< Luka 3 >

1 Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
Now in the fifteenth year of the reign of Tiberius Caesar, Pontius Pilate being Governor of Judaea, Herod Tetrarch of Galilee, his brother Philip Tetrarch of Ituraea and Trachonitis, and Lysanias Tetrarch of Abilene,
2 Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
during the High-priesthood of Annas and Caiaphas, a message from God came to John, the son of Zechariah, in the Desert.
3 Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
John went into all the district about the Jordan proclaiming a baptism of the penitent for the forgiveness of sins;
4 Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
as it is written in the book of the prophet Isaiah, "The voice of one crying aloud! 'In the Desert prepare ye a road for the Lord: make His highway straight.
5 Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
Every ravine shall be filled up, and every mountain and hill levelled down, the crooked places shall be turned into straight roads, and the rugged ways into smooth;
6 Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
and then shall all mankind see God's salvation.'"
7 Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
Accordingly John used to say to the crowds who came out to be baptized by him, "O vipers' brood, who has warned you to flee from the coming wrath?
8 Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
Live lives which shall prove your change of heart; and do not begin to say to yourselves, 'We have Abraham as our forefather,' for I tell you that God can raise up descendants for Abraham from these stones.
9 Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
And even now the axe is lying at the root of the trees, so that every tree which fails to yield good fruit will quickly be hewn down and thrown into the fire."
10 Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
The crowds repeatedly asked him, "What then are we to do?"
11 Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
"Let the man who has two coats," he answered, "give one to the man who has none; and let the man who has food share it with others."
12 Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
There came also a party of tax-gatherers to be baptized, and they asked him, "Rabbi, what are we to do?"
13 Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
"Do not exact more than the legal amount," he replied.
14 Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
The soldiers also once and again inquired of him, "And we, what are we to do?" His answer was, "Neither intimidate any one nor lay false charges; and be content with your pay."
15 Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
And while the people were in suspense and all were debating in their minds whether John might possibly be the Anointed One,
16 Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
he answered the question by saying to them all, "As for me, I am baptizing you with water, but One mightier than I is coming, whose very sandal-strap I am not worthy to unfasten: He will baptize you in the Holy Spirit and with fire.
17 Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
His winnowing-shovel is in His hand to clear out His threshing-floor, and to gather the wheat into His storehouse; but the chaff He will burn up in fire unquenchable."
18 Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
With many exhortations besides these he declared the Good News to the people.
19 Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
But Herod the Tetrarch, being repeatedly rebuked by him about Herodias his brother's wife, and about all the wicked deeds that he had done,
20 Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
now added this to crown all the rest, that he threw John into prison.
21 Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
Now when all the people had been baptized, and Jesus also had been baptized and was praying, the sky opened,
22 Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
and the Holy Spirit came down in bodily shape, like a dove, upon Him, and a voice came from Heaven, which said, "Thou art My Son, dearly loved: in Thee is My delight."
23 Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
And He--Jesus--when He began His ministry, was about thirty years old. He was the son (it was supposed) of Joseph, son of Heli,
24 mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
son of Matthat, son of Levi, son of Melchi, son of Jannai, son of Joseph,
25 mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
son of Mattathias, son of Amos, son of Nahum, son of Esli, son of Naggai,
26 mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
son of Mahath, son of Mattathias, son of Semein, son of Josech, son of Joda,
27 mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
son of Johanan, son of Resa, son of Zerubbabel, son of Shealtiel, son of Neri,
28 mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
son of Melchi, son of Addi, son of Cosam, son of Elmadam, son of Er,
29 mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
son of Joshua, son of Eliezar, son of Jorim, son of Maththat, son of Levi,
30 mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
son of Symeon, son of Judah, son of Joseph, son of Jonam, son of Eliakim, son of
31 mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
Melea, son of Menna, son of Mattatha, son of Nathan, son of David,
32 mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
son of Jesse, son of Obed, son of Boaz, son of Salmon, son of Nahshon,
33 mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
son of Amminadab, son of Admin, son of Arni, son of Hezron, son of Perez, son of Judah,
34 mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
son of Jacob, son of Isaac, son of Abraham, son of Terah, son of Nahor,
35 mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
son of Serug, son of Reu, son of Peleg, son of Eber, son of Shelah,
36 mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
son of Cainan, son of Arpachshad, son of Shem, son of Noah, son of Lamech,
37 mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
son of Methuselah, son of Enoch, son of Jared, son of Mahalalel, son of Kenan,
38 mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.
son of Enosh, son of Seth, son of Adam, son of God.

< Luka 3 >