< Nehemiya 7 >

1 Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
When the wall was finished and I had set up the doors in place, and the gatekeepers and singers and Levites had been appointed,
2 Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
I gave my brother Hanani charge over Jerusalem, along with Hananiah who had oversight of the fortress, for he was a faithful man and feared God more than many.
3 Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
I said to them, “Do not open the gates of Jerusalem until the sun is hot. While the gatekeepers are on guard, you may shut the doors and bar them. Appoint guards from those who live in Jerusalem, some at the place of their guard station, and some in front of their own homes.”
4 Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
Now the city was wide and large, but there were few people within it, and no houses had yet been rebuilt.
5 Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
My God put into my heart to gather together the nobles, the officials, and the people to enroll them by their families. I found the book of the genealogy of those who returned at the first and found the following written in it.
6 Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
“These are the people of the province who went up out of the captivity of those exiles whom Nebuchadnezzar the king of Babylon took into exile. They returned to Jerusalem and to Judah, each to his city.
7 Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
They came with Zerubbabel, Jeshua, Nehemiah, Azariah, Raamiah, Nahamani, Mordecai, Bilshan, Mispereth, Bigvai, Nehum, and Baanah. The number of the men of the people of Israel included the following.
8 Zidzukulu za Parosi 2,172
The descendants of Parosh, 2,172.
9 Zidzukulu za Sefatiya 372
The descendants of Shephatiah, 372.
10 Zidzukulu za Ara 652
The descendants of Arah, 652.
11 Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
The descendants of Pahath-Moab, through the descendants of Jeshua and Joab, 2,818.
12 Zidzukulu za Elamu 1,254
The descendants of Elam, 1,254.
13 Zidzukulu za Zatu 845
The descendants of Zattu, 845.
14 Zidzukulu za Zakai 760
The descendants of Zakkai, 760.
15 Zidzukulu za Binuyi 648
The descendants of Binnui, 648.
16 Zidzukulu za Bebai 628
The descendants of Bebai, 628.
17 Zidzukulu za Azigadi 2,322
The descendants of Azgad, 2,322.
18 Zidzukulu za Adonikamu 667
The descendants of Adonikam, 667.
19 Zidzukulu za Abigivai 2,067
The descendants of Bigvai, 2,067.
20 Zidzukulu za Adini 655
The descendants of Adin, 655.
21 Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
The descendants of Ater, of Hezekiah, 98.
22 Zidzukulu za Hasumu 328
The descendants of Hashum, 328.
23 Zidzukulu za Bezayi 324
The descendants of Bezai, 324.
24 Zidzukulu za Harifu 112
The descendants of Hariph, 112.
25 Zidzukulu za Gibiyoni 95.
The descendants of Gibeon, 95.
26 Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
The men from Bethlehem and Netophah, 188.
27 Anthu a ku Anatoti 128
The men from Anathoth, 128.
28 Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
The men of Beth Azmaveth, 42.
29 Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
The men of Kiriath Jearim, Kephirah, and Beeroth, 743.
30 Anthu a ku Rama ndi Geba 621
The men of Ramah and Geba, 621.
31 Anthu a ku Mikimasi 122
The men of Michmas, 122.
32 Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
The men of Bethel and Ai, 123.
33 Anthu a ku Nebo winayo 52
The men of the other Nebo, 52.
34 Ana a Elamu wina 1,254
The people of the other Elam, 1,254.
35 Zidzukulu za Harimu 320
The men of Harim, 320.
36 Zidzukulu za Yeriko 345
The men of Jericho, 345.
37 Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
The men of Lod, Hadid, and Ono, 721.
38 Zidzukulu za Senaya 3,930.
The men of Senaah, 3,930.
39 Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
The priests: The descendants of Jedaiah (of the house of Jeshua), 973.
40 Zidzukulu za Imeri 1,052
The descendants of Immer, 1,052.
41 Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
The descendants of Pashhur, 1,247.
42 Zidzukulu za Harimu 1,017.
The descendants of Harim, 1,017.
43 Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
The Levites: The descendants of Jeshua, of Kadmiel, of Binnui, and of Hodevah, 74.
44 Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
The singers: The descendants of Asaph, 148.
45 Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
The gatekeepers of the descendants of Shallum, the descendants of Ater, the descendants of Talmon, the descendants of Akkub, the descendants of Hatita, the descendants of Shobai, 138.
46 Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
The temple servants: The descendants of Ziha, the descendants of Hasupha, the descendants of Tabbaoth,
47 Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
the descendants of Keros, the descendants of Sia, the descendants of Padon,
48 Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
the descendants of Lebana, the descendants of Hagaba, the descendants of Shalmai,
49 Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
the descendants of Hanan, the descendants of Giddel, the descendants of Gahar.
50 Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
The descendants of Reaiah, the descendants of Rezin, the descendants of Nekoda,
51 Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
the descendants of Gazzam, the descendants of Uzza, the descendants of Paseah,
52 Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
the descendants of Besai, the descendants of Meunim, the descendants of Nephushesim.
53 Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
The descendants of Bakbuk, the descendants of Hakupha, the descendants of Harhur,
54 Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
the descendants of Bazluth, the descendants of Mehida, the descendants of Harsha,
55 Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
the descendants of Barkos, the descendants of Sisera, the descendants of Temah,
56 Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
the descendants of Neziah, the descendants of Hatipha.
57 Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
The descendants of Solomon's servants: the descendants of Sotai, the descendants of Sophereth, the descendants of Perida,
58 zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
the descendants of Jaala, the descendants of Darkon, the descendants of Giddel,
59 zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
the descendants of Shephatiah, the descendants of Hattil, the descendants of Pochereth Hazzebaim, the descendants of Amon.
60 Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
All the temple servants, and the descendants of Solomon's servants, were 392.
61 Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
These were the people who went up from Tel Melah, Tel Harsha, Kerub, Addon, and Immer. But they could not prove that they or their ancestors' families were descendants from Israel:
62 Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
the descendants of Delaiah, the descendants of Tobiah, and the descendants of Nekoda, 642.
63 Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
Those who were from the priests: the descendants of Habaiah, Hakkoz, and Barzillai (who took his wife from the daughters of Barzillai of Gilead and was called by their name).
64 Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
These sought their records among those enrolled by their genealogy, but they could not be found, so they were excluded from the priesthood as unclean.
65 Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
Then the governor said to them that they should not be allowed to eat the priests' share of food from the sacrifices until there rose up a priest with Urim and Thummim.
66 Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
The whole assembly together was 42,360,
67 Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
besides their male servants and their female servants, of whom there were 7,337. They had 245 singing men and women.
68 Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
Their horses were 736 in number, their mules, 245,
69 Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
their camels, 435, and their donkeys, 6,720.
70 Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
Some from among the heads of ancestors' families gave gifts for the work. The governor gave to the treasury one thousand darics of gold, 50 basins, and 530 priestly garments.
71 Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
Some of the heads of ancestors' families gave into the treasury for the work twenty thousand darics of gold and 2,200 minas of silver.
72 Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
The rest of the people gave twenty thousand darics of gold, and two thousand minas of silver, and sixty-seven priestly garments.
73 Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.
So the priests, the Levites, the gatekeepers, the singers, some of the people, the temple servants, and all Israel lived in their cities. By the seventh month the people of Israel were settled in their cities.”

< Nehemiya 7 >