< Luka 5 >

1 Tsiku lina Yesu anayima mʼmbali mwa nyanja ya Genesareti, gulu la anthu litamuzungulira likumvetsera mawu a Mulungu.
Now it came about that while the people came pushing to be near him, and to have knowledge of the word of God, he was by a wide stretch of water named Gennesaret;
2 Iye anaona mabwato awiri ali mʼmphepete mwa nyanja, asodzi amene ankachapa makhoka awo atawasiya pamenepo.
And he saw two boats by the edge of the water, but the fishermen had gone out of them and were washing their nets.
3 Iye analowa mʼbwato limodzi limene linali la Simoni, ndi kumupempha kuti alikankhire mʼkati mwa nyanja pangʼono. Kenaka Iye anakhala pansi nayamba kuphunzitsa anthu ali mʼbwatomo.
And he got into one of the boats, the property of Simon, and made a request to him to go a little way out from the land. And being seated he gave the people teaching from the boat.
4 Atatha kuyankhula anati kwa Simoni, “Kankhirani kwa kuya ndipo muponye makhoka kuti mugwire nsomba.”
And when his talk was ended, he said to Simon, Go out into deep water, and let down your nets for fish.
5 Simoni anayankha kuti, “Ambuye, tagwira ntchito molimbika usiku wonse, koma sitinagwire kanthu. Koma pakuti mwatero, ndiponya makhoka.”
And Simon, answering, said, Master, we were working all night and we took nothing: but at your word I will let down the nets.
6 Atachita izi, anagwira nsomba zambiri kotero kuti makhoka awo anayamba kungʼambika.
And when they had done this, they got such a great number of fish that it seemed as if their nets would be broken;
7 Choncho anakodola anzawo a bwato linalo kuti abwere ndi kuwathandiza, ndipo anabwera nadzaza mabwato onse awiri mpaka kuyamba kumira.
And they made signs to their friends in the other boat to come to their help. And they came, and the two boats were so full that they were going down.
8 Simoni Petro ataona izi, anagwa pa mawondo a Yesu nati, “Chokani kwa ine Ambuye: Ine ndine munthu wochimwa!”
But Simon, when he saw it, went down at the knees of Jesus and said, Go away from me, O Lord, for I am a sinner.
9 Iye ndi anzake onse anadabwa ndi nsomba zimene anagwira,
For he was full of wonder and so were all those who were with him, at the number of fish which they had taken;
10 chimodzimodzinso Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anzake a Simoniyo. Kenaka Yesu anati kwa Simoni, “Musachite mantha; kuyambira tsopano ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
And so were James and John, the sons of Zebedee, who were working with Simon. And Jesus said to Simon, Have no fear; from this time forward you will be a fisher of men.
11 Kenaka anakokera mabwato awo ku mtunda, nasiya zonse namutsata Iye.
And when they had got their boats to the land, they gave up everything and went after him.
12 Yesu ali ku mudzi wina, munthu amene anali ndi khate thupi lonse anabwera kwa Iye. Munthuyo ataona Yesu, anagwa chafufumimba ndipo anamupempha Iye kuti, “Ambuye, ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
And it came about that while he was in one of the towns, there was a leper there: and when he saw Jesus he went down on his face in prayer to him, saying, Lord, if it is your pleasure, you have power to make me clean.
13 Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo. Iye anati, “Ine ndikufuna, yeretsedwa!” Ndipo nthawi yomweyo khate lake linachoka.
And he put out his hand to him and said, It is my pleasure; be clean. And straight away his disease went from him.
14 Kenaka Yesu anamulamula kuti, “Usawuze wina aliyense, koma pita, kadzionetse kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose anakulamulirani za kuyeretsedwa kwanu monga umboni kwa iwo.”
And he gave him orders: Say nothing to any man, but let the priest see you and give an offering so that you may be made clean, as the law of Moses says, and for a witness to them.
15 Koma mbiri yake inafalikirabe kwambiri kotero kuti magulu a anthu anabwera kudzamvetsera ndi kuti achiritsidwe ku matenda awo.
But news of him went out all the more, in every direction, and great numbers of people came together to give hearing to his words and to be made well from their diseases.
16 Koma Yesu nthawi zambiri ankachoka kupita ku malo a yekha kukapemphera.
But he went away by himself to a waste place for prayer.
17 Tsiku lina pamene ankaphunzitsa, Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, amene anachokera ku midzi yonse ya Galileya ndi ku Yudeya ndi Yerusalemu, anakhala pansi pomwepo. Ndipo mphamvu ya Ambuye inalipo yakuti Iye achiritse odwala.
And it came about that on one of these days he was teaching; and some Pharisees and teachers of the law were seated there, who had come from every town of Galilee and Judaea and from Jerusalem; and the power of the Lord was with him, to make those who were ill free from their diseases.
18 Amuna ena anabwera atanyamula munthu wofa ziwalo pa mphasa ndipo anayesa kumulowetsa mʼnyumba kuti amugoneke pamaso pa Yesu.
And some men had with them, on a bed, a man who was ill, without power of moving; and they made attempts to get him in and put him before Jesus.
19 Atalephera kupeza njira yochitira zimenezi chifukwa cha gulu la anthu, anakwera naye pa denga ali pa mphasa pomwepo ndi kumutsitsira mʼkati pakati pa gulu la anthu, patsogolo penipeni pa Yesu.
And because of the mass of people, there was no way to get him in; so they went up on the top of the house and let him down through the roof, on his bed, into the middle in front of Jesus.
20 Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati, “Mnzanga, machimo ako akhululukidwa.”
And seeing their faith he said, Man, you have forgiveness for your sins.
21 Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anayamba kuganiza mwa iwo okha kuti, “Kodi munthu uyu ndi ndani amene ayankhula zamwano? Kodi ndani amene angakhululukire machimo kupatula Mulungu?”
And the scribes and Pharisees were having an argument, saying, Who is this, who has no respect for God? who is able to give forgiveness for sins, but God only?
22 Yesu anadziwa zomwe iwo amaganiza ndipo anafunsa kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukuganiza zimenezi mʼmitima mwanu?
But Jesus, who had knowledge of their thoughts, said to them, Why are you reasoning in your hearts?
23 Kodi chapafupi ndi chiti: kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Nyamuka ndipo yenda?’”
Which is the simpler: to say, You have forgiveness for your sins; or to say, Get up and go?
24 Koma kuti inu mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo, Iye anati kwa munthu wofa ziwaloyo, “Ine ndikuwuza iwe kuti, ‘Imirira, nyamula mphasa ndipo uzipita kwanu.’”
But so that you may see that on earth the Son of man has authority for the forgiveness of sins, (he said to the man who was ill, ) I say to you, Get up, and take up your bed, and go into your house.
25 Nthawi yomweyo anayimirira patsogolo pawo, nanyamula mphasa yake ndipo anapita kwawo akuyamika Mulungu.
And straight away he got up before them, and took up his bed and went away to his house giving praise to God.
26 Aliyense anadabwa ndi kuchita mantha ndipo anayamika Mulungu. Iwo anadabwa kwambiri ndipo anati, “Lero taona zinthu zosayiwalika.”
And wonder overcame them all, and they gave glory to God; and they were full of fear, saying, We have seen strange things today.
27 Zitatha izi, Yesu anachoka ndipo anaona wolandira msonkho dzina lake Levi atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anati kwa iye, “Nditsate Ine.”
And after these things he went out, and saw Levi, a tax-farmer, seated at the place where taxes were taken, and said to him, Come after me.
28 Ndipo Levi anayimirira, nasiya zonse ndi kumutsata Iye.
And giving up his business, he got up and went after him.
29 Kenaka Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu ku nyumba yake ndipo gulu lalikulu la amisonkho ndi ena ankadya naye pamodzi.
And Levi made a great feast for him in his house: and a great number of tax-farmers and others were seated at table with them.
30 Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amene anali a gulu lawo anadandaula kwa ophunzira ake, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukudya ndi kumwa pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
And the Pharisees and their scribes made protests against his disciples, saying, Why do you take food and drink with tax-farmers and sinners?
31 Yesu anawayankha kuti, “Amene sakudwala safuna singʼanga, koma odwala.
And Jesus, answering, said to them, Those who are well have no need of a medical man, but those who are ill.
32 Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa kuti atembenuke mtima.”
I have come, not to get the upright, but sinners, so that they may be turned from their sins.
33 Iwo anati kwa Iye, “Ophunzira a Yohane amasala kudya ndi kupemphera kawirikawiri, monganso ophunzira a Afarisi, koma anu amangodya ndi kumwa.”
And they said to him, The disciples of John frequently go without food, and make prayers, and so do the disciples of the Pharisees; but your disciples take food and drink.
34 Yesu anawayankha kuti, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya pamene mkwati ali pakati pawo?
And Jesus said, Are you able to make the friends of the newly-married man go without food when he is with them?
35 Koma nthawi ikubwera pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo. Masiku amenewo adzasala kudya.”
But the days will come when he will be taken away from them, and then they will go without food.
36 Iye anawawuza fanizo ili: “Palibe amene amangʼamba chigamba kuchokera pa chovala chatsopano ndi kuchisokerera pa chakale. Ngati atatero, ndiye kuti adzangʼamba chovala chatsopanocho, ndipo chigamba chochokera pa chovala chatsopano chija sichidzagwirizana ndi chakale.
And he said to them, in a story, No man takes a bit of cloth from a new coat and puts it on to an old coat, for so the new coat would be damaged and the bit from the new would not go well with the old.
37 Ndipo palibe amene amakhuthulira vinyo watsopano mʼmatumba a vinyo akale. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa zikopazo, vinyo adzatayika ndipo zikopa za vinyozo zidzawonongeka.
And no man puts new wine into old wine-skins, for fear that the skins will be burst by the new wine, and the wine be let out, and the skins come to destruction.
38 Ayi, vinyo watsopano ayenera kuthiridwa mʼmatumba a vinyo azikopa zatsopano.
But new wine has to be put into new wine-skins.
39 Ndipo palibe amene atamwa vinyo wakale amafuna watsopano, pakuti amati, ‘Wakale ndi okoma.’”
And no man, having had old wine, has any desire for new, for he says, The old is better.

< Luka 5 >