< Malaki 3 >

1 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga amene adzakonza njira pamaso panga. Kenaka mwadzidzidzi Ambuye amene mukumufunafuna adzafika ku Nyumba yake. Mthenga wapangano amene mukumuyembekezera adzabwera.”
Lo! Y sende myn aungel, and he schal make redi weie bifor my face; and anoon the lordshipere, whom ye seken, schal come to his hooli temple, and the aungel of testament, whom ye wolen. Lo! he cometh, seith the Lord of oostis;
2 Koma ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Ndani adzatha kuyima pamene Iye wafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wa pa ngʼanjo, kapenanso ngati sopo wa munthu wochapa.
and who schal mowe thenke the dai of his comyng? and who schal stonde for to se hym? For he schal be as fier wellynge togidere, and as erbe of fulleris;
3 Iye adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri woyenga ndi woyeretsa siliva. Iye adzayeretsa Alevi ndi kuwayenga ngati golide ndi siliva. Pamenepo Yehova adzakhala ndi anthu amene azidzabweretsa zopereka mwachilungamo,
and he schal sitte wellynge togidere and clensynge siluer, and he schal purge the sones of Leuy; and he schal purge hem as gold and as siluer, and thei schulen be offrynge to the Lord sacrifices in riytfulnesse.
4 ndipo Yehova adzalandira zopereka za Yuda ndi Yerusalemu, ngati masiku akale, masiku amakedzana.
And the sacrifice of Juda and of Jerusalem schal plese to the Lord, as the daies of the world, and as olde yeeris.
5 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsono ndidzakuyandikirani kuti ndikuweruzeni. Mosataya nthawi ndidzanena mawu otsutsa mfiti, achigololo, a umboni wonama, amene salipira bwino antchito awo, amene amazunza akazi ndi ana amasiye, amene saweruza alendo mwachilungamo, komanso amene sandiopa Ine.”
And Y schal come to you in doom, and Y schal be a swift witnesse to mysdoeris, `ether enchaunteris of deuelis craft, and to auouteris, and forsworn men, and that falsli calengen the hire of the hirid man, and widewis, and fadirles, `ether modirles, children, and oppressen a pilgrym, `nether dredden me, seith the Lord of oostis.
6 “Ine ndine Yehova, ndipo sindisintha. Choncho inu zidzukulu za Yakobo, simunawonongedwe.
Forsothe Y am the Lord, and am not chaungid; and ye sones of Jacob ben not wastid.
7 Kuyambira nthawi ya makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga ndipo simunawatsatire. Bwererani kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Tibwerere motani kwa Yehova?’
Forsothe fro daies of youre fadris ye wenten awei fro my lawful thingis, and kepten not; turne ye ayen to me, and Y schal ayen turne to you, seith the Lord of oostis. And ye seiden, In what thing schulen we turne ayen?
8 “Kodi munthu angathe kuba za Mulungu? Komatu inu mumandibera. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi timakuberani motani?’ “Pa zakhumi ndi pa zopereka.
If a man schal turmente God, for ye `togidere fitchen me. And ye seiden, In what thing `togidere fitchen we thee? In tithis and in `firste fruitis;
9 Mtundu wanu wonse ndinu otembereredwa, chifukwa mukundibera.
and ye ben cursid in nedynesse, and alle ye folc disseyuen me, and `togidere fitchen.
10 Bweretsani chakhumi chathunthu ku nyumba yosungira, kuti mukhale chakudya mʼnyumba mwanga.” Akutero Yehova Wamphamvuzonse, “Tandiyesani, ndipo muone ngati sindidzatsekula zipata zakumwamba, ndi kukugwetserani madalitso ochuluka amene mudzasowe malo owayikamo.
Brynge ye yn ech tithe in to my berne, that mete be in myn hous, and preue ye me on this thing, seith the Lord, if Y schal not opene to you the goteris of heuene, and schal schede out to you blessyng, til to aboundaunce.
11 Ndidzaletsa tizirombo kuti tisawononge mbewu zanu, ndipo mpesa wa mʼminda mwanu zipatso zake sizidzayoyoka,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
And Y schal blame for you that that deuourith, and he schal not distrie the fruit of youre lond; nether bareyn vyneyerd schal be in the feeld,
12 “Motero anthu amitundu yonse adzakutchulani odala, pakuti dziko lanu lidzakhala lokondweretsa,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
seith the Lord of oostis, and alle folkis schulen seie you blessid; for ye schulen be a desirable lond, seith the Lord of oostis.
13 Yehova akuti, “Mwayankhula mawu owawa onena za Ine. “Komabe inu mukufunsa kuti, ‘Kodi tanena chiyani chotsutsana nanu?’
Youre wordis wexiden strong on me, seith the Lord; and ye seiden, What han we spokun ayens thee?
14 “Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse?
And ye seiden, He is veyn, that serueth God; and what wynnyng for we kepten hise heestis, and for we wenten sorewful bifore the Lord of oostis?
15 Koma tsono ife timati anthu odzikuza ndiye odalitsika. Kunena zoona anthu oyipa ndiye amapeza bwino, ngakhale amene amanyoza Mulungu amapulumuka.’”
Therfor now we seien proude men blessid; for thei ben bildid doynge vnpitee, and thei temptiden God, and ben maad saaf.
16 Ndipo woopa Yehova anayamba kukambirana, ndipo Yehova anamvetsera. Buku la chikumbutso linalembedwa pamaso pake, lonena za amene amaopa Yehova ndi kulemekeza dzina lake.
Thanne men dredynge God spaken, ech with his neiybore; and the Lord perseyuede, and herde, and a book of mynde is writun bifor hym to `men dredynge God, and thenkynge his name.
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu amenewo adzakhala anga, tsiku limene Ine ndidzachita izi, adzakhala angaanga. Ndidzawaleka osawalanga monga mmene munthu amachitira chifundo mwana wake amene amamutumikira.
And thei schulen be to me, seith the Lord of oostis, in the dai in which Y schal make, in to a special tresour; and Y schal spare hem, as a man sparith his sone seruynge to hym.
18 Pamenepo mudzaonanso kusiyana pakati pa anthu olungama ndi oyipa, pakati pa amene amatumikira Mulungu ndi amene satumikira Mulungu.”
And ye schulen be conuertid, and ye schulen se, what is bitwixe the iust man and vnpitouse, bitwixe `the seruynge to the Lord and `not seruynge to hym.

< Malaki 3 >