< Luka 8 >

1 Zitatha izi, Yesu anayendayenda kuchoka mzinda wina kupita wina ndiponso mudzi wina kupita wina, akulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu. Ophunzira ake khumi ndi awiri aja anali naye,
Og det skete i Tiden derefter, at han rejste igennem Byer og Landsbyer og prædikede og forkyndte Evangeliet om Guds Rige, og med ham de tolv
2 komanso akazi ena amene anachiritsidwa ku mizimu yoyipa ndi matenda: Mariya, wotchedwa Magadalena, amene mwa iye munatuluka ziwanda zisanu ndi ziwiri;
og nogle Kvinder, som vare helbredede fra onde Aander og Sygdomme, nemlig: Maria, der kaldes Magdalene, af hvem syv onde Aander vare udfarne;
3 Yohana mkazi wa Kuza, woyangʼanira mʼnyumba ya Herode; Suzana; ndi ena ambiri analinso. Akazi awa ankawathandiza ndi chuma chawo.
og Johanna, Herodes's Husfoged Kuzas Hustru, og Susanna og mange andre, som tjente dem med, hvad de ejede.
4 Anthu ambiri ankasonkhana, ndipo pamene anthu ankabwera kwa Yesu kuchokera ku midzi, Iye anawawuza fanizo ili,
Men da en stor Skare kom sammen, og de droge til ham fra de forskellige Byer, sagde han ved en Lignelse:
5 “Mlimi anapita kukafesa mbewu zake. Akufesa mbewuzo, zina zinagwa mʼmbali mwa njira; zinapondedwa, ndipo mbalame zamlengalenga zinadya.
„En Sædemand gik ud at saa sin Sæd; og idet han saaede, faldt noget ved Vejen og blev nedtraadt, og Himmelens Fugle aade det op.
6 Zina zinagwa pa thanthwe, ndipo pamene zinamera, zinafota chifukwa panalibe chinyezi.
Og noget faldt paa Klippen; og da det voksede op, visnede det, fordi det ikke havde Væde.
7 Mbewu zina zinagwera pakati pa minga, zinakulira pamodzi ndi mingazo ndipo zinalepheretsa mmerawo kukula.
Og noget faldt midt iblandt Torne, og Tornene voksede op med og kvalte det.
8 Mbewu zina zinagwera pa nthaka yabwino. Zinamera ndipo zinabala mowirikiza 100 kuposa zimene zinafesedwa zija.” Atanena izi, anafuwula kuti, “Amene ali ndi makutu, amve.”
Og noget faldt i den gode Jord, og det voksede op og bar hundrede Fold Frugt.‟ Da han sagde dette, raabte han: „Den, som har Øren at høre med, han høre!‟
9 Ophunzira ake anamufunsa tanthauzo lake la fanizolo.
Men hans Disciple spurgte ham, hvad denne Lignelse skulde betyde?
10 Iye anati, “Kudziwa zinsinsi za ufumu wa Mulungu kwapatsidwa kwa inu, koma kwa ena ndimawayankhula mʼmafanizo kuti, “ngakhale akuona, asapenye; ngakhale akumva, asazindikire.”
Og han sagde: „Eder er det givet at kende Guds Riges Hemmeligheder, men de andre i Lignelser, for at de, skønt seende, ikke skulle se, og, skønt hørende, ikke skulle forstaa.
11 “Tanthauzo la fanizoli ndi ili: Mbewu ndi mawu a Mulungu.
Men dette er Lignelsen: Sæden er Guds Ord.
12 Mbewu za mʼmbali mwa njira ndi anthu amene amamva mawu, ndipo kenaka mdierekezi amabwera ndi kuchotsa mawuwo mʼmitima mwawo kuti asakhulupirire ndi kupulumutsidwa.
Men de ved Vejen ere de, som høre det; derefter kommer Djævelen og tager Ordet bort af deres Hjerte, for at de ikke skulle tro og blive frelste.
13 Mbewu za pa thanthwe ndi anthu amene amalandira mawu mwachimwemwe pamene akumva, koma mawuwo sazika mizu. Iwo amakhulupirira kwa kanthawi, koma pa nthawi ya mayesero, amagwa.
Men de paa Klippen ere de, som modtage Ordet med Glæde, naar de høre det, og disse have ikke Rod; de tro til en Tid og falde fra i Fristelsens Tid.
14 Mbewu zimene zinagwa pakati pa minga zikuyimira anthu amene amamva mawu, koma akamayenda mʼnjira zawo amatsamwitsidwa ndi zodandaulitsa za moyo uno, chuma ndi zosangalatsa, ndipo iwo samakhwima.
Men det, som faldt iblandt Torne, det er dem, som have hørt og saa gaa hen og kvæles under Livets Bekymringer og Rigdom og Nydelser og ikke bære moden Frugt.
15 Koma mbewu za pa nthaka yabwino zikuyimira anthu amene ali ndi mtima woona ndi wabwino, amene amamva mawu nawasunga, ndipo amalimbikira mpaka amabala zipatso.
Men det i den gode Jord, det er dem, som, naar de have hørt Ordet, beholde det i et smukt og godt Hjerte og bære Frugt i Udholdenhed.
16 “Palibe amayatsa nyale ndi kuyibisa mu mtsuko kapena kuyika pansi pa bedi. Koma mʼmalo mwake, amayika pa choyikapo chake, kuti anthu olowamo aone kuwala.
Men ingen, som tænder et Lys, skjuler det med et Kar eller sætter det under en Bænk; men han sætter det paa en Lysestage, for at de, som komme ind, kunne se Lyset.
17 Pakuti palibe kanthu kobisika kamene sikadzawululika, ndipo palibe kanthu kophimbika kamene sikadzadziwika kapena kuonetsedwa poyera.
Thi der er ikke noget skjult, som jo skal blive aabenbart; og ikke noget lønligt, som jo skal blive kendt og komme for Lyset.
18 Choncho ganizirani mozama. Iye amene ali nazo adzapatsidwa zambiri, iye amene alibe, ngakhale chimene akuganiza kuti ali nacho adzalandidwa.”
Ser derfor til, hvorledes I høre; thi den, som har, ham skal der gives; og den, som ikke har, fra ham skal endog det tages, han synes at have.‟
19 Tsopano amayi ndi abale a Yesu anabwera kudzamuona Iye, koma analephera kuti afike pafupi ndi Iye chifukwa cha gulu la anthu.
Men hans Moder og Brødre kom til ham og kunde ikke naa frem til ham for Skaren.
20 Wina anamuwuza Iye kuti, “Amayi ndi abale anu ayima kunja, akufuna kukuonani.”
Og det blev ham meddelt: „Din Moder og dine Brødre staa udenfor og begære at se dig.‟
21 Yesu anayankha kuti, “Amayi ndi abale anga ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kumachita zimene mawuwo akunena.”
Men han svarede og sagde til dem: „Min Moder og mine Brødre ere disse, som høre Guds Ord og gøre efter det.‟
22 Tsiku lina Yesu anati kwa ophunzira ake, “Tiyeni tiwolokere tsidya lina la nyanja.” Ndipo analowa mʼbwato nanyamuka.
Og det skete en af de Dage, at han gik om Bord i et Skib tillige med sine Disciple, og han sagde til dem: „Lader os fare over til hin Side af Søen; ‟ og de sejlede ud.
23 Akuwoloka, Iye anagona tulo. Namondwe wamkulu anayamba pa nyanja, ndipo bwatolo linayamba kudzaza ndi madzi ndipo anali pa chiopsezo chachikulu.
Men medens de sejlede, faldt han i Søvn; og en Stormvind for ned over Søen, og Skibet blev fuldt af Vand, og de vare i Fare.
24 Ophunzira anapita ndi kukamudzutsa Iye, nati, “Ambuye, Ambuye, ife tikumira!” Anadzuka ndipo anadzudzula mphepo ndi madzi owindukawo. Namondwe anasiya, ndipo panali bata.
Da traadte de hen og vækkede ham og sagde: „Mester, Mester! vi forgaa.‟ Men han stod op og truede Vinden og Vandets Bølger; og de lagde sig, og det blev blikstille.
25 Iye anafunsa ophunzira ake kuti, “Chikhulupiriro chanu chili kuti?” Koma pogwidwa ndi mantha ndi kudabwa anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Uyu ndi ndani? Iye alamulira ngakhale mphepo ndi madzi, ndipo zimumvera Iye.”
Og han sagde til dem: „Hvor er eders Tro?‟ Men de frygtede og undrede sig og sagde til hverandre: „Hvem er dog denne, siden han byder baade over Vindene og Vandet, og de ere ham lydige?‟
26 Iwo anawolokera ku chigawo cha Gerasa chimene chili tsidya lina la nyanja kuchokera ku Galileya.
Og de sejlede ind til Gadarenernes Land, som ligger lige over for Galilæa.
27 Yesu ataponda pa mtunda, anakumana ndi munthu wogwidwa ndi ziwanda wochokera mu mzindawo. Kwa nthawi yayitali munthuyu sanavale zovala kapena kukhala mʼnyumba, koma amakhala ku manda.
Men da han traadte ud paa Landjorden, mødte der ham en Mand fra Byen, som i lang Tid havde været besat af onde Aander og ikke havde haft Klæder paa og ikke opholdt sig i Hus, men i Gravene.
28 Iye ataona Yesu, anakuwa nagwa pa mapazi ake akufuwula kwambiri kuti, “Mukufuna chiyani ndi ine, Yesu Mwana wa Mulungu Wammwambamwamba? Ndikupemphani Inu, musandizunze ine!”
Men da han saa Jesus, raabte han og faldt ned for ham og sagde med høj Røst: „Hvad har jeg med dig at gøre, Jesus, den højeste Guds Søn? jeg beder dig om, at du ikke vil pine mig.‟
29 Pakuti Yesu analamula mzimu woyipawo kuti utuluke mwa munthuyo. Kawirikawiri umamugwira iye, ndipo ngakhale anali womangidwa ndi unyolo dzanja ndi mwendo ndi kuti ankamuyangʼanira, koma amadula maunyolo akewo ndipo ziwanda zimamutengera kumalo a yekha.
Thi han bød den urene Aand at fare ud af Manden; thi i lange Tider havde den revet ham med sig, og han blev bunden med Lænker og Bøjer og bevogtet, og han sønderrev, hvad man bandt ham med, og dreves af den onde Aand ud i Ørkenerne.
30 Yesu anamufunsa kuti, “Dzina lako ndani?” Iye anayankha kuti, “Legiyo,” chifukwa ziwanda zambiri zinalowa mwa iye.
Men Jesus spurgte ham og sagde: „Hvad er dit Navn?‟ Men han sagde: „Legion‟; thi mange onde Aander vare farne i ham.
31 Ndipo ziwandazo zimamupempha mobwerezabwereza kuti asazitumize ku dzenje la mdima. (Abyssos g12)
Og de bade ham om, at han ikke vilde byde dem at fare ned i Afgrunden; (Abyssos g12)
32 Gulu lalikulu la nkhumba limadya pamenepo mʼmbali mwa phiri. Ziwandazo zinamupempha Yesu kuti azilole kuti zikalowe mu nkhumbazo ndipo Iye anazilola.
men der var sammesteds en stor Hjord Svin, som græssede paa Bjerget; og de bade ham om, at han vilde tilstede dem at fare i dem; og han tilstedte dem det.
33 Ziwanda zija zitatuluka mwa munthuyo, zinakalowa mwa nkhumbazo, ndipo gulu lonselo linathamangira ku mtsetse ndi kukalowa mʼnyanja ndi kumira.
Men de onde Aander fore ud af Manden og fore i Svinene, og Hjorden styrtede sig ned over Brinken ud i Søen og druknede.
34 Oweta nkhumbazo ataona zimene zinachitikazo, anathamanga ndi kukanena izi mu mzinda ndi ku madera a ku midzi.
Men da Hyrderne saa det, som var sket, flyede de og forkyndte det i Byen og paa Landet.
35 Ndipo anthu anapita kukaona zimene zinachitika. Atafika kwa Yesu, anapeza munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja atakhala pa mapazi a Yesu, atavala ndipo ali ndi nzeru zake; ndipo iwo anachita mantha.
Da gik de ud for at se det, som var sket, og de kom til Jesus og fandt Manden, af hvem de onde Aander vare udfarne, siddende ved Jesu Fødder, paaklædt og ved Samling; og de frygtede.
36 Amene anaona izi anawuza anthu mmene munthu wogwidwa ndi ziwandayo anachiritsidwira.
Og de, som havde set det, fortalte dem, hvorledes den besatte var bleven frelst.
37 Kenaka anthu onse a ku chigawo cha Gerasa anamupempha Yesu kuti achoke kwa iwo, chifukwa anadzazidwa ndi mantha. Choncho Iye analowa mʼbwato nachoka.
Og hele Mængden fra Gadarenernes Omegn bad ham om, at han vilde gaa bort fra dem; thi de vare betagne af stor Frygt. Men han gik om Bord i et Skib og vendte tilbage igen.
38 Munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja, anapempha Yesu kuti apite nawo, koma Yesu anamubweza nati,
Men Manden, af hvem de onde Aander vare udfarne, bad ham om, at han maatte være hos ham; men han lod ham fare og sagde:
39 “Bwerera kwanu kafotokoze zimene Mulungu wakuchitira.” Ndipo munthuyo anachoka ndi kukanena ku mzinda wonsewo zimene Yesu anamuchitira iye.
„Vend tilbage til dit Hus, og fortæl, hvor store Ting Gud har gjort imod dig.‟ Og han gik bort og kundgjorde over hele Byen, hvor store Ting Jesus havde gjort imod ham.
40 Yesu atabwerera, gulu lalikulu la anthu linamulandira, chifukwa onse ankamuyembekezera.
Men det skete, da Jesus kom tilbage, tog Skaren imod ham; thi de ventede alle paa ham.
41 Nthawi yomweyo munthu wotchedwa Yairo, woweruza wa mu sunagoge, anabwera ndi kugwa pa mapazi a Yesu, namupempha Iye kuti apite ku nyumba kwake,
Og se, der kom en Mand, som hed Jairus, og han var Forstander for Synagogen; og han faldt ned for Jesu Fødder og bad ham komme ind i hans Hus;
42 chifukwa mwana wake yekhayo wamkazi, kamtsikana ka zaka khumi ndi ziwiri, kanali pafupi kufa. Pamene Yesu ankapita gulu la anthu linkamupanikiza.
thi han havde en enbaaren Datter, omtrent tolv Aar gammel, og hun droges med Døden. Men idet han gik, trængte Skarerne sig sammen om ham.
43 Ndipo pomwepo panali mayi wina amene ankataya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri, koma panalibe wina akanamuchiritsa.
Og en Kvinde, som havde haft Blodflod i tolv Aar og havde kostet al sin Formue paa Læger og ikke kunde blive helbredet af nogen,
44 Iye anafika kumbuyo kwake ndi kukhudza mothera mwa chovala chake, ndipo nthawi yomweyo magazi ake analeka kutuluka.
hun gik til bagfra og rørte ved Fligen af hans Klædebon, og straks standsedes hendes Blodflod.
45 Yesu anafunsa kuti, “Wandikhudza ndani?” Onse atakana, Petro anati, “Anthu akukupanikizani ndi kukukankhani.”
Og Jesus sagde: „Hvem var det, som rørte ved mig?‟ Men da alle nægtede det, sagde Peter og de, som vare med ham: „Mester! Skarerne trykke og trænge dig, og du siger: Hvem var det, som rørte ved mig?‟
46 Koma Yesu anati, “Wina wandikhudza; ndikudziwa chifukwa mphamvu yachoka mwa Ine.”
Men Jesus sagde: „Der rørte nogen ved mig; thi jeg mærkede, at der udgik en Kraft fra mig.‟
47 Ndipo mayiyo podziwa kuti sanathe kuchoka wosadziwika, anabwera akunjenjemera ndipo anagwa pa mapazi a Yesu. Pamaso pa anthu onse, anafotokoza chifukwa chimene anamukhudzira Iye ndi mmene iye anachiritsidwira nthawi yomweyo.
Men da Kvinden saa, at det ikke var skjult, kom hun bævende og faldt ned for ham og fortalte i alt Folkets Paahør, af hvad Aarsag hun havde rørt ved ham, og hvorledes hun straks var bleven helbredet.
48 Kenaka anati kwa iye, “Mwana wamkazi, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Pita mu mtendere.”
Men han sagde til hende: „Datter! din Tro har frelst dig; gaa bort med Fred!‟
49 Pamene Yesu ankayankhulabe, munthu wina anabwera kuchokera ku nyumba ya Yairo, woweruza wa ku sunagoge uja. Iye anati, “Mwana wanu wa mkazi wamwalira, musawavutitsenso Aphunzitsiwa.”
Medens han endnu talte, kommer der en fra Synagogeforstanderens Hus og siger til ham: „Din Datter er død; umag ikke Mesteren!‟
50 Atamva zimenezi, Yesu anati kwa Yairo, “Usachite mantha, ingokhulupirira basi ndipo adzachiritsidwa.”
Men da Jesus hørte det, svarede han ham: „Frygt ikke; tro blot; saa skal hun blive frelst.‟
51 Iye atafika ku nyumba ya Yairo, sanalole wina aliyense kulowa kupatula Petro, Yohane, ndi Yakobo ndi abambo ndi amayi a mwanayo.
Men da han kom til Huset, tillod han ingen at gaa ind med sig uden Peter og Johannes og Jakob og Pigens Fader og Moder.
52 Pa nthawiyi nʼkuti anthu onse akubuma ndi kumulirira iye. Yesu anati, “Lekani kulira, sanafe koma wagona tulo.”
Og de græd alle og holdt Veklage over hende; men han sagde: „Græder ikke; hun er ikke død, men sover.‟
53 Iwo anamuseka podziwa kuti anali atamwalira.
Og de lo ad ham; thi de vidste, at hun var død.
54 Koma Iye anamugwira dzanja lake ndipo anati, “Mwana wanga, dzuka!”
Men han greb hendes Haand og raabte og sagde: „Pige, staa op!‟
55 Mzimu wake unabwerera, ndipo nthawi yomweyo anayimirira. Kenaka Yesu anawawuza kuti amupatse chakudya.
Og hendes Aand vendte tilbage, og hun stod straks op; og han befalede, at de skulde give hende noget at spise.
56 Makolo ake anadabwa, koma Iye anawalamulira kuti asawuze wina aliyense zimene zinachitikazo.
Og hendes Forældre bleve forfærdede; men han bød dem, at de ikke maatte sige nogen det, som var sket.

< Luka 8 >