< Luka 3 >

1 Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
En l'an quinze du règne de Tibère César, — Ponce-Pilate étant procurateur de la Judée, — Hérode, tétrarque de la Galilée, —Philippe, son frère, tétrarque de l'Iturée et des terres de la Trachonite, — Lysanias, tétrarque de l'Abilène, —
2 Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
sous le pontificat de Banne et de Kaïphe, la parole de Dieu fut adressée à Jean, fils de Zaccharie, dans le désert.
3 Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
Et Jean s'en alla dans toute la région du Jourdain, prêchant un baptême de repentance pour la rémission des péchés,
4 Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
ainsi que cela est écrit au livre des paroles du prophète Ésaïe: «Une voix crie dans le désert: Préparez la voie du Seigneur, Aplanissez ses sentiers;
5 Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
Toute vallée sera comblée; Toute montagne et toute colline seront abaissées; Les voies tortueuses seront changées en droits chemins; Et les voies rocailleuses en routes unies;
6 Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
Et toute chair verra le salut de Dieu»
7 Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
Aux foules qui accouraient pour être baptisées par lui, il disait: «Engeance de vipères, qui vous a appris à fuir la colère à venir?
8 Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
Produisez donc des fruits dignes de la repentance, et n'allez pas dire en vous-mêmes: Nous avons pour père Abraham; car je vous le dis, Dieu peut faire surgir, des pierres que voici, des enfants à Abraham.
9 Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
Déjà la cognée touche la racine des arbres. Tout arbre donc qui ne produit pas de bon fruit, sera coupé et jeté au feu.» —
10 Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
«Qu'avons-nous à faire?» lui demandèrent alors les multitudes.
11 Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
Il leur répondit par ces paroles: «Que celui qui possède deux tuniques en donne une à celui qui n'en a pas et que celui qui a des aliments pour se nourrir fasse de même.»
12 Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
Des publicains vinrent pour être baptisés et lui dirent aussi: «Maître, qu'avons-nous à faire?» —
13 Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
«N'exigez rien de plus, leur répondit-il, que ce qui vous a été prescrit.»
14 Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
Des soldats aussi le questionnèrent: «Et nous, qu'avons-nous à faire?» A eux il dit: «Ne faites violence à personne; ne faites tort à personne; contentez-vous de votre paye.»
15 Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
Le peuple était en suspens; et chacun se demandait, dans le secret de son coeur, si Jean n'était pas peut-être le Christ.
16 Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
Pour répondre à tous, Jean dit: «Moi, je vous baptise d'eau; mais il va venir celui qui est plus puissant que moi; je ne suis pas même digne de délier la courroie de ses sandales; lui, vous baptisera avec l'Esprit saint et le feu.
17 Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
Il a le van dans la main pour nettoyer son aire et rassembler le froment dans son grenier; mais la paille il la brûlera au feu inextinguible.»
18 Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
C'est ainsi qu'il annonçait la Bonne Nouvelle au peuples par des exhortations nombreuses et variées.
19 Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
Le tétrarque Hérode, cependant, ayant été repris par lui tant au sujet d'Hérodiade, femme de son frère, qu'au sujet des mille crimes qu'il avait commis,
20 Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
ajouta encore celui-ci à tous les autres: il fit jeter Jean en prison.
21 Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
Or tout le peuple ayant reçu le baptême, et Jésus aussi ayant été baptisé, il advint que le ciel s'ouvrit, pendant qu'il priait,
22 Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
et que l'Esprit saint descendit sur lui sous une forme corporelle, sous la figure d'une colombe; et une voix vint du ciel: «Tu es mon Fils bien-aimé, en toi je me complais.»
23 Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
Jésus, en ce commencement, avait environ trente ans et passait pour être le fils de Joseph, Fils d'Héli,
24 mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
Fils de Maththath, Fils de Lévi, Fils de Melchi, Fils de Jannaï, Fils de Joseph,
25 mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
Fils de Mattathias, Fils d'Amos, Fils de Naoum, Fils d'Eslei, Fils de Nangaï,
26 mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
Fils de Maath, Fils de Mattathias, Fils de Semeein, Fils de Josech, Fils de Joda,
27 mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
Fils de Joanan, Fils de Rèsa, Fils de Zorobabel, Fils de Salathiel, Fils de Nèrei,
28 mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
Fils de Melchei, Fils d'Addei, Fils de Kosam, Fils de Elmadam, Fils de Hèr,
29 mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
Fils de Jésus, Fils d'Éliézer, Fils de Jorem, Fils de Maththath, Fils de Lévi,
30 mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
Fils de Siméon, Fils de Judas, Fils de Joseph, Fils de Jonam, Fils d'Éliakim, Fils de Méléa,
31 mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
Fils de Menna, Fils de Mattatha, Fils de Natham, Fils de David,
32 mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
Fils de Jessaï, Fils de Jobed, Fils de Boos, Fils de Sala, Fils de Naasson,
33 mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
Fils d'Aminadab, Fils d'Admein, Fils d'Ami, Fils d'Esrom, Fils de Pharès, Fils de Judas,
34 mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
Fils de Jacob, Fils d'Isaac, Fils d'Abraham, Fils de Unira, Fils de Nachor, Fils de Serouch,
35 mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
Fils de Ragau, Fils de Phalek, Fils de Eber, Fils de Sala,
36 mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
Fils de Kainam, Fils d'Arphaxad, Fils de Sein, Fils de Noé, Fils de Lamech,
37 mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
Fils de Mathousalem. Fils d'Enoch, Fils de Jaret, Fils de Meleleèl, Fils de Kainam
38 mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.
Fils d'Enos, Fils de Seth, Fils d'Adam, Fils de Dieu.

< Luka 3 >