< Malaki 3 >

1 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga amene adzakonza njira pamaso panga. Kenaka mwadzidzidzi Ambuye amene mukumufunafuna adzafika ku Nyumba yake. Mthenga wapangano amene mukumuyembekezera adzabwera.”
»Glejte, poslal bom svojega poslanca in pripravil bo pot pred menoj in Gospod, ki ga iščete, bo nenadoma prišel k svojemu templju, celo poslanec zaveze, v katerem se razveseljujete. Glejte, prišel bo, « govori Gospod nad bojevniki.
2 Koma ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Ndani adzatha kuyima pamene Iye wafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wa pa ngʼanjo, kapenanso ngati sopo wa munthu wochapa.
Toda kdo lahko prenese dan njegovega prihoda? In kdo bo obstal, ko se pojavi? Kajti podoben je prečiščevalčevemu ognju in podoben pralčevemu milu.
3 Iye adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri woyenga ndi woyeretsa siliva. Iye adzayeretsa Alevi ndi kuwayenga ngati golide ndi siliva. Pamenepo Yehova adzakhala ndi anthu amene azidzabweretsa zopereka mwachilungamo,
Sédel bo kakor prečiščevalec in čistilec srebra in očistil bo Lévijeve sinove in jih presejal kakor zlato in srebro, da bodo lahko Gospodu darovali daritev v pravičnosti.
4 ndipo Yehova adzalandira zopereka za Yuda ndi Yerusalemu, ngati masiku akale, masiku amakedzana.
Potem bo daritev Juda in Jeruzalema prijetna Gospodu, kakor v dneh iz davnine in kakor v prejšnjih letih.
5 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsono ndidzakuyandikirani kuti ndikuweruzeni. Mosataya nthawi ndidzanena mawu otsutsa mfiti, achigololo, a umboni wonama, amene salipira bwino antchito awo, amene amazunza akazi ndi ana amasiye, amene saweruza alendo mwachilungamo, komanso amene sandiopa Ine.”
In prišel bom bliže k vam, da sodim in bom hitra priča zoper čarodeje in zoper zakonolomce in zoper krivoprisežnike in zoper tiste, ki zatirajo najemnika pri njegovih plačilih, vdovo in osirotelega in ki odvračajo tujca pred njegovo pravico, mene pa se ne bojijo, « govori Gospod nad bojevniki.
6 “Ine ndine Yehova, ndipo sindisintha. Choncho inu zidzukulu za Yakobo, simunawonongedwe.
»Kajti jaz sem Gospod, jaz se ne spreminjam; zatorej vi, Jakobovi sinovi, niste uničeni.
7 Kuyambira nthawi ya makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga ndipo simunawatsatire. Bwererani kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Tibwerere motani kwa Yehova?’
Celo od dni svojih očetov ste odstopali od mojih odredb in se jih niste držali. Vrnite se k meni in jaz se bom vrnil k vam, « govori Gospod nad bojevniki. »Toda rekli ste: ›V čem se bomo vrnili?‹
8 “Kodi munthu angathe kuba za Mulungu? Komatu inu mumandibera. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi timakuberani motani?’ “Pa zakhumi ndi pa zopereka.
Ali bo človek oropal Boga? Vendar ste me oropali. Toda vi pravite: ›V čem smo te oropali?‹ V desetinah in daritvah.
9 Mtundu wanu wonse ndinu otembereredwa, chifukwa mukundibera.
Prekleti ste s prekletstvom, kajti oropali ste me, celó ves ta narod.
10 Bweretsani chakhumi chathunthu ku nyumba yosungira, kuti mukhale chakudya mʼnyumba mwanga.” Akutero Yehova Wamphamvuzonse, “Tandiyesani, ndipo muone ngati sindidzatsekula zipata zakumwamba, ndi kukugwetserani madalitso ochuluka amene mudzasowe malo owayikamo.
Prinesite vse desetine v skladišče, da bo lahko hrana v moji hiši in preizkusite me sedaj s tem, « govori Gospod nad bojevniki, »če vam ne bom odprl oken neba in vam izlil blagoslova, tako da ne bo dovolj prostora, da bi ga sprejeli.«
11 Ndidzaletsa tizirombo kuti tisawononge mbewu zanu, ndipo mpesa wa mʼminda mwanu zipatso zake sizidzayoyoka,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Zaradi vas bom oštel požiralca in ne bo uničil sadov vaše zemlje niti vaša trta na polju svojega sadu ne bo odvrgla pred časom, « govori Gospod nad bojevniki.
12 “Motero anthu amitundu yonse adzakutchulani odala, pakuti dziko lanu lidzakhala lokondweretsa,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
»In vsi narodi vas bodo klicali blagoslovljeni, kajti vi boste krasna dežela, « govori Gospod nad bojevniki.
13 Yehova akuti, “Mwayankhula mawu owawa onena za Ine. “Komabe inu mukufunsa kuti, ‘Kodi tanena chiyani chotsutsana nanu?’
»Vaše besede so bile arogantne zoper mene, « govori Gospod. »Vendar pravite: ›Kaj smo tako zelo govorili zoper tebe?‹
14 “Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse?
Rekli ste: ›Prazno je služiti Bogu in kakšna korist je to, da smo se držali njegove odredbe in da smo žalujoč hodili pred Gospodom nad bojevniki?
15 Koma tsono ife timati anthu odzikuza ndiye odalitsika. Kunena zoona anthu oyipa ndiye amapeza bwino, ngakhale amene amanyoza Mulungu amapulumuka.’”
In sedaj ponosnega imenujemo srečen. Da, tisti, ki počnejo zlobnost, so povzdignjeni; da, tisti, ki skušajo Boga, so celo osvobojeni.‹«
16 Ndipo woopa Yehova anayamba kukambirana, ndipo Yehova anamvetsera. Buku la chikumbutso linalembedwa pamaso pake, lonena za amene amaopa Yehova ndi kulemekeza dzina lake.
Potem so tisti, ki so se bali Gospoda, pogosto govorili drug drugemu. Gospod je prisluhnil in to slišal in knjiga spominov je bila napisana pred njim za tiste, ki so se bali Gospoda in tiste, ki mislijo na njegovo ime.
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu amenewo adzakhala anga, tsiku limene Ine ndidzachita izi, adzakhala angaanga. Ndidzawaleka osawalanga monga mmene munthu amachitira chifundo mwana wake amene amamutumikira.
»Oni bodo moji, « govori Gospod nad bojevniki, »na tisti dan, ko bom pripravil svoje dragocenosti; in jim prizanesel, kakor mož prizanese svojemu lastnemu sinu, ki mu služi.
18 Pamenepo mudzaonanso kusiyana pakati pa anthu olungama ndi oyipa, pakati pa amene amatumikira Mulungu ndi amene satumikira Mulungu.”
Potem se boste vrnili in razločevali med pravičnim in zlobnim, med tistim, ki služi Bogu in tistim, ki mu ne služi.«

< Malaki 3 >