< Nahumu 2 >

1 Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
He stiede up, that schal scatere bifore thee, that schal kepe bisechyng; biholde thou the weie, coumforte leendis, strengthe thou vertu greetli.
2 Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
For as the Lord yeldide the pride of Jacob, so the pride of Israel; for distrieris scateriden hem, and distrieden the generaciouns of hem.
3 Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
The scheld of stronge men of hym ben firi, men of the oost ben in rede clothis; raynes of fire of chare, in the dai of his makyng redi; and the leederis therof ben asleep.
4 Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
In weies thei ben troblid togidere, cartis of foure horsis ben hurtlid togidere in stretis; the siyte of hem as laumpis, as leitis rennynge aboute.
5 Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
He schal bithenke of his stronge men, thei schulen falle in her weies; and swiftli thei schulen stie on the wallis therof, and schadewyng place schal be maad redi.
6 Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
Yatis of floodis ben openyd, and the temple is brokun doun to erthe.
7 Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
And a knyyt is led awei caitif, and the handmaidis therof schulen be dryuun sorewynge as culueris, grutchynge in her hertis.
8 Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
And Nynyue, as a cisterne of watris the watris therof; forsothe thei fledden; stonde ye, stonde ye, and there is not that schal turne ayen.
9 Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
Rauysche ye siluer, rauysche ye gold; and there is noon ende of richessis, of alle desirable vessels.
10 Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
It is distried, and kit, and to-rent, and herte failynge, and vnknyttinge of smale knees, and failynge in alle reynes; and the face of alle ben as blacnesse of a pot.
11 Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
Where is the dwellyng of liouns, and lesewis of whelpis of liouns? To whiche citee the lioun yede, that the whelp of the lioun schulde entre thidur, and there is not that schal make aferd.
12 Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
The lioun took ynow to hise whelpis, and slowy to his lionessis; and fillide her dennes with prei, and his couche with raueyn.
13 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”
Lo! Y to thee, seith the Lord God of oostis; and Y schal brenne thi cartis of foure horsis til to the hiyeste, and swerd schal ete thi smale liouns; and Y schal distrie thi prei fro the lond, and the vois of thi messangeris schulen no more be herd.

< Nahumu 2 >