< Mika 5 >

1 Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo, pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe. Adzakantha ndi ndodo pa chibwano cha wolamulira wa Israeli.
Saberi se sada u èete, èetnice, opsjedi nas, neka biju prutom po obrazu sudiju Izrailjeva.
2 “Koma iwe Betelehemu Efurata, ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda, mwa iwe mudzatuluka munthu amene adzalamulira Israeli, amene chiyambi chake nʼchakalekale, nʼchamasiku amakedzana.”
A ti, Vitlejeme Efrato, ako i jesi najmanji meðu tisuæama Judinijem, iz tebe æe mi izaæi koji æe biti gospodar u Izrailju, kojemu su izlasci od poèetka, od vjeènijeh vremena.
3 Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire. Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
Zato æe ih ostaviti dokle ne rodi ona koja æe roditi; tada æe se ostatak braæe njegove vratiti sa sinovima Izrailjevijem.
4 Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake mwa mphamvu ya Yehova, mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake. Ndipo iwo adzakhala mu mtendere, pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
I stajaæe i pašæe ih silom Gospodnjom, velièanstvom imena Gospoda Boga svojega; i oni æe nastavati, jer æe on tada biti velik do krajeva zemaljskih.
5 Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo. Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa, tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri, ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
I on æe biti mir; kad doðe Asirac u našu zemlju, i kad stupi u dvore naše, tada æemo podignuti na nj sedam pastira i osam knezova iz naroda.
6 Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga, dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo. Adzatipulumutsa kwa Asiriya akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu kudzatithira nkhondo.
I oni æe opasti zemlju Asirsku maèem i zemlju Nevrodovu na vratima njegovijem; i on æe nas izbaviti od Asirca kad doðe u našu zemlju i kad stupi na meðu našu.
7 Otsalira a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu ngati mame ochokera kwa Yehova, ngati mvumbi pa udzu, omwe sulamulidwa ndi munthu kapena kudikira lamulo la anthu.
I ostatak æe Jakovljev biti usred mnogih naroda kao rosa od Gospoda i kao sitan dažd po travi, koja ne èeka èovjeka niti se uzda u sinove èovjeèije.
8 Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu, mʼgulu la anthu a mitundu yambiri, ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango. Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa, amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula, ndipo palibe angathe kuzilanditsa.
I ostatak æe Jakovljev biti meðu narodima, usred mnogih naroda, kao lav meðu zvijerima šumskim, kao laviæ meðu stadima ovaca, koji kad ide tlaèi i rastrže i nema nikoga da izbavi.
9 Mudzagonjetsa adani anu, ndipo adani anu onse adzawonongeka.
Ruka æe ti se uzvisiti nad protivnicima tvojim, i svi æe se neprijatelji tvoji istrijebiti.
10 Yehova akuti, “Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse ndi kuphwasula magaleta anu.
I u ono æu vrijeme, govori Gospod, istrijebiti konje isred tebe i potræu kola tvoja.
11 Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu ndi kugwetsa malinga anu onse.
I zatræu gradove u tvojoj zemlji, i razvaliæu sva tvrda mjesta tvoja;
12 Ndidzawononga ufiti wanu ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.
I istrijebiæu vraèanje iz ruku tvojih, i neæeš imati gatara;
13 Ndidzawononga mafano anu osema pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu; simudzagwadiranso zinthu zopanga ndi manja anu.
I istrijebiæu likove tvoje rezane i stupove tvoje isred tebe, i neæeš se više klanjati djelu ruku svojih;
14 Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu, ndipo ndidzawononga mizinda yanu.
I iskorijeniæu gajeve tvoje isred tebe, i raskopaæu gradove tvoje,
15 Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya mitundu imene sinandimvere Ine.”
I izvršiæu osvetu s gnjevom i ljutinom na narodima koji ne slušaše.

< Mika 5 >