< Luka 6 >

1 Tsiku lina la Sabata Yesu ankadutsa mʼminda yatirigu, ndipo ophunzira ake anayamba kubudula ngala zatirigu, namazifikisa mʼmanja mwawo ndi kumadya.
Догоди Му се пак у прву суботу по другом дану пасхе да иђаше кроз усеве, и ученици Његови тргаху класје, и сатираху рукама те јеђаху.
2 Ena mwa Afarisi anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mukuchita zosaloledwa pa tsiku la Sabata?”
А неки од фарисеја рекоше им: Зашто чините шта не ваља чинити у суботу?
3 Yesu anawayankha iwo kuti, “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita pamene iye ndi anzake anali ndi njala?
И одговарајући Исус рече им: Зар нисте читали оно што учини Давид кад огладне, он и који беху с њим?
4 Iye analowa mʼnyumba ya Mulungu ndipo atatenga buledi wopatulika anadya amene ndi ololedwa kudya ansembe okha. Ndipo anaperekanso wina kwa anzake.”
Како уђе у кућу Божију, и узе хлебове постављене и изједе, и даде их онима што беху с њим, којих никоме не ваљаше јести осим јединих свештеника.
5 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Mwana wa Munthu ndi Ambuye wa Sabata.”
И рече им: Син је човечији Господар и од суботе.
6 La Sabata lina Iye analowa mʼsunagoge kukaphunzitsa ndipo mʼmenemo anapeza munthu wadzanja lolumala.
А догоди се у другу суботу да Он уђе у зборницу и учаше, и беше онде човек коме десна рука беше сува.
7 Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo ankamuyangʼana kuti apeze chifukwa Yesu, choncho anamuyangʼanitsitsa kuti aone ngati Iye akanamuchiritsa pa Sabata.
Књижевници пак и фарисеји гледаху за Њим неће ли у суботу исцелити, да Га окриве.
8 Koma Yesu anadziwa zimene ankaganiza ndipo anati kwa munthu wadzanja lolumalayo, “Tanyamuka ndipo uyime patsogolo pa onsewa.” Choncho iye ananyamuka nayima pamenepo.
А Он знаше помисли њихове, и рече човеку који имаше суву руку: Устани и стани на среду. А он устаде и стаде.
9 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Ndikufunseni, kodi chololedwa pa Sabata ndi chiti: kuchita chabwino kapena kuchita choyipa, kupulumutsa moyo kapena kuwononga?”
А Исус рече им: Да вас запитам: Шта ваља у суботу чинити, добро или зло? Одржати душу или погубити? А они ћутаху.
10 Iye atawayangʼana onsewo, anati kwa munthuyo, “Wongola dzanja lako.” Iye anaterodi, ndipo dzanja lake linachiritsidwa.
И погледавши на све њих рече му: Пружи руку своју. А он учини тако; и рука поста здрава као и друга.
11 Koma iwo anapsa mtima nayamba kukambirana wina ndi mnzake chomwe akanamuchitira Yesu.
А они се сви напунише безумља, и говораху један другом шта би учинили Исусу.
12 Tsiku lina, masiku amenewo, Yesu anapita ku phiri kukapemphera ndipo anakhala usiku wonse akupemphera kwa Mulungu.
Тих, пак, дана изиђе на гору да се помоли Богу; и проведе сву ноћ на молитви Божијој.
13 Kutacha, anayitana ophunzira ake ndipo anasankha khumi ndi awiri a iwo amene anawayika kukhala atumwi:
И кад би дан, дозва ученике своје, и изабра из њих дванаесторицу, које и апостолима назва:
14 Simoni (amene anamutcha Petro), mʼbale wake wa Andreya, Yakobo, Yohane, Filipo, Bartumeyu,
Симона, кога назва Петром, и Андрију брата његовог, Јакова и Јована, Филипа и Вартоломија,
15 Mateyu, Tomasi, Yakobo mwana wa Alufeyo, Simoni amene amatchedwa Zaleti,
Матеја и Тому, Јакова Алфејевог и Симона прозваног Зилота,
16 Yudasi mwana wa Yakobo ndi Yudasi Isikarioti amene anamupereka.
Јуду Јаковљевог, и Јуду Искариотског, који Га и издаде.
17 Iye anatsika pamodzi ndi atumwiwo ndipo anayima pamalo athyathyathya. Gulu lalikulu la ophunzira ake, gulu lalikulu la anthu ochokera ku Yudeya konse, ku Yerusalemu ndi ochokera mʼmphepete mwa nyanja ya Turo ndi Sidoni anali pomwepo.
И изишавши с њима стаде на месту равном, и гомила ученика Његових; и мноштво народа из све Јудеје и из Јерусалима, и из приморја тирског и сидонског,
18 Iwo anabwera kudzamvetsera ndi kuchiritsidwa ku matenda awo. Osautsidwa ndi mizimu yoyipa anachiritsidwa,
Који дођоше да Га слушају и да се исцељују од својих болести, и које мучаху духови нечисти; и исцељиваху се.
19 ndipo anthu ankayesetsa kuti amukhudze chifukwa mphamvu imatuluka mwa Iye ndi kuchiritsa onse.
И сав народ тражаше да Га се дотакну; јер из Њега излажаше сила и исцељиваше их све.
20 Akuyangʼana ophunzira ake, Iye anati, “Odala ndinu amene ndi osauka, chifukwa ufumu wa Mulungu ndi wanu.
И Он подигнувши очи на ученике своје говораше: Благо вама који сте сиромашни духом; јер је ваше царство Божије.
21 Inu amene mukumva njala tsopano, ndinu odala chifukwa mudzakhutitsidwa. Inu amene mukulira tsopano, ndinu odala chifukwa mudzasekerera.
Благо вама који сте гладни сад; јер ћете се наситити. Благо вама који плачете сад; јер ћете се насмејати.
22 Ndinu odala, anthu akamakudani, kukusalani ndi kukunyozani ndi kumayipitsa dzina lanu chifukwa cha Mwana wa Munthu.
Благо вама кад на вас људи омрзну и кад вас раставе и осрамоте, и разгласе име ваше као зло Сина ради човечијег.
23 “Nthawi imeneyo sangalalani ndipo lumphani ndi chimwemwe chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba. Pakuti ndi zomwezonso zimene makolo awo anachitira aneneri.
Радујте се у онај дан и играјте, јер гле, ваша је велика плата на небу. Јер су тако чинили пророцима очеви њихови.
24 “Ndinu atsoka, anthu olemera, popeza mwalandiriratu zokusangalatsani.
Али тешко вама богати; јер сте већ примили утеху своју.
25 Tsoka inu amene mukudya bwino tsopano, chifukwa mudzakhala ndi njala. Ndinu atsoka, amene mukusekerera tsopano, chifukwa mudzabuma ndi kulira.
Тешко вама сити сад; јер ћете огладнети. Тешко вама који се смејете сад; јер ћете заплакати и заридати.
26 Ndinu atsoka, anthu akamakuyamikirani, popeza makolo anu anawachitira aneneri onama zomwezi.”
Тешко вама кад стану сви добро говорити за вама; јер су тако чинили и лажним пророцима очеви њихови.
27 “Koma Ine ndikuwuza inu amene mukundimva: Kondani adani anu, chitirani zabwino amene amakudani.
Али вама кажем који слушате: љубите непријатеље своје, добро чините онима који на вас мрзе;
28 Dalitsani amene amakutembererani, apempherereni amene amakusautsani.
Благосиљајте оне који вас куну, и молите се Богу за оне који вас вређају.
29 Ngati wina akumenyani patsaya limodzi mupatseninso tsaya linalo. Ngati wina akulanda mwinjiro wako, umulole atenge ndi mkanjo omwe.
Који те удари по образу, окрени му и други; и који хоће да ти узме кабаницу, подај му и кошуљу.
30 Mupatseni aliyense amene akupemphani kanthu ndipo ngati wina atenga chinthu chanu, musamulamule kuti akubwezereni.
А свакоме који иште у тебе, подај; и који твоје узме, не ишти.
31 Inu muwachitire anthu ena, zomwe mukanafuna kuti iwo akuchitireni.
И како хоћете да чине вама људи чините и ви њима онако.
32 “Ngati mukonda okhawo amene amakukondani, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amakonda amene amawakondanso.
И ако љубите оне који вас љубе, каква вам је хвала? Јер и грешници љубе оне који њих љубе.
33 Ndipo ngati muchita zabwino kwa amene ndi abwino kwa inu, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amachita izi.
И ако чините добро онима који вама добро чине, каква вам је хвала? Јер и грешници чине тако.
34 Ndipo ngati mukongoza amene mukuyembekeza kuti abweza, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amabwereketsa kwa ochimwa anzawo, ndipo amayembekezera kubwezeredwa zonse.
И ако дајете у зајам онима од којих се надате да ћете узети, каква вам је хвала? Јер и грешници грешницима дају у зајам да узму опет онолико.
35 Koma kondani adani anu, achitireni zabwino, akongozeni koma osayembekezera kulandira kanthu. Pamenepo mphotho yanu idzakhala yayikulu ndipo inu mudzakhala ana a Wammwambamwamba, chifukwa ndi wokoma mtima kwa anthu osayamika ndi oyipa.
Али, љубите непријатеље своје, и чините добро, и дајте у зајам не надајући се ничему; и биће вам велика плата, и бићете синови Највишега, јер је Он благ и неблагодарнима и злима.
36 Khalani achifundo, monga momwe Atate anu ali achifundo.”
Будите дакле милостиви као и Отац ваш што је милостив.
37 “Musaweruze, ndipo inu simudzaweruzidwa. Musatsutse ndipo inu simudzatsutsidwa. Khululukirani ena ndipo mudzakhululukidwa.
И не судите, и неће вам судити; и не осуђујте, и нећете бити осуђени; опраштајте, и опростиће вам се.
38 Perekani ndipo mudzapatsidwa. Adzakupatsani mʼthumba mwanu muyeso wabwino, wotsenderezeka, wokhutchumuka ndi wosefukira. Pakuti muyeso umene mumagwiritsa ntchito, ndi omwewo adzakuyeserani.”
Дајте, и даће вам се: меру добру и набијену и стресену и препуну даће вам у наручје ваше. Јер каквом мером дајете онаквом ће вам се вратити.
39 Iye anawawuzanso fanizo ili, “Kodi munthu wakhungu angatsogolere munthu wakhungu mnzake? Kodi onse sadzagwera mʼdzenje?
И каза им причу: Може ли слепац слепца водити? Неће ли оба пасти у јаму?
40 Wophunzira sangapose mphunzitsi wake, koma yense amene waphunzitsidwa bwinobwino adzakhala ngati mphunzitsi wake.
Нема ученика над учитељем својим, него и сасвим кад се изучи, биће као и учитељ његов.
41 “Kodi ndi chifukwa chiyani mumaona kachitsotso mʼdiso la mʼbale wanu ndi kusasamala mtengo uli mʼdiso mwanu?
А зашто видиш трун у оку брата свог, а брвна у свом оку не осећаш?
42 Kodi munganene bwanji kwa mʼbale wanu kuti, ‘Mʼbale nʼtakuchotsa kachitsotso mʼdiso mwako,’ pamene inu eni ake mukulephera kuona mtengo uli mʼdiso mwanu? Inu achiphamaso, yambani mwachotsa mtengo uli mʼdiso mwanu, ndipo kenaka mudzaona bwinobwino ndi kuchotsa kachitsotso mʼdiso la mʼbale wanu.”
Или како можеш рећи брату свом: Брате! Стани да извадим трун који је у оку твом, кад сам не видиш брвна у свом оку? Лицемере! Извади најпре брвно из ока свог, па ћеш онда видети извадити трун из ока брата свог.
43 Palibe mtengo wabwino umene umabala chipatso choyipa, kapena mtengo oyipa umene umabala chipatso chabwino.
Јер нема дрвета доброг да рађа зао род; нити дрвета злог да рађа добар род.
44 Mtengo uliwonse umadziwika ndi chipatso chake. Anthu sathyola nkhuyu pa mtengo waminga, kapena mphesa pa nthungwi.
Јер се свако дрво по роду свом познаје: јер се смокве не беру с трња, нити се грожђе бере с купине,
45 Munthu wabwino amatulutsa zinthu zabwino zosungidwa mu mtima mwake, koma munthu oyipa amatulutsa zinthu zoyipa zosungidwa mu mtima mwake. Pakamwa pake pamayankhula zimene zadzaza mu mtima mwake.
Добар човек из добре клети срца свог износи добро, а зао човек из зле клети срца свог износи зло, јер уста његова говоре од сувишка срца.
46 “Kodi nʼchifukwa chiyani munditchula kuti, ‘Ambuye, Ambuye’ koma simuchita zimene Ine ndinena?
А што ме зовете: Господе! Господе! А не извршујете шта вам говорим?
47 Ine ndidzakuonetsani mmene alili munthu amene amabwera kwa Ine ndi kumva mawu anga ndi kuwachita.
Сваки који иде за мном и слуша речи моје и извршује их, казаћу вам какав је:
48 Iye ali ngati munthu womanga nyumba, amene anakumba mozama nayika maziko ake pa mwala. Madzi osefukira atabwera ndi mphamvu, nawomba nyumbayo koma sinagwedezeka, chifukwa anayimanga bwino.
Он је као човек који гради кућу, па ископа и удуби и удари темељ на камену; а кад дођоше воде, навали река на ону кућу и не може је покренути, јер јој је темељ на камену.
49 Koma amene amamva mawu anga koma osawachita, akufanana ndi munthu amene anamanga nyumba yake koma yopanda maziko. Nthawi yomwe madziwo anawomba nyumbayo, inagwa ndipo inawonongekeratu.”
А који слуша и не извршује он је као човек који начини кућу на земљи без темеља, на коју навали река и одмах је обори, и распаде се кућа она страшно.

< Luka 6 >