< Marko 5 >

1 Ndipo anawoloka nyanja napita ku dera la Gerasa.
Tedy přeplavili se přes moře do krajiny Gadarenských.
2 Yesu atatuluka mʼbwato, munthu amene anali ndi mzimu woyipa anachoka ku manda ndi kukumana naye.
A jakž vyšel z lodí, hned se s ním potkal člověk z hrobů, maje ducha nečistého.
3 Munthuyu amakhala ku manda, ndipo panalibe amene akanatha kumumanganso ngakhale ndi unyolo.
Kterýž bydlil v hrobích, a aniž ho kdo mohl řetězy svázati,
4 Pakuti nthawi zambiri akamumanga manja ndi miyendo amadula maunyolo ndi kudula zitsulo zimene zinali mʼmapazi ake. Panalibe amene anali ndi mphamvu yoti ndi kumugonjetsa.
Proto že často byv pouty a řetězy okován, polámal řetězy, a pouta roztrhal, a žádný nemohl ho skrotiti.
5 Usana ndi usiku ankakhala ku manda ndi kumapiri, akulira ndi kudzicheka ndi miyala.
A vždycky ve dne i v noci na horách a v hrobích byl, křiče a tepa se kamením.
6 Ataona Yesu ali patali, anathamanga nagwa pa mawondo ake pamaso pake.
Uzřev pak Ježíše zdaleka, běžel a poklonil se jemu,
7 Iye anafuwula kwambiri nati, “Mukufuna muchite nane chiyani, Yesu Mwana wa Mulungu Wammwambamwamba? Lumbirani kwa Mulungu kuti simundizunza!”
A křiče hlasem velikým, řekl: Co jest tobě do mne, Ježíši, Synu Boha nejvyššího? Zaklínám tě skrze Boha, abys mne netrápil.
8 Pakuti Yesu anati kwa iye, “Tuluka mwa munthuyu, iwe mzimu woyipa!”
(Nebo pravil jemu: Vyjdiž, duchu nečistý, z člověka tohoto.)
9 Ndipo Yesu anamufunsa iye, “Dzina lako ndani?” Iye anayankha kuti, “Dzina langa ndine Legiyo, pakuti tilipo ambiri.”
I otázal se ho: Jakť říkají? A on odpovídaje, řekl: Množství jméno mé jest, nebo jest nás mnoho.
10 Ndipo anamupempha Yesu mobwerezabwereza kuti asazitulutse mʼderalo.
I prosil ho velmi, aby jich nevyháněl z té krajiny.
11 Gulu lalikulu la nkhumba limadya mʼmbali mwa phiri limene linali pafupi.
Bylo pak tu při horách stádo vepřů veliké pasoucích se.
12 Ziwandazo zinapempha Yesu kuti, “Titumizeni pakati pa nkhumbazo; ndipo mutilole tilowe mwa izo.”
I prosili ho všickni ti ďáblové, řkouce: Pusť nás do vepřů, ať do nich vejdeme.
13 Iye anazipatsa chilolezo, ndipo mizimu yoyipayo inatuluka ndi kukalowa mu nkhumbazo. Gulu la nkhumba, zokwana pafupifupi 2,000 zinathamanga kutsetserekera ku nyanja ndipo zinamira.
I povolil jim hned Ježíš. A vyšedše duchové nečistí, vešli do těch vepřů. I běželo to stádo s vrchu dolů do moře, (a bylo jich ke dvěma tisícům, ) i ztonuli v moři.
14 Omwe amaweta nkhumbazo anathawa ndi kukawuza anthu za izi mu mzinda ndi ku madera a ku midzi, ndipo anthu anapita kukaona zomwe zinachitika.
Ti pak, kteříž ty vepře pásli, utekli, a oznámili to v městě i ve vsech. I vyšli, aby viděli, co by to bylo, což se stalo.
15 Atafika kwa Yesu, anaona munthu amene anagwidwa ndi ziwanda zambiri uja atakhala pansi pomwepo, atavala, ndipo ali bwinobwino. Iwo anachita mantha.
I přišli k Ježíšovi, a uzřeli toho, kterýž býval trápen od ďábelství, an sedí, odín jsa, a maje zdravý rozum, toho, kterýž míval množství. I báli se.
16 Amene anaona zimenezi anawuza anthu zomwe zinachitika kwa munthu wogwidwa ndi ziwandayo ndipo anawawuzanso za nkhumbazo.
A kteříž to viděli, vypravovali jim, kterak se stalo tomu, kterýž měl ďábelství i o vepřích.
17 Ndipo anthu anayamba kumupempha Yesu kuti achoke mʼdera lawo.
Tedy počali ho prositi, aby odšel z krajin jejich.
18 Yesu akulowa mʼbwato, munthu amene anagwidwa ndi ziwanda uja anamupempha kuti apite nawo.
A když vstoupil na lodí, prosil ho ten, kterýž trápen býval od ďábelství, aby s ním byl.
19 Yesu sanamulole, koma anati, “Pita kwanu ku banja lako ndipo ukawawuze zimene Ambuye wakuchitira, ndi chifundo chimene wakuchitira.”
Ježíš pak nedopustil mu, ale řekl jemu: Jdi k svým do domu svého, a zvěstuj jim, kterak veliké věci učinil tobě Pán, a že slitoval se nad tebou.
20 Pomwepo munthuyo anapita nayamba kuwuza anthu a ku Dekapoli zinthu zimene Yesu anamuchitira. Ndipo anthu onse anadabwa.
I odšel, a počal ohlašovati v krajině Desíti měst, kterak veliké věci učinil mu Ježíš. I divili se všickni.
21 Yesu atawolokeranso pa bwato kupita mbali ina ya nyanja, gulu lalikulu la anthu linasonkhana momuzungulira. Ali mʼmbali mwa nyanja,
A když se přeplavil Ježíš na lodí zase na druhou stranu, sšel se k němu zástup mnohý. A byl u moře.
22 mmodzi wa akulu a mʼsunagoge, dzina lake Yairo anafika pamenepo. Ataona Yesu, anagwa pa mapazi ake,
A aj, přišel jeden z knížat školy, jménem Jairus, a uzřev jej, padl k nohám jeho.
23 ndi kumudandaulira kwambiri nati, “Mwana wanga wamkazi wamngʼono ali pafupi kufa. Chonde tiyeni kuti mukamusanjike manja kuti akachiritsidwe nakhala ndi moyo.”
A velmi ho prosil, řka: Dcerka má skonává. Poď, vlož na ni ruce, aby uzdravena byla, a budeť živa.
24 Ndipo Yesu anapita naye. Gulu lalikulu la anthu linamutsata ndi kumamupanikiza Iye.
I šel s ním, a zástup mnohý šel za ním, i tiskl jej.
25 Pomwepo panali mayi amene amadwala nthenda yotaya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri.
(Tedy žena jedna, kteráž tok krve měla dvanácte let,
26 Iye anavutika kwambiri pamene asingʼanga ambiri ankamusamalira ndipo anagwiritsa ntchito zonse anali nazo, koma mʼmalo mochira, nthenda yake inkakulakulabe.
A mnoho byla trápena od mnohých lékařů, a vynaložila všecken statek svůj, a nic jí bylo neprospělo, ale vždy se hůře měla,
27 Atamva za Yesu, anabwera kumbuyo kwake mʼgulu la anthu ndipo anakhudza mkanjo wake,
Uslyšavši o Ježíšovi, přišla v zástupu po zadu, a dotkla se roucha jeho.
28 chifukwa anaganiza kuti, “Ngati nditangokhudza mkanjo wake, ndidzachiritsidwa.”
Nebo řekla byla: Dotknu-li se jen roucha jeho, uzdravena budu.
29 Nthawi yomweyo magazi ake analeka kutuluka ndipo anamva mʼthupi mwake kuti wamasulidwa ku vuto lake.
A hned přestal krvotok její, a pocítila na těle, že by uzdravena byla od neduhu svého.
30 Pomwepo Yesu anazindikira kuti mphamvu inachoka mʼthupi mwake. Anatembenuka mʼgulu la anthu ndipo anafunsa kuti, “Ndani wakhudza zovala zanga?”
A hned Ježíš poznav sám v sobě, že z něho moc vyšla, obrátiv se v zástupu, řekl: Kdo se dotekl roucha mého?
31 Ophunzira ake anayankha kuti, “Mukuona kuti anthu akukupanikizani, ndipo Inu mukufunsa kuti, ‘Ndani wandikhudza?’”
I řekli mu učedlníci jeho: Vidíš, že tě zástup tiskne, a pravíš: Kdo se mne dotekl?
32 Koma Yesu anapitirizabe kuyangʼana kuti aone amene anachita zimenezi.
I hleděl vůkol, aby ji uzřel, která to učinila.
33 Kenaka mayi uja pozindikira chimene chinamuchitikira, anabwera ndi kugwa pa mapazi ake, ndipo akunjenjemera ndi mantha, anamuwuza zoona zokhazokha.
Ta pak žena s bázní a s třesením, věduci, co se stalo při ní, přistoupila a padla před ním, a pověděla mu všecku pravdu.
34 Anati kwa iye, “Mwana wamkazi, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Pita mu mtendere ndipo khala womasulidwa ku mavuto ako.”
On pak řekl jí: Dcero, víra tvá tě uzdravila, jdiž u pokoji, a buď zproštěna od trápení svého.)
35 Pamene Yesu ankayankhulabe, amuna ena anafika kuchokera ku nyumba ya Yairo, mkulu wa sunagoge. Iwo anati, “Mwana wanu wamkazi wamwalira, muvutitsiranjinso aphunzitsiwa?”
A když on ještě mluvil, přišli z domu knížete školy, řkouce: Dcera tvá umřela, proč již zaměstknáváš Mistra?
36 Posasamala zomwe ananena, Yesu anamuwuza mkulu wa sunagoge uja kuti, “Usachite mantha; ingokhulupirira.”
Ježíš pak, hned jakž uslyšel to, což oni mluvili, řekl knížeti školy: Neboj se, toliko věř.
37 Iye sanalole munthu wina aliyense kuti amutsatire koma Petro, Yakobo ndi Yohane mʼbale wa Yakobo.
I nedal žádnému za sebou jíti, jediné Petrovi, Jakubovi a Janovi, bratru Jakubovu.
38 Atafika ku nyumba ya mkulu wa sunagoge, Yesu anaona chipiringu cha anthu akulira ndi kufuwula kwambiri.
I přišel do domu knížete školy, a viděl tam hluk, ano plačí a kvílí velmi.
39 Analowa nati kwa iwo, “Mukuchita phokoso ndi kulira chifukwa chiyani? Mwanayu sanamwalire koma ali mtulo.”
I všed tam, řekl jim: Co se bouříte a plačete? Neumřelať děvečka, ale spí.
40 Koma anamuseka Iye. Atawatulutsa onse panja, Iye anatenga abambo ndi amayi ake a mwanayo ndi ophunzira omwe anali naye, ndipo analowa mʼmene munali mwanayo.
I posmívali se jemu. On pak vyhnav všecky, pojal otce a matku děvečky, a ty, kteříž s ním byli, i všel tam, kdež děvečka ležela.
41 Anagwira dzanja lake nanena kwa iye, “Talita Kumi!” (Kutanthauza kuti, “Mtsikana, ndikunena ndi iwe, imirira!”)
A vzav ruku děvečky, řekl jí: Talitha kumi. Což se vykládá: Děvečko, (toběť pravím, ) vstaň.
42 Nthawi yomweyo anayimirira nayenda mozungulira (anali wa zaka khumi ndi ziwiri). Pa ichi onse anadabwa kwambiri.
A hned vstala děvečka, a chodila; nebo byla ve dvanácti letech. I zděsili se divením převelikým.
43 Anawalamulira kwambiri kuti asawuze wina aliyense za ichi, ndipo anawawuza kuti amupatse kanthu koti adye.
A přikázal jim pilně, aby žádný o tom nezvěděl. I rozkázal jí dáti jísti.

< Marko 5 >