< Luka 6 >

1 Tsiku lina la Sabata Yesu ankadutsa mʼminda yatirigu, ndipo ophunzira ake anayamba kubudula ngala zatirigu, namazifikisa mʼmanja mwawo ndi kumadya.
And it came to pass on the second sabbath after the first, that he was going through grain-fields; and his disciples plucked the ears of grain, and ate them, rubbing them with their hands.
2 Ena mwa Afarisi anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mukuchita zosaloledwa pa tsiku la Sabata?”
And some of the Pharisees said, Why are ye doing that which it is not lawful to do on the sabbath?
3 Yesu anawayankha iwo kuti, “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita pamene iye ndi anzake anali ndi njala?
And Jesus answering them, said, Have ye not even read what David did, when he was himself hungry, and they who were with him?
4 Iye analowa mʼnyumba ya Mulungu ndipo atatenga buledi wopatulika anadya amene ndi ololedwa kudya ansembe okha. Ndipo anaperekanso wina kwa anzake.”
how he went into the house of God, and took and ate the show-bread, and gave it also to those who were with him, which it is not lawful for any to eat but the priests alone?
5 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Mwana wa Munthu ndi Ambuye wa Sabata.”
And he said to them, The Son of man is lord even of the sabbath.
6 La Sabata lina Iye analowa mʼsunagoge kukaphunzitsa ndipo mʼmenemo anapeza munthu wadzanja lolumala.
And it came to pass on another sabbath, that he entered into the synagogue, and taught; and there was a man there whose right hand was withered.
7 Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo ankamuyangʼana kuti apeze chifukwa Yesu, choncho anamuyangʼanitsitsa kuti aone ngati Iye akanamuchiritsa pa Sabata.
And the scribes and the Pharisees were watching whether he would heal on the sabbath, that they might find an accusation against him.
8 Koma Yesu anadziwa zimene ankaganiza ndipo anati kwa munthu wadzanja lolumalayo, “Tanyamuka ndipo uyime patsogolo pa onsewa.” Choncho iye ananyamuka nayima pamenepo.
But he knew their thoughts; and he said to the man having the withered hand, Rise, and stand up in the midst. And he arose, and stood up.
9 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Ndikufunseni, kodi chololedwa pa Sabata ndi chiti: kuchita chabwino kapena kuchita choyipa, kupulumutsa moyo kapena kuwononga?”
And Jesus said to them, I ask you whether it is lawful on the sabbath to do good, or to do evil; to save life, or to kill?
10 Iye atawayangʼana onsewo, anati kwa munthuyo, “Wongola dzanja lako.” Iye anaterodi, ndipo dzanja lake linachiritsidwa.
And looking round on them all, he said to him, Stretch forth thy hand. And he did so; and his hand was restored.
11 Koma iwo anapsa mtima nayamba kukambirana wina ndi mnzake chomwe akanamuchitira Yesu.
But they were filled with madness, and conferred with one another as to what they should do to Jesus.
12 Tsiku lina, masiku amenewo, Yesu anapita ku phiri kukapemphera ndipo anakhala usiku wonse akupemphera kwa Mulungu.
And it came to pass in those days, that he went out into the mountain to pray; and he continued all night in prayer to God.
13 Kutacha, anayitana ophunzira ake ndipo anasankha khumi ndi awiri a iwo amene anawayika kukhala atumwi:
And when it was day, he called to him his disciples; and he chose from them twelve, whom he also named apostles;
14 Simoni (amene anamutcha Petro), mʼbale wake wa Andreya, Yakobo, Yohane, Filipo, Bartumeyu,
Simon, whom he named Peter, and Andrew his brother, and James and John, and Philip and Bartholomew,
15 Mateyu, Tomasi, Yakobo mwana wa Alufeyo, Simoni amene amatchedwa Zaleti,
and Matthew and Thomas, and James the Son of Alphaeus, and Simon called the zealot,
16 Yudasi mwana wa Yakobo ndi Yudasi Isikarioti amene anamupereka.
and Judas the brother of James, and Judas Iscariot, who became a traitor.
17 Iye anatsika pamodzi ndi atumwiwo ndipo anayima pamalo athyathyathya. Gulu lalikulu la ophunzira ake, gulu lalikulu la anthu ochokera ku Yudeya konse, ku Yerusalemu ndi ochokera mʼmphepete mwa nyanja ya Turo ndi Sidoni anali pomwepo.
And he came down with them, and stood on a level place with a great multitude of his disciples, and a great crowd of the people from all Judaea and Jerusalem and the sea-coast of Tyre and Sidon, who came to hear him, and to be healed of their diseases.
18 Iwo anabwera kudzamvetsera ndi kuchiritsidwa ku matenda awo. Osautsidwa ndi mizimu yoyipa anachiritsidwa,
And they that were harassed with unclean spirits were cured.
19 ndipo anthu ankayesetsa kuti amukhudze chifukwa mphamvu imatuluka mwa Iye ndi kuchiritsa onse.
And the whole multitude sought to touch him, because power went out of him and healed all.
20 Akuyangʼana ophunzira ake, Iye anati, “Odala ndinu amene ndi osauka, chifukwa ufumu wa Mulungu ndi wanu.
And raising his eyes toward his disciples, he said, Blessed are ye poor; for yours is the kingdom of God.
21 Inu amene mukumva njala tsopano, ndinu odala chifukwa mudzakhutitsidwa. Inu amene mukulira tsopano, ndinu odala chifukwa mudzasekerera.
Blessed are ye that hunger now; for ye will be filled. Blessed are ye that weep now; for ye will laugh.
22 Ndinu odala, anthu akamakudani, kukusalani ndi kukunyozani ndi kumayipitsa dzina lanu chifukwa cha Mwana wa Munthu.
Blessed are ye when men hate you, and when they exclude you, and revile and cast out your name as evil, on account of the Son of man.
23 “Nthawi imeneyo sangalalani ndipo lumphani ndi chimwemwe chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba. Pakuti ndi zomwezonso zimene makolo awo anachitira aneneri.
Rejoice in that day, and leap for joy; for lo! your reward is great in heaven; for thus their fathers did to the prophets.
24 “Ndinu atsoka, anthu olemera, popeza mwalandiriratu zokusangalatsani.
But woe to you that are rich! for ye have received your consolation.
25 Tsoka inu amene mukudya bwino tsopano, chifukwa mudzakhala ndi njala. Ndinu atsoka, amene mukusekerera tsopano, chifukwa mudzabuma ndi kulira.
Woe to you that are full now! for ye will hunger. Woe to you that laugh now! for ye will mourn and weep.
26 Ndinu atsoka, anthu akamakuyamikirani, popeza makolo anu anawachitira aneneri onama zomwezi.”
Woe, when all men speak well of you! for so did their fathers of the false prophets.
27 “Koma Ine ndikuwuza inu amene mukundimva: Kondani adani anu, chitirani zabwino amene amakudani.
But I say to you who hear: Love your enemies; do good to those who hate you;
28 Dalitsani amene amakutembererani, apempherereni amene amakusautsani.
bless those who curse you; pray for those who are spiteful to you.
29 Ngati wina akumenyani patsaya limodzi mupatseninso tsaya linalo. Ngati wina akulanda mwinjiro wako, umulole atenge ndi mkanjo omwe.
To him that smiteth thee on one cheek, offer also the other; and him that taketh away thy cloak, forbid not to take thy coat also.
30 Mupatseni aliyense amene akupemphani kanthu ndipo ngati wina atenga chinthu chanu, musamulamule kuti akubwezereni.
Give to every one that asketh of thee; and from him that taketh away thy goods, demand them not again.
31 Inu muwachitire anthu ena, zomwe mukanafuna kuti iwo akuchitireni.
And as ye would that men should do to you, do ye also in like manner to them.
32 “Ngati mukonda okhawo amene amakukondani, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amakonda amene amawakondanso.
And if ye love those who love you, what thanks do ye deserve? for sinners also love those who love them.
33 Ndipo ngati muchita zabwino kwa amene ndi abwino kwa inu, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amachita izi.
For if ye do good to those who do good to you, what thanks do ye deserve? even sinners do the same.
34 Ndipo ngati mukongoza amene mukuyembekeza kuti abweza, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amabwereketsa kwa ochimwa anzawo, ndipo amayembekezera kubwezeredwa zonse.
And if ye lend to those from whom ye expect to receive, what thanks do ye deserve? even sinners lend to sinners, to receive as much in return.
35 Koma kondani adani anu, achitireni zabwino, akongozeni koma osayembekezera kulandira kanthu. Pamenepo mphotho yanu idzakhala yayikulu ndipo inu mudzakhala ana a Wammwambamwamba, chifukwa ndi wokoma mtima kwa anthu osayamika ndi oyipa.
But love your enemies, and do good and lend, despairing of no one; and your reward will be great, and ye will be sons of the Most High; for he is kind to the unthankful and wicked.
36 Khalani achifundo, monga momwe Atate anu ali achifundo.”
Be merciful, as your Father is merciful.
37 “Musaweruze, ndipo inu simudzaweruzidwa. Musatsutse ndipo inu simudzatsutsidwa. Khululukirani ena ndipo mudzakhululukidwa.
And judge not, and ye will not be judged; and condemn not, and ye will not be condemned; forgive, and ye will be forgiven;
38 Perekani ndipo mudzapatsidwa. Adzakupatsani mʼthumba mwanu muyeso wabwino, wotsenderezeka, wokhutchumuka ndi wosefukira. Pakuti muyeso umene mumagwiritsa ntchito, ndi omwewo adzakuyeserani.”
give, and it will be given to you; good measure, pressed down, shaken together, running over, will men give into your bosom; for with what measure ye mete, it will be measured to you in return.
39 Iye anawawuzanso fanizo ili, “Kodi munthu wakhungu angatsogolere munthu wakhungu mnzake? Kodi onse sadzagwera mʼdzenje?
And he spoke also a parable to them: Can the blind lead the blind? Will they not both fall into a ditch?
40 Wophunzira sangapose mphunzitsi wake, koma yense amene waphunzitsidwa bwinobwino adzakhala ngati mphunzitsi wake.
A disciple is not above his teacher; but every one when fully instructed will be as his teacher.
41 “Kodi ndi chifukwa chiyani mumaona kachitsotso mʼdiso la mʼbale wanu ndi kusasamala mtengo uli mʼdiso mwanu?
And why dost thou look at the mote in thy brother's eye, and not perceive the beam that is in thine own eye?
42 Kodi munganene bwanji kwa mʼbale wanu kuti, ‘Mʼbale nʼtakuchotsa kachitsotso mʼdiso mwako,’ pamene inu eni ake mukulephera kuona mtengo uli mʼdiso mwanu? Inu achiphamaso, yambani mwachotsa mtengo uli mʼdiso mwanu, ndipo kenaka mudzaona bwinobwino ndi kuchotsa kachitsotso mʼdiso la mʼbale wanu.”
How canst thou say to thy brother, Brother, let me take out the mote that is in thine eye, when thou thyself perceivest not the beam in thine own eye? Hypocrite! first cast the beam out of thine own eye, and then thou wilt see clearly to take out the mote that is in thy brother's eye.
43 Palibe mtengo wabwino umene umabala chipatso choyipa, kapena mtengo oyipa umene umabala chipatso chabwino.
For there is no good tree that beareth bad fruit; and again, there is no bad tree that beareth good fruit.
44 Mtengo uliwonse umadziwika ndi chipatso chake. Anthu sathyola nkhuyu pa mtengo waminga, kapena mphesa pa nthungwi.
For every tree is known by its own fruit; for from thorns men do not gather figs, nor from a bramble-bush do they gather grapes.
45 Munthu wabwino amatulutsa zinthu zabwino zosungidwa mu mtima mwake, koma munthu oyipa amatulutsa zinthu zoyipa zosungidwa mu mtima mwake. Pakamwa pake pamayankhula zimene zadzaza mu mtima mwake.
The good man out of the good treasure of his heart bringeth forth that which is good; and the evil man out of the evil treasure bringeth forth that which is evil; for out of the abundance of his heart his mouth speaketh.
46 “Kodi nʼchifukwa chiyani munditchula kuti, ‘Ambuye, Ambuye’ koma simuchita zimene Ine ndinena?
But why call ye me Lord, Lord, and do not the things which I say?
47 Ine ndidzakuonetsani mmene alili munthu amene amabwera kwa Ine ndi kumva mawu anga ndi kuwachita.
Every one that cometh to me and heareth my sayings and doeth them, I will show you whom he is like.
48 Iye ali ngati munthu womanga nyumba, amene anakumba mozama nayika maziko ake pa mwala. Madzi osefukira atabwera ndi mphamvu, nawomba nyumbayo koma sinagwedezeka, chifukwa anayimanga bwino.
He is like a man building a house, who dug deep, and laid its foundation on a rock; and when a flood arose, the stream dashed against that house, and could not shake it; because it was well built.
49 Koma amene amamva mawu anga koma osawachita, akufanana ndi munthu amene anamanga nyumba yake koma yopanda maziko. Nthawi yomwe madziwo anawomba nyumbayo, inagwa ndipo inawonongekeratu.”
But he that heareth and doeth not, is like a man that built a house upon the earth without a foundation; against which the stream dashed, and it fell at once, and the ruin of that house was great.

< Luka 6 >