< Malaki 1 >

1 Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
Brzemię słowa PANA do Izraela przez Malachiasza.
2 Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
Umiłowałem was, mówi PAN, a [wy] mówicie: W czym nas umiłowałeś? Czy Ezaw nie [był] bratem Jakuba? – mówi PAN, a jednak umiłowałem Jakuba;
3 koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
A Ezawa znienawidziłem i wydałem jego góry [na] spustoszenie, a jego dziedzictwo – smokom na pustkowiu.
4 Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
Choćby Edom powiedział: Staliśmy się ubodzy, ale wrócimy i odbudujemy spustoszone [miejsca], to tak mówi PAN zastępów: Niech oni budują, a ja zburzę; i nazwą ich granicą bezbożności oraz ludem, na który PAN zapałał gniewem aż na wieki.
5 Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
Wasze oczy spojrzą i powiecie: PAN będzie uwielbiony w granicach Izraela.
6 “Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
Syn czci ojca, a sługa swego pana. Jeśli więc jestem ojcem, gdzie jest moja cześć? Jeśli jestem panem, gdzie [jest] bojaźń przede mną? – mówi PAN zastępów do was, kapłani, którzy lekceważycie moje imię. Wy jednak mówicie: W czym lekceważymy twoje imię?
7 “Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
Przynosicie na mój ołtarz pokarm nieczysty i mówicie: Czym cię zanieczyściliśmy? [Tym], że mówicie: Stołem PANA [można] wzgardzić.
8 Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Gdy bowiem przyprowadzacie na ofiarę to, co jest ślepe, [czyż] nie jest [to] zła rzecz? I gdy przyprowadzacie kulawe i chore, [czy to] nie [jest] zła rzecz? Ofiaruj to twemu namiestnikowi, zobaczysz, czy będzie mu się podobać. Czy przyjmie twoją osobę? – mówi PAN zastępów.
9 “Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Dlatego teraz, proszę, przebłagajcie Boga, aby się zlitował nad nami. To się dzieje z waszych rąk, czy więc przyjmie waszą osobę? – mówi PAN zastępów.
10 “Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
Kto spośród was za darmo zamknąłby drzwi albo zapaliłby ogień na moim ołtarzu? Nie mam w was upodobania, mówi PAN zastępów, i nie przyjmę ofiary z waszej ręki.
11 Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Od wschodu słońca bowiem aż do jego zachodu moje imię [będzie] wielkie wśród pogan; na każdym miejscu będą składane mojemu imieniu kadzidło i ofiara czysta. Moje imię bowiem będzie wielkie wśród narodów, mówi PAN zastępów.
12 “Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
Lecz wy bezcześcicie je, [gdy] mówicie: Stół PANA [jest] nieczysty; a to, co kładziecie na nim, jest wzgardzonym pokarmem.
13 Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
Mówicie też: [Jakiż to] wysiłek! I parskacie na to, co mówi PAN zastępów, i przynosicie to, co jest rozszarpane, kulawe i chore, takie ofiary przynosicie. Czy [mam] to przyjąć z waszej ręki? – mówi PAN.
14 “Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”
[Niech] będzie przeklęty oszust, który mając w swej trzodzie samca, ślubuje, a składa Panu w ofierze to, co jest ułomne. Jestem bowiem wielkim Królem, mówi PAN zastępów, a moje imię jest straszne między narodami.

< Malaki 1 >