< Luka 3 >

1 Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
La quinzième année du règne de Tibère César, — Ponce Pilate étant gouverneur de la Judée, Hérode tétrarque de la Galilée, Philippe, son frère, tétrarque de l'Iturée et de la province de la Trachonite, et Lysanias tétrarque de l'Abylène,
2 Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
Anne et Caïphe étant souverains sacrificateurs, — la parole de Dieu fut adressée à Jean, fils de Zacharie, dans le désert.
3 Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
Alors Jean parcourut toute la contrée voisine du Jourdain, prêchant le baptême de la repentance, pour la rémission des péchés,
4 Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
ainsi qu'il est écrit dans le livre des paroles du prophète Ésaïe: «Une voix crie dans le désert: Préparez le chemin du Seigneur; aplanissez ses sentiers.
5 Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
Toute vallée sera comblée, toute montagne et toute colline seront abaissées; les chemins tortueux seront redressés, les chemins raboteux seront aplanis;
6 Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
et toute créature verra le salut de Dieu.»
7 Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
Il disait donc à la foule qui venait pour être baptisée par lui: Race de vipères, qui vous a appris à fuir la colère à venir?
8 Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
Produisez donc des fruits dignes d'une vraie repentance! Et n'allez pas dire en vous-mêmes: Nous avons Abraham pour père. Car je vous dis que, de ces pierres. Dieu peut faire naître des enfants à Abraham.
9 Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
Déjà la cognée est mise à la racine des arbres. Tout arbre qui ne produit pas de bons fruits va être coupé et jeté au feu.
10 Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
Alors la foule lui demanda: Que ferons-nous donc?
11 Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
Il leur répondit: Que celui qui a deux tuniques, en donne une à celui qui n'en a point; et que celui qui a de quoi manger agisse de même.
12 Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
Il vint aussi des péagers pour être baptisés; et ils lui dirent: Maître, que ferons-nous?
13 Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
Il leur répondit: N'exigez rien au delà de ce qui vous est ordonné.
14 Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
Des gens de guerre lui demandèrent aussi: Et nous, que ferons-nous? Il leur répondit: N'usez ni de violence ni de fraude envers personne; mais contentez-vous de votre solde.
15 Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
Comme le peuple était dans l'attente, et que tous se demandaient en leur coeur si Jean ne serait pas le Christ,
16 Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
Jean, prenant la parole, dit à tous: Pour moi, je vous baptise d'eau; mais il vient, celui qui est plus puissant que moi! Je ne suis pas digne de délier la courroie de ses chaussures; c'est lui qui vous baptisera d'Esprit saint et de feu.
17 Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
Il a son van dans sa main, il nettoiera parfaitement son aire et amassera le froment dans son grenier; mais il brûlera la paille au feu qui ne s'éteint point.
18 Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
Il adressait encore plusieurs autres exhortations au peuple, en lui annonçant la bonne nouvelle.
19 Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
Mais Hérode le tétrarque, étant repris par Jean au sujet d'Hérodias, femme de son frère, et au sujet de tous les crimes qu'il avait commis,
20 Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
ajouta encore à tous les autres celui de faire mettre Jean en prison.
21 Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
Or, comme tout le peuple se faisait baptiser, Jésus se fit baptiser, lui aussi. Pendant qu'il priait, le ciel s'ouvrit,
22 Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
et le Saint-Esprit descendit sur lui, sous une forme corporelle, comme une colombe; et il vint du ciel une voix qui dit: Tu es mon Fils bien-aimé, en qui j'ai mis toute mon affection!
23 Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
Jésus avait environ trente ans, lorsqu'il commença son ministère. Il était, à ce que l'on croyait, fils de Joseph, fils d'Héli,
24 mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
fils de Matthat, fils de Lévi, fils de Melchi, fils de Janné, fils de Joseph,
25 mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
fils de Mattathias, fils d'Amos, fils de Nahum, fils d'Esli, fils de Naggé,
26 mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
fils de Maath, fils de Mattathias, fils de Siméin, fils de Josech, fils de Joda,
27 mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
fils de Joanan, fils de Rhésa, fils de Zorobabel, fils de Salathiel, fils de Néri,
28 mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
fils de Melchi, fils d'Addi, fils de Cosam, fils d'Elmadam, fils d'Er,
29 mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
fils de Jésus, fils d'Éliézer, fils de Jorim, fils de Matthat, fils de Lévi,
30 mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
fils de Siméon, fils de Juda, fils de Joseph, fils de Jonam, fils d'Éliakim,
31 mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
fils de Méléa, fils de Menna, fils de Mattatha, fils de Nathan, fils de David,
32 mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
fils de Jessé, fils de Jobed, fils de Booz, fils de Sala, fils de Naasson,
33 mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
fils d'Aminadab, fils d'Admin, fils d'Arni, fils d'Esrom, fils de Pharez, fils de Juda,
34 mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
fils de Jacob, fils d'Isaac, fils d'Abraham, fils de Thara, fils de Nachor,
35 mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
fils de Séruch, fils de Ragaù, fils de Phalek, fils de Héber, fils de Sala,
36 mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
fils de Caïnam, fils d'Arphaxad, fils de Sem, fils de Noé, fils de Lamech,
37 mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
fils de Mathusala, fils d'Hénoch, fils de Jared, fils de Maléléel, fils de Caïnam,
38 mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.
fils d'Énos, fils de Seth, fils d'Adam, fils de Dieu.

< Luka 3 >