< Nehemiya 3 >

1 Pambuyo pake Eliyasibu mkulu wa ansembe ndi ansembe anzake anayamba kugwira ntchito ndipo anamanganso Chipata cha Nkhosa. Iwo anachipatulira Mulungu ndipo anayika zitseko zake. Khoma limene analipatula linafika mpaka pa Nsanja ya Zana ndi Nsanja ya Hananeli.
I usta Elijasiv poglavar sveštenièki i braæa njegova sveštenici i zidaše vrata ovèija, i osvetiše ih i metnuše im krila, i osvetiše ih do kule Meje, do kule Ananeilove.
2 Anthu a ku Yeriko anamanga chigawo china pambali pake ndipo Zakuri mwana wa Imuri anamanga chigawo chinanso choyandikana nawo.
A do njega zidaše Jerihonjani, a do njih zida Zahur sin Imrijev;
3 Chipata cha Nsomba chinamangidwanso ndi ana a fuko la Hasena. Iwo anayika mitanda yake ndi zitseko, zotsekera zake, ndi mipiringidzo yake.
A vrata riblja zidaše sinovi Asenajini, oni ih pobrvnaše i metnuše krila i brave i prijevornice.
4 Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi, anakonza chigawo choyandikana nacho. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya, mwana wa Mesezabeli anakonza chigawo china. Pambali pake, Zadoki mwana wa Baana anakonzanso chigawo china.
A do njih opravlja Merimot sin Urije sina Akosova; a do njih opravlja Mesulam sin Varahije sina Mesizaveilova; a do njih opravlja Sadok sin Vanin.
5 Pambali pa iwowa anthu a ku Tekowa anakonza chigawo china. Koma wolemekezeka awo anakana kugwira ntchito imene akuluakulu awo anawapatsa.
A do njih opravljaše Tekojani, ali poglavice njihove ne saviše vrata svojega na službu Gospodu svojemu.
6 Chipata cha Yesana chinakonzedwa ndi Yoyada mwana wa Paseya ndi Mesulamu mwana wa Besodeya. Iwo anayika mitanda yake ndi kuyika zitseko, zotsekera zake ndi mipiringidzo yake.
A stara vrata opravlja Jodaj sin Fasejin i Mesulam sin Vesodijin, oni ih pobrvnaše i metnuše krila i brave i prijevornice.
7 Pambali pawo Melatiya Mgibeyoni ndi Yadoni Mmerenoti ndiponso anthu a ku Gibiyoni ndi a ku Mizipa anakonza chigawo chawo mpaka ku nyumba ya bwanamkubwa wa chigawo cha Patsidya pa Yufurate.
A do njih opravljaše Melatija Gavaonjanin i Jadon Meronjanin, ljudi iz Gavaona i iz Mispe do stolice kneza s ove strane rijeke.
8 Pambali pawo Uzieli mwana wa Harihaya wa mʼgulu amisiri osula golide anakonzanso chigawo china. Pambali pake Hananiya mmodzi mwa anthu oyenga mafuta onunkhira, anakonzanso chigawo china. Iwo anakonzanso Yerusalemu mpaka ku Khoma Lotambasuka.
Do njih opravlja Uzilo sin Arahijin zlatar; a do njega opravlja Ananija sin apotekarski. I ostaviše Jerusalim do širokoga zida.
9 Refaya mwana wa Huri wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu anakonza chigawo china motsatana nawo.
A do njih opravlja Refaja sin Orov poglavar nad polovinom kraja Jerusalimskoga.
10 Kulumikiza ichi, Yedaya mwana wa Harumafi anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba yake, ndipo Hatusi mwana wa Hasabaneya anakonzanso motsatana naye.
A do njih opravlja Jedaja sin Arumafov prema svojoj kuæi, a do njega opravlja Hatus sin Asavnijin.
11 Malikiya mwana wa Harimu ndi Hasubu mwana wa Pahati-Mowabu anakonzanso chigawo china ndiponso Nsanja ya Ngʼanjo.
Toliko opravlja Malhija sin Harimov i Asuv sin Fat-Moavov i kulu kod peæi.
12 Salumu mwana wa Halohesi wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu, anakonzanso chigawo chotsatana nawo mothandizidwa ndi ana ake akazi.
A do njega opravlja Salum sin Loisov, poglavar nad polovinom kraja Jerusalimskoga sa kæerima svojim.
13 Chipata cha ku chigwa chinakonzedwa ndi Hanuni ndi anthu okhala ku Zanowa. Iwo anachimanganso ndi kuyika zitseko zake ndi zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iwo anakonzanso khoma lotalika mamita 450 mpaka ku Chipata cha Zinyalala.
Vrata dolinska opravlja Anun sa stanovnicima Zanojskim; oni ih sagradiše i metnuše krila i brave i prijevornice, i tisuæu lakata zida do gnojnijeh vrata.
14 Chipata cha Zinyalala chinakonzedwa ndi Malikiya mwana wa Rekabu, wolamulira chigawo cha Beti-Hakeremu. Iye anachimanganso ndi kuyika zitseko zake, zotsekera zake ndi mipiringidzo.
A gnojna vrata opravlja Malhija sin Rihavov poglavar nad krajem Vet-Keremskim, on ih sagradi i metnu krila i brave i prijevornice.
15 Chipata cha Kasupe chinakonzedwa ndi Saluni mwana wa Koli-Hoze, wolamulira chigawo cha Mizipa. Iye anachimanganso ndi kuyikanso denga ndiponso zitseko, zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iye anakonzanso khoma la Dziwe la Siloamu limene lili pafupi ndi munda wa mfumu mpaka ku makwerero otsikira potuluka mzinda wa Davide.
A vrata izvorska opravlja Salum sin Hol-Ozin, poglavar nad krajem u Mispi, on ih sagradi i pokri i metnu im krila i brave i prijevornice; i zid kod banje Siloamske od vrta careva do basamaka koji slaze iz grada Davidova.
16 Pambali pa iyeyo, Nehemiya mwana wa Azibuki, wolamulira theka la chigawo cha Beti Zuri anakonza chigawo china mpaka kumalo oyangʼanana ndi manda a Davide, mpaka ku dziwe lokumba ndi ku nyumba ya anthu ankhondo.
Za njim opravlja Nemija sin Azvukov poglavar nad polovinom kraja Vet-Surskoga do prema grobovima Davidovijem i do jezera naèinjenoga i do kuæe junaèke.
17 Pambali pake Alevi anakonza chigawo china, ndipo mtsogoleri wawo anali Rehumi mwana wa Bani. Pambali pa iye Hasabiya wolamulira theka la chigawo cha Keyila anagwira ntchito ku chigawo chake.
Za njim opravljaše Leviti, Reum sin Vanijev, a do njega opravlja Asavija poglavar nad polovinom kraja Keilskoga sa svojim krajem.
18 Pambuyo pa iyeyu abale awo anapitiriza kukonza, ndipo mtsogoleri wawo anali Bawai mwana wa Henadadi, wolamulira theka lina la chigawo cha Keyila.
Za njim opravljaše braæa njihova, Vavaj sin Inadadov poglavar nad polovinom kraja Keilskoga.
19 Motsatana naye Ezeri mwana wa Yesuwa, wolamulira Mizipa anakonza chigawo chinanso choyangʼanana ndi chikweza chofikira ku nyumba yosungira zida za nkhondo pa ngodya.
A do njega opravlja Eser sin Isusov poglavar od Mispe toliko prema mjestu kuda se ide k riznici na uglu.
20 Motsatana naye, Baruki mwana wa Zakai anakonzanso chigawo china kuchokera pa ngodya mpaka pa chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe.
Za njim razgorjevši se Varuh sin Zavajev opravlja toliko od ugla do vrata od kuæe Elijasiva poglavara sveštenièkoga.
21 Motsatana naye, Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi anakonzanso chigawo china kuchokera ku chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mpaka kumapeto kwake.
Za njim opravlja Merimot sin Urije sina Akosova toliko od vrata kuæe Elijasivove do kraja kuæe Elijasivove.
22 Pambuyo pake ansembe okhala ku chidikha anakonzanso chigawo china.
A za njim opravljaše sveštenici koji življahu u ravnici.
23 Pambuyo pawo, Benjamini ndi Hasubu anakonza kutsogolo kwa nyumba zawo. Ndipo motsatana nawo, Azariya mwana wa Maaseya mwana wa Ananiya, anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba zawo.
Za njima opravlja Venijamin i Asuv prema svojim kuæama; a za njima opravlja Azarija sin Masije sina Ananijina uz svoju kuæu.
24 Motsatana naye, Binuyi mwana wa Henadadi anakonzanso chigawo china, kuchokera pa nyumba ya Azariya kukafika potsirizira pa ngodya.
Za njim opravlja Vinuj sin Inadadov toliko od kuæe Azarijine do savitka i do ugla.
25 Palali mwana Uzai anakonza chigawo china choyangʼanana ndi ngodya ndi nsanja yotuluka pa nyumba yapamwamba ya mfumu ku bwalo la alonda. Motsatana naye, Pedaya mwana wa Parosi,
Falal sin Uzajev opravlja prema savitku i prema kuli koja se izdiže iz gornjega doma careva kod trijema tamnièkoga; za njim Fedaja sin Farosov;
26 ndi otumikira mʼNyumba ya Mulungu amene amakhala pa khoma la Ofeli anakonza chigawo china mpaka pa malo oyangʼanana ndi Chipata cha Madzi kuloza kummawa ndiponso nsanja yayitali ija.
I Netineji koji življahu u Ofilu, do prema vratima vodenijem na istok i kuli visokoj;
27 Motsatana nawo, anthu a ku Tekowa anakonzanso chigawo china choyangʼanana ndi nsanja ija yayikulu ndi yayitali mpaka ku khoma la Ofeli.
Za njima opravljaše Tekojani toliko prema velikoj kuli visokoj do zida Ofilskoga;
28 Kuyambira ku Chipata cha Akavalo anakonza ndi ansembe ena ndipo aliyense amakonza khoma loyangʼanana ndi nyumba yake.
Od vrata konjskih opravljaše sveštenici svaki prema svojoj kuæi;
29 Motsatana nawo, Zadoki mwana wa Imeri anakonza chigawo china choyangʼanana ndi nyumba yake. Motsatana naye, Semeya mwana wa Sekaniya, mlonda wa Chipata cha Kummawa, anakonzanso khoma.
Za njima opravlja Sadok sin Imirov prema svojoj kuæi; a za njim opravlja Semaja sin Sehanijin èuvar vrata istoènijeh;
30 Hananiya mwana wa Selemiya ndiponso Hanuni mwana wachisanu ndi chimodzi wa Zalafi anakonza chigawo china. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya anakonza chigawo choyangʼanana ndi chipinda chake.
Za njim opravlja Ananija sin Selemijin i Anun šesti sin Salafov, toliko; za njima opravlja Mesulam sin Varahijin prema svojoj klijeti;
31 Motsatana naye, Malikiya mmodzi mwa amisiri a golide anakonza chigawo china mpaka ku nyumba ya atumiki a ku Nyumba ya Mulungu ndiponso ku nyumba ya anthu amalonda moyangʼanana ndi chipata cha Mifikade ndiponso mpaka pa chipinda chapamwamba chapangodya.
Za njim opravlja Malhija sin zlatarev do kuæe Netinejske i trgovaèke prema vratima Mifkadskim do uzbrdice na uglu;
32 Ndipo pakati pa chipinda chapamwamba chapangodya ndi Chipata cha Nkhosa anakonza ndi amisiri a golide ndi anthu amalonda.
A izmeðu uzbrdice na uglu i ovèjih vrata opravljaše zlatari i trgovci.

< Nehemiya 3 >