< Mateyu 5 >

1 Iye ataona anthu ambiri, anakwera pa phiri nakhala pansi. Ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye,
A [Jezus], widząc tłumy, wszedł na górę, a gdy usiadł, podeszli do niego jego uczniowie.
2 ndipo anayamba kuwaphunzitsa kuti,
Wtedy otworzył usta i nauczał ich:
3 “Odala ndi amene ali osauka mu mzimu, chifukwa ufumu wakumwamba ndi wawo.
Błogosławieni ubodzy w duchu, ponieważ do nich należy królestwo niebieskie.
4 Odala ndi amene ali achisoni, chifukwa adzatonthozedwa.
Błogosławieni, którzy się smucą, ponieważ oni będą pocieszeni.
5 Odala ndi amene ali ofatsa, chifukwa adzalandira dziko lapansi.
Błogosławieni cisi, ponieważ oni odziedziczą ziemię.
6 Odala ndi amene akumva njala ndi ludzu la chilungamo, chifukwa adzakhutitsidwa.
Błogosławieni, którzy łakną i pragną sprawiedliwości, ponieważ oni będą nasyceni.
7 Odala ndi amene ali ndi chifundo, chifukwa adzawachitira chifundo.
Błogosławieni miłosierni, ponieważ oni dostąpią miłosierdzia.
8 Odala ndi amene ali oyera mtima, chifukwa adzaona Mulungu.
Błogosławieni czystego serca, ponieważ oni zobaczą Boga.
9 Ndi odala amene amabweretsa mtendere, chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.
Błogosławieni czyniący pokój, ponieważ oni będą nazwani synami Bożymi.
10 Odala ndi amene akuzunzidwa chifukwa cha chilungamo, pakuti ufumu wakumwamba ndi wawo.”
Błogosławieni, którzy cierpią prześladowanie z powodu sprawiedliwości, ponieważ do nich należy królestwo niebieskie.
11 “Inu ndinu odala anthu akamakunyozani, kukuzunzani, kukunenerani zoyipa zilizonse ndi kukunamizirani chifukwa cha Ine.
Błogosławieni jesteście, gdy z mego powodu będą wam złorzeczyć, prześladować was i mówić kłamliwie wszystko, co złe, przeciwko wam.
12 Sangalalani, kondwerani chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba, chifukwa moterenso ndi mmene anazunzira aneneri inu musanabadwe.
Radujcie się i weselcie, ponieważ obfita jest wasza nagroda w niebie; tak bowiem prześladowali proroków, którzy [byli] przed wami.
13 “Inu ndinu mchere wa dziko lapansi. Koma ngati mcherewo usukuluka, adzawukometsanso ndi chiyani? Ulibenso ntchito koma kungowutaya kunja, anthu nawuponda.
Wy jesteście solą ziemi; lecz jeśli sól zwietrzeje, czym [ją] posolą? Na nic się już nie przyda, tylko na wyrzucenie i podeptanie przez ludzi.
14 “Inu ndinu kuwunika kwa dziko lapansi. Mzinda wa pa phiri sungathe kubisika.
Wy jesteście światłością świata. Nie może się ukryć miasto położone na górze.
15 Anthu sayatsa nyale ndikuyivundikira ndi mbiya, mʼmalo mwake amayika poonekera ndipo imawunikira onse mʼnyumbamo.
Nie zapala się świecy i nie stawia jej pod naczyniem, ale na świeczniku, i świeci wszystkim, którzy [są] w domu.
16 Momwemonso kuwunika kwanu kuwale pamaso pa anthu kuti aone ntchito zanu zabwino ndi kulemekeza Atate anu akumwamba.
Tak niech wasza światłość świeci przed ludźmi, aby widzieli wasze dobre uczynki i chwalili waszego Ojca, który jest w niebie.
17 “Musaganize kuti ndinadza kudzathetsa malamulo kapena zonena za aneneri; sindinabwere kudzathetsa koma kukwaniritsa.
Nie sądźcie, że przyszedłem znieść Prawo albo Proroków. Nie przyszedłem znieść, ale wypełnić.
18 Ine ndikukuwuzani zoonadi kuti, kufikira kutha kwa thambo ndi dziko lapansi, chilichonse chimene chinalembedwa mʼmalamulo, ngakhale kalemba kakangʼonongʼono, chidzakwaniritsidwa.
Zaprawdę bowiem powiadam wam: Dopóki niebo i ziemia nie przeminą, ani jedna jota, ani jedna kreska nie przeminie z prawa, aż wszystko się wypełni.
19 Chifukwa chake aliyense amene aphwanya limodzi la malamulowa ngakhale lalingʼonongʼono ndi kuphunzitsa ena kuti achite chimodzimodzi, adzakhala wotsirizira mu ufumu wakumwamba, koma aliyense amene achita ndi kuphunzitsa malamulo awa adzakhala wamkulu mu ufumu wakumwamba.
Kto by więc złamał jedno z tych najmniejszych przykazań i uczyłby tak ludzi, będzie nazwany najmniejszym w królestwie niebieskim. A kto by [je] wypełniał i uczył, ten będzie nazwany wielkim w królestwie niebieskim.
20 Chifukwa chake ndikuwuzani kuti ngati chilungamo chanu sichiposa cha Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, zoonadi, simudzalowa mu ufumu wakumwamba.
Mówię wam bowiem: Jeśli wasza sprawiedliwość nie będzie obfitsza niż uczonych w Piśmie i faryzeuszy, żadnym sposobem nie wejdziecie do królestwa niebieskiego.
21 “Munamva kuti kunanenedwa kwa anthu kale kuti, ‘Usaphe ndipo kuti aliyense amene apha munthu adzaweruzidwa.’
Słyszeliście, że powiedziano przodkom: Nie będziesz zabijał, a kto by zabił, podlega sądowi.
22 Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wokwiyira mʼbale wake adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene wonena mʼbale wake kuti, ‘Ndiwe wopanda phindu,’ adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu lalikulu. Ndipo aliyense amene anganene mnzake ‘wopandapake’ adzatengeredwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene angamunene mnzake kuti, ‘Chitsiru iwe,’ adzaponyedwa ku gehena. (Geenna g1067)
Lecz ja wam mówię: Każdy, kto się gniewa na swego brata bez przyczyny, podlega sądowi, a kto powie swemu bratu: Raka, podlega Radzie, a kto powie: Głupcze, podlega [karze] ognia piekielnego. (Geenna g1067)
23 “Nʼchifukwa chake, pamene ukupereka chopereka chako pa guwa lansembe ndipo nthawi yomweyo ukumbukira kuti mʼbale wako ali nawe chifukwa,
Jeśli więc przyniesiesz swój dar na ołtarz i tam przypomnisz sobie, że twój brat ma coś przeciwko tobie;
24 usiye choperekacho pa guwa lansembepo, choyamba pita kayanjane ndi mʼbale wako; ukatero bwera kudzapereka chopereka chakocho.
Zostaw swój dar tam przed ołtarzem, idź i najpierw pojednaj się ze swoim bratem, a potem przyjdź i ofiaruj swój dar.
25 “Fulumira kuyanjana ndi mnzako amene unamulakwira nthawi ya milandu isanafike chifukwa angakupereke kwa oweruza amene angakupereke kwa mlonda ndipo mlondayo angakutsekere mʼndende.
Pogódź się ze swoim przeciwnikiem szybko, dopóki jesteś z nim w drodze, aby przeciwnik nie wydał cię sędziemu, a sędzia strażnikowi, i aby nie wtrącono cię do więzienia.
26 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti sudzatuluka mʼndende mpaka utalipira zonse.
Zaprawdę powiadam ci: Nie wyjdziesz stamtąd, dopóki nie oddasz ostatniego grosza.
27 “Munamva kuti kunanenedwa kuti, ‘Usachite chigololo.’
Słyszeliście, że powiedziano przodkom: Nie będziesz cudzołożył.
28 Koma Ine ndikuwuzani kuti aliyense woyangʼana mkazi momusirira wachita naye kale chigololo mu mtima mwake.
Lecz ja wam mówię: Każdy, kto patrzy na kobietę, aby jej pożądać, już popełnił z nią cudzołóstwo w swoim sercu.
29 Ngati diso lako lakumanja likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna g1067)
Jeśli więc twoje prawe oko jest ci powodem upadku, wyłup je i odrzuć od siebie. Pożyteczniej bowiem jest dla ciebie, aby zginął jeden z twoich członków, niż żeby całe twoje ciało było wrzucone do ognia piekielnego. (Geenna g1067)
30 Ndipo ngati dzanja lako lamanja likuchimwitsa, ulidule ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna g1067)
A jeśli twoja prawa ręka jest ci powodem upadku, odetnij ją i odrzuć od siebie. Pożyteczniej bowiem jest dla ciebie, aby zginął jeden z twoich członków, niż żeby całe twoje ciało było wrzucone do ognia piekielnego. (Geenna g1067)
31 “Ananena kuti, ‘Aliyense wosudzula mkazi wake ayenera amupatse kalata ya chisudzulo.’
Powiedziano też: Kto oddala swoją żonę, niech jej da list rozwodowy.
32 Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake pa chifukwa china chilichonse osati chifukwa cha chiwerewere, akumuchititsa mkaziyo chigololo ndipo aliyense wokwatira mkaziyo, akuchitanso chigololo.
Lecz ja wam mówię: Kto oddala swoją żonę – poza przypadkiem nierządu – prowadzi ją do cudzołóstwa, a kto żeni się z oddaloną, cudzołoży.
33 “Munamvanso kuti kunanenedwa kwa anthu akale kuti, ‘Musaphwanye lonjezo; koma sungani malonjezo anu amene mwachita kwa Yehova.’
Słyszeliście też, że powiedziano przodkom: Nie będziesz fałszywie przysięgał, ale dotrzymasz Panu swych przysiąg.
34 Koma ndikuwuzani kuti musalumbire ndi pangʼono pomwe kutchula kumwamba chifukwa kuli mpando waufumu wa Mulungu.
Lecz ja wam mówię: Wcale nie przysięgajcie – ani na niebo, gdyż jest tronem Boga;
35 Kapena kutchula dziko lapansi, chifukwa ndi chopondapo mapazi ake; kapena kutchula Yerusalemu, chifukwa ndi mzinda wa mfumu yayikulu.
Ani na ziemię, gdyż jest podnóżkiem jego stóp, ani na Jerozolimę, gdyż jest miastem wielkiego króla.
36 Ndipo musalumbire ndi mutu wanu chifukwa simungathe kuyeretsa ngakhale kudetsa tsitsi limodzi.
Ani na swoją głowę nie będziesz przysięgał, gdyż nie możesz jednego włosa uczynić białym albo czarnym.
37 Koma ‘Inde’ wanu akhaledi ‘Inde’ kapena ‘Ayi’ wanu akhaledi ‘Ayi,’ chilichonse choposera apa, chichokera kwa woyipayo.
Ale wasza mowa niech będzie: Tak – tak, nie – nie. A co jest ponadto, pochodzi od złego.
38 “Munamva kuti, ‘Diso kulipira diso ndi dzino kulipira dzino.’
Słyszeliście, że powiedziano: Oko za oko i ząb za ząb.
39 Koma ndikuwuzani kuti musamukanize munthu woyipa, akakumenya patsaya mupatseni tsaya linalo.
Lecz ja wam mówię: Nie sprzeciwiajcie się złemu, ale jeśli ktoś uderzy cię w prawy policzek, nadstaw mu i drugi.
40 Ndipo ngati wina afuna kukuzenga mlandu kuti akulande malaya ako, umupatsenso mkanjo wako.
Temu, kto chce się z tobą procesować i wziąć twoją szatę, zostaw i płaszcz.
41 Ngati wina akukakamiza kuti uyende naye mtunda umodzi, iwe uyende naye mitunda iwiri.
A jeśli ktoś cię przymusza, żebyś [szedł] z nim jedną milę, idź z nim [i] dwie.
42 Wina akakupempha kanthu umupatse, ndipo wofuna kubwereka usamukanize.
Temu, kto cię prosi, daj, a od tego, kto chce od ciebie pożyczyć, nie odwracaj się.
43 “Munamva kuti, ‘Konda mnansi wako ndi kudana ndi mdani wako.’
Słyszeliście, że powiedziano: Będziesz miłował swego bliźniego, a swego nieprzyjaciela będziesz nienawidził.
44 Koma Ine ndikuwuzani kuti, ‘Kondani adani anu ndi kuwapempherera okuzunzani
Lecz ja wam mówię: Miłujcie waszych nieprzyjaciół, błogosławcie tym, którzy was przeklinają, dobrze czyńcie tym, którzy was nienawidzą i módlcie się za tych, którzy wam wyrządzają zło i prześladują was;
45 kuti mukhale ana a Atate anu akumwamba, amene awalitsa dzuwa lake pa oyipa ndi pa abwino, nagwetsa mvula pa olungama ndi pa osalungama.’
Abyście byli synami waszego Ojca, który [jest] w niebie. On bowiem sprawia, że jego słońce wschodzi nad złymi i nad dobrymi i deszcz zsyła na sprawiedliwych i niesprawiedliwych.
46 Ngati mukonda amene akukondani inu, mudzapeza mphotho yanji? Kodi ngakhale amisonkho sachita chimodzimodzi?
Jeśli bowiem miłujecie tych, którzy was miłują, jakąż macie nagrodę? Czyż i celnicy tego nie czynią?
47 Ndipo ngati inu mupatsa moni abale anu okhaokha mukuchita chiyani choposa ena? Kodi ngakhale akunja sachita chimodzimodzi?
A jeśli tylko waszych braci pozdrawiacie, cóż szczególnego czynicie? Czyż i celnicy tak nie czynią?
48 Nʼchifukwa chake, inu khalani angwiro monga Atate anu akumwamba ali wangwiro.”
Bądźcie więc doskonali, tak jak doskonały jest wasz Ojciec, który jest w niebie.

< Mateyu 5 >