< Malaki 1 >

1 Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
Breme Gospodove besede Izraelu, po Malahiju.
2 Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
»Ljubil sem vas, « govori Gospod. Vendar pravite: »V čem si nas ljubil?« » Mar ni bil Ezav Jakobov brat?« govori Gospod, »vendar sem ljubil Jakoba,
3 koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
Ezava pa sovražil ter opustošil njegove gore in njegovo dediščino za zmaje divjine.«
4 Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
Kakor govori Edóm: »Obubožani smo, toda vrnili se bomo in pozidali zapuščene kraje, « tako govori Gospod nad bojevniki: »Gradili bodo, toda jaz bom rušil. Imenovali jih bodo: ›Meja zlobnosti‹ in ›Ljudstvo, zoper katero ima Gospod ogorčenje na veke.‹«
5 Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
Vaše oči bodo videle in rekli boste: » Gospod bo poveličan prek Izraelove meje.«
6 “Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
»Sin časti svojega očeta in služabnik svojega gospodarja. Če sem jaz potem oče, kje je moja čast? In če sem jaz gospodar, kje je moj strah?« govori Gospod nad bojevniki, »vam, oh duhovniki, ki prezirate moje ime. Vi pa pravite: ›V čem smo prezirali tvoje ime?‹
7 “Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
Na mojem oltarju ste darovali oskrunjen kruh, vi pa pravite: ›V čem smo te oskrunili?‹ V tem, da pravite: › Gospodova miza je zaničevanja vredna.‹
8 Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
In če darujete slepo za žrtev, mar ni to zlo? In če darujete hromo in bolno, mar ni to zlo? Daruj to sedaj svojemu voditelju; ali bo zadovoljen s teboj, ali sprejme tvojo osebo?« govori Gospod nad bojevniki.
9 “Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
»In sedaj vas prosim, rotite Boga, da nam bo milostljiv. To je bilo z vašimi sredstvi. Mar bo cenil vaše osebe?« govori Gospod nad bojevniki.
10 “Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
»Kdo je tam, celo med vami, da bi zaman zaprl vrata? Niti na mojem oltarju ognja ne netite zaman. Nobenega zadovoljstva nimam z vami, « govori Gospod nad bojevniki, »niti ne bom sprejel daritve iz vaše roke.
11 Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Kajti od sončnega vzhoda, celo do zahajanja istega bo moje ime veliko med pogani in na vsakem kraju bo mojemu imenu darovano kadilo in čista daritev, kajti moje ime bo veliko med pogani, « govori Gospod nad bojevniki.
12 “Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
»Toda vi ste to oskrunili v tem, ko pravite: › Gospodova miza je oskrunjena; in njen sad, celó njegova jed, je zaničevanja vredna.‹
13 Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
Pravite tudi: ›Glej, kakšna težava je to!‹ In vi ste nad tem vihali nos, « govori Gospod nad bojevniki, »in privedli to, kar je bilo raztrgano in hromo in bolno. Tako daritev ste privedli. Mar naj bi to sprejel iz vaše roke?« govori Gospod.
14 “Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”
Toda preklet bodi slepar, ki ima v svojem tropu samca, pa prisega in žrtvuje Gospodu pokvarjeno stvar, kajti jaz sem velik Kralj, « govori Gospod nad bojevniki, »in moje ime je grozno med pogani.«

< Malaki 1 >