< Mika 4 >

1 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse. Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.
Men det skal skje i de siste dager, da skal fjellet der Herrens hus står, være grunnfestet på toppen av fjellene, og høit hevet skal det være over alle høider; og folkeslag skal strømme op på det.
2 Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
Og mange hedningefolk skal gå avsted og si: Kom, la oss gå op til Herrens berg og til Jakobs Guds hus, så han kan lære oss sine veier, og vi ferdes på hans stier! For fra Sion skal lov utgå, og Herrens ord fra Jerusalem.
3 Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
Og han skal dømme mellem mange folkeslag og skifte rett for veldige hedningefolk helt til de fjerneste land, og de skal smi sine sverd om til hakker og sine spyd til vingårdskniver; folkene skal ikke lenger løfte sverd mot hverandre og ikke mere lære å føre krig,
4 Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu, ndipo palibe amene adzawachititse mantha, pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.
men de skal sitte hver under sitt vintre og sitt fikentre, og ingen skal skremme dem; for Herrens, hærskarenes Guds munn har talt.
5 Mitundu yonse ya anthu itha kutsatira milungu yawo; ife tidzayenda mʼnjira za Yehova Mulungu wathu mpaka muyaya.
For alle folkene vandrer hvert i sin guds navn; men vi vandrer i Herrens, vår Guds navn evindelig og alltid.
6 “Tsiku limenelo, Yehova akuti, “ndidzasonkhanitsa olumala; ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa ndiponso amene ndinawalanga.
På den dag, sier Herren, vil jeg samle de haltende og sanke sammen de bortdrevne og dem jeg har faret ille med,
7 Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala. Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu. Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.
og jeg vil la de haltende bli i live som en rest og gjøre de langt bortdrevne til et tallrikt folk. Og Herren skal være konge over dem på Sions berg fra nu og til evig tid.
8 Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga, iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni, ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe; ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”
Og du hjordens tårn, du Sions datters haug! Til dig skal det nå, ja, det skal komme det forrige herredømme, kongedømmet over Jerusalems datter.
9 Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula, kodi ulibe mfumu? Kodi phungu wako wawonongedwa, kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?
Hvorfor skriker du nu så høit? Er det da ingen konge i dig, eller er din rådgiver omkommet, siden veer har grepet dig som den fødende kvinnes?
10 Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, ngati mayi pa nthawi yake yobereka, pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda ndi kugona kunja kwa mzindawo. Udzapita ku Babuloni; kumeneko udzapulumutsidwa, kumeneko Yehova adzakuwombola mʼmanja mwa adani ako.
Vri dig og jamre dig, Sions datter, som en fødende kvinne! For nu må du dra ut av byen og bo ute på marken, og du skal komme like til Babel. Der skal du bli utfridd, der skal Herren løse dig ut av dine fienders hånd.
11 Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu yasonkhana kulimbana nawe. Iwo akuti, “Tiyeni timudetse, maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”
Nu har mange folkeslag samlet sig mot dig, og de sier: Måtte det bli vanhelliget, så våre øine kan se med lyst på Sion!
12 Koma iwo sakudziwa maganizo a Yehova; iwo sakuzindikira cholinga chake, Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.
Men de kjenner ikke Herrens tanker og forstår ikke hans råd, at han har samlet dem som kornbånd til treskeplassen.
13 “Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo; ndidzakupatsa ziboda zamkuwa ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.” Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova, chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.
Stå op og tresk, du Sions datter! For ditt horn vil jeg gjøre til jern, og dine klover vil jeg gjøre til kobber, og du skal knuse mange folk, og jeg vil lyse deres rov i bann til Herren og deres gods til all jordens herre.

< Mika 4 >