< Nehemiya 4 >

1 Sanibalati atamva kuti tikumanganso khoma anapsa mtima nayamba kuseka ndi kunyogodola Ayuda kwambiri.
Forsothe it was doon, whanne Sanaballath hadde herd, that we bildiden the wal, he was ful wrooth, and he was stirid greetli, and scornede the Jewis.
2 Ndipo anayankhula pamaso pa abale ake ndi asilikali a Samariya kuti, “Kodi Ayuda ofowokawa akuchita chiyani? Kodi iwo nʼkumanganso khoma? Kodi adzaperekanso nsembe? Kodi adzatsiriza ntchitoyi tsiku limodzi? Kodi adzachita kutenga miyala yakale ija ndi mmene inapseramo?”
And he seide bifor hise britheren, and the multitude of Samaritans, What doen the feble Jewis? Whether hethene men schulen suffre hem? Whether thei schulen fille, and make sacrifice in o dai? Whether thei moun bilde stonys of the heepis of the dust, that ben brent?
3 Tobiya wa ku Amoni, amene anali naye anati, “Chimene akumangacho ngati nkhandwe itakwerapo, itha kugwetsa khoma lawolo!”
But also Tobie Amanytes, his neiybore, seide, Bilde thei; if a fox stieth, he schal `skippe ouer the stony wal `of hem.
4 Tsono ndinayamba kupemphera kuti, “Timvereni, Inu Mulungu wathu, mmene akutinyozera. Mulole kuti mawu awo onyoza awabwerere, ndipo atengedwe ukapolo ku dziko lachilendo.
And Neemye seide, Oure God, here thou, for we ben maad dispising; turne thou the schenschip on her heed, and yyue thou hem in to dispisyng in the lond of caytifte;
5 Musawakhululukire mphulupulu zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu popeza aputa ukali wanu pamaso pa anthu omanga khoma.”
hile thou not the wickidnesse of hem, and her synnes be not doon awei bifor thi face; for thei scorneden bilderis.
6 Choncho ife tinamangabe khomalo kufikira lonse litafika theka la msinkhu wake, chifukwa chakuti anthu anagwira ntchitoyo ndi mtima wawo wonse.
Therfor we bildiden the wal, and ioyneden togidere al `til to the half part, and the herte of the puple was exitid to worche.
7 Koma pamene Sanibalati, Tobiya, Aarabu, Aamoni ndi anthu a ku Asidodi anamva kuti ntchito yokonzanso makoma a Yerusalemu ikupitirirabe ndipo kuti mipata ikutsekedwa, anapsa mtima kwambiri.
Forsothe it was doon, whanne Sanaballat `hadde herd, and Tobie, and Arabiens, and Amanytys, and men of Azotus hadden herd, that the brekyng of the wal of Jerusalem was stoppid, and that the crasyngis hadden bigunne to be closid togidere, thei weren ful wrothe.
8 Tsono onse anapangana za chiwembu kuti abwere ndi kudzathira nkhondo anthu a ku Yerusalemu ndi kuyambitsa mapokoso pakati pawo.
And alle weren gaderid togidere to come and fiyte ayens Jerusalem, and to caste tresouns.
9 Koma ife tinapemphera kwa Mulungu wathu ndipo tinayika alonda otiteteza kwa adaniwo usiku ndi usana.
And we preieden oure Lord God, and we settiden keperis on the wal bi dai and niyt ayens hem.
10 Pa nthawi yomweyi anthu a ku Yuda anati, “Mphamvu za anthu onyamula zinyalala zikutha ndipo pali zinyalala zambiri. Choncho ife sititha kumanga khomali.”
Forsothe Juda seide, The strengthe of the berere is maad feble, and the erthe is ful myche, and we moun not bilde the wal.
11 Adani athunso anati, “Iwo asanadziwe izi, kapena kutiona, tidzakhala tili pakati pawo ndipo tidzawapha ndi kuyimitsa ntchitoyo.”
And oure enemyes seiden, Wite thei not, and knowe thei not, til we comen in to the myddil of hem, and sleen hem, and maken the werk to ceesse.
12 Ndipo Ayuda amene ankhala pafupi ndi adani athuwo anabwera kakhumi konse kuchokera konse kumene ankakhala kudzatiwuza kuti tibwereko ku ntchito.
Forsothe it was doon, whanne Jewis came, that dwelliden bisidis hem, and seiden to vs `bi ten tymes, fro alle places fro whiche thei camen to vs,
13 Choncho kumbuyo kwa khoma, cha mʼmunsi mwake komanso malo amene anali asanathe ndinayikamo anthu mʼmabanja atatenga malupanga, mikondo ndi mauta awo.
Y ordeynede the puple in ordre, with her swerdis, and speris, and bouwis, in a place bihynde the wal bi cumpas.
14 Popeza anthu ankachita mantha, tsono ndinawawuza anthu olemekezeka, akuluakulu ndiponso anthu onse kuti, “Musawaope. Kumbukirani kuti Ambuye ndi wamkulu ndipo ndi woopsa. Choncho menyerani nkhondo abale anu, ana aamuna ndi aakazi, akazi anu ndi nyumba zanu.”
Y bihelde, and roos, and seide to the principal men, and magistratis, and to `the tother part of the comyn puple, Nyle ye drede of her face; haue ye mynde of the greet Lord, and ferdful, and fiyte ye for youre britheren, and youre sones, and youre douytris, for youre wyues, and housis.
15 Adani athu atamva kuti ife tadziwa za chiwembu chawo, anadziwanso kuti Yehova walepheretsa zimene ankafuna kutichita. Choncho tinabwerera aliyense ku ntchito yake yomanga khoma.
Forsothe it was doon, whanne oure enemyes hadden herd that it was teld to vs, God distriede her counsel; and alle we turneden ayen to the wallis, ech man to his werk.
16 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo mwake, theka la antchito anga linkagwira ntchito, pamene theka linalo limatenga mikondo, zishango, mauta ndi kuvala malaya azitsulo. Akuluakulu ankalimbikitsa Ayuda onse
And it was doon fro that dai, the half part of yonge men made werk, and the half part was redi to batel; `and speris, and scheldis, and bouwis, and harburiouns, and princes aftir hem, in al the hows of men of Juda,
17 amene ankamanga khoma. Anthu onyamula zinyalala aja ankagwira ntchito ndi dzanja limodzi, dzanja linali atanyamula chida chankhondo.
bildynge in the wal, and berynge birthuns, and puttynge on; with her oon hond thei maden werk, and with the tother thei helden swerd.
18 Mʼmisiri aliyense ankamangirira lupanga lake mʼchiwuno mwake akamagwira ntchito. Koma munthu woyimba lipenga anali pambali panga nthawi zonse.
For ech of the bilderis was gird with the swerd on the reynes; and thei bildiden, and sowneden with clariouns bisidis me.
19 Ndipo ine ndinati kwa anthu olemekezeka ndi anthu ena onse, “Ntchitoyi ndi yayikulu ndipo ili padera lalikulu ndipo ifeyo takhala motayanatayana kwambiri pa khoma.
And Y seide to the principal men, and magistratis, and to the tothir part of the comyn puple, The werk is greet and brood, and we ben departid fer in the wal, oon from anothir;
20 Tsono kulikonse kumene muliko, mukamva kulira kwa lipenga bwerani mudzasonkhane kumene kuli ine kuno. Mulungu wathu adzatimenyera nkhondo.”
in what euer place ye heren the sown of the trumpe, renne ye togidere thidur to vs; for oure God schal fiyte for vs.
21 Choncho enafe tinapitiriza kugwira ntchito, pamene theka lina linkanyamula mikondo kuyambira mʼbandakucha mpaka nyenyezi zitaoneka.
And we `vs silf schal make the werk, and the half part of vs holde speris, fro `the stiyng of the moreutid til that sterris go out.
22 Pa nthawi imeneyo ndinawuzanso anthuwo kuti, “Aliyense pamodzi ndi wantchito wake agone mu Yerusalemu kuti tikhale ndi otilondera usiku ndi kuti masana tizigwira ntchito.”
And `in that tyme Y seide to the puple, Ech man with his child dwelle in the myddil of Jerusalem, and whilis be to vs `bi nyyt and dai to worche.
23 Choncho ine, anzanga, antchito anga, ndi anthu otiteteza amene ankanditsata panalibe ndi mmodzi yemwe anavula zovala zake pogona. Aliyense anasunga chida chake chankhondo pambali pake.
But Y, and my britheren, and my keperis, and children, that weren after me, diden not of oure clothis; ech man was maad nakid oneli to waischyng.

< Nehemiya 4 >