt ina za naljev donesi uz žrtvu paljenicu ili uz drugu žrtvu, na svako jagnje.
6 “Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, muzikakonzanso chopereka cha chakudya cholemera makilogalamu awiri a ufa wosalala, wosakaniza ndi mafuta okwanira lita imodzi ndi theka,
A uz ovna donesi dar, dvije desetine bijeloga brašna pomiješana s treæinom ina ulja,
7 ndi vinyo wokwanira lita imodzi ndi theka ngati chopereka cha chakumwa. Muzikapereka monga nsembe yopereka fungo lokoma kwa Yehova.
I vina za naljev treæinu ina prinijeæeš za miris ugodni Gospodu.
8 “‘Pamene mukukonza mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse: ya lumbiro lapadera kapena nsembe yachiyanjano kwa Yehova,
A kad prinosiš tele na žrtvu paljenicu ili na žrtvu radi zavjeta ili na žrtvu zahvalnu Gospodu,
9 pamodzi ndi mwana wangʼombe wamwamunayo muzibweretsa nsembe yachakudya yolemera makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta okwana malita awiri.
Onda neka se donese uz tele dar, tri desetine efe bijeloga brašna pomiješana s po ina ulja,
10 Komanso muzibweretsa vinyo wokwanira malita awiri monga chopereka chachakumwa. Imeneyi idzakhala chopereka chotentha pa moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
I vina donesi za naljev po ina; to je žrtva ognjena za miris ugodni Gospodu.
11 Ngʼombe yayimuna iliyonse kapena nkhosa yayimuna iliyonse, mwana wankhosa aliyense kapena mbuzi yayingʼono, zizikonzedwa motere.
Tako neka bude uza svakoga vola i uza svakoga ovna i uza svako živinèe izmeðu ovaca ili koza.
12 Ngakhale zingachuluke chotani, chitani izi kwa iliyonse ya nyamazo.
Prema broju koliko prinesete, uèinite tako uza svako, koliko ih bude.
13 “‘Mbadwa iliyonse ya mu Israeli izichita zimenezi pamene ibweretsa nsembe yotentha pa moto kuti ikhale fungo lokoma kwa Yehova.
Svaki domorodac tako neka èini prinoseæi žrtvu paljenicu za miris ugodni Gospodu.
14 Ku mibado yanu yonse ya mʼtsogolo, pamene mlendo kapena wina aliyense wokhala pakati panu apereka chopereka chotentha pa moto kuti chikhale fungo lokoma kwa Yehova, azichita mofanana ndi momwe inu mumachitira.
Tako ako bude meðu vama i došljak ili ko bi se bavio meðu vama, pa bi prinio žrtvu ognjenu za miris ugodni Gospodu, neka èini onako kako vi èinite.
15 Gulu lonse likhale ndi malamulo ofanana a inu kapena mlendo wokhala pakati panu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya kwa mibado imene ikubwera. Inuyo ndi mlendo mudzakhala wofanana pamaso pa Yehova.
Zbore! vama i došljaku koji je meðu vama jedan da je zakon, zakon vjeèan od koljena na koljeno; došljak æe biti kao i vi pred Gospodom.
16 Mudzakhale ndi malamulo ndi miyambo yofanana, inuyo ndi mlendo wokhala pakati panu.’”
Jedan zakon i jedna uredba da bude vama i došljaku, koji je meðu vama.
17 Yehova anawuza Mose kuti,
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
18 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo unene kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukutengeraniko
Kaži sinovima Izrailjevijem i reci im: kad doðete u zemlju, u koju æu vas ja odvesti,
19 ndipo mukakadya chakudya cha mʼdzikolo, mukapereke gawo lina kwa Yehova monga chopereka.
Pa stanete jesti hljeb one zemlje, tada prinesite prinos Gospodu.
20 Pa buledi wanu woyamba, mukapereke mmodzi monga nsembe, ngati chopereka chochokera ku malo wopunthira tirigu.
Od prvina tijesta svojega prinosite u prinos kolaè, kao prinos od gumna tako ga prinosite.
21 Pa mibado yanu yonse muzidzapereka chopereka ichi kwa Yehova kuchokera ku zakudya zanu zoyamba za mʼnthaka.
Od prvina tijesta svojega dajite Gospodu prinos od koljena do koljena.
22 “‘Ndipo ngati muchimwa mosadziwa posasunga ena mwa malamulo awa amene Yehova wapereka kwa Mose,
A kad biste pogriješili, te ne biste uèinili svijeh ovijeh zapovijesti, koje kaza Gospod Mojsiju,
23 lina lililonse mwa malamulo a Yehova amene wapereka kwa inu kudzera mwa Mose, kuyambira tsiku limene Yehova anawapereka mpaka mibado ya mʼtsogolo,
Sve što vam je zapovjedio Gospod preko Mojsija, od dana kad zapovjedi Gospod i poslije od koljena do koljena,
24 ndipo ngati zimenezi zachitika osati mwadala ndipo gulu lonse silinadziwe, zikatero gulu lonselo lipereke mwana wangʼombe wamwamuna monga nsembe yopsereza kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova pamodzinso ndi chopereka chachakudya ndi chopereka cha chakumwa ndi mbuzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo potsata zimene zinalamulidwa.
Ako se bude uèinilo pogrješkom, da zbor ne zna, onda sav zbor neka prinese na žrtvu paljenicu za miris ugodni Gospodu tele s darom njegovijem i s naljevom njegovijem po uredbi, i jedno jare na žrtvu za grijeh.
25 Wansembe apereke nsembe yopepesera machimo a gulu lonse la Aisraeli, ndipo adzakhululukidwa, pakuti linali tchimo lochita mosadziwa. Ndipo chifukwa cha tchimo lawolo, abweretse kwa Yehova nsembe yotentha pa moto ndi nsembe yopepesera machimo.
I sveštenik neka oèisti sav zbor sinova Izrailjevijeh, i oprostiæe im se, jer je pogrješka i oni donesoše pred Gospoda svoj prinos za žrtvu ognjenu Gospodu i prinos za grijeh svoj radi pogrješke svoje.
26 Gulu lonse la Aisraeli ndi alendo okhala pakati pawo adzakhululukidwa chifukwa anthu onsewo anachimwa mosadziwa.
Oprostiæe se svemu zboru sinova Izrailjevijeh i došljaku koji se bavi meðu njima, jer je pogrješka svega naroda.
27 “‘Koma ngati munthu mmodzi achimwa mosadziwa, ayenera kubweretsa mbuzi yayikazi ya chaka chimodzi kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
Ako li jedna duša zgriješi ne znajuæi, neka prinese kozu od godine na žrtvu za grijeh.
28 Wansembe apereke nsembe yopepesera machimowo pamaso pa Yehova chifukwa cha munthu yemwe anachimwa mosadziwayo. Nsembe yopepesera tchimo lakelo ikaperekedwa, munthuyo adzakhululukidwa.
I sveštenik neka oèisti dušu koja bude zgriješila ne znajuæi pred Gospodom, i kad je oèisti oprostiæe joj se.
29 Lamulo lomweli ligwiritsidwe ntchito kwa aliyense wochimwa mosadziwa, kaya ndi mbadwa ya mu Israeli kapena mlendo.
I za roðenoga u zemlji sinova Izrailjevijeh i za došljaka, koji se bavi meðu vama, jedan zakon da bude kad ko zgriješi ne znajuæi.
30 “‘Koma aliyense amene achimwa mwadala, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, nachitira chipongwe Yehova, ameneyo achotsedwe ndithu pakati pa anthu ake.
Ali ko od sile zgriješi izmeðu roðenijeh u zemlji ili izmeðu došljaka, on ruži Gospoda; neka se istrijebi ona duša iz naroda svojega.
31 Popeza wanyoza mawu a Yehova ndi kuphwanya malamulo ake. Munthu ameneyo achotsedwe ndithu, kuchimwa kwake kudzakhala pa iyeyo.’”
Jer prezre rijeè Gospodnju, i zapovijest njegovu pogazi; neka se istrijebi ona duša; bezakonje je njezino na njoj.
32 Aisraeli ali mʼchipululu, munthu wina anapezeka akutola nkhuni tsiku la Sabata.
A kad bijahu sinovi Izrailjevi u pustinji, naðoše jednoga gdje kupi drva u subotu.
33 Amene anamupeza akutola nkhunizo anabwera naye kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa gulu lonse
I koji ga naðoše gdje kupi drva, dovedoše ga k Mojsiju i k Aronu i ka svemu zboru.
34 ndipo anamutsekera mʼndende chifukwa sankadziwa choti achite naye.
I metnuše ga pod stražu, jer ne bješe kazano šta æe se èiniti s njim.
35 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Munthu ameneyu ayenera kuphedwa. Gulu lonse liyenera kumugenda ndi miyala kunja kwa msasa.”
A Gospod reèe Mojsiju: neka se pogubi taj èovjek; neka ga zaspe kamenjem sav zbor iza okola.
36 Choncho gululo linamutengera kunja kwa msasa ndi kumupha pomugenda ndi miyala, monga momwe Yehova analamulira Mose.
I sav zbor izvede ga iza okola i zasuše ga kamenjem, i umrije, kao što zapovjedi Gospod Mojsiju.
37 Yehova anawuza Mose kuti,
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
38 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pa mibado yanu yonse muzisokerera mphonje pa ngodya za zovala zanu ndipo pa ngodya ya mphonje iliyonse azisokererapo chingwe chobiriwira.
Reci sinovima Izrailjevijem i kaži im, neka udaraju rese po skutovima od haljina svojih od koljena do koljena, i nad rese neka meæu vrvcu plavu.
39 Mudzakhala ndi mphonje zimenezi kuti mukaziona muzikakumbukira malamulo onse a Yehova ndi kuwamvera kuti musamatsatenso zilakolako za mʼmitima mwanu ndi za maso anu.
I imaæete rese zato da se gledajuæi ih opominjete svijeh zapovijesti Gospodnjih i tvorite ih, i da se ne zanosite za srcem svojim i za oèima svojima, za kojima èinite preljubu;
40 Motero mudzakumbukira kumvera malamulo anga ndipo mudzakhala opatulikira a Mulungu wanu.
Nego da pamtite i tvorite sve zapovijesti moje, i budete sveti Bogu svojemu.
41 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Ja sam Gospod Bog vaš, koji sam vas izveo iz zemlje Misirske, da vam budem Bog. Ja sam Gospod Bog vaš.

< Numeri 15 >