< Mika 6 >

1 Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
Slušajte šta govori Gospod: ustani, sudi se s gorama, i neka èuju humovi glas tvoj.
2 Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
Slušajte, gore i tvrdi temelji zemaljski, parbu Gospodnju, jer Gospod ima parbu s narodom svojim, i s Izrailjem se sudi.
3 “Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
Narode moj, šta sam ti uèinio? i èim sam ti dosadio? Odgovori mi.
4 Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
Jer te izvedoh iz zemlje Misirske i iskupih iz kuæe ropske i poslah pred tobom Mojsija, Arona i Mariju.
5 Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
Narode moj, opomeni se što naumi Valak car Moavski i što mu odgovori Valam sin Veorov, od Sitima do Galgala šta bi, da poznaš pravdu Gospodnju.
6 Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
Su èim æu doæi pred Gospoda da se poklonim Bogu višnjemu? hoæu li doæi preda nj sa žrtvama paljenicama? s teocima od godine?
7 Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
Hoæe li Gospodu biti mile tisuæe ovnova? desetine tisuæa potoka ulja? hoæu li dati prvenca svojega za prijestup svoj? plod utrobe svoje za grijeh duše svoje?
8 Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
Pokazao ti je, èovjeèe, što je dobro; i šta Gospod ište od tebe osim da èiniš što je pravo i da ljubiš milost i da hodiš smjerno s Bogom svojim?
9 Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
Glas Gospodnji vièe gradu, i ko je mudar vidi ime tvoje; slušajte prut i onoga koji ga je odredio.
10 Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
Nije li jošte u kuæi bezbožnikovoj blago nepravo? i efa krnja, gadna?
11 Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
Hoæe li mi biti èist u koga su mjerila lažna i u tobocu prijevarno kamenje?
12 Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
Jer su bogatuni njegovi puni nepravde, i stanovnici govore laž, i u ustima im je jezik prijevaran.
13 Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
Zato æu te i ja biti da oboliš, pustošiæu te za grijehe tvoje.
14 Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
Ti æeš jesti, ali se neæeš nasititi, i padanje tvoje biæe usred tebe; i sklanjaæeš, ali neæeš izbaviti, i što izbaviš predaæu maèu.
15 Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
Ti æeš sijati, ali neæeš žeti; ti æeš cijediti masline, ali se neæeš namazati uljem, i mast, ali neæeš piti vina.
16 Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”
Jer se drže uredbe Amrijeve i sva djela doma Ahavova, i hodite po savjetima njihovijem, da te predam u pogibao, i stanovnike njegove u potsmijeh, i nosiæete sramotu naroda mojega.

< Mika 6 >