Aionian Verses
Ngakhale kuti ana ake onse aamuna ndi aakazi anasonkhana kudzamutonthoza, iye anakana kutonthozedwa. Iye anati, “Ayi. Ndidzalira mpaka ndidzapite kwa mwana wanga ku manda.” Choncho Israeli anapitirirabe kulira mwana wake. (Sheol )
(parallel missing)
Koma Yakobo anati, “Mwana wanga sapita nanu kumeneko; mkulu wake anamwalira ndipo watsala yekha. Ngati choyipa chitamuchitikira pa ulendo mukupitawu, ndiye kuti ndi mmene ndakalambiramu inu mudzandipha ndi chisoni chotere.” (Sheol )
(parallel missing)
Tsopano mukanditengeranso uyu, nakaphedwa mu njira ndiye kuti mudzandikankhira ku manda ndi chisoni.’ (Sheol )
(parallel missing)
ndipo akakaona kuti mnyamatayu palibe, basi akafa. Ife tidzakhala ngati takankhira abambo athu ku manda ndi chisoni. (Sheol )
(parallel missing)
Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol )
(parallel missing)
Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol )
(parallel missing)
Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol )
(parallel missing)
“Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol )
(parallel missing)
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
(parallel missing)
Iwe uchite kwa iye molingana ndi nzeru zako, koma usalole kuti afe ndi ukalamba ndi kupita ku manda mwamtendere. (Sheol )
(parallel missing)
Koma tsopano usamuyese ngati munthu wosalakwa. Iwe ndiwe munthu wanzeru. Udzadziwa choti uchite naye. Ngakhale ndi wokalamba, aphedwe ndithu.” (Sheol )
(parallel missing)
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol )
(parallel missing)
Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol )
(parallel missing)
“Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol )
(parallel missing)
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol )
(parallel missing)
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol )
(parallel missing)
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol )
(parallel missing)
Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa. (Sheol )
(parallel missing)
Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol )
(parallel missing)
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol )
Ker spomina nate ni v smrti sami; v grobu kdo te bode slavil? (Sheol )
Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol )
Nazaj se bodo podili krivični noter do groba; vsi narodi, ki so pozabili Boga. (Sheol )
chifukwa Inu simudzandisiya ku manda, simudzalola kuti woyera wanu avunde. (Sheol )
Ker duše moje ne bodeš pustil v grobu, ne pripustil ljubljencu svojemu, da vidi trohnobo. (Sheol )
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
Groba bolečine me obhajajo, smrtne zanke so mi na poti. (Sheol )
Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol )
Gospod, izpeljal si iz groba dušo mojo, ohranil me živega, da ne idem v grob. (Sheol )
Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol )
Gospod, naj se ne osramotim, ker te kličem; osramoté se naj krivični, pogubé se v grob. (Sheol )
Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol )
Kakor živino pasla jih bode smrt razpostavljene v grobu, dokler jim gospodujejo pravični tisto jutro, in obliko njih pokonča pekel, iz prebivališča njegovega. (Sheol )
Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol )
Ali Bog bode rešil dušo mojo groba, ko me bode sprejel mogočno. (Sheol )
Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol )
Napadla jih bode smrt terjalka, živi pogreznejo se v grob; ker hudobija je, kjer bivajo oni, v njih sredi. (Sheol )
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu kwa ine; mwandipulumutsa ku malo ozama a manda. (Sheol )
Ker velika je milost tvoja do mene, in rešil si dušo mojo iz spodnjega groba. (Sheol )
Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol )
Ker nasitena je z nadlogami duša moja, in življenje moje se bliža grobu. (Sheol )
Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa? Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda? (Sela) (Sheol )
Kateri mož bi živel tako, da ne izkusi smrti, reši se sam groba? (Sheol )
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
Ko me obdajajo smrtne bolečine, in me obhajajo grobne stiske; nadlogo in žalost nahajam. (Sheol )
Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol )
Ko bi stopil na nebesa, tam si; ali bi ležišče izbral v grobu, glej tu si. (Sheol )
Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza, ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.” (Sheol )
Kakor bi kdo razsekal in razklal zemljo, raztresejo se naše kosti, v groba žrelo. (Sheol )
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
(parallel missing)
Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol )
(parallel missing)
Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol )
(parallel missing)
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol )
(parallel missing)
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol )
(parallel missing)
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol )
(parallel missing)
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol )
(parallel missing)
Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol )
(parallel missing)
Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol )
(parallel missing)
Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru. (Sheol )
(parallel missing)
Undiyike pamtima pako ngati chidindo, ngati chidindo cha pa dzanja lako; pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa, nsanje ndiyaliwuma ngati manda. Chikondi chimachita kuti lawilawi ngati malawi a moto wamphamvu. (Sheol )
(parallel missing)
Nʼchifukwa chake ku manda sikukhuta ndipo kwayasama kwambiri kukamwa kwake; mʼmandamo mudzagweranso anthu otchuka a mu Yerusalemu pamodzi ndi anthu wamba ochuluka; adzagweramo ali wowowo, nʼkuledzera kwawoko. (Sheol )
(parallel missing)
“Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol )
(parallel missing)
Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol )
(parallel missing)
Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol )
(parallel missing)
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol )
(parallel missing)
Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol )
(parallel missing)
Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol )
(parallel missing)
Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol )
(parallel missing)
Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol )
(parallel missing)
Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol )
(parallel missing)
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene mkungudzawo unatsikira ku manda, ndinawuza nyanja kuti iwulire maliro pakuwuphimba. Ndinawumitsa mitsinje ndipo madzi ambiri anaphwa. Ndinabweretsa mdima pa Lebanoni chifukwa cha mtengowo ndipo mitengo yonse ya mʼdzikomo inawuma. (Sheol )
(parallel missing)
Mitundu ya anthu inagwedezeka pakumva mkokomo wa kugwa kwake, pamene ndinawutsitsira ku manda pamodzi ndi iwo amene anafa. Pamenepo ku dziko la akufa mitengo yonse ya ku Edeni pamodzi ndi ya ku Lebanoni yosankhidwa bwino inasangalatsidwa chifukwa cha zimenezi. (Sheol )
(parallel missing)
Amene ankakhala mu mthunzi wake, amene ankayanjana nawo, iwonso anapita nawo pamodzi ku manda, kukakhala pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga pakati pa mitundu ya anthu. (Sheol )
(parallel missing)
Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’ (Sheol )
(parallel missing)
Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo. (Sheol )
(parallel missing)
“Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol )
(parallel missing)
Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa, dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko. Ngakhale atakwera kumwamba Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko. (Sheol )
(parallel missing)
Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol )
(parallel missing)
Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo; ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika. Pakuti ngodzikonda ngati manda, ngosakhutitsidwa ngati imfa, wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse. (Sheol )
(parallel missing)
Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wokwiyira mʼbale wake adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene wonena mʼbale wake kuti, ‘Ndiwe wopanda phindu,’ adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu lalikulu. Ndipo aliyense amene anganene mnzake ‘wopandapake’ adzatengeredwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene angamunene mnzake kuti, ‘Chitsiru iwe,’ adzaponyedwa ku gehena. (Geenna )
A jaz vam pravim, da vsak, kdor se brez razloga jezí na brata svojega, kriv bo sodbe; kdorkoli pa reče bratu svojemu: Raka! kriv bo zbora; a kdorkoli reče: Prismoda! kriv bo peklenskega ognja. (Geenna )
Ngati diso lako lakumanja likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna )
Če te pa oko tvoje desno pohujšuje, izderi ga, in vrzi od sebe; kajti bolje ti je, da pogine eden udov tvojih, nego da bo vse telo tvoje vrženo v pekel. (Geenna )
Ndipo ngati dzanja lako lamanja likuchimwitsa, ulidule ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna )
In če te desna tvoja roka pohujšuje, odseci jo, in vrzi od sebe; kajti bolje ti je, da pogine eden udov tvojih, nego da bo vse telo tvoje vrženo v pekel. (Geenna )
Musamaope amene amapha thupi koma sangathe kuchotsa moyo. Koma muziopa Iye amene akhoza kupha mzimu ndi kuwononga thupi mu gehena. (Geenna )
In ne bojte se tistih, kteri ubijajo telo, duše pa ne morejo ubiti; bojte se pa marveč tistega, kteri more dušo in telo pogubiti v peklu. (Geenna )
Ndipo iwe Kaperenawo, kodi udzakwezedwa kufika kumwamba? Ayi, udzatsitsidwa mpaka pansi kufika ku Hade. Ngati zodabwitsa zimene zinachitika mwa iwe, zikanachitika mu Sodomu, bwenzi iye alipo kufikira lero. (Hadēs )
In ti, Kapernaum! ki si se do neba povzdignil, zagnan boš noter do pekla; kajti ko bi se bili v Sodomi zgodili čudeži, ki so se zgodili v tebi, prebila bi bila do današnjega dne. (Hadēs )
Aliyense amene anena mawu otsutsana ndi Mwana wa Munthu adzakhululukidwa koma aliyense wonena motsutsana ndi Mzimu Woyera sadzakhululukidwa mu mʼbado uno kapena umene ukubwerawo. (aiōn )
In če reče kdo besedo zoper sina človečjega, odpustilo mu se bo; kdor pa reče zoper svetega Duha, ne bo mu se odpustilo, ne v tem veku ne v prihodnjem. (aiōn )
Zimene zinafesedwa pakati pa minga, ndi munthu amene amamva mawu koma nkhawa za moyo uno ndi chinyengo cha chuma zimalepheretsa mawuwo kuti abale chipatso. (aiōn )
Ki je pa posejan v trnji, ta je, kdor besedo sliši; ali skrb tega svetá in ničemurnost bogastva uduší besedo, in brez sadú ostane. (aiōn )
Ndipo amene anafesa namsongole ndi Satana. Kukolola ndiko kutha kwa dzikoli ndipo otuta ndi angelo. (aiōn )
Sovražnik, kteri ga je posejal, je hudič; žetev je pa konec svetá; a kosci so angelji. (aiōn )
“Monga momwe namsongole azulidwa ndi kutenthedwa ndi moto, momwemonso kudzakhala pakutha kwa dziko. (aiōn )
Kakor se torej kukolj pobira, in v ognji sežiga, tako bo na koncu tega sveta. (aiōn )
Umu ndi mmene kudzakhalira pakutha kwa dziko. Angelo adzabwera ndi kulekanitsa oyipa ndi olungama. (aiōn )
Tako bo na koncu sveta. Angelji pojdejo, in odločili bodo hudobne izsred pravičnih. (aiōn )
Ndipo Ine ndikuwuza iwe kuti ndiwe Petro ndipo pa thanthwe ili Ine ndidzamangapo mpingo wanga ndipo makomo a ku gehena sadzawugonjetsa. (Hadēs )
Pravim pa tudi jaz tebi, da si ti Peter; in na tej skali bom sezidal cerkev svojo, in vrata peklenska je ne bodo premagala. (Hadēs )
Ngati dzanja lako kapena phazi lako likuchimwitsa, lidule ndi kulitaya. Ndi bwino kwa iwe kulowa mʼmoyo wosatha wolumala kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri kapena mapazi awiri ndi kukaponyedwa ku moto wosatha. (aiōnios )
Če te pa roka tvoja ali noga tvoja pohujšuje, odseci ji, in vrzi od sebe; bolje ti je hromemu ali brez roke priti v življenje, nego dve roki in dve nogi imeti, in vrženemu biti v večni ogenj. (aiōnios )
Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Ndi bwino kwa iwe kuti ukalowe ku moyo wosatha ndi diso limodzi kuposa ndi kukhala ndi maso awiri ndi kukaponyedwa ku moto wa gehena.” (Geenna )
In če te pohujšuje oko tvoje, izderi ga, in vrzi od sebe; bolje ti je z enim očesom priti v življenje, nego dve očesi imeti, in vrženemu biti v peklenski ogenj. (Geenna )
Taonani mnyamata wina anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Aphunzitsi, ndi chinthu chiti chabwino chimene ndiyenera kuchita kuti ndipeze moyo wosatha?” (aiōnios )
In glej, eden pristopi in mu reče: Dobri učenik! kaj dobrega naj storim, da bom imel večno življenje? (aiōnios )
Ndipo aliyense amene wasiya nyumba, kapena abale, kapena alongo, kapena bambo kapena mayi kapena mkazi, kapena ana, kapena minda chifukwa cha Ine adzalandira madalitso ochuluka ndi kulandiranso moyo wosatha. (aiōnios )
In vsak, kdor je zapustil hiše, ali brate, ali sestre, ali očeta, ali mater, ali ženo, ali otroke, ali njive, za voljo imena mojega, prejel bo stokrat več, in zadobil bo večno življenje. (aiōnios )
Ataona mtengo wamkuyu mʼmbali mwa msewu, anapitapo koma sanapeze kanthu koma masamba okhaokha. Pamenepo anati kwa mtengowo, “Usadzabalenso chipatso!” Nthawi yomweyo mtengowo unafota. (aiōn )
In ugledavši kraj poti eno smokvo, pride k njej, in ničesar ne najde na njej, razen samo listje; in reče jej: Nikoli več naj ne bo na tebi sadú na vekomaj! In usahnila je smokva precej. (aiōn )
“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumayenda maulendo ambiri pa mtunda ndi pa nyanja kuti mutembenuze munthu mmodzi, ndipo akatembenuka, mumamusandutsa kukhala mwana wa gehena kawiri kuposa inu. (Geenna )
Gorjé vam, pismarji in Farizeji, hinavci! da prehodite morje in zemljo, da pridobite enega, kteri se pojudi; in ko se je pojudil, naredite iž njega peklenskega sinú, dvakrat hujega od sebe. (Geenna )
“Njoka inu! Ana amamba! Mudzachithawa bwanji chilango cha gehena? (Geenna )
Kače! gadja zalega! kako boste ubežali sodbi peklenskega ognja? (Geenna )
Pamene Yesu anakhala pansi pa phiri la Olivi, ophunzira ake anabwera kwa Iye mwamseri nati, “Tiwuzeni, kodi izi zidzachitika liti, ndipo chizindikiro cha kubwera kwanu ndi zizindikiro za kutha kwa dziko zidzakhala chiyani?” (aiōn )
Ko je pa sedel na Oljskej gori, pristopijo posebéj k njemu učenci, govoreč: Povej nam, kedaj bo to? In kaj bo znamenje prihodu tvojemu in koncu sveta? (aiōn )
“Pamenepo adzanena kwa akumanzere kwake kuti, ‘Chokani kwa Ine, inu otembereredwa, pitani ku moto wosatha wokonzedwera mdierekezi ndi angelo ake. (aiōnios )
Tedaj poreče tudi tistim na levici: Pojdite od mene, prekleti! v večni ogenj, kteri je pripravljen hudiču in angeljem njegovim. (aiōnios )
“Amenewa adzapita ku chilango chosatha pamene olungama ku moyo wosatha.” (aiōnios )
In ti pojdejo v večno trpljenje; pravični pa v večno življenje. (aiōnios )
ndi kuwaphunzitsa amvere zonse zimene ndinakulamulirani. Ndipo onani, Ine ndidzakhala pamodzi ndi inu kufikira kutha kwa dziko lapansi pano.” (aiōn )
Učeč jih, naj izpolnjujejo vse, kar sem vam ukazal; in glej, jaz sem z vami vse dní do konca sveta. Amen. (aiōn )
koma aliyense amene achitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa pakuti wachita tchimo losatha.” (aiōn , aiōnios )
Kdor se pa zarotí proti svetemu Duhu, nima odpuščanja na vekomaj, nego kriv je večne sodbe. (aiōn , aiōnios )
koma nkhawa zamoyo uno, chinyengo cha chuma ndi zokhumba za zinthu zina zimabwera ndi kutchinga mawu, ndipo amawachititsa kukhala osabala chipatso. (aiōn )
Pa skrbí tega sveta, in ničemurnost bogastva, in druge slasti se prikradejo, in udušé besedo, in brez sadú je. (aiōn )
Ngati dzanja lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo ndi dzanja limodzi kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri ndi kupita ku gehena, kumene moto wake suzima. (Geenna )
In če te pohujšuje roka tvoja, odseci jo; bolje ti je brez roke vniti v življenje, nego obe roki imeti, in oditi v pekel, v ogenj neugasljivi, (Geenna )
Ndipo ngati phazi lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo olumala kusiyana ndi kukhala ndi mapazi awiri ndi kuponyedwa mu gehena. (Geenna )
In če te noga tvoja pohujšuje, odseci jo; bolje ti je hromemu vniti v življenje, nego obe nogi imeti, in vrženemu bili v pekel, v neugasljivi ogenj, (Geenna )
Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, likolowole. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa ufumu wa Mulungu ndi diso limodzi, kusiyana ndi kukhala ndi maso awiri ndi kuponyedwa mu gehena, (Geenna )
In če te oko tvoje pohujšuje, izderi ga; bolje ti je z enim očesom vniti v kraljestvo Božje, nego obe očesi imeti, in vrženemu biti v pekel ognjeni, (Geenna )
Yesu atanyamuka, munthu wina anamuthamangira nagwa mogwada pamaso pake. Iye anafunsa kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios )
In ko izide na cesto, pribeží nekdo k njemu, in pokleknivši pred njim, vpraša ga: Dobri učenik, kaj naj storim, da zadobom večno življenje? (aiōnios )
adzalephera kulandira 100 (nyumba, abale, alongo, amayi, ana ndi minda, pamodzi ndi mazunzo) mʼbado uno ndi moyo wosatha nthawi ya mʼtsogolo. (aiōn , aiōnios )
Da ne bi prejel sedaj na tem svetu stokrat toliko, hiš in bratov in sester in mater in otrók in njiv, s preganjanjem, na drugem pa večnega življenja. (aiōn , aiōnios )
Ndipo Iye anati kwa mtengo, “Palibe amene adzadyenso chipatso kuchokera kwa iwe.” Ndipo ophunzira ake anamva Iye akunena izi. (aiōn )
In Jezus odgovorí in jej reče: Naj na vekomaj nikoli nihče s tebe sadú ne jé! In slišali so ga učenci njegovi. (aiōn )
ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn )
In kraljeval bo v hiši Jakobovej vekomaj, in kraljestvu njegovemu ne bo konca. (aiōn )
Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn )
(Kakor je govoril očetom našim, ) Abrahamu in semenu njegovemu na vekomaj. (aiōn )
(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn )
(Kakor je govoril z ustmi svetih prerokov svojih, ki so bili od nekedaj: ) (aiōn )
Ndipo ziwandazo zimamupempha mobwerezabwereza kuti asazitumize ku dzenje la mdima. (Abyssos )
In prosili so ga, naj jim ne zapové iti v brezno. (Abyssos )
Kodi iwe Kaperenawo, adzakukweza mpaka kumwamba? Ayi, adzakutsitsa mpaka ku Malo a anthu akufa. (Hadēs )
In ti, Kapernaum, ki si se do neba povzdignil, zagnan boš do pekla. (Hadēs )
Nthawi ina katswiri wa malamulo anayimirira kuti ayese Yesu. Iye anati, “Aphunzitsi, ndichite chiyani kuti ndikhale ndi moyo wosatha?” (aiōnios )
In glej, učenik postave vstane, in izkušajoč ga, reče: Učenik, kaj naj storim, da zadobóm večno življenje? (aiōnios )
Koma Ine ndidzakuonetsani amene muyenera kumuopa: Wopani Iye, amene pambuyo pakupha thupi, ali ndi mphamvu yakukuponyani ku gehena. Inde, Ine ndikuwuzani, muopeni Iye. (Geenna )
Pokazal pa vam bom, koga se bojte: bojte se tistega, kteri ima oblast, po tem ko je ubil, zagnati v pekel. Dà, pravim vam, tega se bojte. (Geenna )
“Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. (aiōn )
In gospodar pohvali krivičnega hlapca, da je pametno storil. Kajti sinovi tega sveta so pametniji od sinov svetlobe v svojem rodu. (aiōn )
Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya. (aiōnios )
Tudi jaz vam pravim: Naredite si prijateljev s krivičnim bogastvom, da vas, kedar ubožate, sprejmó v večna stanovališča. (aiōnios )
Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. (Hadēs )
In v peklu, ko je bil v bolečinah, povzdigne očí svoje, in ugleda Abrahama od daleč, in Lazarja na naročji njegovem. (Hadēs )
Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios )
In vpraša ga en starešina, govoreč: Učenik dobri, kaj naj storim, da zadobóm večno življenje? (aiōnios )
adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn , aiōnios )
Da ne bi prejel veliko več v tem času, a na drugem svetu večnega življenja. (aiōn , aiōnios )
Yesu anayankha kuti, “Anthu a mʼbado uno amakwatira ndi kukwatiwa. (aiōn )
In odgovarjajoč, reče jim Jezus: Sinovi tega sveta se ženijo in možé; (aiōn )
Koma mʼmoyo umene ukubwerawo, anthu amene adzaukitsidwe kwa akufa sadzakwatira kapena kukwatiwa. (aiōn )
Ali ti, kteri bodo vredni, da zadobé drugi svet, in da vstanejo od mrtvih, ne bodo se ženili ne možile, (aiōn )
kuti aliyense amene akhulupirira Iye akhale ndi moyo wosatha. (aiōnios )
Da kdorkoli veruje va-nj, ne pogine, nego da ima večno življenje. (aiōnios )
“Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi, kotero anapereka Mwana wake wobadwa yekha, kuti aliyense wokhulupirira Iye asatayike koma akhale ndi moyo wosatha. (aiōnios )
Kajti tako je Bog ljubil svet, da je sina svojega edinorojenega dal, da kdorkoli veruje va-nj, ne pogine, nego da ima večno življenje. (aiōnios )
Aliyense wokhulupirira Mwanayo ali ndi moyo wosatha, koma iye amene samvera Mwanayo sadzawuona moyo, pakuti mkwiyo wa Mulungu umakhala pa iye.” (aiōnios )
Kdor veruje v sina, ima večno življenje; a kdor ne veruje v sina, ne bo videl življenja, nego jeza Božja prebiva na njem. (aiōnios )
koma aliyense amene adzamwa madzi amene Ine ndidzamupatsa sadzamvanso ludzu. Ndithudi, madzi amene ndidzamupatsa adzakhala kasupe wamadzi wotumphukira ku moyo wosatha.” (aiōn , aiōnios )
Kdorkoli bo pa pil od vode, ktero mu bom jaz dal, ne bo ožejal vekomaj; nego voda, ktero mu bom dal, postala bo v njem studenec vode, ktera teče v večno življenje. (aiōn , aiōnios )
Ngakhale tsopano amene akukolola akulandira malipiro ake, ndipo akututa mbewu ku moyo wosatha kuti wofesa ndi wokolola asangalale pamodzi. (aiōnios )
In kdor žanje, prejema plačilo, in zbira sad za večno življenje: da se radujeta oba ob enem, kdor seje in kdor žanje. (aiōnios )
“Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene amamva mawu anga ndi kukhulupirira Iye amene ananditumiza Ine, ali ndi moyo wosatha ndipo sadzaweruzidwa. Iye wachoka mu imfa ndipo walowa mʼmoyo. (aiōnios )
Resnično resnično vam pravim, da kdor mojo besedo posluša, in veruje temu, kteri me je poslal, ima večno življenje; in ne pride na sodbo, nego prešel je iz smrti v življenje. (aiōnios )
Inu mumasanthula malemba chifukwa mumaganiza kuti mʼmalembamo muli moyo wosatha. Awa ndi malemba amene akundichitira umboni. (aiōnios )
Preglejte pisma, ker vi mislite, da imate v njih življenje, in ta so, ktera pričajo za-me. (aiōnios )
Gwirani ntchito, osati chifukwa cha chakudya chimene chimawonongeka koma chifukwa cha chakudya chimene sichiwonongeka mpaka ku moyo wosatha, chimene Mwana wa Munthu adzakupatsani. Mulungu Atate anamusindikiza chizindikiro chomuvomereza.” (aiōnios )
Trudite se, ne za jed, ktera mine, nego za jed, ktera ostane za večno življenje, ktero vam bo sin človečji dal: kajti tega je potrdil oče Bog. (aiōnios )
Pakuti chifuniro cha Atate anga ndi chakuti aliyense amene aona Mwanayo namukhulupirira akhale ndi moyo wosatha, ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza.” (aiōnios )
In volja tega, kteri me je poslal, je ta, da ima vsak, kdor vidi sina in veruje va-nj, večno življenje, in jaz ga bom obudil poslednji dan. (aiōnios )
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti Iye amene akhulupirira ali nawo moyo wosatha. (aiōnios )
Resnično resnično vam pravim: Kdor veruje v mé, ima večno življenje. (aiōnios )
Ine ndine chakudya chamoyo chochokera kumwamba. Ngati munthu adya chakudya ichi, adzakhala ndi moyo nthawi zonse. Chakudya chimenechi ndi thupi langa, limene Ine ndidzalipereka kuti anthu pa dziko lapansi akhale ndi moyo.” (aiōn )
Jaz sem živi kruh, kteri sem z neba prišel; če kdo jé od tega kruha, živel bo vekomaj. Kruh pa, kterega bom jaz dal, je telo moje, ktero bom jaz dal za življenje sveta. (aiōn )
Aliyense amene adya thupi langa ndi kumwa magazi anga ali ndi moyo wosatha ndipo Ine ndidzamuukitsa kwa akufa pa tsiku lomaliza. (aiōnios )
Kdor jé moje telo, in pije mojo kri, ima večno življenje, in jaz ga bom obudil poslednji dan. (aiōnios )
Ichi ndiye chakudya chimene chinatsika kuchokera kumwamba. Makolo athu akale anadya mana ndi kufa, koma iye amene adya chakudya ichi, adzakhala ndi moyo nthawi yonse.” (aiōn )
Ta je kruh, kteri je z neba prišel; ne kakor so očetje vaši jedli mano, in so pomrli; kdor ta kruh jé, živel bo vekomaj. (aiōn )
Simoni Petro anamuyankha Iye kuti, “Ambuye, ife tidzapita kwa yani? Inu muli ndi mawu amoyo wosatha. (aiōnios )
Pa mu odgovorí Simon Peter: Gospod, h komu pojdemo? Besede večnega življenja imaš. (aiōnios )
Pajatu kapolo alibe malo wokhazikika mʼbanja, koma mwana ndi wa mʼbanjamo nthawi zonse. (aiōn )
Suženj pa ne ostane v hiši vekomaj; sin ostane vekomaj. (aiōn )
Ine ndikukuwuzani choonadi, munthu akasunga mawu anga, sadzafa konse.” (aiōn )
Resnično resnično vam pravim: če kdo mojo besedo ohrani, ne bo videl smrti vekomaj. (aiōn )
Pamenepo Ayuda anafuwula kuti, “Tsopano ife tadziwadi kuti Inu ndi wogwidwa ndi chiwanda! Abrahamu anafa ndiponso aneneri, koma Inu mukunena kuti, ‘Ngati munthu asunga mawu anga, sadzafa.’ (aiōn )
Rekó mu torej Judje: Sedaj smo razpoznali, da hudiča imaš; Abraham je umrl in preroki, a ti praviš: Če kdo mojo besedo ohrani, ne bo okusil smrti vekomaj. (aiōn )
Palibe amene anamvapo za kutsekula maso a munthu wobadwa wosaona. (aiōn )
Od vekomaj se ni slišalo, da bi bil kdo od rojstva slepemu očí odprl. (aiōn )
Ine ndimazipatsa moyo wosatha ndipo sizidzawonongeka. Palibe amene adzazikwatula mʼdzanja langa. (aiōn , aiōnios )
In jaz jim bom dal večno življenje; in na vekomaj ne bodo poginile, in nihče jih ne bo iztrgal iz moje roke. (aiōn , aiōnios )
Aliyense amene ali ndi moyo ndi kukhulupirira Ine sadzamwalira. Kodi iwe ukukhulupirira izi?” (aiōn )
In vsak, kdor živí in veruje v mé, ne bo umrl vekomaj. Veruješ li to? (aiōn )
Munthu amene amakonda moyo wake adzawutaya, pamene munthu amene amadana ndi moyo wake mʼdziko lino lapansi adzawusungira ku moyo wosatha. (aiōnios )
Kdor dušo svojo ljubi, izgubil jo bo; a kdor dušo svojo sovraži, ohranil jo bo za večno življenje. (aiōnios )
Gulu la anthu linayankha kuti, “Ife tinamva kuchokera mʼmalamulo kuti Khristu adzakhala kwamuyaya, nanga bwanji Inu mukunena kuti, ‘Mwana wa Munthu ayenera kukwezedwa?’ Kodi Mwana wa Munthuyu ndani?” (aiōn )
Odgovorí mu ljudstvo: Mi smo slišali iz zakona, da bo Kristus ostal vekomaj; in kako praviš ti: Sin človečji mora biti povišan? Kdo je ta sin človečji? (aiōn )
Ine ndikudziwa kuti lamulo lake ndi moyo wosatha. Choncho chilichonse chimene Ine ndinena ndi chimene Atate andiwuza.” (aiōnios )
In vém, da je zapoved njegova večno življenje. Kar torej jaz govorim, govorim tako, kakor mi je oče povedal. (aiōnios )
Petro anati, “Ayi, Inu simudzandisambitsa konse mapazi anga.” Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine sindisambitsa mapazi ako, ulibe gawo mwa Ine.” (aiōn )
Reče mu Peter: Ne boš mi umival nog, na vekomaj ne! Odgovorí mu Jezus: Če te ne umijem, ne boš imel deleža z menoj. (aiōn )
Ine ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani Nkhoswe ina kuti izikhala nanu nthawi zonse. (aiōn )
In jaz bom prosil očeta, in drugega tolažnika vam bo dal, da ostane z vami vekomaj, (aiōn )
Pakuti Inu munamupatsa Iye ulamuliro pa anthu onse kuti apereke moyo wosatha kwa onse amene mwamupatsa. (aiōnios )
Kakor si mu dal oblast nad vsem človeštvom, da vsem ktere si mu dal, dá večno življenje. (aiōnios )
Tsono moyo wosathawo ndi uwu: Iwo akudziweni Inu, Mulungu yekhayo woona, ndi Yesu Khristu, amene Inu mwamutuma. (aiōnios )
Večno življenje je pa to, da poznajo tebe edinega resničnega Boga, in kogar si poslal, Jezusa Kristusa. (aiōnios )
Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda, kapena kulekerera Woyerayo kuti awole. (Hadēs )
Ker ne boš pustil duše moje v peklu, in tudi ne boš dal, da bi svetnik tvoj videl trohnenje. (Hadēs )
Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. (Hadēs )
Videl je naprej, in povedal je za vstajenje Kristusovo, da se duša njegova ni pustila v peklu, in tudi telo njegovo ni videlo trohnenja. (Hadēs )
Iye ayenera kukhalabe kumwamba mpaka nthawi ya kukonzanso zinthu zonse monga Mulungu analonjeza kale kudzera mwa aneneri ake oyera mtima. (aiōn )
Kterega mora sicer nebo sprejeti do časov, ko se uravna vse, kar je Bog povedal z ustmi svetih prerokov svojih od nekedaj. (aiōn )
Ndipo Paulo ndi Barnaba anawayankha molimba mtima kuti, “Ife tinayenera kuyankhula Mawu a Mulungu kwa inu poyamba. Popeza inu mwawakana ndi kudziyesa nokha osayenera moyo wosatha, ife tsopano tikupita kwa anthu a mitundu ina. (aiōnios )
Tedaj Pavel in Barnaba srčno rečeta: Vam se je morala najprej govoriti beseda Božja; ko jo pa zametujete, in se nevredne štejete večnega življenja, glej, obračava se do poganov. (aiōnios )
Anthu a mitundu ina atamva izi, anakondwa ndipo analemekeza Mawu Ambuye; ndipo onse amene anawasankha kuti alandire moyo osatha anakhulupirira. (aiōnios )
Ko so pa pogani to slišali, veselili so se, in slavili so besedo Gospodovo, in verovali so, kolikor jih je bilo odločenih za večno življenje. (aiōnios )
zinaululidwa kuyambira kalekale.’ (aiōn )
Bogu so od vekomaj znana vsa dela njegova. (aiōn )
Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula. (aïdios )
Ker kar se na njem ne more videti, to se od ustvarjenja sveta opaža in vidi na delih: njegova večna moč in božanstvo, da jih ni moči zagovarjati. (aïdios )
Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Kteri so premenili resnico Božjo v laž in so izkazali večo čast in službo stvoru nego stvarniku, kteri je blagoslovljen na veke. Amen. (aiōn )
Iye adzapereka moyo wosatha kwa amene amafunafuna ulemerero, ulemu ndi moyo pochita ntchito zabwino mopirira. (aiōnios )
Tistim namreč, kteri s stanovitnostjo v dobrem delu slavo in čast in netrohljivost iščejo, večno življenje; (aiōnios )
Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu. (aiōnios )
Da bi, kakor je zakraljeval greh za smrt, tako tudi zakraljevala milost s pravico na večno življenje po Jezusu Kristusu Gospodu našem. (aiōnios )
Koma tsopano pakuti inu mwamasulidwa ku tchimo ndipo mwasanduka akapolo a Mulungu, phindu lomwe mulipeza ndi kuyera mtima ndipo chotsatira chake ndi moyo wosatha. (aiōnios )
Sedaj pa, osvobodivši se greha, a postavši Božji služabniki, imate sad svoj posvečenje, a konec večno življenje. (aiōnios )
Pakuti malipiro a tchimo ndi imfa, koma mphatso yaulere imene Mulungu amapereka ndi moyo wosatha mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōnios )
Kajti plača za greh je smrt, a dar Božji večno življenje v Kristusu Jezusu Gospodu našem. (aiōnios )
Awo ndi makolo athu. Kuchokera kwa iwo mʼthupi ndi kumene kunachokera makolo a Khristu Yesu amene ndi Mulungu wolamulira zinthu zonse, alemekezeke mpaka muyaya! Ameni. (aiōn )
Kteri so očetje, in od kterih je Kristus po mesu, kteri je Bog nad vsemi blagoslovljen na veke. Amen. (aiōn )
“kapena ‘Ndani adzatsikira ku dziko la anthu akufa?’” (ndiko, kukamutenga Khristu kwa akufa). (Abyssos )
Ali: "Kdo pojde dol v brezno? to je, da Kristusa iz mrtvih gor popelje." (Abyssos )
Pakuti Mulungu anasandutsa anthu onse a mʼndende ya kusamvera kuti Iye akaonetse chifundo kwa onse. (eleēsē )
Kajti zaprl je Bog vse v neverstvo, da bi se vseh usmilil. (eleēsē )
Pakuti zinthu zonse nʼzochokera kwa Iye, nʼzolengedwa ndi Iye ndipo zimabweretsa ulemerero kwa Iye. Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya! Ameni. (aiōn )
Kajti od njega in po njem in v njem je vse, njemu slava na veke! Amen. (aiōn )
Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro. (aiōn )
In ne ravnajte se poleg veka tega, nego premenjujte se z obnavljanjem uma svojega, da izkusite ktera je volja Božja dobra in prijetna in popolna. (aiōn )
Tsopano kwa Iye amene ali ndi mphamvu yokhazikitsa monga mwa uthenga wanga wabwino ndikulalikidwa kwa Yesu Khristu, monga mwa vumbulutso lachinsinsi chobisika kwa nthawi yayitali, (aiōnios )
Tistemu pa, kteri je mogoč vas utrditi po evangelji mojem in oznanjevanji Jezusa Kristusa, po odkritji skrivnosti od večnih časov zamolčane, (aiōnios )
koma tsopano chavumbulutsidwa ndi kudziwika kudzera mʼMalemba a uneneri mwa lamulo la Mulungu wosatha, kuti mitundu yonse ikhulupirire ndi kumvera Iye, (aiōnios )
a razodete sedaj po preroških pismih, poleg zapovedi večnega Boga, za poslušnost vere med vse pogane oznanjene, (aiōnios )
kwa Mulungu yekhayo wanzeru kukhale ulemerero kwamuyaya kudzera mwa Yesu Khristu! Ameni. (aiōn )
Samemu modremu Bogu po Jezusu Kristusu slava na veke! Amen. Rimljanom je napisan od Korinta po Febi služabnici cerkve Kenhrejske. (aiōn )
Munthu wanzeru ali kuti? Munthu wozama ndi maphunziro ali kuti? Munthu wodziwa zakuya zamakono ali kuti? Kodi Mulungu sanazipusitse nzeru za dziko lapansi? (aiōn )
Kje je modri? Kje pismar? Kje preiskovalec tega veka? Jeli ni v neumnost preobrnil Bog modrosti tega sveta? (aiōn )
Komabe ife timayankhula uthenga wa nzeru kwa okhwima, koma osati ndi nzeru ya mʼbado uno kapena ya olamula a mʼbado uno, amene mphamvu yawo ikutha. (aiōn )
Ali modrost govorimo, ktera je med popolnimi, a ne modrosti tega veka, niti poglavarjev tega veka, kteri se uničujejo. (aiōn )
Ayi, ife timayankhula za nzeru yobisika ya Mulungu, nzeru imene inabisidwa ndipo imene Mulungu anatikonzera mu ulemerero wathu isanayambe nthawi. (aiōn )
Nego govorimo modrost Božjo v skrivnosti, tisto skrito, ktero je odločil Bog pred vekovi za našo slavo, (aiōn )
Palibe olamulira aliyense wa mʼbado uno amene anamumvetsetsa popeza anakamumvetsetsa sakanamupachika Ambuye wa ulemerero. (aiōn )
Ktere nikdor izmed poglavarjev tega veka ni spoznal; ker ko bi jo bili spoznali, ne bi bili Gospoda slave na križ razpeli. (aiōn )
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn )
Nikdor naj sebe ne ukanjuje; če kdo misli, da je moder med vami v tem veku, naj neumen postane, da postane moder. (aiōn )
Nʼchifukwa chake ngati zimene ine ndimadya zichititsa mʼbale wanga kugwa mu tchimo, sindidzadyanso chakudyacho kuti mʼbaleyo ndisamuchimwitse. (aiōn )
Za to če jed pohujšuje brata mojega, ne bom jedel mesa na veke, da si brata ne pohujšam. (aiōn )
Zinthu izi zinawachitikira kuti zikhale chitsanzo ndipo zinalembedwa kuti zikhale chenjezo kwa ife, amene tiyandikira nthawi ya kutha kwa zonse. (aiōn )
To se je pa vse godilo njim za izglede, a napisalo se je za svarilo nam, na ktere so prišli konci vekov. (aiōn )
“Iwe imfa, kupambana kwako kuli kuti? Iwe imfa, ululu wako uli kuti?” (Hadēs )
"Kje je, smrt, tvoje želo? kje je, pekel, tvoja zmaga?" (Hadēs )
Mulungu wa dziko lapansi anachititsa khungu anthu osakhulupirira, kuti asathe kuona kuwala kwa Uthenga Wabwino umene umaonetsa ulemerero wa Khristu, amene ndi chifaniziro cha Mulungu. (aiōn )
V kterih je Bog tega veka oslepil pameti nevernih, da jim ne zasveti svetlost evangelja slave Kristusa, kteri je podoba Božja. (aiōn )
Pakuti masautso athu ndi opepuka ndi a kanthawi, koma akutitengera ulemerero wamuyaya umene ndi wopambana kwambiri. (aiōnios )
Kajti sedanja lahka stiska naša spravlja nam obilno, preobilno večno vse pretežno slavo, (aiōnios )
Motero sitiyangʼana zinthu zimene ndi zooneka ndi maso, koma zinthu zimene ndi zosaoneka. Pakuti zimene zimaoneka ndi zosakhalitsa, koma zimene sizioneka ndi zamuyaya. (aiōnios )
Ker ne gledamo nato, kar se vidi, nego na to, kar se ne vidi; kajti to, kar se vidi, začasno je, ali kar se ne vidi, večno je. (aiōnios )
Popeza tikudziwa kuti ngati msasa wa dziko lapansi umene tikukhalamo uwonongeka, tili ndi nyumba yochokera kwa Mulungu, nyumba yamuyaya yakumwamba, osati yomangidwa ndi manja a anthu. (aiōnios )
Ker vemo, če zemeljska naša hiša prebivanja razpade, da imamo prebivališče od Boga, hišo ne z rokami napravljeno, večno v nebesih. (aiōnios )
Paja analemba kuti, “Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya.” (aiōn )
(Kakor je pisano: "Razsul je, dal je ubogim, njegova pravica ostaje na vek." (aiōn )
Mulungu, Atate a Ambuye Yesu, amene tiyenera kumutamanda nthawi zonse, akudziwa kuti sindikunama. (aiōn )
Bog in oče Gospoda našega Jezusa Kristusa, kteri je blagoslovljen na veke, ve, da ne lažem. (aiōn )
Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. (aiōn )
Kteri je dal sebe za grehe naše, da nas reši iz sedanjega hudega veka po volji Boga in očeta našega, (aiōn )
Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Kteremu slava na veke vekov. Amen. (aiōn )
Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. (aiōnios )
Ker kdor seje v meso svoje, od mesa bo žel pogubo, a kdor seje v duha, od duha bo žel življenje večno. (aiōnios )
Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. (aiōn )
Nad vsako poglavarstvo in oblast in moč in gospostvo, in vsako ime, ki se imenuje ne samo na tem svetu, nego tudi na prihodnjem; (aiōn )
mmene inu munkakhalamo pamene munkatsatira njira za dziko lapansi ndi za ulamuliro waufumu wa mlengalenga, mzimu umene ukugwira ntchito tsopano mwa amene samvera. (aiōn )
V katerih ste nekdaj hodili po duhu tega sveta, po knezu oblasti v zraku, duha delujočega zdaj v nevere sinovih, (aiōn )
ndi cholinga chakuti mʼnthawi imene ikubwera, Iyeyo adzaonetse chuma choposa cha chisomo chake, choonetsedwa mwa kukoma mtima kwake kwa ife mwa Khristu Yesu. (aiōn )
Da pokaže v vékih prihodnjih presilno bogastvo milosti svoje v blagodušnosti do nas v Kristusu Jezusu. (aiōn )
Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. (aiōn )
In razsvetliti vse, katero je deleštvo skrivnosti od vekomaj skrite v Bogu, kateri je vse vstvaril po Jezusu Kristusu, (aiōn )
Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōn )
Po sklepu od vekomaj, katerega je storil v Kristusu Jezusu, Gospodu našem, (aiōn )
Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Njemu slava v občini v Kristusu Jezusu na vse rodove, na vekov veke! Amen. (aiōn )
Pakuti sitikulimbana ndi thupi ndi magazi, koma tikulimbana ndi maufumu, maulamuliro, mphamvu za dziko la mdima, ndi mphamvu zoyipa kwambiri zauzimu zamlengalenga. (aiōn )
Ker boj nam ni zoper kri in meso, nego zoper poglavarstva, zoper oblasti, zoper svétovne mogočnike temé tega svetá, zoper duhove hudobe v nebesih. (aiōn )
Kwa Mulungu ndi Atate athu, kukhale ulemerero mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Bogu pa in očetu našemu slava na vekov veke! Amen. (aiōn )
chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. (aiōn )
Skrivnost skrito od vekov in od rodov; zdaj pa se je razodela svetim njegovim; (aiōn )
Adzalangidwa ndi chiwonongeko chamuyaya ndipo sadzaonanso nkhope ya Ambuye ndi ulemerero wamphamvu zake (aiōnios )
Kateri bodo za kazen trpeli večno pogubo izpred obličja Gospodovega in izpred slave moči negove, (aiōnios )
Ambuye athu Yesu Khristu mwini ndi Mulungu Atate wathu, amene anatikonda ife ndipo mwachisomo chake anatipatsa kulimba mtima kwamuyaya ndi chiyembekezo chabwino, (aiōnios )
Sam pa Gospod naš Jezus Kristus in Bog in oče naš, ki nas je ljubil in dal nam večno tolažbo in dobro upanje v milosti, (aiōnios )
Ndipo pa chifukwa chimenechi, Mulungu anandichitira chifundo, kuti mwa ine, wochimwitsitsa, Khristu Yesu aonetse kuleza mtima kwake konse kuti ndikhale chitsanzo cha omwe angathe kumukhulupirira ndi kulandira moyo wosatha. (aiōnios )
Ali za to sem usmiljenje zadobil, da bi v meni prvem Kristus pokazal vso svojo potrpežljivost za zgled njim, ki bodo verovali vanj za večno življenje. (aiōnios )
Tsopano kwa Mfumu yamuyaya, yosafa, yosaoneka, amene Iye yekha ndiye Mulungu, kukhale ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Kralju pa svetov, neminljivemu, nevidnemu, samemu modremu Bogu, čast in slava na vekov veke! Amen. (aiōn )
Menya nkhondo yabwino yachikhulupiriro. Gwiritsitsa moyo wosatha umene anakuyitanira pamene unavomereza bwino lomwe pamaso pa mboni zambiri. (aiōnios )
Bij lepi boj vere; poprimi se večnega življenja, za katero si bil tudi poklican in si spoznal lepo spoznanje pred mnogimi pričami. (aiōnios )
Ndiye yekha wosafa ndipo amakhala mʼkuwala koopsa. Mulungu amene munthu aliyense sanamuone. Kwa Iye kukhale ulemu ndi mphamvu mpaka muyaya. Ameni. (aiōnios )
Kateri ima sam neumrjočnost, v svetlobi bivajoč ne dohodni; katerega ni videl ljudî nobeden, in tudi videti ne more; njemu čast in moč večna! Amen. (aiōnios )
Anthu onse amene ali ndi chuma uwalamule kuti asanyade kapena kuyika mitima yawo pa chuma chimene nʼchosadalirika. Koma chiyembekezo chawo chikhale mwa Mulungu amene amatipatsa mowolowamanja zonse zotisangalatsa. (aiōn )
Bogatinom na tem svetu naročaj, naj se ne prevzemajo; in naj ne zaupajo v bogastva negotovost, nego v Boga živega, kateri nam delí vsega obilo v uživanje; (aiōn )
Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. (aiōnios )
Kateri je nas rešil in poklical sè svetim poklicem: ne po delih naših, nego po svojem sklepu in milosti, dani nam v Kristusu Jezusu pred večnimi časi; (aiōnios )
Choncho ndikupirira chilichonse chifukwa cha osankhidwa, kuti nawonso apulumutsidwe ndi Khristu Yesu ndi kulandira ulemerero wosatha. (aiōnios )
Zato vse pretrpim zaradi izvoljenih, da tudi oni zveličanje zadobé v Kristusu Jezusu z večno slavo. (aiōnios )
Paja Dema anandisiya chifukwa chokonda dziko lapansi lino, ndipo anapita ku Tesalonika. Kresike anapita ku Galatiya ndipo Tito anapita ku Dalimatiya. (aiōn )
Kajti Dema me je zapustil iz ljubezni do tega sveta, in potoval je v Tesaloniko; Krescent v Galacijo, Tit v Dalmacijo; (aiōn )
Ambuye adzandilanditsa ku chilichonse chofuna kundichita choyipa ndipo adzandisamalira bwino mpaka kundilowetsa chonse mu ufumu wake wakumwamba. Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya. (aiōn )
In otél me bode Gospod vsakega hudega dela in rešil v kraljestvo svoje nebeško; njemu slava na vekov veke! Amen. (aiōn )
ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. (aiōnios )
Na zaupanje večnega življenja, katero je obljubil Bog resnični pred večnimi časi; (aiōnios )
Chisomo chimatiphunzitsa kukana moyo osalemekeza Mulungu komanso zilakolako za dziko lapansi. Ndipo chimatiphunzitsa kukhala moyo odziletsa, olungama ndi opembedza Mulungu nthawi ino, (aiōn )
Opominjajoč nas, da zatajivši brezbožnost in posvetno poželenje zmerno in pravično in pobožno živimo na tem svetu, (aiōn )
kuti titalungamitsidwa mwachisomo chake, tikhale olowamʼmalo okhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha. (aiōnios )
Da bi, opravičeni po milosti njegovi, dediči postali poleg upanja večnega življenja. (aiōnios )
Mwina chifukwa chimene unasiyana naye kwa kanthawi ndi chakuti ukhale nayenso nthawi zonse. (aiōnios )
Kajti lahko da je bil zato nekaj časa ločen od tebe, da bi ga imel vekomaj; (aiōnios )
Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. (aiōn )
govoril nam je o teh zadnjih dnevih v sinu, Katerega je postavil za dediča vseh stvari, po katerem je tudi svetove naredil, (aiōn )
Koma za Mwana wake akuti, “Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya, ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu. (aiōn )
In sinu: "Prestol tvoj, o Bog, na veka vek. Pravičnosti žezlo je kraljestva tvojega žezlo. (aiōn )
Ndipo penanso anati, “Iwe ndiwe wansembe mpaka muyaya, monga mwa unsembe wa Melikizedeki.” (aiōn )
Kakor tudi drugjé pravi: "Ti, si duhovnik na vek po redu Melhizedekovem." (aiōn )
Atasanduka wangwiro kotheratu, anakhala gwero la chipulumutso chosatha kwa onse omvera Iye. (aiōnios )
In popolnjen je postal njim vsem, ki so mu poslušni, večnega zveličanja začetnik; (aiōnios )
za maubatizo, za kusanjika manja, za kuuka kwa akufa ndi za chiweruzo chotsiriza. (aiōnios )
Učnih krstov in pokladanj rók in vstajanja mrtvih in večne sodbe. (aiōnios )
Analawa kukoma kwa mawu a Mulungu ndi mphamvu za nthawi ikubwera. (aiōn )
In okusili lepo besedo Božjo, in prihodnjega življenja moči, (aiōn )
Yesu anatitsogolera kupita kumeneko, nalowako mʼmalo mwathu. Iye anasanduka Mkulu wa ansembe onse wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki. (aiōn )
Kamor je predhodnik za nas vstopil Jezus, postavši po redu Melhizedekovem višji duhovnik na vekomaj. (aiōn )
Pakuti Mulungu anamuchitira umboni kuti, “Iwe ndi wansembe wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.” (aiōn )
Priča namreč: "Ti si duhovnik na vek po redu Melhizedekovem. (aiōn )
Koma Yesu ankakhala wansembe ndi lumbiro pamene Mulungu anati, “Ambuye analumbira ndipo sangasinthe maganizo ake, ‘Iwe ndi wansembe wamuyaya.’” (aiōn )
(Oni namreč so duhovniki postali brez prisege; ta pa s prisego po njem, ki mu govori: "Prisegel je Gospod in ne bode se kesal, ti si duhovnik na vek po redu Melhizedekovem"), (aiōn )
Koma Yesu popeza ndi wamuyaya, unsembe wake ndi wosatha. (aiōn )
Ta pa, ker ostane na vek, ima duhovništvo nepremenljivo; (aiōn )
Pakuti lamulo limasankha anthu amene ndi ofowoka kukhala akulu a ansembe; koma lumbiro, lomwe linabwera pambuyo pa lamulo, linasankha Mwana, amene anapangidwa kukhala wangwiro kwamuyaya. (aiōn )
Postava namreč stavi ljudî za višje duhovnike, imajoče slabost; beseda prisege pa poleg postave sina popolnjenega vekomaj. (aiōn )
Iye sanalowemo ndi magazi ambuzi yayimuna, ana angʼombe amphongo, koma analowa Malo Opatulika kamodzi kokha ndi magazi ake, atatikonzera chipulumutso chosatha. (aiōnios )
Tudi ne po krvi kozlov in telét, nego po svoji krvi, enkrat za vselej v svetišče in je našel večno rešitev. (aiōnios )
nʼkoposa kotani magazi a Khristu, amene mwa Mzimu wamuyaya anadzipereka yekha kwa Mulungu kukhala nsembe yopanda chilema. Iye adzayeretsa chikumbumtima chathu pochotsa ntchito za imfa, kuti ife titumikire Mulungu wamoyo. (aiōnios )
Kolikanj bolj bode kri Kristusa, kateri se je po Duhu večnem daroval brez madeža Bogu, očistila vest vašo mrtvih dél, da služite Bogu živemu? (aiōnios )
Pa chifukwa chimenechi Khristu ndi mʼkhalapakati wa pangano latsopano, kuti iwo amene anayitanidwa alandire chuma chamuyaya, pakuti Iye tsopano anafa ngati dipo lomasula iwo ku machimo amene anachita ali pansi pa pangano loyamba lija. (aiōnios )
In zato je nove zaveze srednik, da, ko se je zgodila smrt za rešenje grehov po prvi zavezi, poklicani obljubo zadobé večne dedščine. (aiōnios )
Zikanatero bwenzi Khristu atamva zowawa kambirimbiri chilengedwere cha dziko lapansi. Koma tsopano anaoneka kamodzi kokha chifukwa cha onse pa nthawi yotsiriza kuti achotse tchimo podzipereka yekha nsembe. (aiōn )
(Kajti večkrat bi bil moral trpeti od ustanove sveta), sedaj pa se je enkrat prikazal po žrtvi svoji na konci sveta v izbrisanje greha. (aiōn )
Ndi chikhulupiriro timazindikira kuti dziko lapansi ndi la mmwamba zinapangidwa ndi Mawu a Mulungu, ndikuti zinthu zoonekazi zinachokera ku zinthu zosaoneka. (aiōn )
Po veri umemo, da so svetovi osnovani bili po besedi Božji, tako da ni iz prikazujočega se postalo, kar je vidno. (aiōn )
Yesu Khristu ndi yemweyo dzulo, lero ndi kunthawi zonse. (aiōn )
Jezus Kristus je včeraj in danes isti in na veke. (aiōn )
Mulungu wamtendere, amene kudzera mʼmagazi a pangano lamuyaya anaukitsa Ambuye athu Yesu kwa akufa, amene ndi Mʼbusa wamkulu, (aiōnios )
Bog pa mirú, on, ki je od mrtvih nazaj pripeljal ovác pastirja vélikega v krvi večne zaveze, (aiōnios )
akupatseni chilichonse chabwino kuti muchite chifuniro chake ndipo Mulungu achite mwa ife, chimene chingamukomere kudzera mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ku nthawi zanthawi, Ameni. (aiōn )
Gospoda našega Jezusa, pripravi vas v slehernem dobrem delu, da delate voljo njegovo, in delaj v vas, kar je njemu po volji, po Jezusu Kristusu, kateremu slava na vekov veke! Amen. (aiōn )
Lilime nalonso ndi moto, dziko la zoyipa pakati pa ziwalo za thupi. Limawononga munthu yense wathunthu. Limayika zonse za moyo wake pa moto, ndipo moto wake ndi wochokera ku gehena. (Geenna )
Tudi jezik je ogenj, svet krivice. Tako se kaže jezik med udi našimi, ki oskrunja cel život in zažiga rojstva kolo, njega pa zažiga pekel; (Geenna )
Popeza mwabadwanso, osati ndi mbewu imene imawonongeka, koma imene siwonongeka, ndiye kuti ndi Mawu a Mulungu amoyo ndi okhalitsa. (aiōn )
Prerojeni ne iz semena minljivega, nego neminljivega, po besedi Boga, ki živi in ostane vekomaj. (aiōn )
koma mawu a Ambuye adzakhala mpaka muyaya.” Ndipo awa ndi mawu amene tinalalikira kwa inu. (aiōn )
Beseda pa Gospodova ostane vekomaj." Ta pa je beseda, katera se vam je oznanila. (aiōn )
Ngati wina ayankhula, ayankhuledi mawu enieni a Mulungu. Ngati wina atumikira, atumikire ndi mphamvu imene Mulungu amapereka, kuti pa zonse Mulungu alemekezedwe mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn )
Če kdo govori, kakor izreke Božje; če kdo streže, kakor iz moči, katero deli Bog; da se v vsem oslavlja Bog po Jezusu Kristusu, kateremu je slava in moč na vekov veke. Amen. (aiōn )
Ndipo Mulungu wachisomo chonse, amene anakuyitanani ku ulemerero wake wamuyaya mwa Khristu, mutamva zowawa pa kanthawi, adzakukonzaninso ndi kukulimbitsani pa maziko olimba. (aiōnios )
Bog pa vse milosti, kateri nas je poklical v večno slavo svojo v Kristusu Jezusu, po kratkem trpljenji pripravi vas sam, utrdi, pokrepčaj, ustanóvi! (aiōnios )
Kwa Iye kukhale mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn )
Njemu slava in moč na vekov veke! Amen. (aiōn )
Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. (aiōnios )
Kajti tako se vam bode obilo dovolil vhod v večno kraljestvo Gospoda našega in zveličarja Jezusa Kristusa. (aiōnios )
Pakuti Mulungu sanalekerere angelo atachimwa paja, koma anawaponya mʼndende, nawayika mʼmaenje amdima, kuwasunga kuti adzaweruzidwe. (Tartaroō )
Kajti Bog ni prizanesel angelom, ki so grešili, temuč jih z verigami temé v pekel pahnil in hraniti jih dal v sodbo. (Tartaroō )
Koma kulani mu chisomo ndi mʼchidziwitso cha Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Temveč rastite v milosti in spoznanji Gospoda našega in zveličarja Jezusa Kristusa. Njemu slava sedaj in vekomaj! Amen. (aiōn )
Moyowo unaoneka, tinawuona ndipo tikuchitira umboni. Tikukulalikirani za moyo wosatha umene unali ndi Atate ndipo unaonekera kwa ife. (aiōnios )
(In življenje se je prikazalo, in videli smo in pričamo, in oznanjamo vam večno življenje, katero je bilo pri očetu, in prikazalo se je nam: ) (aiōnios )
Dziko lapansi likupita pamodzi ndi zilakolako zake, koma amene amachita chifuniro cha Mulungu amakhalapo mpaka muyaya. (aiōn )
In svet izgine in poželenje njegovo; kdor pa dela voljo Božjo, ostane vekomaj. (aiōn )
Ndipo chimene anatilonjeza nʼchimenechi: moyo wosatha. (aiōnios )
In ta je obljuba, katero nam je on obljubil, večno življenje. (aiōnios )
Aliyense amene amadana ndi mʼbale wake ndi wakupha, ndipo inu mukudziwa kuti wopha anthu mwa iye mulibe moyo wosatha. (aiōnios )
Vsak, kdor sovraži brata svojega, je ljudomorec; in veste, da noben ljudomorec nima večnega življenja, ki bi ostalo v njem. (aiōnios )
Ndipo umboniwo ndi uwu: Mulungu anatipatsa moyo wosatha, ndipo moyowu uli mwa Mwana wake. (aiōnios )
In to je pričanje, da nam je Bog dal večno življenje, in to življenje je v sinu njegovem. (aiōnios )
Ine ndikulemba zimenezi kwa inu, amene mwakhulupirira dzina la Mwana wa Mulungu kuti mudziwe kuti muli ndi moyo wosatha. (aiōnios )
To sem vam pisal, kateri verujete v ime sina Božjega, da veste, da imate večno življenje, in da verujete v ime sina Božjega. (aiōnios )
Tikudziwa kuti Mwana wa Mulungu anafika ndipo anatipatsa nzeru, kuti timudziwe Iye amene ali woona. Ndipo ife tili mwa Iye amene ndi woona, Mwana wake, Yesu Khristu. Iye ndi Mulungu woona ndi moyo wosatha. (aiōnios )
Vemo pa, da je sin Božji prišel, in je nam dal razum, da spoznamo resničnega; in v resničnem smo, v sinu njegovem Jezusu Kristusu. Ta je resnični Bog in življenje večno. (aiōnios )
Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya. (aiōn )
Po resnici, katera ostaja v nas, in z nami bode vekomaj; (aiōn )
Ndipo mukumbukire angelo amene sanakhutire ndi maudindo awo, koma anasiya malo awo. Angelo amenewa Mulungu anawamanga ndi maunyolo osatha, ndipo akuwasunga mʼmalo a mdima mpaka tsiku lalikulu lachiweruzo. (aïdios )
In angele, ki niso hranili poglavarstva svojega, nego so zapustili lastno domovje, shranil je v sodbo vélikega dneva z večnimi vezmí pod temo; (aïdios )
Musayiwale mizinda ya Sodomu ndi Gomora ija, ndi mizinda yoyandikana nayo. Anthu mʼmenemo anadziperekanso kuchita zadama ndi kuchita zonyansa zachilendo. Mizinda imeneyi yakhala ngati chitsanzo cha amene adzalangidwa ndi moto wosatha. (aiōnios )
Kakor Sodoma in Gomora, in mesta okolo njih, ki so enako kakor té, kurbala se in hodila za drugim mesom, so zgled, ker trpé kazen večnega ognja. (aiōnios )
Iwowa ali ngati mafunde awukali apanyanja, amene amatulutsa thovu la zonyansa zawo. Amenewa ali ngati nyenyezi zosochera, ndipo Mulungu akuwasungira mdima wandiweyani mpaka muyaya. (aiōn )
Divji morski valovi, ki izpenjavajo lastno sramoto: zvezde tavajoče, katerim je mrak teme hranjen vekomaj. (aiōn )
Khalani mʼchikondi cha Mulungu pamene mukudikira chifundo cha Ambuye athu Yesu Khristu kuti akubweretsereni moyo wosatha. (aiōnios )
Hranite se v ljubezni Božji, pričakujte usmiljenje Gospoda našega Jezusa Kristusa v večno življenje! (aiōnios )
kwa Mulungu yekhayo, Mpulumutsi wathu, kwa Iye kukhale ulemerero, ukulu, mphamvu ndi ulamuliro, mwa Yesu Khristu Ambuye athu, kuyambira isanayambe nthawi, tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Edinemu modremu Bogu, zveličarju našemu, slava in veličastvo, krepost in oblast zdaj in na vse veke! Amen. (aiōn )
ndipo watisandutsa mafumu ndi ansembe kuti tizitumikira Mulungu ndi Atate ake. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu ku nthawi zosatha, Ameni. (aiōn )
(In naredil nas za kralje in duhovnike Bogu in očetu svojemu), njemu slava in krepost na vekov veke! Amen. (aiōn )
Ine ndine Wamoyo; ndinali wakufa ndipo taona ndine wamoyo mpaka muyaya! Ndipo ndili ndi makiyi a imfa ndi Hade. (aiōn , Hadēs )
In bil sem mrtev, in glej, živ sem na vekov veke, amen; in ključe imam od pekla in smrti. (aiōn , Hadēs )
Nthawi zonse zamoyozo zimapereka ulemerero, ulemu ndi mayamiko kwa uja wokhala pa mpando waufumu, amene ali ndi moyo wamuyaya. (aiōn )
In kader bodejo dale živali slavo in čast in hvalo sedečemu na prestolu, živečemu na vekov veke, (aiōn )
Izi zikamachitika akuluakulu 24 aja amadzigwetsa pansi pamaso pa wokhala pa mpando waufumuyo, namupembedza wokhala ndi moyo wamuyayayo. Iwo amaponya pansi zipewa zawo zaufumu patsogolo pa mpando waufumu nati: (aiōn )
Padli bodo štiri in dvajseteri starejšine pred sedečega na prestolu in molili živečega na vekov veke in vrgli vence svoje pred prestol, govoreč: (aiōn )
Kenaka ndinamva mawu a cholengedwa chilichonse kumwamba, pa dziko lapansi, kunsi kwa dziko lapansi, pa nyanja ndi zonse zili mʼmenemo zikuyimba kuti, “Kwa wokhala pa mpando waufumu ndi kwa Mwana Wankhosa, kukhale mayamiko, ulemu, ulemerero ndi mphamvu (aiōn )
In vsaka stvar, katera je na nebu in na zemlji in pod zemljo, in na morji kar je, in kar je v njih vse, čul sem govoreče: Sedečemu na prestolu in jagnjetu hvala in čast in slava in moč na vekov veke! (aiōn )
Nditayangʼana patsogolo panga ndinaona kavalo wotuwa! Wokwerapo wake dzina lake linali Imfa ndipo Hade inali kumutsatira pambuyo pake. Anapatsidwa ulamuliro pa gawo limodzi la magawo anayi a dziko lapansi kuti aphe ndi lupanga, njala, mliri, ndi zirombo zakuthengo za mʼdziko lapansi. (Hadēs )
In videl sem, in glej: konj bled, in sedeči na njem, imé mu smrt, in pekel ga spremlja; in dala se jima je oblast pomoriti četrtino zemlje z mečem in lakoto in kugo, in od zveri zemeljskih. (Hadēs )
Iwo anati, “Ameni! Matamando ndi ulemerero, nzeru, mayamiko, ulemu, ulamuliro ndi mphamvu zikhale kwa Mulungu wathu kunthawi zanthawi, Ameni!” (aiōn )
Amen! Hvala in slava in modrost in zahvala in čast in moč in krepost Bogu našemu na vekov veke! Amen. (aiōn )
Mngelo wachisanu anayimba lipenga lake, ndipo ndinaona nyenyezi ikugwa pa dziko lapansi kuchokera ku thambo. Nyenyeziyo inapatsidwa kiyi ya ku chidzenje chakuya. (Abyssos )
In peti angelj zatrobi, in videl sem zvezdo iz neba padšo na zemljo, in dal se ji je ključ od vodnjaka brezna; (Abyssos )
Nyenyeziyo itatsekula pa chidzenje chakuyacho panatuluka utsi ngati wochokera mʼngʼanjo yayikulu. Dzuwa ndi thambo zinada chifukwa cha utsi ochokera mʼdzenjemo. (Abyssos )
In odpre vodnjak brezna, in privali se dim iz vodnjaka, kakor dim peči velike, in solnce otemni in zrak od dima iz vodnjaka. (Abyssos )
Mfumu yawo inali mngelo wolamulira Chidzenje chakuya chija. Mʼchihebri dzina lake ndi Abadoni ndipo mʼChigriki ndi Apoliyoni (tanthauzo lake ndiye kuti, Wowononga). (Abyssos )
In nad seboj imajo kralja angela brezna; ime mu po hebrejsko: Abadon, in po grško ima ime: Pogubnik. (Abyssos )
Mngeloyo analumbira mʼdzina la Iye wokhala ndi moyo mpaka muyaya, amene analenga kumwamba ndi zonse zili kumeneko, dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo, nati, “Pasakhalenso zochedwa tsopano! (aiōn )
In priseže pri živem na vekov veke, kateri je vstvaril nebo in kar je v njem, in zemljo in kar je na njej; in morje in kar je v njem: Časa ne bode več; (aiōn )
Tsono zikadzatsiriza umboni wawowo, chirombo chotuluka mʼChidzenje chakuya chija chidzachita nawo nkhondo nʼkuzigonjetsa mpaka kuzipha. (Abyssos )
In kader bodeti izpolnili pričanje svoje, bode zver, ki vzhaja iz brezna, vojsko napravila z njima in zmagala ji in umorila ji. (Abyssos )
Mngelo wachisanu ndi chiwiri anawomba lipenga lake, ndipo kumwamba kunamveka mawu ofuwula amene anati, “Ufumu wa dziko lapansi uli mʼmanja mwa Ambuye athu ndi Khristu wake uja, ndipo adzalamulira mpaka muyaya.” (aiōn )
In sedmi angelj zatrobi, in nastanejo glasovi veliki na nebu govoreči: Kraljestva sveta so postala Gospoda našega in Kristusa njegovega, in kraljeval bode na vekov veke. (aiōn )
Kenaka ndinaona mngelo wina akuwuluka mu mlengalenga ndipo anali ndi Uthenga Wabwino wamuyaya woti akalalikire kwa anthu okhala pa dziko lapansi, kwa a mtundu uliwonse, a fuko lililonse, a chiyankhulo chilichonse ndi kwa anthu onse. (aiōnios )
In videl sem druzega angela letečega po sredi neba, imajočega evangelj večni oznanjati prebivalcem na zemlji, in vsem narodom in rodom in jezikom in ljudstvom; (aiōnios )
Ndipo utsi wa moto wowazunzawo udzakwera kumwamba mpaka muyaya. Sikudzakhala kupumula usana ndi usiku kwa amene anapembedza chirombo chija ndi fano lake kapena kwa aliyense amene analembedwa chizindikiro cha dzina lake lija.” (aiōn )
In njih mučenja dim vzhaja na vekov veke; in oddihljaja nimajo noč in dan, kateri molijo zver in podobo njeno; in če vzame kdo znamenje njenega imena. (aiōn )
Ndipo kenaka chimodzi cha zamoyo zinayi zija chinapereka kwa angelo asanu ndi awiri mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi ukali wa Mulungu amene ali ndi moyo mpaka muyaya. (aiōn )
In iz četverih živali dá ena sedmerim angelom sedem čaš zlatih, polnih jeze Boga živega na vekov veke. (aiōn )
Chirombo chimene wachionachi chinalipo kale koma tsopano kulibe ndipo chidzatuluka ku chidzenje chakuya ndi kupita kukawonongedwa. Anthu okhala pa dziko lapansi amene mayina awo sanalembedwe mʼbuku lamoyo kuyambira pa kulengedwa kwa dziko lapansi adzadabwa pamene adzaona chirombocho, chifukwa chinalipo kale, tsopano kulibe, komabe chidzabwera. (Abyssos )
Zver, katero si videl, bila je, in ni je, in priti ima gor iz brezna in iti v pogubo. In čudili se bodo prebivalci na zemlji, (katerih imena niso zapisana v knjigi življenja od ustanovitve sveta), gledajoč zver, katera je bila in je ni, dasi je. (Abyssos )
Ndipo anafuwulanso kuti, “Haleluya! Utsi wochokera kwa mkazi wadamayo udzakwera kumwamba mpaka muyaya.” (aiōn )
In drugič so rekli: Aleluja! In dim njen vzhaja na vekov veke. (aiōn )
Koma chirombocho chinagwidwa pamodzi ndi mneneri wonyenga uja amene anachita zizindikiro zodabwitsa pamaso pake. Ndi zizindikirozi anasocheretsa amene analembedwa chizindikiro cha chirombocho napembedza fano lake. Onse awiri anaponyedwa amoyo mʼnyanja yamoto yasulufule wotentha. (Limnē Pyr )
In zgrabljena je bila zver, in z njo lažiprerok, kateri je delal znamenja pred njo, s katerimi je slepil njé, ki so bili sprejeli znamenje zveri, in njé, ki so molili podobo njeno; živa sta bila vržena ta dva v jezero ognjeno, sè žveplom goreče. (Limnē Pyr )
Ndipo ndinaona mngelo akutsika kuchokera kumwamba ali ndi kiyi ya ku chidzenje chakuya chija atanyamula mʼdzanja lake unyolo waukulu. (Abyssos )
In videl sem angela, idočega dol z nebes, imajočega od brezna ključ, in verigo veliko na roki svoji. (Abyssos )
Anamuponya ku chidzenje chakuya chija namutsekera ndi kiyi ndi kumatirira pa khomopo kuti asatulukenso kukanyenga mitundu ya anthu mpaka patapita zaka 1,000. Zikadzatha zakazo, adzamumasula kwa kanthawi pangʼono chabe. (Abyssos )
In vrže ga v brezno, in zapre ga in zapečati nad njim, da ne slepi več narodov, dokler se ne izpolni tisoč let; in potem se mora rešiti nekaj časa. (Abyssos )
Ndipo Mdierekezi amene anawanyenga, anaponyedwa mʼnyanja ya sulufule wotentha, kumene kunaponyedwa chirombo chija ndi mneneri wonama uja. Iwo adzazunzika usiku ndi usana kwamuyaya. (aiōn , Limnē Pyr )
In hudič, ki jih je slepil, bil je vržen v jezero ognjeno in žvepljeno, kjer je zver in lažiprerok; in mučili se bodo noč in dan na vekov veke. (aiōn , Limnē Pyr )
Nyanja inapereka amene anaferamo ndipo imfa ndi Hade zinapereka akufa ake ndipo munthu aliyense anaweruzidwa monga mwa ntchito zake. (Hadēs )
In dalo je morje mrtve iz sebe; in smrt in pekel dala sta mrtve iz sebe; in sodili so se vsak po delih svojih. (Hadēs )
Kenaka imfa ndi Hade zinaponyedwa mʼnyanja ya moto. Nyanja yamoto ndiyo imfa yachiwiri. (Hadēs , Limnē Pyr )
In smrt in pekel sta bila vržena v jezero ognjeno; ta je druga smrt. (Hadēs , Limnē Pyr )
Ngati dzina la wina aliyense silinapezeke mʼBuku Lamoyo, anaponyedwa mʼnyanja yamoto. (Limnē Pyr )
In če se kdo ni našel zapisan v knjigi življenja, vržen je bil v jezero ognjeno. (Limnē Pyr )
Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.” (Limnē Pyr )
Strahopetnim pa in nevernim in ostudnim in morilcem in kurbirjem in zavdajalcem in malikovalcem in vsem lažnjivcem, delež njih je v jezeru gorečim z ognjem in žveplom, kar je druga smrt. (Limnē Pyr )
Sipadzakhalanso usiku. Sadzafuna kuwala kwa nyale kapena kwa dzuwa pakuti Ambuye Mulungu adzakhala kuwala kwawo. Ndipo adzalamulira kwamuyaya. (aiōn )
In noči ne bode tam; in potreba jim ni svetilnice in uči solnčne, ker Gospod Bog jih razsvetljuje; in kraljevali bodo na vekov veke. (aiōn )