< Nehemiya 8 >

1 Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
Wówczas zebrał się cały lud jak jeden mąż na placu, który [był] przed Bramą Wodną, i powiedział do Ezdrasza, uczonego w Piśmie, aby przyniósł księgę Prawa Mojżesza, które PAN nadał Izraelowi.
2 Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
Wtedy Ezdrasz, kapłan, przyniósł Prawo przed zgromadzenie mężczyzn i kobiet oraz wszystkich, którzy mogli słuchać i rozumieć, [a działo się] to pierwszego dnia siódmego miesiąca.
3 Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
I czytał je przed tym placem, który znajdował się przed Bramą Wodną, od rana aż do południa, przed mężczyznami i kobietami oraz tymi, którzy mogli zrozumieć; a uszy całego ludu były skupione na księdze Prawa.
4 Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
Ezdrasz, uczony w Piśmie, stanął na drewnianym podwyższeniu, które przygotowano na ten cel, a obok niego, po prawej stronie, stali: Mattitiasz, Szema, Ananiasz, Uriasz, Chilkiasz i Maasejasz, a po lewej [stronie]: Pedajasz, Miszael, Malkiasz, Chaszum, Chaszbadana, Zachariasz [i] Meszullam.
5 Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
Ezdrasz otworzył księgę na oczach całego ludu – gdyż stał wyżej niż on – a gdy ją otworzył, cały lud powstał.
6 Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
I Ezdrasz błogosławił PANU, wielkiemu Bogu, a cały lud, podnosząc ręce, odpowiadał: Amen! Amen! Potem skłonili głowy i oddali pokłon PANU, padając twarzą ku ziemi.
7 Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
Także Jeszua, Bani, Szerebiasz, Jamin, Akkub, Szabbetaj, Hodiasz, Maasejasz, Kelita, Azariasz, Jozabad, Chanan, Pelajasz i Lewici nauczali lud prawa. A lud stał na swoim miejscu.
8 Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
Czytali więc z księgi Prawa Bożego wyraźnie i wyjaśniali znaczenie tak, żeby zrozumiano to, co czytali.
9 Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
Potem Nehemiasz, to [jest] Tirszata, i Ezdrasz, kapłan i uczony w Piśmie, oraz Lewici, którzy nauczali lud, powiedzieli do całego ludu: Ten dzień jest poświęcony PANU, waszemu Bogu. Nie smućcie się ani nie płaczcie. Cały lud bowiem płakał, słuchając słowa Prawa.
10 Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
I powiedział im: Idźcie, jedzcie tłuste potrawy i pijcie słodki napój, i poślijcie porcje tym, którzy sobie [nic] nie przygotowali. Dzień ten jest bowiem święty dla naszego PANA. Dlatego nie smućcie się, gdyż radość PANA jest waszą siłą.
11 Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
A Lewici uspokajali cały lud, mówiąc: Uciszcie się, bo ten dzień jest święty. Nie smućcie się.
12 Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
Rozszedł się więc cały lud, aby jeść i pić, aby rozsyłać porcje i radować się bardzo, gdyż zrozumiał słowa, które mu ogłoszono.
13 Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
Następnego dnia naczelnicy rodów całego ludu, kapłani i Lewici zebrali się wokół Ezdrasza, uczonego w Piśmie, aby zrozumieć słowa Prawa.
14 Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
I znaleźli przepis w Prawie, które PAN nadał przez Mojżesza, aby synowie Izraela mieszkali w szałasach podczas święta siódmego miesiąca;
15 Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
I aby ogłoszono i obwieszczono we wszystkich ich miastach i w Jerozolimie: Wejdźcie na górę i przynieście gałęzie oliwne, gałęzie sosnowe i gałęzie mirtowe, gałęzie palmowe i gałęzie drzew gęstych, abyście czynili szałasy, jak jest napisane.
16 Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
Lud więc wyszedł i przyniósł [je], i czynił sobie szałasy, każdy na swoim dachu, na swoich dziedzińcach, na dziedzińcach domu Bożego, na placu Bramy Wodnej i na placu Bramy Efraima.
17 Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
Całe zgromadzenie, wszyscy, którzy powrócili z niewoli, uczynili szałasy i mieszkali w nich, gdyż synowie Izraela nie czynili tego od dni Jozuego, syna Nuna, aż do tego dnia. I panowała wielka radość.
18 Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.
I [Ezdrasz] czytał z księgi Prawa Bożego każdego dnia, od pierwszego dnia aż do ostatniego. Przez siedem dni obchodzili święto, a dnia ósmego [odbyło się] uroczyste zgromadzenie według zwyczaju.

< Nehemiya 8 >