< Nahumu 1 >

1 Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
Breme Nineviji; knjiga od utvare Nauma Elkošanina.
2 Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
Bog je revnitelj i Gospod je osvetnik; osvetnik je Gospod i gnjevi se; Gospod se sveti protivnicima svojim, i drži gnjev prema neprijateljima svojim.
3 Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
Gospod je spor na gnjev i velike je moæi; ali nikako ne pravda krivca; put je Gospodnji u vihoru i buri, i oblaci su prah od nogu njegovijeh.
4 Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
Zapreæuje moru i isušuje ga, i sve rijeke isušuje, vene Vasan i Karmil, i cvijet Vasanski vene.
5 Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
Gore se tresu od njega, i humovi se rastapaju, a zemlja gori pred njim i vasiljena i sve što živi u njoj.
6 Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
Pred gnjevom njegovijem ko æe se održati? i ko æe se oprijeti jarosti gnjeva njegova? jarost se njegova izlijeva kao oganj, i stijene se raspadaju pred njim.
7 Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
Dobar je Gospod, grad je u nevolji, i poznaje one koji se uzdaju u nj.
8 koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
Ali æe silnom poplavom uèiniti kraj mjestu njezinu, i tama æe goniti neprijatelje njegove.
9 Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
Šta smišljate Gospodu? on æe uèiniti kraj; neæe se dva puta podignuti pogibao.
10 Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
Jer kao trnje spleteni i kao od vina pijani proždrijeæe se kao suha slama.
11 Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
Iz tebe je izašao koji smišlja zlo Gospodu, savjetnik nevaljao.
12 Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
Ovako veli Gospod: ako i jesu u sili i mnogo ih ima, opet æe se isjeæi i proæi. Muèio sam te, neæu te više muèiti.
13 Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
Nego æu sada slomiti jaram njegov s tebe, i pokidaæu tvoje okove.
14 Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
Ali za tebe zapovjedi Gospod da se ne sije više ime tvoje; iz doma bogova tvojih istrijebiæu likove rezane i livene; naèiniæu ti od njega grob kad budeš prezren.
15 Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.
Eto, na gorama noge onoga koji nosi dobre glase, koji oglašuje mir. Praznuj, Juda, svoje praznike, ispunjaj zavjete svoje, jer zlikovac neæe više prolaziti po tebi; sasvijem se zatro.

< Nahumu 1 >