< Nehemiya 4 >

1 Sanibalati atamva kuti tikumanganso khoma anapsa mtima nayamba kuseka ndi kunyogodola Ayuda kwambiri.
A gdy Sanballat usłyszał, że odbudowujemy mur, rozgniewał się i bardzo się oburzył, i zaczął szydzić z Żydów.
2 Ndipo anayankhula pamaso pa abale ake ndi asilikali a Samariya kuti, “Kodi Ayuda ofowokawa akuchita chiyani? Kodi iwo nʼkumanganso khoma? Kodi adzaperekanso nsembe? Kodi adzatsiriza ntchitoyi tsiku limodzi? Kodi adzachita kutenga miyala yakale ija ndi mmene inapseramo?”
I powiedział wobec swoich braci i wojska Samarii: Co ci niedołężni Żydzi wyprawiają? Czy pozwolimy im na to? Czy będą składać ofiary? Czy zdołają to skończyć w jeden dzień? Czy wskrzeszą kamienie z kupy gruzu, które spalono?
3 Tobiya wa ku Amoni, amene anali naye anati, “Chimene akumangacho ngati nkhandwe itakwerapo, itha kugwetsa khoma lawolo!”
Ale Tobiasz Ammonita, który stał obok niego, powiedział: Nawet jeśli zbudują, przyjdzie lis i przewróci ich kamienny mur.
4 Tsono ndinayamba kupemphera kuti, “Timvereni, Inu Mulungu wathu, mmene akutinyozera. Mulole kuti mawu awo onyoza awabwerere, ndipo atengedwe ukapolo ku dziko lachilendo.
Wysłuchaj, nasz Boże, bo jesteśmy wzgardzeni, i odwróć ich zhańbienie na ich głowę, i wydaj ich na łup w ziemi niewoli.
5 Musawakhululukire mphulupulu zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu popeza aputa ukali wanu pamaso pa anthu omanga khoma.”
Nie zakrywaj ich nieprawości, a niech ich grzech nie będzie wymazany przed tobą. Ciebie bowiem pobudzili do gniewu na oczach budujących.
6 Choncho ife tinamangabe khomalo kufikira lonse litafika theka la msinkhu wake, chifukwa chakuti anthu anagwira ntchitoyo ndi mtima wawo wonse.
Lecz my nadal odbudowywaliśmy ten mur i mur został spojony aż do połowy, bo lud miał serce do pracy.
7 Koma pamene Sanibalati, Tobiya, Aarabu, Aamoni ndi anthu a ku Asidodi anamva kuti ntchito yokonzanso makoma a Yerusalemu ikupitirirabe ndipo kuti mipata ikutsekedwa, anapsa mtima kwambiri.
Gdy Sanballat i Tobiasz, Arabowie, Ammonici i Aszdodyci usłyszeli, że mury Jerozolimy są odbudowywane, że wyłomy zaczęły się wypełniać, bardzo się rozgniewali.
8 Tsono onse anapangana za chiwembu kuti abwere ndi kudzathira nkhondo anthu a ku Yerusalemu ndi kuyambitsa mapokoso pakati pawo.
I wszyscy sprzysięgli się razem, aby przyjść i walczyć przeciw Jerozolimie, i przeszkadzać w [robocie].
9 Koma ife tinapemphera kwa Mulungu wathu ndipo tinayika alonda otiteteza kwa adaniwo usiku ndi usana.
My jednak modliliśmy się do naszego Boga i postawiliśmy przeciwko nim straż we dnie i w nocy, ponieważ się ich baliśmy.
10 Pa nthawi yomweyi anthu a ku Yuda anati, “Mphamvu za anthu onyamula zinyalala zikutha ndipo pali zinyalala zambiri. Choncho ife sititha kumanga khomali.”
I Judejczycy powiedzieli: Osłabła siła dźwigających, a gruzu [jeszcze] wiele. Nie będziemy mogli odbudować muru.
11 Adani athunso anati, “Iwo asanadziwe izi, kapena kutiona, tidzakhala tili pakati pawo ndipo tidzawapha ndi kuyimitsa ntchitoyo.”
Ponadto nasi wrogowie powiedzieli: Zanim się dowiedzą i spostrzegą, przyjdziemy między nich i ich wymordujemy, i wstrzymamy tę pracę.
12 Ndipo Ayuda amene ankhala pafupi ndi adani athuwo anabwera kakhumi konse kuchokera konse kumene ankakhala kudzatiwuza kuti tibwereko ku ntchito.
A gdy Żydzi mieszkający obok nich przyszli, powiedzieli nam dziesięć razy: Ze wszystkich miejsc, z których przyjdziecie do nas, [oni przyjdą na was].
13 Choncho kumbuyo kwa khoma, cha mʼmunsi mwake komanso malo amene anali asanathe ndinayikamo anthu mʼmabanja atatenga malupanga, mikondo ndi mauta awo.
Ustawiłem więc lud w niższych miejscach za murem [i] na wysokich miejscach; ustawiłem [ich] według rodzin z ich mieczami, włóczniami i łukami.
14 Popeza anthu ankachita mantha, tsono ndinawawuza anthu olemekezeka, akuluakulu ndiponso anthu onse kuti, “Musawaope. Kumbukirani kuti Ambuye ndi wamkulu ndipo ndi woopsa. Choncho menyerani nkhondo abale anu, ana aamuna ndi aakazi, akazi anu ndi nyumba zanu.”
A gdy popatrzyłem, wstałem i powiedziałem do dostojników, przełożonych i pozostałych z ludu: Nie bójcie się ich. Wspomnijcie na PANA, wielkiego i budzącego grozę, i walczcie za swoich braci, za swoich synów i swoje córki, za swoje żony i domy.
15 Adani athu atamva kuti ife tadziwa za chiwembu chawo, anadziwanso kuti Yehova walepheretsa zimene ankafuna kutichita. Choncho tinabwerera aliyense ku ntchito yake yomanga khoma.
I kiedy nasi wrogowie usłyszeli, że nam to oznajmiono, Bóg zniweczył ich radę, a my wszyscy wróciliśmy do muru, każdy do swojej pracy.
16 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo mwake, theka la antchito anga linkagwira ntchito, pamene theka linalo limatenga mikondo, zishango, mauta ndi kuvala malaya azitsulo. Akuluakulu ankalimbikitsa Ayuda onse
Jednak od tego czasu połowa moich sług pracowała, a druga połowa trzymała włócznie, tarcze, łuki i pancerze. Naczelnicy zaś [stali] za całym domem Judy.
17 amene ankamanga khoma. Anthu onyamula zinyalala aja ankagwira ntchito ndi dzanja limodzi, dzanja linali atanyamula chida chankhondo.
Ci, którzy odbudowywali mur, i ci, którzy dźwigali ciężar, i ci, którzy go nakładali, każdy z nich jedną ręką pracował, a w drugiej trzymał broń.
18 Mʼmisiri aliyense ankamangirira lupanga lake mʼchiwuno mwake akamagwira ntchito. Koma munthu woyimba lipenga anali pambali panga nthawi zonse.
A z tych, którzy budowali, każdy miał swój miecz przypasany do boku i [tak] budowali. A trębacz [stał] obok mnie.
19 Ndipo ine ndinati kwa anthu olemekezeka ndi anthu ena onse, “Ntchitoyi ndi yayikulu ndipo ili padera lalikulu ndipo ifeyo takhala motayanatayana kwambiri pa khoma.
Powiedziałem bowiem do dostojników, przełożonych i pozostałych z ludu: Praca jest wielka i rozległa, a my jesteśmy rozdzieleni na murze, jeden z dala od drugiego.
20 Tsono kulikonse kumene muliko, mukamva kulira kwa lipenga bwerani mudzasonkhane kumene kuli ine kuno. Mulungu wathu adzatimenyera nkhondo.”
W jakimkolwiek miejscu usłyszycie dźwięk trąby, tam ruszajcie do nas. Nasz Bóg będzie walczył za nas.
21 Choncho enafe tinapitiriza kugwira ntchito, pamene theka lina linkanyamula mikondo kuyambira mʼbandakucha mpaka nyenyezi zitaoneka.
Pracowaliśmy więc przy tym dziele, a druga połowa trzymała włócznie, od pojawienia się zorzy aż do wzejścia gwiazd.
22 Pa nthawi imeneyo ndinawuzanso anthuwo kuti, “Aliyense pamodzi ndi wantchito wake agone mu Yerusalemu kuti tikhale ndi otilondera usiku ndi kuti masana tizigwira ntchito.”
W tym czasie powiedziałem też do ludu: Niech każdy nocuje ze swoim sługą w Jerozolimie, aby w nocy [słudzy] trzymali straż, a w dzień pracowali.
23 Choncho ine, anzanga, antchito anga, ndi anthu otiteteza amene ankanditsata panalibe ndi mmodzi yemwe anavula zovala zake pogona. Aliyense anasunga chida chake chankhondo pambali pake.
Tak więc ani ja, ani moi bracia, ani moi słudzy, ani straż, która była przy mnie, nie zdejmowaliśmy swoich szat, [zrobiliśmy to] wyłącznie przy obmywaniu.

< Nehemiya 4 >