< Luka 9 >

1 Yesu atawayitana khumi ndi awiriwo pamodzi, Iye anawapatsa mphamvu ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda zonse ndi kuchiritsa matenda.
Then called he the. xii. to gether and gave them power and auctorite over all devyls and that they myght heale diseases.
2 Ndipo Iye anawatumiza kukalalikira za ufumu wa Mulungu ndi kukachiritsa odwala.
And he sent them to preache the kyngdome of God and to cure the sick.
3 Iye anawawuza kuti, “Musatenge kanthu paulendo. Musatenge ndodo, thumba, buledi, ndalama, ndi malaya apadera.
And he sayd to them: Take nothinge to sucker you by ye waye: nether staffe nor scripe nether breed nether money nether have twoo cootes.
4 Nyumba iliyonse imene mulowa, mukhale momwemo kufikira mutachoka mu mzindawo.
And whatsoever housse ye enter into there abyde and thence departe.
5 Ngati anthu sakulandirani, sasani fumbi la kumapazi anu pomwe mukuchoka mu mzinda wawo ngati umboni owatsutsa.”
And whosoever will not receave you when ye go out of that cite shake of the very dust from youre fete for a testimony agaynst them.
6 Ndipo iwo ananyamuka napita, mudzi ndi mudzi, kulalikira Uthenga Wabwino ndi kuchiritsa anthu paliponse.
And they went out and went thorow the tounes preachinge the gospell and healynge every wheare.
7 Tsopano Herode olamulirayo anamva zonse zimachitikazi. Ndipo iye anavutika kwambiri chifukwa ena amati Yohane waukitsidwa kwa akufa,
And Herod the tetrarch herde of all that was done of him and douted because that it was sayde of some that Iohn was rysen agayne from deeth:
8 ena amati Eliya waonekera, ndipo ena anatinso mmodzi wa aneneri akalekale waukanso.
and of some that Helyas had apered: and of other that one of the olde prophetes was rysen agayne.
9 Koma Herode anati, “Ine ndinamudula mutu Yohane. Nanga uyu ndani amene ndikumva zinthu zotere za Iye?” Ndipo iye anayesetsa kuti amuone Iye.
And Herod sayde: Iohn have I behedded: who then is this of whom I heare suche thinges? And he desyred to se him.
10 Atumwi atabwerera, anamuwuza Yesu zimene anachita. Kenaka Iye anawatenga napita kwa okha ku mudzi wa Betisaida.
And the Apostles retourned and tolde him what great thinges they had done. And he toke them and went a syde into a solitary place nye to a citie called Bethsaida.
11 Koma gulu la anthu linadziwa ndipo anamutsatira. Iye anawalandira ndi kuyankhula nawo za ufumu wa Mulungu, ndi kuchiritsa amene amafuna machiritso.
And ye people knewe of it and folowed him. And he receaved them and spake vnto them of the kyngdome of God and healed them that had nede to be healed.
12 Chakumadzulo dzuwa litapita, khumi ndi awiriwo anabwera kwa Iye ndipo anati, “Uzani gulu la anthuli lichoke kuti apite ku midzi yotizungulira ndi madera a ku mudzi kuti akapeze chakudya ndi pogona, chifukwa kuno ndi kuthengo.”
And when ye daye beganne to weare awaye then came the twelve and sayde vnto him: sende ye people awaye that they maye goo into the tounes and villages roundabout and lodge and get meate for we are here in a place of wyldernes.
13 Iye anayankha kuti, “Apatseni chakudya kuti adye.” Iwo anayankha kuti, “Ife tili ndi malofu a buledi asanu okha ndi nsomba ziwiri, pokhapokha titapita kukagula chakudya cha gulu la anthu onsewa.”
But he sayde vnto them: Geve ye the to eate. And they sayde. We have no moo but fyve loves and two fisshes except we shuld goo and bye meate for all this people.
14 (Pamenepo panali amuna pafupifupi 5,000). Koma Iye anati kwa ophunzira ake, “Akhazikeni pansi mʼmagulu a anthu pafupifupi makumi asanu.”
And they were about a fyve thousand men. And he sayde to his disciples: Cause them to syt doune by fyfties in a company.
15 Ophunzira ake anachita zomwezo ndipo aliyense anakhala pansi.
And they dyd soo and made them all syt doune.
16 Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri zija anayangʼana kumwamba, nayamika ndipo anazigawa. Kenaka anazipereka kwa ophunzira ake kuti azipereke kwa anthu.
And he toke the fyve loves and the two fisshes and loked vp to heven and blessed them and brake and gave to the disciples to set before ye people.
17 Onse anadya nakhuta, ndipo ophunzira ake anatolera madengu khumi ndi awiri odzaza ndi nyenyeswa zomwe zinatsala.
And they ate and were all satisfied. And ther was taken vp of that remayned to the twelve baskettes full of broken meate.
18 Nthawi ina pamene Yesu amapemphera malo a yekha ali ndi ophunzira ake, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati Ine ndine yani?”
And it fortuned as he was alone prayinge his disciples were wt him and he axed the sayinge: Who saye ye people yt I am?
19 Iwo anayankha kuti, “Ena amati Yohane Mʼbatizi; ena amati Eliya; ndipo enanso amati mmodzi wa aneneri akalekale waukanso.”
They answered and sayd: Iohn Baptist. Some saye Helyas. And some saye one of the olde prophetes is rysen agayne.
20 Iye anafunsa kuti, “Koma nanga inu mumati Ine ndine yani?” Petro anayankha kuti, “Mpulumutsi wolonjezedwa uja wa Mulungu.”
He sayde vnto the: Who saye ye that I am? Peter answered and sayde: thou arte the Christ of god.
21 Yesu anawachenjeza kwambiri kuti asawuze wina aliyense za izi.
And he warned and commaunded them that they shuld tell no man yt thinge
22 Ndipo Iye anati, “Mwana wa Munthu ayenera kuzunzika kwambiri ndi kukanidwa ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, Iye ayenera kuphedwa ndipo tsiku lachitatu adzauka kwa akufa.”
sayinge: that the sonne of man must suffre many thinges and be reproved of the elders and of the hye prestes and scribes and be slayne and the thirde daye ryse agayne.
23 Ndipo Iye anawuza onse kuti, “Ngati wina aliyense akufuna kutsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kusenza mtanda wake tsiku ndi tsiku nʼkumanditsata Ine.
And he sayde to them all yf eny man will come after me let him denye him sylfe and take vp his crosse dayly and folowe me.
24 Popeza aliyense amene akufuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene adzataya moyo wake chifukwa cha Ine adzawupulumutsa.
Whosoever will save his lyfe shall lose it. And who soever shall lose his lyfe for my sake the same shall save it.
25 Kodi chabwino ndi chiti kwa munthu, kupata zonse zapansi pano, koma ndi kutaya moyo wake kapena kudziwononga iye mwini?
For what avauntageth it a man to wynne the whole worlde yf he loose him sylfe or runne in domage of him sylfe?
26 Ngati wina aliyense achita nane manyazi ndi ndiponso mawu anga, Mwana wa Munthu adzachita naye manyazi pamene adzabwera mu ulemerero wake ndi mu ulemerero wa Atate ndi angelo oyera.
For whosoever is ashamed of me and of my sayinges: of him shall the sonne of man be ashamed when he cometh in his awne glorie and in the glorie of his father and of the holy angels.
27 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti ena mwa inu amene mwayima pano simudzalawa imfa musanaone ufumu wa Mulungu.”
And I tell you of a surety: There be some of the yt stonde here which shall not tast of deeth tyll they se ye kyngdome of god.
28 Patatha pafupifupi masiku asanu ndi atatu Yesu atanena izi, Iye anatenga Petro, Yohane ndi Yakobo ndi kukwera ku phiri kukapemphera.
And it folowed about an. viii. dayes after thoose sayinges that he toke Peter Iames and Iohn and went vp into a moutayne to praye.
29 Pamene Iye ankapemphera, maonekedwe a nkhope yake, ndi zovala zake zinawala monyezimira kwambiri.
And as he prayed ye facion of his countenaunce was changed and his garment was whyte and shoone.
30 Anthu awiri, Mose ndi Eliya,
And beholde two men talked wt him and they were Moses and Helyas
31 anaonekera mu ulemerero opambana akuyankhulana ndi Yesu. Iwo amayankhulana za kuchoka kwake, kumene Iye anali pafupi kukakwaniritsa ku Yerusalemu.
which appered gloriously and spake of his departinge which he shuld ende at Ierusalem.
32 Petro ndi anzake anali ndi tulo tambiri, koma atadzuka, iwo anaona ulemerero wake ndi anthu awiri atayima pamodzi ndi Iye.
Peter and they that were with him were hevy with slepe. And when they woke they sawe his glorie and two men stondinge with him.
33 Pamene anthuwo ankamusiya Yesu, Petro anati kwa Iye, “Ambuye, ndi chabwino kwa ife kuti tikhale pano. Tiloleni kuti timange misasa itatu, umodzi wanu, umodzi wa Mose ndi umodzi wa Eliya.” (Iye sanadziwe chimene amayankhula).
And it chaunsed as they departed fro him Peter sayde vnto Iesus: Master it is good beinge here for vs. Let vs make thre tabernacles one for the and one for Moses and one for Helyas: and wist not what he sayde.
34 Pamene Iye ankayankhula, mtambo unaonekera ndi kuwaphimba iwo, ndipo anachita mantha pamene mtambowo unawakuta.
Whyll he thus spake ther came a cloude and shadowed them: and they feared when they were come vnder the cloude.
35 Mawu anachokera mu mtambomo nati, “Uyu ndi Mwana wanga amene ndamusankha; mumvereni Iye.”
And ther came a voyce out of the cloude sayinge: This is my deare sonne heare him.
36 Atamveka mawuwa, anaona kuti Yesu anali yekha. Ophunzirawo anazisunga izi mwa iwo okha ndipo sanawuze wina aliyense pa nthawiyi za zomwe iwo anaziona.
And assone as ye voyce was past Iesus was founde alone. And they kept it cloose and tolde noo man in thoose dayes eny of those thinges which they had sene.
37 Mmawa mwake, akutsika ku phiri, anthu ambiri anakumana naye.
And it chaunsed on the nexte daye as they came doune from the hyll moche people met him.
38 Munthu wina mʼgulu la anthulo anayitana kuti, “Aphunzitsi, ndikupemphani kuti muone mwana wangayu, pakuti ndi mmodzi yekhayu.
And beholde a man of the copany cryed out sayinge: Master I beseche ye beholde my sonne for he is all that I have:
39 Chiwanda chikamugwira amafuwula mwadzidzidzi; chimamugwedeza kolimba mpaka kutuluka thovu kukamwa. Sichimusiya ndipo chikumuwononga.
and se a sprete taketh him and sodenly he cryeth and he teareth him that he fometh agayne and with moche payne departeth fro him when he hath rent him and
40 Ine ndinapempha ophunzira anu kuti achitulutse, koma alephera.”
I besought thy disciples to cast him out and they coulde not.
41 Yesu anayankha kuti, “Haa! Anthu osakhulupirira ndi mʼbado wokhota. Kodi Ine ndidzakhala nanu nthawi yayitali yotani ndi kukupirirani? Bweretsa mwana wako kuno.”
Iesus answered and sayde: O generacion with oute fayth and croked: how longe shall I be with you? and shall suffre you? Bringe thy sonne hidder.
42 Ngakhale pamene mnyamata amabwera kwa Yesu, chiwandacho chinamugwetsa pansi ndi kumugwedeza. Koma Yesu anadzudzula mzimu woyipawo nachiritsa mwa mnyamatayo ndi kumuperekanso kwa abambo ake.
As he yet was a cominge the fende ret him and tare him. And Iesus rebuked ye vnclene sprete and healed the childe and delivered him to his father.
43 Ndipo iwo onse anadabwa ndi ukulu wa Mulungu. Aliyense akudabwa ndi zimene Yesu anachita, Iyeyo anati kwa ophunzira ake,
And they were all amased at ye mighty power of God. Whyll they wondred every one at all thinges which he dyd he sayd vnto his disciples:
44 “Tamvetsetsani zimene ndikufuna kukuwuzani: Mwana wa Munthu akupita kukaperekedwa mʼmanja mwa anthu.”
Let these sayinges synke doune into youre eares. The tyme will come when the sonne of man shalbe delivered into the hondes of men.
45 Koma iwo sanazindikire zimene amatanthauza. Izi zinawadabwitsa kotero sanathe kuzimvetsa ndipo anaopa kumufunsa.
But they wist not what yt worde meant and yt was hyd fro the that they vnderstode yt not. And they feared to axe him of that sayinge.
46 Mkangano unayambika pakati pa ophunzira wa kuti wamkulu koposa akanakhala ndani mwa iwo.
Then ther arose a disputacion amoge the: who shuld be the greatest.
47 Yesu podziwa maganizo awo, anatenga kamwana nakayimika pambali pake.
When Iesus perceaved ye thoughtes of their hertes he toke a chylde and set him hard by him
48 Ndipo Iye anawawuza kuti, “Aliyense wolandira bwino kamwana aka mʼdzina langa, ndiye kuti akulandiranso bwino Ine; ndipo aliyense wolandira bwino Ine, ndiye kuti akulandiranso bwino amene anandituma Ine. Pakuti amene ndi wamngʼono pakati panu, ndiye amene ali wamkulu koposa.”
and sayd vnto the: Whosoever receaveth this chylde in my name receaveth me. And whosoever receaveth me receaveth him yt sent me. For he yt is least amonge you all the same shalbe greate.
49 Yohane anati, “Ambuye, ife tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo tinayesa kumuletsa, chifukwa iyeyo si mmodzi wa ife.”
And Iohn answered and sayde: Master we sawe one castinge out devyls in thy name and we forbade him because he foloweth not with vs.
50 Yesu anati, “Wosamuletsa, pakuti amene satsutsana nanu ali mbali yanu.”
And Iesus sayde vnto him: forbyd ye him not. For he that is not agaynst vs is wt vs.
51 Nthawi itayandikira yoti Iye atengedwe kupita kumwamba, Yesu anatsimikiza zopita ku Yerusalemu,
And it folowed when the tyme was come yt he shulde be receaved vp then he set his face to goo to Hierusalem
52 ndipo anatuma nthumwi kuti zitsogole. Iwo anapita mʼmudzi wa Asamariya kuti akonzekere kumulandira,
and sent messengers before him. And they went and entred into a citie of the Samaritans to make redy for him.
53 koma anthu kumeneko sanamulandire chifukwa Iye ankapita ku Yerusalemu.
But they wolde not receave him be cause his face was as though he wolde goo to Ierusalem.
54 Ophunzira awa, Yohane ndi Yakobo ataona zimenezi, anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukufuna ife tiyitane moto kuchokera kumwamba kuti uwawononge?”
When his disciples Iames and Iohn sawe yt they sayde: Lorde wilt thou that we comaunde that fyre come doune from heven and consume them even as Helias dyd?
55 Koma Yesu anatembenuka ndi kuwadzudzula,
Iesus turned about and rebuked them sayinge: ye wote not what maner sprete ye are of.
56 ndipo iwo anapita ku mudzi wina.
The sonne of ma ys not come to destroye mennes lives but to save them. And they went to another toune.
57 Pamene iwo ankayenda mu msewu, munthu wina anati kwa Iye, “Inu ndikutsatirani kulikonse kumene mudzapita.”
And it chaunsed as he went in the waye a certayne man sayd vnto him: I will folowe the whither soever thou goo.
58 Yesu anayankha kuti, “Nkhandwe zili ndi mapanga ake, mbalame zili ndi zisa zake, koma Mwana wa Munthu alibe malo wogonekapo mutu wake.”
Iesus sayd vnto him: foxes have holes and bryddes of ye ayer have nestes: but the sonne of man hath not where on to laye his heed.
59 Iye anati kwa wina, “Nditsate Ine.” Koma munthuyo anayankha kuti, “Ambuye, choyamba loleni ndipite kuti ndikayike maliro a abambo anga.”
And he sayde vnto another: folowe me. And the same sayde: Lorde suffre me fyrst to goo and bury my father.
60 Yesu anati kwa iye, “Aleke akufa ayikane akufa okhaokha, koma iwe pita ukalalikire ufumu wa Mulungu.”
Iesus sayd vnto him: Let the deed bury their deed: but goo thou and preache the kyngdome of God.
61 Koma winanso anati, “Ine ndidzakutsatani Ambuye; koma choyamba ndiloleni ndibwerere kuti ndikatsanzikane nalo banja langa.”
And another sayde: I wyll folowe the Lorde: but let me fyrst goo byd them fare well which are at home at my housse.
62 Yesu anayankha kuti, “Munthu amene akulima ndi khasu lokokedwa nʼkumayangʼana mʼmbuyo, si woyenera kugwira ntchito mu ufumu wa Mulungu.”
Iesus sayde vnto him: No man that putteth his honde to the plowe and loketh backe is apte to the kyngdome of God.

< Luka 9 >