< Luka 5 >

1 Tsiku lina Yesu anayima mʼmbali mwa nyanja ya Genesareti, gulu la anthu litamuzungulira likumvetsera mawu a Mulungu.
I stało się, gdy nań lud nalegał, aby słuchał słowa Bożego, że on stał podle jeziora Gienezaretskiego.
2 Iye anaona mabwato awiri ali mʼmphepete mwa nyanja, asodzi amene ankachapa makhoka awo atawasiya pamenepo.
I ujrzał dwie łodzi stojące przy jeziorze; ale rybitwi wyszedłszy z nich, płukali sieci.
3 Iye analowa mʼbwato limodzi limene linali la Simoni, ndi kumupempha kuti alikankhire mʼkati mwa nyanja pangʼono. Kenaka Iye anakhala pansi nayamba kuphunzitsa anthu ali mʼbwatomo.
A wstąpiwszy w jedną z tych łodzi, która była Szymonowa, prosił go, aby maluczko odjechał od brzegu; a usiadłszy, uczył on lud z onej łodzi.
4 Atatha kuyankhula anati kwa Simoni, “Kankhirani kwa kuya ndipo muponye makhoka kuti mugwire nsomba.”
A gdy przestał mówić, rzekł do Szymona: Zajedź na głębię, a zapuśćcie sieci wasze ku łowieniu.
5 Simoni anayankha kuti, “Ambuye, tagwira ntchito molimbika usiku wonse, koma sitinagwire kanthu. Koma pakuti mwatero, ndiponya makhoka.”
A odpowiadając Szymon, rzekł mu: Mistrzu! przez całą noc robiąc, niceśmy nie pojmali, wszakże na słowo twoje zapuszczę sieć.
6 Atachita izi, anagwira nsomba zambiri kotero kuti makhoka awo anayamba kungʼambika.
A gdy to uczynili, zagarnęli ryb mnóstwo wielkie, tak że się rwała sieć ich.
7 Choncho anakodola anzawo a bwato linalo kuti abwere ndi kuwathandiza, ndipo anabwera nadzaza mabwato onse awiri mpaka kuyamba kumira.
I skinęli na towarzysze, którzy byli w drugiej łodzi, aby przybywszy ratowali ich; i przybyli i napełnili obie łodzi, aż się zanurzały.
8 Simoni Petro ataona izi, anagwa pa mawondo a Yesu nati, “Chokani kwa ine Ambuye: Ine ndine munthu wochimwa!”
Co widząc Szymon Piotr, przypadł do kolan Jezusowych, mówiąc: Wynijdź ode mnie; bom jest człowiek grzeszny, Panie!
9 Iye ndi anzake onse anadabwa ndi nsomba zimene anagwira,
Albowiem go był strach ogarnął, i wszystkie, co z nim byli, z onego obłowu ryb, które byli zagarnęli.
10 chimodzimodzinso Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anzake a Simoniyo. Kenaka Yesu anati kwa Simoni, “Musachite mantha; kuyambira tsopano ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
Także i Jakóba i Jana, syny Zebedeuszowe, którzy byli towarzysze Szymonowi. I rzekł Jezus do Szymona: Nie bój się; od tego czasu ludzi łowić będziesz.
11 Kenaka anakokera mabwato awo ku mtunda, nasiya zonse namutsata Iye.
A oni wyciągnąwszy łódź na brzeg, wszystko opuściwszy, poszli za nim.
12 Yesu ali ku mudzi wina, munthu amene anali ndi khate thupi lonse anabwera kwa Iye. Munthuyo ataona Yesu, anagwa chafufumimba ndipo anamupempha Iye kuti, “Ambuye, ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
I stało się, gdy był w niektórem mieście, że oto był tam mąż pełen trądu, który ujrzawszy Jezusa, padł na twarz, i prosił go, mówiąc: Panie! jeźli chcesz, możesz mię oczyścić.
13 Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo. Iye anati, “Ine ndikufuna, yeretsedwa!” Ndipo nthawi yomweyo khate lake linachoka.
Tedy wyciągnąwszy Jezus rękę, dotknął się go, mówiąc: Chcę, bądź oczyszczony; i zaraz odszedł trąd od niego.
14 Kenaka Yesu anamulamula kuti, “Usawuze wina aliyense, koma pita, kadzionetse kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose anakulamulirani za kuyeretsedwa kwanu monga umboni kwa iwo.”
I przykazał mu, aby tego nikomu nie powiadał: ale rzekł: Idź, a ukaż się kapłanowi, i ofiaruj za oczyszczenie twoje, tak jako rozkazał Mojżesz, na świadectwo przeciwko nim.
15 Koma mbiri yake inafalikirabe kwambiri kotero kuti magulu a anthu anabwera kudzamvetsera ndi kuti achiritsidwe ku matenda awo.
I rozchodziła się tem więcej powieść o nim; i schodziły się mnóstwa wielkie, aby go słuchały i uzdrowieni byli od niego od niemocy swoich.
16 Koma Yesu nthawi zambiri ankachoka kupita ku malo a yekha kukapemphera.
Ale on odchodził na pustynią, i modlił się.
17 Tsiku lina pamene ankaphunzitsa, Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, amene anachokera ku midzi yonse ya Galileya ndi ku Yudeya ndi Yerusalemu, anakhala pansi pomwepo. Ndipo mphamvu ya Ambuye inalipo yakuti Iye achiritse odwala.
I stało się dnia niektórego, że on nauczał, a siedzieli też tam i Faryzeuszowie i nauczyciele Zakonu, którzy się byli zeszli ze wszystkich miasteczek Galilejskich i Judzkich, i z Jeruzalemu; a moc Pańska przytomna była uzdrawianiu ich.
18 Amuna ena anabwera atanyamula munthu wofa ziwalo pa mphasa ndipo anayesa kumulowetsa mʼnyumba kuti amugoneke pamaso pa Yesu.
A oto mężowie nieśli na łożu człowieka powietrzem ruszonego, i szukali, jakoby go wnieść i postawić przed nim.
19 Atalephera kupeza njira yochitira zimenezi chifukwa cha gulu la anthu, anakwera naye pa denga ali pa mphasa pomwepo ndi kumutsitsira mʼkati pakati pa gulu la anthu, patsogolo penipeni pa Yesu.
A gdy nie znaleźli, którędy by go wnieśli, dla ciżby, wstąpiwszy na dach, przez posowę spuścili go łożem w pośrodek przed Jezusa.
20 Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati, “Mnzanga, machimo ako akhululukidwa.”
Który ujrzawszy wiarę ich, rzekł mu: Człowiecze! odpuszczone są tobie grzechy twoje.
21 Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anayamba kuganiza mwa iwo okha kuti, “Kodi munthu uyu ndi ndani amene ayankhula zamwano? Kodi ndani amene angakhululukire machimo kupatula Mulungu?”
Tedy poczęli myślić nauczeni w Piśmie i Faryzeuszowie, mówiąc: Któż to jest, co mówi bluźnierstwa? Któż może odpuszczać grzechy, tylko sam Bóg.
22 Yesu anadziwa zomwe iwo amaganiza ndipo anafunsa kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukuganiza zimenezi mʼmitima mwanu?
Ale Jezus poznawszy myśli ich, odpowiadając rzekł do nich: Cóż myślicie w sercach waszych?
23 Kodi chapafupi ndi chiti: kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Nyamuka ndipo yenda?’”
Cóż jest łatwiejszego, rzec: Odpuszczone są tobie grzechy twoje, czyli rzec: Wstań a chodź?
24 Koma kuti inu mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo, Iye anati kwa munthu wofa ziwaloyo, “Ine ndikuwuza iwe kuti, ‘Imirira, nyamula mphasa ndipo uzipita kwanu.’”
Ale iżbyście wiedzieli, że Syn człowieczy ma moc na ziemi odpuszczać grzechy, (rzekł powietrzem ruszonemu: ) Tobie mówię: Wstań, a wziąwszy na się łoże swoje, idź do domu twego.
25 Nthawi yomweyo anayimirira patsogolo pawo, nanyamula mphasa yake ndipo anapita kwawo akuyamika Mulungu.
A on zarazem wstawszy przed nimi, wziąwszy na się to, na czem leżał, szedł do domu swego, wielbiąc Boga.
26 Aliyense anadabwa ndi kuchita mantha ndipo anayamika Mulungu. Iwo anadabwa kwambiri ndipo anati, “Lero taona zinthu zosayiwalika.”
I zdumieli się wszyscy, i chwalili Boga, i napełnieni byli bojaźnią, mówiąc: Widzieliśmy dziś dziwne rzeczy.
27 Zitatha izi, Yesu anachoka ndipo anaona wolandira msonkho dzina lake Levi atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anati kwa iye, “Nditsate Ine.”
A potem wyszedł i ujrzał celnika, imieniem Lewiego, siedzącego na cle, i rzekł mu: Pójdź za mną.
28 Ndipo Levi anayimirira, nasiya zonse ndi kumutsata Iye.
I opuścił wszystko, a wstawszy, szedł za nim.
29 Kenaka Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu ku nyumba yake ndipo gulu lalikulu la amisonkho ndi ena ankadya naye pamodzi.
I sprawił mu lewi ucztę wielką w domu swoim; a było wielkie zgromadzenie celników i innych, którzy z nim za stołem siedzieli.
30 Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amene anali a gulu lawo anadandaula kwa ophunzira ake, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukudya ndi kumwa pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
Tedy szemrali nauczeni w Piśmie i Faryzeuszowie, mówiąc do uczniów jego: Przecz z celnikami i z grzesznikami jecie i pijecie?
31 Yesu anawayankha kuti, “Amene sakudwala safuna singʼanga, koma odwala.
A Jezus odpowiadając, rzekł do nich: Nie potrzebująć zdrowi lekarza, ale ci, co się źle mają;
32 Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa kuti atembenuke mtima.”
Nie przyszedłem, wzywać sprawiedliwych, ale grzesznych do pokuty.
33 Iwo anati kwa Iye, “Ophunzira a Yohane amasala kudya ndi kupemphera kawirikawiri, monganso ophunzira a Afarisi, koma anu amangodya ndi kumwa.”
A oni mu rzekli: Przecz uczniowie Janowi często poszczą i modlą się, także i Faryzejscy, a twoi jedzą i piją?
34 Yesu anawayankha kuti, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya pamene mkwati ali pakati pawo?
A on im rzekł: Izali możecie uczynić, żeby synowie łożnicy małżeńskiej pościli, póki z nimi jest oblubieniec?
35 Koma nthawi ikubwera pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo. Masiku amenewo adzasala kudya.”
Lecz przyjdą dni, gdy oblubieniec odjęty będzie od nich; tedy w one dni pościć będą.
36 Iye anawawuza fanizo ili: “Palibe amene amangʼamba chigamba kuchokera pa chovala chatsopano ndi kuchisokerera pa chakale. Ngati atatero, ndiye kuti adzangʼamba chovala chatsopanocho, ndipo chigamba chochokera pa chovala chatsopano chija sichidzagwirizana ndi chakale.
Powiedział im też podobieństwo: Iż żaden łaty z szaty nowej nie przyprawia do szaty wiotchej; bo inaczej to, co jest nowego, drze wiotche, a do wiotchego nie zgadza się łata z nowego.
37 Ndipo palibe amene amakhuthulira vinyo watsopano mʼmatumba a vinyo akale. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa zikopazo, vinyo adzatayika ndipo zikopa za vinyozo zidzawonongeka.
I nikt nie leje wina nowego w stare statki; bo inaczej wino młode rozsadzi statki, i samo wyciecze, i statki się popsują.
38 Ayi, vinyo watsopano ayenera kuthiridwa mʼmatumba a vinyo azikopa zatsopano.
Ale młode wino ma być wlewane w statki nowe; a tak oboje bywają zachowane.
39 Ndipo palibe amene atamwa vinyo wakale amafuna watsopano, pakuti amati, ‘Wakale ndi okoma.’”
A nikt, kto się napił starego, nie zaraz chce młodego; ale mówi: Lepsze jest stare.

< Luka 5 >