< Marko 6 >

1 Yesu anachoka kumeneko napita ku mudzi kwawo, pamodzi ndi ophunzira ake.
On leaving that place, Jesus, followed by his disciples, went to his own part of the country.
2 Tsiku la Sabata litafika, anayamba kuphunzitsa mʼsunagoge, ndipo ambiri amene anamumva anadabwa. Iwo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu anazitenga kuti zimenezi? Kodi ndi nzeru yotani imene munthu ameneyu wapatsidwa, kuti Iye akuchitanso zodabwitsa!
When the Sabbath came, he began to teach in the Synagogue; and the people, as they listened, were deeply impressed. “Where did he get this?” they said, “and what is this wisdom that has been given him? and these miracles which he is doing?
3 Kodi uyu si mpalamatabwa uja? Kodi uyu si mwana wa Mariya ndi mʼbale wa Yakobo, Yose, Yudasi ndi Simoni? Kodi alongo ake si ali ndi ife?” Ndipo anakhumudwa naye.
Is not he the carpenter, the son of Mary, and the brother of James, and Joses, and Judas, and Simon? And are not his sisters, too, living here among us?” This proved a hindrance to their believing in him;
4 Yesu anawawuza kuti, “Mneneri amalemekezedwa kulikonse kupatula kwawo, ndi pakati pa abale ake ndi a mʼbanja mwake.”
on which Jesus said: “A prophet is not without honour, except in his own country, and among his own relations, and in his own home.”
5 Sanachite zodabwitsa kumeneko, koma anangosanjika manja pa odwala ochepa ndi kuwachiritsa.
And he could not work any miracle there, beyond placing his hands upon a few infirm persons, and curing them;
6 Ndipo Iye anadabwa chifukwa chakusowa chikhulupiriro kwawo. Pamenepo Yesu anayenda mudzi ndi mudzi kuphunzitsa.
and he wondered at the want of faith shown by the people. Jesus went round the villages, one after another, teaching.
7 Atayitana khumi ndi awiriwo, Iye anawatuma awiriawiri ndipo anawapatsa ulamuliro pa mizimu yoyipa.
He called the Twelve to him, and began to send them out as his Messengers, two and two, and gave them authority over foul spirits.
8 Zomwe anawalangiza ndi izi: “Musatenge kanthu ka paulendo koma ndodo yokha; osatenga buledi, thumba, kapena ndalama.
He instructed them to take nothing but a staff for the journey — not even bread, or a bag, or pence in their purse;
9 Muvale nsapato koma osatenga malaya apadera.
but they were to wear sandals, and not to put on a second coat.
10 Pamene mulowa mʼnyumba mukakhale momwemo kufikira mutachoka mʼmudzimo.
“Whenever you go to stay at a house,” he said, “remain there till you leave that place;
11 Ndipo ngati pa malo ena sakakulandirani kapena kukumverani, sasani fumbi la kumapazi anu pamene mukuchoka, kuti ukhale umboni wowatsutsa.”
and if a place does not welcome you, or listen to you, as you go out of it shake off the dust that is on the soles of your feet, as a protest against them.”
12 Anatuluka kupita kukalalikira kuti anthu atembenuke mtima.
So they set out, and proclaimed the need of repentance.
13 Anatulutsa ziwanda zambiri ndi kudzoza mafuta odwala ambiri ndi kuwachiritsa.
They drove out many demons, and anointed with oil many who were infirm, and cured them.
14 Mfumu Herode anamva zimenezi, pakuti dzina la Yesu linali litadziwika kwambiri. Ena amati, “Yohane Mʼbatizi waukitsidwa kwa akufa, ndipo nʼchifukwa chake mphamvu zochita zodabwitsa zinkagwira ntchito mwa Iye.”
Now King Herod heard of Jesus; for his name had become well known. People were saying — “John the Baptizer must have risen from the dead, and that is why these miraculous powers are active in him.”
15 Ena anati, “Iye ndi Eliya.” Enanso anati, “Ndi mneneri, ofanana ndi mmodzi wa aneneri akale.”
Others again said — “He is Elijah,” and others — “He is a Prophet, like one of the great Prophets.”
16 Koma Herode atamva zimenezi anati, “Yohane, munthu amene ndinamudula mutu, waukitsidwa kuchokera kwa akufa.”
But when Herod heard of him, he said — “The man whom I beheaded — John — he must be risen!”
17 Pakuti Herode iye mwini analamula kuti amumange Yohane ndi kumuyika mʼndende. Anachita izi chifukwa cha Herodia, mkazi wa mʼbale wake Filipo, amene iye anamukwatira.
For Herod himself had sent and arrested John, and put him in prison, in chains, to please Herodias, the wife of his brother Philip, because Herod had married her.
18 Pakuti Yohane ankanena kwa Herode kuti, “Sikololedwa kwa inu kuti mukwatire mkazi wa mʼbale wanu.”
For John had said to Herod — “You have no right to be living with your brother’s wife.”
19 Ndipo Herodia anamusungira Yohane chidani ndipo anafuna kumupha, koma sanathe kutero,
So Herodias was incensed against John, and wanted to put him to death, but was unable to do so,
20 chifukwa Herode anaopa Yohane ndipo anamuteteza, podziwa kuti iye anali munthu wolungama ndi woyera mtima. Herode akamamva Yohane, ankathedwa nzeru; komabe amakonda kumumvetsera.
because Herod stood in fear of John, knowing him to be an upright and holy man, and protected him. He had listened to John, but still remained much perplexed, and yet he found pleasure in listening to him.
21 Pomaliza mpata unapezeka. Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwake, Herode anakonzera phwando akuluakulu ake, akulu a ankhondo ndi anthu odziwika a mu Galileya.
A suitable opportunity, however, occurred when Herod, on his birthday, gave a dinner to his high officials, and his generals, and the foremost men in Galilee.
22 Mwana wamkazi wa Herodia atabwera ndi kudzavina, anakondweretsa Herode ndi alendo ake a pa mphwandopo. Mfumu inati kwa mtsikanayo, “Undipemphe chilichonse chimene ukuchifuna, ndipo ndidzakupatsa.”
And when his daughter — that is, the daughter of Herodias — came in and danced, she delighted Herod and those who were dining with him. “Ask me for whatever you like,” the King said to the girl, “and I will give it to you”;
23 Ndipo analonjeza ndi lumbiriro kuti, “Chilichonse chimene upempha ndidzakupatsa, ngakhale theka la ufumu wanga.”
and he swore to her that he would give her whatever she asked him — up to half his kingdom.
24 Iye anatuluka nati kwa amayi ake, “Kodi ndikapemphe chiyani?” Iye anamuyankha kuti, “Mutu wa Yohane Mʼbatizi.”
The girl went out, and said to her mother “What must I ask for?” “The head of John the Baptizer,’ answered her mother.
25 Nthawi yomweyo mtsikana uja anafulumira kupita komwe kunali mfumu ndi pempho lake: “Ndikufuna kuti mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”
So she went in as quickly as possible to the King, and made her request. “I want you,” she said, “to give me at once, on a dish, the head of John the Baptist.”
26 Mfumu inamva chisoni chachikulu, koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo ake a pa mphwandolo, sanafune kumukaniza.
The King was much distressed; yet, on account of his oath and of the guests at his table, he did not like to refuse her.
27 Nthawi yomweyo iye anatumiza yemwe anali ndi ulamuliro wonyonga anthu kuti abweretse mutu wa Yohane. Munthuyo anapita, nakadula mutu wa Yohane mʼndende,
He immediately dispatched one of his bodyguard, with orders to bring John’s head. The man went and beheaded John in the prison,
28 nabweretsa mutuwo mʼmbale. Anawupereka kwa mtsikanayo, ndipo iye anakapereka kwa amayi ake.
and, bringing his head on a dish, gave it to the girl, and the girl gave it to her mother.
29 Atamva izi, ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo ndi kukawuyika mʼmanda.
When John’s disciples heard of it, they came and took his body away, and laid it in a tomb.
30 Atumwi anasonkhana mozungulira Yesu namufotokozera zonse zomwe anachita ndi kuphunzitsa.
When the Apostles came back to Jesus, they told him all that they had done and all that they had taught.
31 Popeza kuti panali anthu ambiri amene amabwera ndi kumapita, analibe mpata wakuti adye, ndipo Iye anawawuza kuti, “Tiyeni kuno kumalo achete kuti tikapume.”
“Come by yourselves privately to some lonely spot,” he said, “and rest for a while” — for there were so many people coming and going that they had not time even to eat.
32 Ndipo anachoka okha pa bwato napita kumalo a okhaokha.
So they set off privately in their boat for a lonely spot.
33 Koma ambiri amene anawaona akuchoka anawazindikira ndipo anathamanga wapansi kuchokera mʼmidzi yonse nakayambirira kufika.
And many people saw them going, and recognised them, and from all the towns they flocked together to the place on foot, and got there before them.
34 Yesu atafika ku mtunda ndi kuona gulu lalikulu la anthu, anamva nawo chisoni chifukwa anali ngati nkhosa zopanda mʼbusa. Ndipo anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambiri.
On getting out of the boat, Jesus saw a great crowd, and his heart was moved at the sight of them, because they were ‘like sheep without a shepherd’; and he began to teach them many things.
35 Pa nthawi iyi nʼkuti dzuwa litapendeka, ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kuthengo, ndipo ano ndi madzulo.
When it grew late, his disciples came up to him, and said: “This is a lonely spot, and it is already late.
36 Awuzeni anthuwa azipita ku midzi ndi madera ozungulira, kuti akadzigulire kanthu kakuti adye.”
Send the people away, so that they may go to the farms and villages around and buy themselves something to eat.”
37 Koma Iye anayankha kuti, “Apatseni kanthu koti adye.” Iwo anati kwa Iye, “Apa pafunika ndalama za miyezi isanu ndi itatu zomwe munthu amalandira! Kodi tipite kukagwiritsa ntchito ndalama zotere kugulira buledi kuti tiwapatse adye?”
But Jesus answered: “It is for you to give them something to eat.” “Are we to go and buy twenty pounds’ worth of bread,” they asked, “to give them to eat?”
38 Iye anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati? Pitani mukaone.” Ataona anati kwa Iye, “Asanu ndi nsomba ziwiri.”
“How many loaves have you?” he asked; “Go, and see.” When they had found out, they told him: “Five, and two fishes.”
39 Pamenepo Yesu anawalamulira kuti awakhazike anthu pansi mʼmagulu pa msipu obiriwira.
Jesus directed them to make all the people take their seats on the green grass, in parties;
40 Ndipo anakhala pansi mʼmagulu a anthu 100 ndi gulu la anthu makumi asanu.
and they sat down in groups — in hundreds, and in fifties.
41 Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri, nayangʼana kumwamba, Iye anayamika nagawa malofu a bulediwo. Kenaka anawapatsa ophunzira ake kuti awapatse anthu. Ndipo anagawanso nsomba ziwirizo kwa onse.
Taking the five loaves and the two fishes, Jesus looked up to Heaven, and said the blessing; he broke the loaves into pieces, and gave them to his disciples for them to serve out to the people, and he divided the two fishes also among them all.
42 Onse anadya ndipo anakhuta,
Every one had sufficient to eat;
43 ndipo ophunzira ake anatola buledi ndi nsomba zotsalira zokwanira madengu khumi ndi awiri.
and they picked up enough broken pieces to fill twelve baskets, as well as some of the fish.
44 Chiwerengero cha amuna amene anadya chinali 5,000.
The men who ate the bread were five thousand in number.
45 Nthawi yomweyo Yesu anawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita ku Betisaida, pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita.
Immediately afterwards Jesus made his disciples get into the boat, and cross over in advance, in the direction of Bethsaida, while he himself was dismissing the crowd.
46 Atawasiya, Iye anakwera ku phiri kukapemphera.
After he had taken leave of the people, he went away up the hill to pray.
47 Pofika madzulo, bwato linali pakati pa nyanja, ndipo Iye anali yekha pa mtunda.
When evening fell, the boat was out in the middle of the Sea, and Jesus on the shore alone.
48 Iye anaona ophunzira ake akuvutika popalasa bwato, chifukwa mphepo imawomba mokumana nawo. Pa nthawi ya mʼbandakucha Iye anafika kwa iwo akuyenda pa nyanja. Anali pafupi kuwapitirira,
Seeing them labouring at the oars — for the wind was against them — about three hours after midnight Jesus came towards them, walking on the water, intending to join them.
49 koma atamuona Iye akuyenda pa nyanja, anaganiza kuti anali mzukwa. Iwo anafuwula,
But, when they saw him walking on the water, they thought it was a ghost, and cried out;
50 pakuti onse anamuona ndipo anachita mantha. Nthawi yomweyo Iye anawayankhula nati, “Limbani mtima! Ndine. Musachite mantha.”
for all of them saw him, and were terrified. But Jesus at once spoke to them. “Courage!” he said, “it is I; do not be afraid!”
51 Ndipo Iye anakwera mʼbwato pamodzi nawo, ndipo mphepo inaleka. Iwo anadabwa kwambiri,
Then he got into the boat with them, and the wind dropped. The disciples were utterly amazed,
52 popeza sanazindikire zimene zinachitika pa malofu a buledi; pakuti mitima yawo inali yowuma.
for they had not understood about the loaves, their minds being slow to learn.
53 Atawoloka, anafika ku Genesareti nayima pa dooko.
When they had crossed over, they landed at Gennesaret, and moored the boat.
54 Atangotuluka mʼbwato, anthu anamuzindikira Yesu.
But they had no sooner left her than the people, recognising Jesus,
55 Anathamanga uku ndi uko mʼdera lonse nakanyamula odwala pa machira kupita nawo kulikonse kumene anamva kuti kuli Iye.
hurried over the whole country-side, and began to carry about upon mats those who were ill, wherever they heard he was.
56 Ndipo kulikonse kumene anapita, ku midzi, mʼmizinda ndi madera a ku midzi, iwo anayika odwala mʼmalo a mʼmisika. Iwo anamupempha kuti awalole kuti akhudze ngakhale mphonje za mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachira.
So wherever he went — to villages, or towns, or farms — they would lay their sick in the market-places, begging him to let them touch only the tassel of his cloak; and all who touched were made well.

< Marko 6 >