< Luka 3 >

1 Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
In the fiftenthe yeer of the empire of Tiberie, the emperoure, whanne Pilat of Pounce gouernede Judee, and Eroude was prince of Galilee, and Filip, his brothir, was prince of Iturye, and of the cuntre of Tracon, and Lisanye was prince of Abilyn,
2 Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
vndir the princis of prestis Annas and Caifas, the word of the Lord was maad on Joon, the sone of Zacarie, in desert.
3 Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
And he cam in to al the cuntre of Jordan, and prechide baptym of penaunce in to remyssioun of synnes.
4 Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
As it is wrytun in the book of the wordis of Isaye, the prophete, The voice of a crier in desert, Make ye redi the weie of the Lord, make ye hise pathis riyt.
5 Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
Ech valey schal be fulfillid, and euery hil and litil hil schal be maad lowe; and schrewid thingis schulen ben in to dressid thingis, and scharp thingis in to pleyn weies;
6 Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
and euery fleisch schal se the heelthe of God.
7 Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
Therfor he seid to the puple, which wente out to be baptisid of hym, Kyndlyngis of eddris, who schewide to you to fle fro the wraththe to comynge?
8 Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
Therfor do ye worthi fruytis of penaunce, and bigynne ye not to seie, We han a fadir Abraham; for Y seie to you, that God is myyti to reise of these stoonys the sones of Abraham.
9 Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
And now an axe is sett to the roote of the tree; and therfor euery tre that makith no good fruyt, schal be kit doun, and schal be cast in to the fier.
10 Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
And the puple axide hym, and seiden, What thanne schulen we do?
11 Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
He answeride, and seide to hem, He that hath twei cootis, yyue to hym that hath noon; and he that hath metis, do in lijk maner.
12 Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
And pupplicans camen to be baptisid; and thei seiden to hym, Maister, what schulen we do?
13 Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
And he seide to hem, Do ye no thing more, than that that is ordeyned to you.
14 Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
And knyytis axiden hym, and seiden, What schulen also we do? And he seide to hem, Smyte ye wrongfuli no man, nethir make ye fals chalenge, and be ye apayed with youre sowdis.
15 Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
Whanne al the puple gesside, and alle men thouyten in her hertis of Joon, lest perauenture he were Crist,
16 Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
Joon answeride, and seide to alle men, Y baptize you in watir; but a stronger than Y schal come aftir me, of whom Y am not worthi to vnbynde the lace of his schoon; he schal baptize you in the Hooli Goost and fier.
17 Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
Whos `wynewyng tool in his hond, and he schal purge his floor of corn, and schal gadere the whete in to his berne; but the chaffis he schal brenne with fier vnquenchable.
18 Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
And many othere thingis also he spak, and prechide to the puple. But Eroude tetrark, whanne he was blamed of Joon for Erodias,
19 Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
the wijf of his brother, and for alle the yuelis that Eroude dide,
20 Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
encreside this ouer alle, and schitte Joon in prisoun.
21 Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
And it was don, whanne al the puple was baptised, and whanne Jhesu was baptised, and preiede, heuene was openyd.
22 Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
And the Hooli Goost cam doun in bodili licnesse, as a dowue on hym; and a vois was maad fro heuene, Thou art my derworth sone, in thee it hath plesid to me.
23 Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
And Jhesu hym silf was bigynninge as of thritti yeer, that he was gessid the sone of Joseph, which was of Heli,
24 mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
which was of Mathath, which was of Leuy, which was of Melchi, that was of Jamne,
25 mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
that was of Joseph, that was of Matatie, that was of Amos, that was of Naum, that was of Hely, that was of Nagge,
26 mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
that was of Mathath, that was of Matatie, that was of Semei, that was of Joseph, that was of Juda, that was of Johanna,
27 mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
that was of Resa, that was of Zorobabel, that was of Salatiel,
28 mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
that was of Neri, that was of Melchi, that was of Addi, that was of Cosan, that was of Elmadan, that was of Her,
29 mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
that was of Jhesu, that was of Eleasar, that was of Jorum, that was of Matath,
30 mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
that was of Leuy, that was of Symeon, that was of Juda, that was of Joseph, that was of Jona, that was of Eliachym,
31 mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
that was of Melca, that was of Menna, that of Mathatha, that was of Nathan,
32 mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
that was of Dauid, that was of Jesse, that was of Obeth, that was of Boz, that was of Salmon, that was of Nason,
33 mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
that was of Amynadab, that was of Aram, that was of Esrom, that was of Fares,
34 mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
that was of Judas, that was of Jacob, that was of Isaac, that was of Abraham, that was of Tare, that was of Nachor,
35 mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
that was of Seruth, that was of Ragau, that was of Faleth, that was of Heber,
36 mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
that was of Sale, that was of Chaynan, that was of Arfaxath, that was of Sem, that was of Noe, that was of Lameth,
37 mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
that was of Matussale, that was of Enok, that was of Jareth, that was of Malaliel, that was of Cainan, that was of Enos,
38 mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.
that was of Seth, that was of Adam, that was of God.

< Luka 3 >