< Luka 6 >

1 Tsiku lina la Sabata Yesu ankadutsa mʼminda yatirigu, ndipo ophunzira ake anayamba kubudula ngala zatirigu, namazifikisa mʼmanja mwawo ndi kumadya.
Un jour de sabbat, Jésus passant par des blés, ses disciples arrachaient des épis, les froissaient entre leurs mains, et ils les mangeaient.
2 Ena mwa Afarisi anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mukuchita zosaloledwa pa tsiku la Sabata?”
Quelques-uns des pharisiens leur dirent: Pourquoi faites-vous ce qu'il n'est pas permis de faire le jour du sabbat?
3 Yesu anawayankha iwo kuti, “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita pamene iye ndi anzake anali ndi njala?
Jésus, prenant la parole, leur dit: N'avez-vous donc pas lu ce que fit David, lorsqu'il eut faim, lui et ceux qui étaient avec lui?
4 Iye analowa mʼnyumba ya Mulungu ndipo atatenga buledi wopatulika anadya amene ndi ololedwa kudya ansembe okha. Ndipo anaperekanso wina kwa anzake.”
Comment il entra dans la maison de Dieu, prit les pains de proposition, en mangea et en donna à ceux qui étaient avec lui, bien qu'il ne soit permis qu'aux seuls sacrificateurs d'en manger?
5 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Mwana wa Munthu ndi Ambuye wa Sabata.”
Et il leur dit: Le Fils de l'homme est maître même du sabbat.
6 La Sabata lina Iye analowa mʼsunagoge kukaphunzitsa ndipo mʼmenemo anapeza munthu wadzanja lolumala.
Un autre jour de sabbat, Jésus entra dans la synagogue, et il se mit à enseigner. Il y avait là un homme dont la main droite était desséchée.
7 Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo ankamuyangʼana kuti apeze chifukwa Yesu, choncho anamuyangʼanitsitsa kuti aone ngati Iye akanamuchiritsa pa Sabata.
Or, les scribes et les pharisiens observaient Jésus pour voir s'il ferait une guérison le jour du sabbat, afin de trouver l'occasion de l'accuser.
8 Koma Yesu anadziwa zimene ankaganiza ndipo anati kwa munthu wadzanja lolumalayo, “Tanyamuka ndipo uyime patsogolo pa onsewa.” Choncho iye ananyamuka nayima pamenepo.
Mais comme il connaissait leurs pensées, il dit à l'homme qui avait la main desséchée: Lève-toi, et tiens-toi debout au milieu de nous! Et lui, s'étant levé, se tint debout.
9 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Ndikufunseni, kodi chololedwa pa Sabata ndi chiti: kuchita chabwino kapena kuchita choyipa, kupulumutsa moyo kapena kuwononga?”
Jésus leur dit: Est-il permis, le jour du sabbat, de faire du bien ou de faire du mal, de sauver une personne ou de la faire périr?
10 Iye atawayangʼana onsewo, anati kwa munthuyo, “Wongola dzanja lako.” Iye anaterodi, ndipo dzanja lake linachiritsidwa.
Puis, ayant porté ses regards sur tous ceux qui étaient autour de lui, il dit à l'homme: Étends ta main. Il le fit, et sa main redevint saine.
11 Koma iwo anapsa mtima nayamba kukambirana wina ndi mnzake chomwe akanamuchitira Yesu.
Mais eux furent remplis de fureur; et ils s'entretenaient ensemble de ce qu'ils pourraient faire à Jésus.
12 Tsiku lina, masiku amenewo, Yesu anapita ku phiri kukapemphera ndipo anakhala usiku wonse akupemphera kwa Mulungu.
En ce temps-là, Jésus alla sur la montagne pour prier; et il passa toute la nuit à prier Dieu.
13 Kutacha, anayitana ophunzira ake ndipo anasankha khumi ndi awiri a iwo amene anawayika kukhala atumwi:
Quand le jour fut venu, il appela ses disciples, et il en choisit douze auxquels il donna le nom d'apôtres:
14 Simoni (amene anamutcha Petro), mʼbale wake wa Andreya, Yakobo, Yohane, Filipo, Bartumeyu,
Simon, qu'il nomma Pierre, et André, son frère; Jacques et Jean; Philippe et Barthélémy;
15 Mateyu, Tomasi, Yakobo mwana wa Alufeyo, Simoni amene amatchedwa Zaleti,
Matthieu et Thomas; Jacques, fils d'Alphée, et Simon, appelé Zélote;
16 Yudasi mwana wa Yakobo ndi Yudasi Isikarioti amene anamupereka.
Jude, fils de Jacques, et Judas Iscariote, celui qui le trahit.
17 Iye anatsika pamodzi ndi atumwiwo ndipo anayima pamalo athyathyathya. Gulu lalikulu la ophunzira ake, gulu lalikulu la anthu ochokera ku Yudeya konse, ku Yerusalemu ndi ochokera mʼmphepete mwa nyanja ya Turo ndi Sidoni anali pomwepo.
Ensuite, étant descendu avec eux, il s'arrêta sur un plateau. Là, se trouvaient un grand nombre de ses disciples et une grande multitude de gens, qui étaient venus de toute la Judée et de Jérusalem, ainsi que du littoral de Tyr et de Sidon, pour l'entendre et pour être guéris de leurs maladies.
18 Iwo anabwera kudzamvetsera ndi kuchiritsidwa ku matenda awo. Osautsidwa ndi mizimu yoyipa anachiritsidwa,
Ceux qui étaient tourmentés par des esprits impurs étaient aussi guéris.
19 ndipo anthu ankayesetsa kuti amukhudze chifukwa mphamvu imatuluka mwa Iye ndi kuchiritsa onse.
Toute la multitude cherchait à le toucher, parce qu'il sortait de lui une force qui les guérissait tous.
20 Akuyangʼana ophunzira ake, Iye anati, “Odala ndinu amene ndi osauka, chifukwa ufumu wa Mulungu ndi wanu.
Alors levant les yeux sur ses disciples, Jésus dit: Heureux, vous qui êtes pauvres, parce que le royaume de Dieu est à vous!
21 Inu amene mukumva njala tsopano, ndinu odala chifukwa mudzakhutitsidwa. Inu amene mukulira tsopano, ndinu odala chifukwa mudzasekerera.
Heureux, vous qui avez faim maintenant, parce que vous serez rassasiés! Heureux, vous qui pleurez maintenant, parce que vous serez dans la joie!
22 Ndinu odala, anthu akamakudani, kukusalani ndi kukunyozani ndi kumayipitsa dzina lanu chifukwa cha Mwana wa Munthu.
Vous serez heureux, lorsque les hommes vous haïront, qu'ils vous chasseront, qu'ils vous diront des outrages et rejetteront votre, nom comme infâme, à cause du Fils de l'homme!
23 “Nthawi imeneyo sangalalani ndipo lumphani ndi chimwemwe chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba. Pakuti ndi zomwezonso zimene makolo awo anachitira aneneri.
Réjouissez-vous en ce jour-là, et tressaillez de joie, parce que votre récompense sera grande dans le ciel; car c'est ainsi que leurs pères traitaient les prophètes.
24 “Ndinu atsoka, anthu olemera, popeza mwalandiriratu zokusangalatsani.
Mais malheur à vous, riches, parce que vous avez déjà reçu votre consolation!
25 Tsoka inu amene mukudya bwino tsopano, chifukwa mudzakhala ndi njala. Ndinu atsoka, amene mukusekerera tsopano, chifukwa mudzabuma ndi kulira.
Malheur à vous qui êtes rassasiés maintenant, parce que vous aurez faim! Malheur à vous qui riez maintenant, parce que vous serez dans le deuil et dans les larmes!
26 Ndinu atsoka, anthu akamakuyamikirani, popeza makolo anu anawachitira aneneri onama zomwezi.”
Malheur à vous, lorsque tous les hommes diront du bien de vous; car leurs pères faisaient de même à l'égard des faux prophètes!
27 “Koma Ine ndikuwuza inu amene mukundimva: Kondani adani anu, chitirani zabwino amene amakudani.
Mais je vous dis, à vous qui m'écoutez: Aimez vos ennemis, faites du bien à ceux qui vous haïssent,
28 Dalitsani amene amakutembererani, apempherereni amene amakusautsani.
bénissez ceux qui vous maudissent, priez pour ceux qui vous outragent.
29 Ngati wina akumenyani patsaya limodzi mupatseninso tsaya linalo. Ngati wina akulanda mwinjiro wako, umulole atenge ndi mkanjo omwe.
A celui qui te frappe sur une joue, présente aussi l'autre; et si quelqu'un t'enlève ton manteau, ne l'empêche pas de prendre aussi ta tunique.
30 Mupatseni aliyense amene akupemphani kanthu ndipo ngati wina atenga chinthu chanu, musamulamule kuti akubwezereni.
Donne à tout homme qui te demande, et si quelqu'un t'enlève ce qui est à toi, ne le réclame pas.
31 Inu muwachitire anthu ena, zomwe mukanafuna kuti iwo akuchitireni.
Ce que vous voulez que les hommes vous fassent, faites-le-leur aussi de même.
32 “Ngati mukonda okhawo amene amakukondani, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amakonda amene amawakondanso.
Si vous aimez ceux qui vous aiment, quel gré vous en saura-t-on? Les pécheurs aussi aiment ceux qui les aiment!
33 Ndipo ngati muchita zabwino kwa amene ndi abwino kwa inu, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amachita izi.
Et si vous faites du bien à ceux qui vous font du bien, quel gré vous en saura-t-on? Les pécheurs font la même chose.
34 Ndipo ngati mukongoza amene mukuyembekeza kuti abweza, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amabwereketsa kwa ochimwa anzawo, ndipo amayembekezera kubwezeredwa zonse.
Et si vous prêtez à ceux de qui vous espérez recevoir, quel gré vous en saura-t-on? Les pécheurs aussi prêtent aux pécheurs, afin de recevoir la pareille!
35 Koma kondani adani anu, achitireni zabwino, akongozeni koma osayembekezera kulandira kanthu. Pamenepo mphotho yanu idzakhala yayikulu ndipo inu mudzakhala ana a Wammwambamwamba, chifukwa ndi wokoma mtima kwa anthu osayamika ndi oyipa.
Mais vous, aimez vos ennemis; faites du bien, et prêtez sans rien espérer en retour. Votre récompense sera grande, et vous serez les fils du Très-Haut, parce qu'il est bon pour les ingrats et les méchants.
36 Khalani achifundo, monga momwe Atate anu ali achifundo.”
Soyez miséricordieux, comme votre Père est miséricordieux.
37 “Musaweruze, ndipo inu simudzaweruzidwa. Musatsutse ndipo inu simudzatsutsidwa. Khululukirani ena ndipo mudzakhululukidwa.
Ne jugez point, et vous ne serez pas jugés; ne condamnez point, et vous ne serez pas condamnés; pardonnez, et on vous pardonnera.
38 Perekani ndipo mudzapatsidwa. Adzakupatsani mʼthumba mwanu muyeso wabwino, wotsenderezeka, wokhutchumuka ndi wosefukira. Pakuti muyeso umene mumagwiritsa ntchito, ndi omwewo adzakuyeserani.”
Donnez, et on vous donnera: on versera dans votre sein une bonne mesure, pressée, secouée, débordante; car on se servira pour vous de la mesure avec laquelle vous mesurez.
39 Iye anawawuzanso fanizo ili, “Kodi munthu wakhungu angatsogolere munthu wakhungu mnzake? Kodi onse sadzagwera mʼdzenje?
Il leur dit aussi une parabole: Un aveugle peut-il conduire un aveugle? Ne tomberont-ils pas tous les deux dans la fosse?
40 Wophunzira sangapose mphunzitsi wake, koma yense amene waphunzitsidwa bwinobwino adzakhala ngati mphunzitsi wake.
Le disciple n'est pas au-dessus de son maître; mais tout disciple accompli sera comme son maître.
41 “Kodi ndi chifukwa chiyani mumaona kachitsotso mʼdiso la mʼbale wanu ndi kusasamala mtengo uli mʼdiso mwanu?
Pourquoi regardes-tu la paille qui est dans l'oeil de ton frère, et n'aperçois-tu pas la poutre qui est dans ton oeil?
42 Kodi munganene bwanji kwa mʼbale wanu kuti, ‘Mʼbale nʼtakuchotsa kachitsotso mʼdiso mwako,’ pamene inu eni ake mukulephera kuona mtengo uli mʼdiso mwanu? Inu achiphamaso, yambani mwachotsa mtengo uli mʼdiso mwanu, ndipo kenaka mudzaona bwinobwino ndi kuchotsa kachitsotso mʼdiso la mʼbale wanu.”
Comment peux-tu dire à ton frère: Frère, laisse-moi ôter la paille qui est dans ton oeil, — toi qui ne vois pas la poutre qui est dans le tien? Hypocrite, ôte premièrement la poutre de ton oeil, et alors tu verras à ôter la paille qui est dans l'oeil de ton frère.
43 Palibe mtengo wabwino umene umabala chipatso choyipa, kapena mtengo oyipa umene umabala chipatso chabwino.
L'arbre qui produit de mauvais fruits n'est pas bon, et l'arbre qui produit de bons fruits n'est pas mauvais;
44 Mtengo uliwonse umadziwika ndi chipatso chake. Anthu sathyola nkhuyu pa mtengo waminga, kapena mphesa pa nthungwi.
car chaque arbre se reconnaît à son propre fruit. On ne cueille pas des figues sur des épines, et on ne récolte pas des raisins sur des ronces.
45 Munthu wabwino amatulutsa zinthu zabwino zosungidwa mu mtima mwake, koma munthu oyipa amatulutsa zinthu zoyipa zosungidwa mu mtima mwake. Pakamwa pake pamayankhula zimene zadzaza mu mtima mwake.
L'homme de bien tire le bien du bon trésor de son coeur, mais le méchant tire le mal de son mauvais trésor; car de l'abondance du coeur la bouche parle.
46 “Kodi nʼchifukwa chiyani munditchula kuti, ‘Ambuye, Ambuye’ koma simuchita zimene Ine ndinena?
Pourquoi m'appelez-vous: Seigneur, Seigneur, et ne faites-vous pas ce que je dis?
47 Ine ndidzakuonetsani mmene alili munthu amene amabwera kwa Ine ndi kumva mawu anga ndi kuwachita.
Je vais vous montrer à qui ressemble tout homme qui vient à moi, qui entend mes paroles et qui les met en pratique.
48 Iye ali ngati munthu womanga nyumba, amene anakumba mozama nayika maziko ake pa mwala. Madzi osefukira atabwera ndi mphamvu, nawomba nyumbayo koma sinagwedezeka, chifukwa anayimanga bwino.
Il est semblable à un homme qui, bâtissant une maison, a creusé profondément la terre, et en a posé les fondements sur le roc: les eaux ont débordé, le torrent s'est précipité avec violence contre cette maison, mais il n'a pu l'ébranler, parce qu'elle avait été bien construite.
49 Koma amene amamva mawu anga koma osawachita, akufanana ndi munthu amene anamanga nyumba yake koma yopanda maziko. Nthawi yomwe madziwo anawomba nyumbayo, inagwa ndipo inawonongekeratu.”
Mais celui qui entend et ne met pas en pratique, est semblable à un homme qui a bâti sa maison sur la terre, sans fondements: le torrent a donné contre elle avec violence, et aussitôt elle est tombée; et la ruine de cette maison a été grande.

< Luka 6 >