< Nehemiya 13 >

1 Pa tsiku limenelo anawerenga buku la Mose anthu akumva. Ndipo anapeza mawu akuti, Mwamoni kapena Mmowabu asalowe konse mu msonkhano wa Mulungu.
I A la ua heluheluia ma ka buke o Mose iloko o na pepeiao o ka poe kanaka; a loaa iloko olaila ka mea i kakauia'i, i ole e komo ka Amona a me ka Moaba iloko o ka ahakanaka o ke Akua i ka manawa pau ole;
2 Paja iwowa sanawachingamire Aisraeli kukawapatsa chakudya ndi madzi. Mʼmalo mwake analemba ganyu Baalamu kuti adzawatemberere. Komabe Mulungu wathu anasandutsa tembererolo kukhala mdalitso.
No ka mea, aole lakou i hele aku e halawai me ka Iseraela me ka berena a me ka wai, aka, ku e ia lakou a hoolimalima ia Balaama e hoino ia lakou; hoololi no nae ko kakou Akua i ka hoino ana i hoomaikai ana.
3 Anthu atamva lamuloli, anachotsa pakati pawo onse amene anali achilendo.
A lohe lakou i ke kanawai, hookaawale ae la lakou i na malihini a pau mai ka Iseraela aku.
4 Izi zisanachitike, wansembe Eliyasibu anali atasankhidwa kukhala woyangʼanira zipinda zosungiramo katundu za Nyumba ya Mulungu. Iyeyu ankagwirizana kwambiri ndi Tobiya.
A mamua o keia manawa, o Eliasiba ke kahuna, ia ia i haawiia ke keena o ka hale o ko kakou Akua, he hoalauna no ia no Tobia.
5 Choncho anamupatsa chipinda chachikulu chimene kale ankasungamo zopereka zakudya, lubani, ziwiya, zopereka za chakhumi za tirigu, vinyo ndi mafuta zoyenera kuperekedwa kwa Alevi, oyimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, komanso mphatso zoyenera kupereka kwa ansembe.
A ua hoomakaukau oia nona, i keena nui kahi a lakou i waiho ai mamua i ka mohai makana, i ka mea ala a me na ipu a me ka hapaumi o ka ai, i ka waina hou a me ka aila, na mea i kauohaiai na na Levi a me ka poe mele a me ka poe kiaipuka; a me ka makana no ka poe kahuna.
6 Koma pamene izi zonse zinkachitika mu Yerusalemu, ine kunalibe popeza mʼchaka cha 32 cha Aritasasita mfumu ya Babuloni ine ndinabwerera kwa mfumu. Patapitanso nthawi ndinapempha chilolezo kwa mfumuyo
Aka, i keia manawa a pau aole au ma Ierusalema: no ka mea, i ka makahiki kanakolukumamalua o Aretasaseta ke alii o Babulona, hiki aku la au i ke alii, a hala kekahi mau la, nonoi aku la au i ke alii no'u.
7 ndipo ndinabwerera ku Yerusalemu. Kumeneko ndinamva za chinthu choyipa chimene Eliyasibu anachita pomupatsa Tobiya chipinda mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
A hiki mai la au i Ierusalema a ike iho la i ka mea ino a Eliasiba i hana'i no Tobia, i ka hoomakaukau ana i keena nona ma na keena o ka hale o ke Akua.
8 Ndinapsa mtima kwambiri ndipo ndinataya kunja katundu yense wa Tobiya amene anali mʼchipindamo.
Alaila, eha loa iho la au; a kiola aku la au mawaho i ka ukana o ka hale o Tobia, mai loko aku o ke keena.
9 Ndinalamulira kuti ayeretse zipinda, ndipo kenaka ndinabwezeramo zida za mʼNyumba ya Mulungu, pamodzi ndi chopereka cha zakudya ndi lubani.
Alaila, kauoha aku la au, a huikala lakou i ke keena; a hoihoi mai la au malaila i na ipu o ka hale o ke Akua, i ka mohai makana a me ka mea ala.
10 Ndinapezanso kuti Alevi sankalandira magawo awo amene amayera kulandira. Chotsatira chake Alevi onse pamodzi ndi oyimba nyimbo amene ankagwira ku Nyumba ya Mulungu anathawa, aliyense kupita ku munda wake.
A ike iho la au, aole i haawiia mai na haawina no na Levi; a na auhee kela kanaka keia kanaka ma kona aina iho, o na Levi a me ka poe mele, ka poe nana e lawelawe i ka hana.
11 Choncho ndinadzudzula akuluakulu aja ndipo ndinawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa?” Ndipo ine ndinawayitanitsa pamodzi ndi kuwayika mʼmalo awo.
Alaila, ao aku la au i na luna, a olelo aku la au, No ke aha la i haaleleia'i ka hale o ke Akua? A houluulu mai la au ia lakou, a hoonoho iho la ia lakou ma ko lakou wahi.
12 Pambuyo pake Ayuda anayambanso kubwera ndi zopereka zawo za chakhumi cha tirigu, vinyo ndi mafuta kuti ziperekedwe ku nyumba yosungiramo chuma.
Alaila, lawe mai la ka Iuda a pau i ka hapaumi o ka ai me ka waina hou a me ka aila ma na keena e waiho ai na mea laa.
13 Ndipo ndinasankha wansembe Selemiya, mlembi Zadoki, ndi Mlevi wotchedwa Pedaya kukhala oyangʼanira zipinda zosungiramo. Ndinasankhanso Hanani mwana wa Zakuri mwana wa Mataniya kukhala wowathandizira chifukwa ndinaona kuti anthu awa anali odalirika. Ntchito yawo inali yogawira abale awo zinthu zofunika.
A hoonoho iho au i na puuku waiwai maluna o na waihona waiwai ia Selomia ke kahuna, a me Zadoka ke kakauolelo, a me Pedaia kekahi o na Levi; a mahope o lakou o Hanana ke keiki a Zakura, ke keiki a Matania; no ka mea, ua manaoia lakou he poe hana pololei, nolaila, na lakou no e mahele na ko lakou poe hoahanau.
14 Inu Mulungu wanga, mundikumbukire pa zimenezi, ndipo musafafanize ntchito zanga zimene ndachita mokhulupirika pa Nyumba yanu pofuna kukutumikirani.
E hoomanao mai oe ia'u, e ko'u Akua, no keia hana, aole hoi e holoi iho oe i ko'u lokomaikai a'u i hana'i no ka hale o ko'u Akua, a no kana mau oihana.
15 Nthawi imeneyo ndinaona anthu a mu Yuda akuponda ndi kufinya mphesa pa tsiku la Sabata. Ena ankawunjika tirigu milumilu ndi kumasenzetsa abulu. Enanso ankabwera ndi vinyo, mphesa, mkuyu ndi katundu wa mitundumitundu ku Yerusalemu pa tsiku la Sabata. Choncho ndinawachenjeza za kugulitsa zakudya pa tsiku la Sabata.
Ia mau la, ike aku la au ma Iuda i kekahi poe e hehi ana i na lua kaomi waina i ka Sabati, a e halihali ana i na pua, a e hoouka ana i na hoki; a e lawe ana i ka waina, i na hua waina, a me na fiku, a me kela mea keia mea kuai ma Ierusalema i ka Sabati: a papa aku la au ia la no, i ko lakou kuai ana i ka ai.
16 Nawonso anthu a ku Turo amene ankakhala mu Yerusalemu ankabweretsa nsomba ndi akatundu ena onse amalonda kudzagulitsa pa Sabata kwa anthu a mʼdziko la Yuda ndi a mu Yerusalemu.
Noho iho la iloko olaila na kanaka o Turo i lawe mai i ka ia, a me kela mea keia mea kuai, a kuai iho no i ka Sabati me ka Iuda iloko no o Ierusalema.
17 Ndipo ndinadzudzula anthu olemekezeka a dziko la Yuda. Ndinawafunsa kuti, “Nʼchoyipa chanji mukuchitachi, kumayipitsa tsiku la Sabata chotere?
Alaila papa aku la au i na kaukaualii o ka Iuda, a olelo aku au ia lakou, Heaha keia mea hewa a oukou e hana nei, a hana ino i ka la Sabati?
18 Makolo anu anachita zomwezi ndipo Mulungu wathu anadzetsa mavuto pa ife ndi pa mzinda uwu. Kodi inu mukufuna kuwutsanso mkwiyo wa Mulungu pa Israeli pamene mukudetsa tsiku la Sabata?”
Aole anei i hana ko oukou poe makua pela, a kau mai la ko kakou Akua i keia popilikia a pau maluna o kakou, a maluna o keia kulanakauhale? Aka, e hoomahuahua ana oukou i ka inaina maluna o ka Iseraela i ka oukou hana ino ana i ka Sabati.
19 Nʼchifukwa chake ndikulamula kuti pamene kuyamba kuda, tsiku la Sabata lisanayambe, azitseka zipata zonse za Yerusalemu ndipo asazitsekule mpaka sabata litatha. Ndinayika ena mwa antchito anga oyangʼanira pa zipata kuti katundu aliyense asalowe mu Yerusalemu pa tsiku la Sabata.
A i ka wa i pouli mai ai na puka o Ierusalema mamua o ka Sabati, olelo aku la au, e pani lakou i na puka, a olelo aku no hoi au, e wehe ole ia lakou a hala ka Sabati; a hoonoho iho la au i kekahi o ka'u poe kauwa ma na puka i komo ole kekahi ukana i ka la Sabati.
20 Choncho kamodzi kapena kawiri anthu amalonda ndi anthu ogulitsa katundu osiyanasiyana ankagona usiku wonse kunja kwa Yerusalemu.
A o ka poe kalepa a me ka poe e kuai ana i kela mea keia mea kuai, akahi a elua hoi ko lakou moe ana mawaho o Ierusalema.
21 Koma ndinawachenjeza ndi kuwafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukugona pafupi ndi khoma? Ngati muchitanso zimenezi, ine ndidzakugwirani.” Kuyambira nthawi imeneyo, sanabwerenso pa tsiku la Sabata.
Alaila papa aku la au ia lakou, a olelo aku la ia lakou, No ke aha la oukou e moe ai ma kahi e pili ana i ka pa? Ina e hana hou oukou pela, e lalau no ko'u lima ia oukou. Mai ia manawa mai, aole lakou i hiki mai i ka Sabati.
22 Ndipo ndinalamulira Alevi kuti adziyeretse okha ndi kubwera kudzalonda pa zipata ndi cholinga choti tsiku la Sabata likhale tsiku loyera. Inu Mulungu wanga, kumbukireninso ine pa zimenezi ndipo mundisunge malingana ndi chikondi chanu chachikulu chosasinthika.
A olelo aku la au i na Levi, i huikala lakou ia lakou iho, a i hele mai lakou a e malama i na puka i hoano ka la Sabati. No keia mea hoi, e hoomanao mai oe ia'u, e ko'u Akua, a e ahonui mai oe ia'u e like me ka nui o kou lokomaikai.
23 Masiku amenewo ndinaonanso anthu a ku Yuda amene anakwatira akazi ochokera ku Asidodi, Amoni ndi Mowabu.
Eia hoi, ia mau la ike aku la au i kekahi poe o ka Iuda i mare i na wahine o Asedoda, a o Amona, a o Moaba;
24 Theka la ana awo linkayankhula chiyankhulo cha Asidodi kapena chiyankhulo chimodzi cha anthu ena, ndipo sankathanso kuyankhula chiyankhulo cha Ayuda.
A he hapa ka olelo ana o ka lakou poe keiki ma ka olelo a Asedoda, aole hoi i ike lakou ke olelo e like me ka Iuda, aka, o like me kela lahuikanaka a me keia lahuikanaka.
25 Tsono ndinakangana nawo ndi kuwatemberera. Ndinamenya ena mwa anthuwo ndi kuzula tsitsi lawo. Ine ndinawalumbiritsa mʼdzina la Mulungu kuti, “Inu musapereke ana anu aakazi kuti akwatiwe ndi ana awo aamuna kapena inuyo ngakhale ana anu aamuna kukwatira ana awo aakazi.
A papa aku au ia lakou, a hoino aku au ia lakou, a kui aku i kekahi poe o lakou, a huki ae la i ko lakou lauoho, a kena'ku ia lakou e hoohiki ma ke Akua, Aole oukou e haawi aku i ka oukou mau kaikamahine na ka lakou poe keikikane, aole hoi e lawe oukou i ka lakou mau kaikamahine na ka oukou keikikane, aole hoi na oukou iho.
26 Kodi Solomoni mfumu ya Israeli suja anachimwa chifukwa cha ukwati ngati umenewu. Pakati pa mitundu yambiri panalibe mfumu ngati iyi. Iye anakondedwa ndi Mulungu wake, ndipo Mulungu anamuyika kukhala mfumu ya Israeli yense, koma iyeyo anachimwa chifukwa cha akazi achilendo.
Aole anei i hana hewa o Solomona ke alii o ka Iseraela ma keia mau mea? Ma na lahuikanaka he nui loa, aole alii e like me ia, ua alohaia oia e kona Akua, a ua hoolilo ke Akua ia ia i alii maluna o ka Iseraela a pau; aka, o na wahine o na aina e, alakai no lakou ia ia ma ka hewa.
27 Kodi tsopano ife tizimva inu kuti mukuchita choyipa chachikulu chimenechi, kupandukira Yehova Mulungu wathu pomakwatira akazi achilendo?”
A e hoolohe anei makou ia oukou e hana i keia hewa nui, a e kipi aku i ko kakou Akua ma ka mare ana i na wahine o na aina e?
28 Mmodzi mwa ana aamuna a Yehoyada mwana Eliyasibu mkulu wa ansembe nʼkuti nthawi imeneyi ali mpongozi wa Sanibalati wa ku Horoni. Choncho ndinamuthamangitsa pamaso panga.
A o kekahi o na keiki a Ioiada, ke keiki a Eliasiba ke kahuna nui, he hunonakane oia na Sanebalata no Horona; a hookuke aku la au ia ia mai o'u aku la.
29 Inu Mulungu wanga, mukumbukire mmene iwo anayipitsira unsembe, pangano la unsembe komanso la Alevi.
E hoomanao mai oe ia lakou, e ko'u Akua, no ko lakou hoohaumia ana i ka oihana kahuna, a me ka berita o ka oihana kahuna, a o na Levi.
30 Motero ndinayeretsa ansembe ndi Alevi powachotsera kalikonse kachilendo. Ndipo ndinakhazikitsa ntchito zawo, kuti aliyense akhale pa ntchito yake.
Pela au i hookaawale aku ai ia lakou mai na malihini aku a pau, a hooponopono iho la au i na oihana a ka poe kahuna a me na Levi, kela kanaka keia kanaka ma kana oihana iho;
31 Ndiponso kupereka nkhuni ndi zipatso zoyamba kucha pa nthawi yake. Ndikumbukireni pondikomera mtima, Inu Mulungu wanga.
A i ka haawi ana mai o ka wahie i na manawa i oleloia'i, a i na hua mua. E hoomanao mai oe ia'u, e ko'u Akua, i mea e pono ai.

< Nehemiya 13 >