< Mateyu 4 >

1 Pambuyo pake Yesu anatsogozedwa ndi Mzimu Woyera kupita ku chipululu kukayesedwa ndi mdierekezi.
Then Jesus was led by the Spirit into the wilderness to be tempted by the devil.
2 Ndipo atasala kudya masiku makumi anayi usana ndi usiku, anamva njala.
And having fasted forty days and forty nights, afterward he was hungry.
3 Woyesayo anadza kwa Iye nati, “Ngati ndinu mwana wa Mulungu, sandutsani miyala iyi kuti ikhale buledi.”
And after he who tempts came, he said to him, If thou are the Son of God, speak so that these stones may become bread.
4 Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa, ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha, koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Mulungu.’”
But having answered, he said, It is written, Man will not live on bread alone, but on every word coming out through the mouth of God.
5 Pamenepo mdierekezi anapita naye ku mzinda woyera namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu.
Then the devil takes him into the holy city, and stands him on the pinnacle of the temple.
6 Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu, dziponyeni nokha pansi. Pakuti kwalembedwa: “‘Adzalamulira angelo ake za iwe, ndipo adzakunyamula ndi manja awo kuti phazi lako lisagunde pa mwala.’”
And he says to him, If thou are the Son of God, cast thyself down, for it is written, He will command his agents about thee, and, They will take thee up in their hands, lest thou dash thy foot against a stone.
7 Yesu anamuyankha kuti, “Kwalembedwanso: ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’”
Jesus said to him, Again it is written, Thou shall not challenge the Lord thy God.
8 Kenaka mdierekezi anamutengera Yesu ku phiri lalitali kwambiri namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi ndi ulemerero wawo.
Again, the devil takes him onto an exceedingly high mountain, and shows him all the kingdoms of the world, and the glory of them.
9 Ndipo anati kwa Iye, “Zonsezi ndidzakupatsani ngati mutandiweramira ndi kundipembedza ine.”
And he says to him, All these things I give thee, if after falling down, thou will worship me.
10 Yesu anati kwa iye, “Choka Satana! Zalembedwa, ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’”
Then Jesus says to him, Get thee behind me, Satan, for it is written, Thou shall worship the Lord thy God, and him only thou shall serve.
11 Pamenepo mdierekezi anamusiya ndipo angelo anamutumikira Iye.
Then the devil leaves him, and behold, agents came and served him.
12 Yesu atamva kuti Yohane anamutsekera mʼndende, anabwerera ku Galileya.
Now when Jesus heard that John was delivered up, he departed into Galilee.
13 Ndipo atachoka ku Nazareti anapita ku Kaperenawo ndi kukhala mʼmbali mwa nyanja, mʼdera la Zebuloni ndi Nafutali;
And having left Nazareth behind, after coming, he dwelt in Capernaum by the sea in the regions of Zebulun and Naphtali,
14 pokwaniritsa zimene zinanenedwa kudzera mwa mneneri Yesaya kuti,
so that what was spoken through Isaiah the prophet might be fulfilled, which says,
15 “Dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, njira ya ku nyanja, kutsidya lija la Yorodani, Galileya wa anthu a mitundu ina,
The land of Zebulun and the land of Naphtali, way of the sea, beyond the Jordan, Galilee of the Gentiles,
16 anthu okhala mu mdima awona kuwala kwakukulu; ndi kwa iwo okhala mʼdziko la mthunzi wa imfa kuwunika kwawafikira.”
the people who dwell in darkness saw a great light, and to those who dwell in the region and shadow of death, light sprang up to them.
17 Kuyambira nthawi imeneyo, Yesu anayamba kulalikira nati, “Tembenukani mtima ufumu wakumwamba wayandikira.”
From that time Jesus began to preach, and to say, Repent ye, for the kingdom of the heavens has approached.
18 Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona abale awiri, Simoni wotchedwa Petro ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja popeza anali asodzi.
And walking by the sea of Galilee, he saw two brothers, Simon who is called Peter, and Andrew his brother, casting a net into the sea, for they were fishermen.
19 Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
And he says to them, Come behind me, and I will make you fishermen of men.
20 Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.
And straightaway having left the nets, they followed him.
21 Atapita patsogolo, anaona abale ena awiri, Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo. Iwowa anali mʼbwato ndi abambo awo, Zebedayo, akukonza makoka awo ndipo Yesu anawayitana.
And having gone on from there he saw two other brothers, James the son of Zebedee, and John his brother, in the boat with Zebedee their father, mending their nets. And he called them.
22 Nthawi yomweyo anasiya bwato ndi abambo awo namutsata Iye.
And straightaway having left the boat and their father, they followed him.
23 Yesu anayendayenda mu Galileya kuphunzitsa mʼmasunagoge awo, nalalikira Uthenga Wabwino wa ufumu ndi kuchiritsa matenda onse pakati pa anthu.
And Jesus went around all Galilee, teaching in their synagogues, and preaching the good news of the kingdom, and healing every sickness and every disease among the people.
24 Mbiri yake yonse inawanda ku Siriya konse ndipo anthu anabweretsa kwa Iye onse amene anali odwala nthenda zosiyanasiyana, womva maululu aakulu, ogwidwa ndi ziwanda, odwala matenda akugwa ndi olumala ndipo Iye anawachiritsa.
And his fame went forth into all Syria. And they brought to him all those faring badly with various diseases, and gripped with pain, and being demon-possessed, and being lunatic, and paralyzed. And he healed them.
25 Magulu ambiri a anthu anachokera ku Galileya, Dekapoli, Yerusalemu, Yudeya ndi ku madera a kutsidya la mtsinje wa Yorodani namutsata Iye.
And many multitudes from Galilee and Decapolis and Jerusalem and Judea and beyond the Jordan followed him.

< Mateyu 4 >