< Luka 4 >

1 Yesu, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anachoka ku mtsinje wa Yorodani ndipo anatsogozedwa ndi Mzimu Woyerayo kupita ku chipululu,
And, Jesus, full of Holy Spirit, returned from the Jordan, and was led in the Spirit in the desert,
2 kumene anayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anayi. Sanadye kena kalikonse pa masiku amenewo, ndipo pa mapeto pake anamva njala.
forty days, —being tempted by the adversary; and he did eat nothing in those days, —and, when they were concluded, he hungered.
3 Mdierekezi anati kwa Iye, “Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, uza mwala uwu kuti usanduke buledi.”
And the adversary said to him—If thou art God’s, Son, speak unto this stone; that it become bread.
4 Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha.’”
And Jesus made answer unto him—It is written: Not, on bread alone, shall, man, live.
5 Mdierekezi anamutengera Iye pamalo aatali ndipo mʼkamphindi namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi.
And, leading him up, he shewed him all the kingdoms of the inhabited earth, in a moment of time.
6 Ndipo anati kwa Iye, “Ndidzakupatsani ulamuliro ndi ulemerero wawo; pakuti anandipatsa ine, ndipo ndingathe kupereka kwa aliyense amene ndikufuna.
And the adversary said to him—Unto thee, will I give this authority, all together, and their glory; because, unto me, hath it been delivered up, and, to whomsoever I please, I give it:
7 Ngati mutandilambira, zonsezi zidzakhala zanu.”
Thou, therefore, if thou wilt worship before me, it shall all, be thine.
8 Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’”
And, answering, Jesus said to him—It is written: The Lord thy God, shalt thou worship, and, unto him alone, render divine service.
9 Mdierekezi anapita naye ku Yerusalemu namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu dziponyeni nokha pansi kuchokera pano.
And he led him into Jerusalem, and set him upon the pinnacle of the temple, —and said [to him]—If thou art God’s, Son, cast thyself, from hence, down;
10 Pakuti kwalembedwa, “Adzalamulira angelo ake za iwe kuti akutchinjirize mosamala;
for it is written—Unto his messengers, will he give command concerning thee, to keep vigilant watch over thee, —
11 ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.”
And, On hands, will they take thee up, lest once thou strike, against a stone, thy foot.
12 Yesu anayankha kuti, “Mawu akuti, ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’”
And Jesus, answering, said to him—It is said: Thou shalt not put to the test the Lord thy God.
13 Mdierekezi atamaliza mayesero awa onse, anamusiya Iye kufikira atapeza mpata wina.
And, having concluded every temptation, the adversary departed from him until a fitting season.
14 Yesu anabwerera ku Galileya mu mphamvu ya Mzimu Woyera, ndipo mbiri yake inafalikira ku madera onse a ku midzi.
And Jesus returned, in the power of the Spirit, into Galilee; and, a report, went out along the whole of the region, concerning him;
15 Iye ankaphunzitsa mʼmasunagoge awo, ndipo aliyense ankamulemekeza.
and, he, began teaching in their synagogues, being glorified by all.
16 Iye anapita ku Nazareti, kumene anakulira, ndipo pa tsiku la Sabata anakalowa mʼsunagoge, monga mwa chikhalidwe chake. Ndipo anayimirira kuti awerenge malemba.
And he came into Nazareth, where he had been brought up, and entered, according to his custom, on the sabbath day, into the synagogue, —and stood up to read.
17 Anamupatsa buku la mneneri Yesaya. Atalitsekula, anapeza pamalo pamene panalembedwa kuti,
And there was handed to him a scroll of the prophet Isaiah; and unfolding the scroll, he found the place where it was written:
18 “Mzimu wa Ambuye ali pa Ine; chifukwa wandidzoza kuti ndilalikire Uthenga Wabwino kwa osauka. Wandituma kuti ndilalikire kwa a mʼndende kuti amasulidwe ndi kwa osaona kuti apenyenso, kumasulidwa kwa osautsidwa,
The Spirit of the Lord, is upon me, because he hath anointed me—to tell glad tidings unto the destitute; He hath sent me forth, —To proclaim, to captives, a release, and, to the blind, a recovering of sight, —to send away the crushed, with a release;
19 ndi kulalikira za nthawi imene Ambuye adzakomere mtima anthu awo.”
To proclaim the welcome year of the Lord.
20 Kenaka Iye anatseka bukulo, nalibwezera kwa wotumikira ndipo anakakhala pansi. Maso a aliyense mʼsunagogemo anali pa Iye,
And, folding up the scroll, he handed it to the attendant, and sat down; and, the eyes of all, in the synagogue, were intently fixed upon him;
21 ndipo anawawuza kuti, “Lero malemba awa akwaniritsidwa mmene mwamveramu.”
and he began to be saying to them—This day, is fulfilled this scripture, in your ears.
22 Onse anayankhula zabwino za Iye ndipo anadabwa ndi mawu ogwira moyo amene anatuluka mʼkamwa mwake. Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu si mwana wa Yosefe?”
And, all, were bearing witness to him, and marvelling at the words of favour which were proceeding out of his mouth; and they were saying—Is not, this, the, son of Joseph?
23 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, mudzandiwuza mwambi uwu: Singʼanga, dzichiritse wekha! Chitanso mʼmudzi wa kwanu kuno zimene ife tamva kuti Iwe unazichita ku Kaperenawo.”
And he said unto them—By all means, ye will speak to me this similitude: Physician! heal, thyself, —Whatsoever things we have heard of coming to pass in Capernaum, do here also, in thine own country.
24 Iye anapitiriza kuti, “Zoonadi, ndikukuwuzani kuti palibe mneneri amene amavomerezedwa ku mudzi kwawo.
And he said—Verily, I say unto you, No prophet, is, welcome, in his own country,
25 Ine ndikukutsimikizirani kunali amayi ambiri amasiye mu Israeli mʼnthawi ya Eliya, kumwamba kutatsekedwa kwa zaka zitatu ndi theka ndipo kunali njala yayikulu mʼdziko lonselo.
And, of a truth, I say unto you—Many widows, were in the days of Elijah, in Israel, when the heaven was shut up three years and six months, when there came a great famine upon all the land;
26 Komabe Eliya sanatumidwe kwa mmodzi mwa iwo, koma kwa mkazi wamasiye wa ku Zerefati ku chigawo cha Sidoni.
And, unto none of them, was Elijah sent, save unto Sarepta of Sidonia, unto a woman that was a widow.
27 Ndipo kunali akhate ambiri ku Israeli mʼnthawi ya mneneri Elisa, koma panalibe mmodzi mwa iwo anachiritsidwa kupatula Naamani wa ku Siriya.”
And, many lepers, were in Israel, in the time of Elisha the prophet, and, not one of them, was cleansed, save Naaman the Syrian.
28 Anthu onse mʼsunagogemo anapsa mtima atamva izi.
And all were filled with wrath, in the synagogue, as they heard these things.
29 Anayimirira namutulutsira kunja kwa mzindawo, ndipo anamutengera pamwamba pa phiri pamene mzindawo unamangidwapo, ndi cholinga chakuti amuponyere ku phompho.
And, rising up, they thrust him forth outside the city, and led him as far as a brow of the hill on which their city was built, —so that they might throw him down headlong.
30 Koma Iye anangoyenda pakati pa gulu la anthulo nachokapo.
But, he, passing through the midst of them, went his way.
31 Kenaka Iye anapita ku Kaperenawo, mudzi wa ku Galileya, ndipo pa Sabata anayamba kuphunzitsa anthu.
And he came down into Capernaum, a city of Galilee. And he was teaching them on the sabbath;
32 Iwo anadabwa ndi chiphunzitso chake chifukwa uthenga wake unali ndi ulamuliro.
and they were being struck with astonishment at his teaching, because, with authority, was his word.
33 Mʼsunagogemo munali munthu wogwidwa ndi mzimu woyipa. Iye analira ndi mawu akulu, akuti
And, in the synagogue, was a man having a spirit of an impure demon; and he cried out with a loud voice—
34 “Aa! Kodi mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
Let be! What have we in common with thee, O Jesus, Nazarene! Hast thou come to destroy us? I know thee, who thou art, —The Holy One of God.
35 Yesu anachidzudzula kwambiri nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye.” Chiwandacho chinamugwetsa munthuyo pansi pamaso pa onse ndipo chinatuluka wosamupweteka.
And Jesus rebuked it, saying—Hold thy peace! and go forth from him. And the demon, throwing him into the midst, went forth from him, doing him no hurt.
36 Anthu onse anadabwa ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi chiphunzitso ichi ndi chotani? Ndi ulamuliro ndi mphamvu Iye akulamulira mizimu yoyipa ndipo ikutuluka!”
And amazement came upon all, and they began to converse one with another, saying—What is this word, that, with authority and power, he giveth orders unto the impure spirits, and they go forth?
37 Ndipo mbiri yake inafalikira madera onse ozungulira.
And a noise concerning him began to go out into every place of the country around.
38 Yesu anatuluka mʼsunagoge ndipo anapita kwa Simoni. Tsopano mpongozi wake wa Simoni amadwala malungo akulu, ndipo anamupempha Yesu kuti amuthandize.
And, rising up, from the synagogue, he went into the house of Simon. Now, the mother-in-law of Simon, was in distress with a great fever; and they made request to him concerning her.
39 Ndipo anawerama nadzudzula malungowo ndipo anamusiya. Anadzuka nthawi yomweyo nayamba kuwatumikira.
And, standing over her, he rebuked the fever, and it left her; and, instantly arising, she began to minister unto them.
40 Pamene dzuwa linkalowa, anthu anabweretsa kwa Yesu onse amene anali ndi matenda osiyanasiyana, ndipo atasanjika manja ake pa aliyense, anachiritsidwa.
But, as the sun was going in, they one and all, as many as had any sick with divers diseases, brought them unto him; and, he, upon each one of them laying, his hands, was curing them.
41 Komanso ziwanda zinkatuluka mwa anthu ambiri, zikufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” Koma Iye anazidzudzula ndipo sanazilole kuyankhula chifukwa zimadziwa kuti Iye ndi Khristu.
And demons also were going forth from many; crying aloud, and saying—Thou, art the Son of God. And, rebuking them, he suffered them not be talking; because they knew him to be, The Christ.
42 Kutacha, Yesu anapita ku malo a yekha. Anthu ankamufunafuna Iye ndipo pamene anafika kumene anali, anthuwo anayesetsa kumuletsa kuti asawachokere.
And, when it was day, going forth, he journeyed into a desert place; and, the multitudes, were seeking after him, and they came unto him, and would have detained him, that he might not depart from them.
43 Koma Iye anati, “Ine ndikuyenera kulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ku mizinda inanso chifukwa ichi ndi chimene ananditumira.”
But, he, said unto them—To the other cities also, I must needs tell the good-news of the kingdom of God, because, hereunto, was I sent forth.
44 Ndipo Iye anapitirirabe kulalikira mʼmasunagoge a ku Yudeya.
And he was proclaiming in the cities of Judaea.

< Luka 4 >