< Luka 8 >

1 Zitatha izi, Yesu anayendayenda kuchoka mzinda wina kupita wina ndiponso mudzi wina kupita wina, akulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu. Ophunzira ake khumi ndi awiri aja anali naye,
Hessafe guye, Yesuusi Xoossaa kawotethaa Wonggelaa sabbakishe katamaaranne gutaara aadhdhis. He wode tammanne nam77u hawaareti iyara de7oosona.
2 komanso akazi ena amene anachiritsidwa ku mizimu yoyipa ndi matenda: Mariya, wotchedwa Magadalena, amene mwa iye munatuluka ziwanda zisanu ndi ziwiri;
Qassi tuna ayyaanaappenne dumma dumma harggiyafe paxida issi issi maccasati iyara de7oosona. Enttika, laappun tuna ayyaanati keyida Magdela Mayraamo,
3 Yohana mkazi wa Kuza, woyangʼanira mʼnyumba ya Herode; Suzana; ndi ena ambiri analinso. Akazi awa ankawathandiza ndi chuma chawo.
Heroodisa shuumaa Kuuza machchiw Yohaanna, Soosinnaranne qassi hara daroti enttana miishen maaddeyssati de7oosona.
4 Anthu ambiri ankasonkhana, ndipo pamene anthu ankabwera kwa Yesu kuchokera ku midzi, Iye anawawuza fanizo ili,
Daro asay dumma dumma katamaappe iyaakko shiiqin leemison enttaw odis.
5 “Mlimi anapita kukafesa mbewu zake. Akufesa mbewuzo, zina zinagwa mʼmbali mwa njira; zinapondedwa, ndipo mbalame zamlengalenga zinadya.
“Issi goshshanchchoy zerethi zeranaw keyis. I zerishin issi issi zerethay oge gaxan wodhdhidi yedhdhettis, salo kafoti maxidosona.
6 Zina zinagwa pa thanthwe, ndipo pamene zinamera, zinafota chifukwa panalibe chinyezi.
Harati shaalloy garssan de7iya biitta bolla wodhdhidosona. Buroo dolida mela biittan laahoy baynna gisho miccidosona.
7 Mbewu zina zinagwera pakati pa minga, zinakulira pamodzi ndi mingazo ndipo zinalepheretsa mmerawo kukula.
Hara zerethay qassi aguntha giddon wodhdhis. Agunthaara wolla diccida gisho agunthay cuullidi bessan ashshis.
8 Mbewu zina zinagwera pa nthaka yabwino. Zinamera ndipo zinabala mowirikiza 100 kuposa zimene zinafesedwa zija.” Atanena izi, anafuwula kuti, “Amene ali ndi makutu, amve.”
Harati lo77o biitta bolla wodhdhidosona. Dolida wode xeetu kushe ayfidosona.” Hessa odi onggidi, ba qaala dhoqqu oothidi, “Si7iya haythi de7iya ubbay si7o” yaagis.
9 Ophunzira ake anamufunsa tanthauzo lake la fanizolo.
Iya tamaareti, “Ha leemisuwa birshshethay aybee?” yaagidi oychchidosona
10 Iye anati, “Kudziwa zinsinsi za ufumu wa Mulungu kwapatsidwa kwa inu, koma kwa ena ndimawayankhula mʼmafanizo kuti, “ngakhale akuona, asapenye; ngakhale akumva, asazindikire.”
I, “Xoossaa kawotethaa xuuraa erana mela hinttew imettis. Shin harati be7ishe demmonna mela, si7ishe akeekonna mela leemison odays.
11 “Tanthauzo la fanizoli ndi ili: Mbewu ndi mawu a Mulungu.
“Hiza, ha leemisuwa birshshethay hayssa: zerethi yaagettiday Xoossaa qaala.
12 Mbewu za mʼmbali mwa njira ndi anthu amene amamva mawu, ndipo kenaka mdierekezi amabwera ndi kuchotsa mawuwo mʼmitima mwawo kuti asakhulupirire ndi kupulumutsidwa.
Oge gaxan wodhdhida zerethay qaala si7eyssata. Gidoshin, entti ammanidi attonna mela Xalahey qaala entta wozanaappe maxi digees.
13 Mbewu za pa thanthwe ndi anthu amene amalandira mawu mwachimwemwe pamene akumva, koma mawuwo sazika mizu. Iwo amakhulupirira kwa kanthawi, koma pa nthawi ya mayesero, amagwa.
Shaalloy garssan de7iya biitta bolla wodhdhida zerethay qaala si7idi ufayssan ekkeyssata. Entti ha77is ammanoosonappe attin xaphoy baynna gisho paacey gakkiya wode ellesidi kaddoosona.
14 Mbewu zimene zinagwa pakati pa minga zikuyimira anthu amene amamva mawu, koma akamayenda mʼnjira zawo amatsamwitsidwa ndi zodandaulitsa za moyo uno, chuma ndi zosangalatsa, ndipo iwo samakhwima.
Aguntha giddon zerettidayssati qaala si7eyssata. Enttika alamiya qofan, duretethaaninne sa7aa duussaa miikkotethan cuulettidi besseyssada ayfibookkona.
15 Koma mbewu za pa nthaka yabwino zikuyimira anthu amene ali ndi mtima woona ndi wabwino, amene amamva mawu nawasunga, ndipo amalimbikira mpaka amabala zipatso.
Lo77o biittan wodhdhida zerethay lo77o wozanan qaala si7idi naageyssatanne dandda7an minnidi ayfe ayfeyssata.
16 “Palibe amayatsa nyale ndi kuyibisa mu mtsuko kapena kuyika pansi pa bedi. Koma mʼmalo mwake, amayika pa choyikapo chake, kuti anthu olowamo aone kuwala.
“Xomppe xomppidi, daachcho kammey woykko arssafe garssan wothey deenna. Geliya asi be7ana mela dhoqqa bessan wothees.
17 Pakuti palibe kanthu kobisika kamene sikadzawululika, ndipo palibe kanthu kophimbika kamene sikadzadziwika kapena kuonetsedwa poyera.
“Hessa gisho, qoncce keyonna qosettidi attiyaabay, erettonna geemmidi attiyaabay deenna.
18 Choncho ganizirani mozama. Iye amene ali nazo adzapatsidwa zambiri, iye amene alibe, ngakhale chimene akuganiza kuti ali nacho adzalandidwa.”
“Hiza, hintte qaala waati si7iyakko akeekite. De7iya ubbaas guzhetidi imettana, baynnayssas hari attoshin iyaw de7iya guuthiyaka iyappe ekettana” yaagis.
19 Tsopano amayi ndi abale a Yesu anabwera kudzamuona Iye, koma analephera kuti afike pafupi ndi Iye chifukwa cha gulu la anthu.
Yesuusa aayeranne ishatara iyaakko yidosona. Shin asaa darotethaafe denddoyssan iya demmanaw dandda7ibookkona.
20 Wina anamuwuza Iye kuti, “Amayi ndi abale anu ayima kunja, akufuna kukuonani.”
Issi asi Yesuusakko, “Ne aayeranne ne ishatara nena koyidi karen naagoosona” yaagis.
21 Yesu anayankha kuti, “Amayi ndi abale anga ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kumachita zimene mawuwo akunena.”
Yesuusi zaaridi, “Xoossaa qaala si7idi qaala ooson peeshsheyssati ubbay taw aayonne taw isha” yaagis.
22 Tsiku lina Yesu anati kwa ophunzira ake, “Tiyeni tiwolokere tsidya lina la nyanja.” Ndipo analowa mʼbwato nanyamuka.
Issi gallas Yesuusaranne iya tamaaretara issife wogolon gelidi, “Abbaa pinnoos” yaagis. Enttika baanaw denddidosona.
23 Akuwoloka, Iye anagona tulo. Namondwe wamkulu anayamba pa nyanja, ndipo bwatolo linayamba kudzaza ndi madzi ndipo anali pa chiopsezo chachikulu.
Abbaa bollara entti pinnanaw bishin Yesuusi dhiskkis. Qopponna mino carkkoy abbaa bolla denddis. Haathay wogoluwan gelin wogoloy mitetethi oykkiya wode ubbay babbidosona.
24 Ophunzira anapita ndi kukamudzutsa Iye, nati, “Ambuye, Ambuye, ife tikumira!” Anadzuka ndipo anadzudzula mphepo ndi madzi owindukawo. Namondwe anasiya, ndipo panali bata.
Iya tamaareti iyaakko shiiqidi, “Nu Godaw, nu Godaw, nu dhayos yaagidi” Yesuusa denthidosona. Yesuusi denddidi carkkuwanne gotiya seeris. Ellesidi carkkoynne gotey woppu gis. Sarotethayka simmis.
25 Iye anafunsa ophunzira ake kuti, “Chikhulupiriro chanu chili kuti?” Koma pogwidwa ndi mantha ndi kudabwa anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Uyu ndi ndani? Iye alamulira ngakhale mphepo ndi madzi, ndipo zimumvera Iye.”
Yesuusi ba tamaaretakko, “Hintte ammanoy awunee” yaagis. Enttika, yayyishenne malaalettishe issoy issuwako, “Carkkoynne haathay kiitetteyssi, I hayssi oonee” yaagidosona.
26 Iwo anawolokera ku chigawo cha Gerasa chimene chili tsidya lina la nyanja kuchokera ku Galileya.
Abbaa pinnidi Galiila baggara de7iya Gerggesoone biittaa gakkidosona.
27 Yesu ataponda pa mtunda, anakumana ndi munthu wogwidwa ndi ziwanda wochokera mu mzindawo. Kwa nthawi yayitali munthuyu sanavale zovala kapena kukhala mʼnyumba, koma amakhala ku manda.
Yesuusi wogoluwappe keyidi sa7an wodhdhishin tuna ayyaanan oykettida uray katamaappe keyidi iyara gayttis. Daro laythi afili ma77onna kallo duufon de7eesippe attin soo gelenna.
28 Iye ataona Yesu, anakuwa nagwa pa mapazi ake akufuwula kwambiri kuti, “Mukufuna chiyani ndi ine, Yesu Mwana wa Mulungu Wammwambamwamba? Ndikupemphani Inu, musandizunze ine!”
Yesuusa be7ida wode iya sinthan gufannidi, ba qaala dhoqqu oothidi, “Ubbaafe Bolla Xoossaa na7aw Yesuusa neera taw aybi issifetethi de7ii? Hayyana tana ha77i un77ethofarkkii” yaagis.
29 Pakuti Yesu analamula mzimu woyipawo kuti utuluke mwa munthuyo. Kawirikawiri umamugwira iye, ndipo ngakhale anali womangidwa ndi unyolo dzanja ndi mwendo ndi kuti ankamuyangʼanira, koma amadula maunyolo akewo ndipo ziwanda zimamutengera kumalo a yekha.
Hessa I giday, tuna ayyaanay uraappe keyana mela Yesuusi hanqettida gishossa. Daro wode tuna ayyaanay iya haarida gisho santhalaataninne toho qachchiya biraatan qashettidi naagettees. Shin qashuwa duuthidi tuna ayyaanan laagettidi bazzo gelis.
30 Yesu anamufunsa kuti, “Dzina lako ndani?” Iye anayankha kuti, “Legiyo,” chifukwa ziwanda zambiri zinalowa mwa iye.
Yesuusi, “Ne sunthay oonee” yaagidi oychchis. I, daro tuna ayyaanati iya oykkidi gisho bana, “Leegiyona” gis.
31 Ndipo ziwandazo zimamupempha mobwerezabwereza kuti asazitumize ku dzenje la mdima. (Abyssos g12)
Tuna ayyaanati banttana Si7oole kiittonna mela woossidosona. (Abyssos g12)
32 Gulu lalikulu la nkhumba limadya pamenepo mʼmbali mwa phiri. Ziwandazo zinamupempha Yesu kuti azilole kuti zikalowe mu nkhumbazo ndipo Iye anazilola.
He bessan zooze bolla miya guduntho wudey hamuttees. Hini gudunthotan gelino gidi woossidosona, ikka ‘Gelite’ gis.
33 Ziwanda zija zitatuluka mwa munthuyo, zinakalowa mwa nkhumbazo, ndipo gulu lonselo linathamangira ku mtsetse ndi kukalowa mʼnyanja ndi kumira.
Tuna ayyaanati uraappe keyidi gudunthotan gelidosona. Wudey deriyappe duge gurgguxidi abban gelis.
34 Oweta nkhumbazo ataona zimene zinachitikazo, anathamanga ndi kukanena izi mu mzinda ndi ku madera a ku midzi.
Henthanchchoti hanidayssa be7ida wode woxxi bidi, katamaninne guta ubban odidosona.
35 Ndipo anthu anapita kukaona zimene zinachitika. Atafika kwa Yesu, anapeza munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja atakhala pa mapazi a Yesu, atavala ndipo ali ndi nzeru zake; ndipo iwo anachita mantha.
Asay hanidabaa be7anaw keyidi Yesuusakko yidosona. Tuna ayyaanay keyida uray ma7o ma77idi, iya wozanay simmin, Yesuusa toho matan uttidayssa demmidi yayyidosona.
36 Amene anaona izi anawuza anthu mmene munthu wogwidwa ndi ziwandayo anachiritsidwira.
Iya be7ida asay tuna ayyaanan oykettida uray waanidi paxidaakko odidosona.
37 Kenaka anthu onse a ku chigawo cha Gerasa anamupempha Yesu kuti achoke kwa iwo, chifukwa anadzazidwa ndi mantha. Choncho Iye analowa mʼbwato nachoka.
Gerggesoone yuushuwan de7iya asay gita yashshi yashettidi Yesuusi bantta matappe baana mela woossidosona. I wogoluwan gelidi guye simmis.
38 Munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja, anapempha Yesu kuti apite nawo, koma Yesu anamubweza nati,
Tuna ayyaanay keyida uray Yesuusara daanaw woossis.
39 “Bwerera kwanu kafotokoze zimene Mulungu wakuchitira.” Ndipo munthuyo anachoka ndi kukanena ku mzinda wonsewo zimene Yesu anamuchitira iye.
Shin Yesuusi iyaakko, “Ne soo simma, Xoossay ay mela gitabaa new oothidaakko oda” yaagidi mooyzis. Uraykka Yesuusi ay mela gitabaa iyaw oothidaakko katama ubban markkattishe bis.
40 Yesu atabwerera, gulu lalikulu la anthu linamulandira, chifukwa onse ankamuyembekezera.
Asay naagidi gam77ida gisho Yesuusi simmiya wode mokki ekkidosona.
41 Nthawi yomweyo munthu wotchedwa Yairo, woweruza wa mu sunagoge, anabwera ndi kugwa pa mapazi a Yesu, namupempha Iye kuti apite ku nyumba kwake,
Ayhude Woosa Keetha halaqa gidida Iyaroosa giya uray ba soo yaana mela Yesuusa tohuwa bolla wodhdhidi woossis.
42 chifukwa mwana wake yekhayo wamkazi, kamtsikana ka zaka khumi ndi ziwiri, kanali pafupi kufa. Pamene Yesu ankapita gulu la anthu linkamupanikiza.
Iyaw tammanne nam77u laythi gidida macca na7a de7iyara sakettada hayqos gakkada de7awusu. Yesuusi biya wode asay iya un77ethees.
43 Ndipo pomwepo panali mayi wina amene ankataya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri, koma panalibe wina akanamuchiritsa.
Tammanne nam77u laythi suuthi goggishe gam77ida maccasi de7iyara de7awusu. Iya baw de7iya miishiya aakimetas immada onggasu. Shin paxanaw dandda7abukku.
44 Iye anafika kumbuyo kwake ndi kukhudza mothera mwa chovala chake, ndipo nthawi yomweyo magazi ake analeka kutuluka.
Iya Yesuusas guye baggara shiiqada, iya afilaa macaraa bochchasu, sohuwara goggiya suuthay eqqi aggis.
45 Yesu anafunsa kuti, “Wandikhudza ndani?” Onse atakana, Petro anati, “Anthu akukupanikizani ndi kukukankhani.”
Yesuusi, “Tana bochchiday oonee?” yaagis. Ubbay ‘Nu bochchibookko’ yaagin, Phexiroosi, “Asttamaariyaw, daro asay kaallishininne un77ethishin be7ashe waanada, ‘Tana bochchiday oonee?’ gay” yaagis.
46 Koma Yesu anati, “Wina wandikhudza; ndikudziwa chifukwa mphamvu yachoka mwa Ine.”
Shin Yesuusi, “Issi asi tana bochchis; ays giikko, wolqqi taappe keyoyssi taw erettis” yaagis.
47 Ndipo mayiyo podziwa kuti sanathe kuchoka wosadziwika, anabwera akunjenjemera ndipo anagwa pa mapazi a Yesu. Pamaso pa anthu onse, anafotokoza chifukwa chimene anamukhudzira Iye ndi mmene iye anachiritsidwira nthawi yomweyo.
Maccasiya, ibay qonccidayssa erida wode kokkorashe yada Yesuusa tohuwa bolla kunddasu. Ays bochchidaakkonne waanada ellesada paxidaakko asaa ubbaa sinthan markkattasu.
48 Kenaka anati kwa iye, “Mwana wamkazi, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Pita mu mtendere.”
I, “Ta naatte ne ammanoy nena pathis; saron ba” yaagis.
49 Pamene Yesu ankayankhulabe, munthu wina anabwera kuchokera ku nyumba ya Yairo, woweruza wa ku sunagoge uja. Iye anati, “Mwana wanu wa mkazi wamwalira, musawavutitsenso Aphunzitsiwa.”
Yesuusi oda onggonna de7ishin, Ayhude Woosa Keetha halaqaa, Iyaroosa sooppe issi asi yidi, “Iyaroosa, ne na7iya hayqqasu; asttamaariya mela daaburissofa” yaagis.
50 Atamva zimenezi, Yesu anati kwa Yairo, “Usachite mantha, ingokhulupirira basi ndipo adzachiritsidwa.”
Shin Yesuusi hessa si7idi Iyaroosakko, “Babbofa! Ammana, ne na7iya paxana” yaagis.
51 Iye atafika ku nyumba ya Yairo, sanalole wina aliyense kulowa kupatula Petro, Yohane, ndi Yakobo ndi abambo ndi amayi a mwanayo.
Yesuusi Iyaroosa soo gakkida wode Phexiroosappe, Yohaannisappe, Yayqoobappe, na7ee aawappenne aayeppe attin hari gelana mela koyibeenna.
52 Pa nthawiyi nʼkuti anthu onse akubuma ndi kumulirira iye. Yesu anati, “Lekani kulira, sanafe koma wagona tulo.”
He bessan de7iya asa ubbay na7ees mishettidi yeekkishin, Yesuusi, “Yeekkofite! Na7iya dhiskkasuppe attin hayqqabuukku” yaagis.
53 Iwo anamuseka podziwa kuti anali atamwalira.
Asay na7iya hayqqidayssa eriya gisho, iya oda leqqidi miicidosona.
54 Koma Iye anamugwira dzanja lake ndipo anati, “Mwana wanga, dzuka!”
Shin Yesuusi na7ee kushiya oykkidi, “Naatte dendda” yaagis.
55 Mzimu wake unabwerera, ndipo nthawi yomweyo anayimirira. Kenaka Yesu anawawuza kuti amupatse chakudya.
Na7ees shemppoy simmin dendda eqqasu. Yesuusi enttako, “Iwu miyabaa immite” yaagis.
56 Makolo ake anadabwa, koma Iye anawalamulira kuti asawuze wina aliyense zimene zinachitikazo.
Na7ee aawaranne aayera malaalettidosona. Shin Yesuusi hayssa, “Oodeskka odoppite” yaagis.

< Luka 8 >