< Luka 22 >

1 Phwando la buledi wopanda yisiti lotchedwa Paska litayandikira,
Avela ine paše o Prazniko e bikvascone marengoro, savo vičini pe Pasha.
2 akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo amafunafuna mpata woti amuphere Yesu, pakuti ankachita mantha ndi anthu.
O šerutne sveštenici hem o učitelja e Zakonestar rodena ine sar te ćeren o Isus te ovel mudardo, ali darandile e narodostar.
3 Kenaka Satana analowa mwa Yudasi, wotchedwa Isikarioti, mmodzi wa khumi ndi a iwiriwo.
Tegani o Sotoni đerdinđa ano Juda vičime Iskariot kova inele jekh oto dešuduj apostolja e Isusesere.
4 Ndipo Yudasi anapita kwa akulu a ansembe ndi akulu oyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndi kukambirana nawo za mmene iye angaperekere Yesu.
Ov dželo koro šerutne sveštenici hem koro narednici e hramesere stražakere hem dogovorinđa pe olencar sar te predel lenđe e Isuse.
5 Iwo anakondwa ndipo anagwirizana zomupatsa ndalama.
On ule radosna hem phende e Judase da ka den le love.
6 Iye anavomera, ndipo anayamba kufunafuna mpata wabwino wakuti amupereke Yesu kwa iwo pamene panalibe gulu la anthu pafupi.
I ov pristaninđa. I ađahar lelja te rodel šukar prilika te izdajini e Isuse kad naka ovel narodo uzalo leste.
7 Kenaka linafika tsiku la buledi wopanda yisiti pamene mwana wankhosa wa Paska amaperekedwa nsembe.
Kad alo o prvo dive oto Prazniko e bikvascone marengoro, ko savo valjanđa te žrtvujini pe bakrore zaki Pasha,
8 Yesu anatuma Petro ndi Yohane nati, “Pitani kukatikonzera Paska kuti tikadye.”
o Isus phenđa e Petrese hem e Jovanese: “Džan hem ćeren amenđe te ha e pashakoro hajba.”
9 Iwo anafunsa kuti, “Kodi mukufuna tikakonzere kuti?”
A on phende lese: “Kaj mangeja te ćera le?”
10 Iye anayankha kuti, “Taonani, mukamalowa mu mzinda, mudzakumana ndi mwamuna atanyamula mtsuko wamadzi. Mulondoleni ku nyumba imene akalowe,
Ov phenđa lenđe: “Šunen. So ka đerdinen ki diz, ka resel tumen jekh manuš kova akhari pani ano khoro. Džan palo leste. Ko čher ko savo ka đerdini
11 ndipo mukamuwuze mwini nyumbayo kuti, ‘Aphunzitsi kufunsa kuti, chili kuti chipinda cha alendo, kumene Ine ndi ophunzira anga tikadyere Paska?’
roden e čherutne hem vaćeren lese: ‘O učitelj pučela ki savi soba šaj te hal e pashakoro hajba ple učenikonencar?’
12 Iyeyo adzakuonetsani chipinda chachikulu chapamwamba, chokhala ndi zonse. Kachiteni zokonzekera mʼmenemo.”
I ov ka mothoj tumenđe i bari upruni soba savi već pripremime. Adari ćeren amenđe zako hajba.”
13 Iwo anapita nakapeza zinthu monga mmene Yesu anawawuzira. Tsono anakonza Paska.
I on džele hem arakhle sa ađahar sar so phenđa lenđe o Isus i adari ćerde zako hajba e pashakoro.
14 Ora litakwana, Yesu ndi ophunzira ake anakhala pa tebulo.
I kad alo o vreme, o Isus čhivđa pe uzalo astali ple apostolencar.
15 Ndipo Iye anawawuza kuti, “Ine ndakhala ndikuyembekezera kudya Paska uyu ndi inu ndisanamve zowawa.
I phenđa lenđe: “Edobor mangljum te hav akaja Pasha tumencar angleder so ka patinav.
16 Pakuti Ine ndikukuwuzani kuti sindidzadyanso Paska wina mpaka Paskayi itakwaniritsidwa mu ufumu wa Mulungu.”
Adalese so, vaćerava tumenđe, naka hav la više đikote lakoro čačimasoro značenje na pherđola ano carstvo e Devlesoro.”
17 Atanyamula chikho, Iye anayamika ndipo anati, “Tengani ndipo patsiranani pakati panu.
Tegani lelja i čaša e moljaja, zahvalinđa e Devlese hem phenđa e apostolenđe: “Len akaja mol hem podelinen la maškara tumende.
18 Pakuti ndikukuwuzani kuti, Ine sindidzamwanso zochokera ku chipatso cha mphesa mpaka ufumu wa Mulungu utabwera.”
Adalese so, vaćerava tumenđe, naka pijav više mol đikote o carstvo e Devlesoro na avela.”
19 Ndipo Iye anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema, nagawira iwo nati, “Ili ndi thupi langa lomwe laperekedwa kwa inu; muzichita zimenezi pokumbukira Ine.”
I lelja o maro, zahvalinđa e Devlese, phaglja le hem dinđa le e apostolenđe vaćerindoj: “Akavai mlo telo savo dela pe zako tumenđe. Ćeren akava te setinen tumen mandar.”
20 Chimodzimodzinso, utatha mgonero, anatenga chikho nati, “Chikho ichi ndi pangano latsopano la magazi anga, amene akhetsedwa chifukwa cha inu.
Ađahar lelja hem i čaša e moljaja palo hajba, vaćerindoj: “Akaja čaša e moljaja nevoi savez ano mlo rat savo čhorela pe tumenđe.
21 Koma dzanja la amene akundipereka Ine lili pamodzi ndi langa pa chakudya pano.
Ali ače, o manuš kova ka izdajini man mancari uzalo astali.
22 Mwana wa Munthu apita monga mmene zinalembedwera, koma tsoka kwa munthu amene amupereka Iye.”
Adalese so, me, o Čhavo e manušesoro, valjani te merav sar soi odredime, ali jao okole manušese kova ka izdajini man!”
23 Iwo anayamba kufunsana pakati pawo kuti ndi ndani wa iwo amene akanachita ichi.
I o apostolja lelje te pučen pe maškara pumende kova olendar šaj te ovel adava so ka ćerel ađahar nešto.
24 Komanso mkangano unabuka pakati pawo kuti ndani mwa iwo amene amaganiziridwa kukhala wamkulu.
I o učenici lelje te raspravinen pe kovai olendar najbaro.
25 Yesu anawawuza kuti, “Mafumu a anthu a mitundu ina amaonetsa mphamvu za ufumu wawo pa anthuwo; ndipo amene ali ndi ulamuliro, amapatsidwa dzina la kuti ‘Opindula.’
A o Isus phenđa lenđe: “Avere nacijengere carija vladinena upro lende hem o vladarija lengere pumen vičinena ‘manuša kola ćerena šukaripe’.
26 Koma inu simuyenera kukhala choncho. Mʼmalo mwake, wamkulu pakati panu akhale ngati wamngʼono pa onse, ndipo iye amene alamulira akhale ngati wotumikira.
Ali tumen ma oven esavke! Nego, o najbaro maškar tumende nek ovel sar najtikoro, a o vođa nek ovel sar sluga.
27 Pakuti wamkulu ndani, iye amene ali pa tebulo kapena iye amene akutumikira? Kodi si iye amene ali pa tebulo? Koma ndili pakati panu ngati mmodzi wokutumikirani.
A kovai po baro? Okova kovai uzalo astali ili okova kova kandela le? Ini okova kovai uzalo astali? A me maškara tumende injum sar okova kova kandela.
28 Inu ndinu amene mwayima nane mʼmayesero.
Tumen injen adala kola ačhile mancar ano mle iskušenja.
29 Ndipo Ine ndikupatsani inu ufumu, monga momwe Atate anga anandipatsiranso Ine,
I me dava tumen te vladinen ano carstvo, sar so mlo Dad dinđa man:
30 kuti inu muthe kudya ndi kumwa pa tebulo langa mu ufumu wanga ndi kukhala pa mipando yaufumu kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israeli.”
te han hem te pijen maje uzalo astali ano carstvo mlo, hem te bešen ko tronja te sudinen upro dešuduj plemija e Izraelesere.”
31 “Simoni, Simoni, Satana wapempha kuti akupete ngati tirigu.
O Isus phenđa: “Simone, Simone, ače o Sotoni rodinđa e Devlestar te mukel lese te iskušini tumen sar kad neko čhorela o điv maškari sita.
32 Koma Ine ndakupempherera Simoni, kuti chikhulupiriro chako chisafowoke ndipo pamene udzabwerera kwa Ine, udzalimbikitse abale ako.”
Ali me molinđum tuće te na našale ti vera. Adalese, kad palem ka irine tut mande, zorjar te phraljen.”
33 Koma iye anayankha kuti, “Ambuye, ndine wokonzeka kupita nanu ku ndende ndi kufa komwe.”
A ov phenđa lese: “Gospode, injum spremno te džav tuja hem ko phandlipe hem ko meriba.”
34 Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuza Petro, tambala asanalire lero lino, udzandikana katatu kuti sukundidziwa Ine.”
A o Isus phenđa: “Vaćerava će, Petre, o bašno naka đilabi avdive đikote trin puti naka hovave da na pendžareja man.”
35 Kenaka Yesu anawafunsa iwo kuti, “Ine nditakutumizani wopanda chikwama cha ndalama, thumba kapena nsapato, kodi inu munasowa kanthu?” Iwo anayankha kuti, “Palibe chimene tinasowa.”
I phenđa e apostolenđe: “Kad bičhalđum tumen ko drom bizo kese lovencar, bizo torbe hem bizi buderi obuća, na li falinđa tumenđe nešto?” A on phende: “Ništa.”
36 Iye anawawuza kuti, “Koma tsopano ngati muli ndi chikwama cha ndalama, chitengeni, ndiponso thumba. Ndipo ngati mulibe lupanga, gulitsani mkanjo wanu ndi kugula.
Tegani o Isus phenđa lenđe: “Ali akana kas isi kesa e lovencar, nek lel la! Ađahar hem i torba! A kas nane mači, nek biknel plo ogrtači hem nek činelfse jekh.
37 Zalembedwa kuti, ‘Ndipo Iye anawerengedwa pamodzi ndi anthu ochimwa,’ ndipo Ine ndikuwuzani kuti izi ziyenera kukwaniritsidwa mwa Ine. Inde, zimene zinalembedwa za Ine, zikukwaniritsidwa.”
Adalese so, vaćerava tumenđe, valjani te pherđol adava soi mandar pisime ko Sveto lil: ‘Dikhle le sar jekhe okolendar kola phagena o zakoni.’ Čače, pherđola sa soi pisime mandar.”
38 Ophunzira anati, “Taonani Ambuye, awa malupanga awiri.” Iye anayankha kuti, “Amenewa akwanira.”
A on phende: “Gospode, ače isi amen duj mačija!” A ov phenđa: “Šukari!”
39 Yesu anapitanso monga mwa masiku onse ku Phiri la Olivi, ndipo ophunzira ake anamutsatira Iye.
I iklindoj adathar, palo plo adeti, dželo ki E maslinakiri gora. Oleja džele hem lesere učenici.
40 Atafika pamalopo, Iye anawawuza kuti, “Pempherani kuti musagwe mʼmayesero.”
I kad resle adari, phenđa lenđe: “Molinen tumen te na peren ko iskušenje!”
41 Iye anapita patsogolo pangʼono patali ngati kuponya mwala, anagwada napephera kuti,
I cidinđa pe dur olendar, edobor kobor šaj te frdel pe o bar, pelo ko kočija hem molinđa pe e Devlese,
42 “Atate ngati mukufuna chotsereni chikho ichi. Komatu muchite zimene mukufuna osati zimene ndikufuna ine.”
vaćerindoj: “Dade! Te mangeja, cide akaja čaša e patnjaja mandar, te na pijav olatar. Ali, nek ovel pali ti volja, a na pali mli.”
43 Mngelo wochokera kumwamba anafika namulimbikitsa.
Tegani o anđeo mothovđa pe lese taro nebo hem hrabrinđa le.
44 Ndipo mopsinjika mtima, anapemphera moona mtima, ndipo thukuta lake linali ngati madontho a magazi akugwera pansi.
A kad inele ani po bari patnja, po zorale molinđa pe. Lesoro znoj ulo sar kapke oto rat save perena ine upri phuv.
45 Iye atamaliza kupemphera, ndi kubwerera kwa ophunzira ake, anawapeza atagona atafowoka ndi chisoni.
I pali molitva uštino, alo đi ple učenici hem arakhlja len sar sovena adalese so inele umorna taro tugujiba.
46 Iye anafunsa kuti, Nʼchifukwa chiyani mukugona? “Dzukani ndipo pempherani kuti inu musagwe mʼmayesero.”
Tegani phenđa lenđe: “Sose sovena? Ušten hem molinen tumen te na peren ko iskušenje!”
47 Pamene Iye ankayankhulabe, gulu la anthu linabwera, ndipo munthu wotchedwa Yudasi, mmodzi wa khumi ndi awiriwo analitsogolera. Iye anamuyandikira Yesu kuti amupsompsone.
Sar pana o Isus vaćeri ine adava, ale nakoro leste but manuša kolen anđa o Juda kova inele jekh oto dešuduj apostolja. Ov alo koro Isus te čumudini le ki čham.
48 Koma Yesu anamufunsa kuti, “Yudasi, kodi ukupereka Mwana wa Munthu ndi mpsopsono?”
A o Isus pučlja le: “Judo, čumudipnaja li predeja man, e Čhave e manušesere?”
49 Otsatira Yesu ataona zimene zimati zichitike, anati, “Ambuye, kodi timenyane ndi malupanga athu?”
Kad o učenici kola inele adari dikhle so o Isus ka ovel dolime, pučle le: “Gospode, te napadina len li e mačencar?”
50 Ndipo mmodzi wa iwo anatema wantchito wamkulu wa ansembe, nadula khutu lake lamanja.
I jekh olendar khuvđa mačeja e šerutne sveštenikosere sluga hem čhinđa lesoro desno kan.
51 Koma Yesu anayankha kuti, “Zisachitikenso zimenezi!” Ndipo Iye anakhudza khutu la munthuyo ndi kumuchiritsa.
A o Isus phenđa ple učenikonenđe: “Ačhaven tumen adalestar! Muken len te ćeren adava!” I čhivđa plo vas ko than kote o sluga inele čhindo hem sasljarđa le.
52 Kenaka Yesu anafunsa akulu a ansembe, akuluakulu oyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndi akuluakulu ena amene anabwerawo kuti, “Kodi Ine ndikutsogolera gulu lowukira kuti mubwere ndi malupanga ndi zibonga?
Tegani phenđa okolenđe so ale te dolen le, e šerutne sveštenikonenđe, e hramesere narednikonenđe hem e starešinenđe: “Mačencar hem kaštencar aljen pala mande sar palo pobunjeniko.
53 Tsiku lililonse ndinali nanu mʼmabwalo a mʼNyumba ya Mulungu ndipo inu simunandigwire. Koma iyi ndi nthawi yanu pamene mdima ukulamulira.”
Divencar injumle tumencar ano Hram, i na dolinđen man. Ali akavai tumaro vreme hem o zoralipe e tominakoro vladini.”
54 Pamenepo anamugwira Iye, napita naye ndipo anamutengera ku nyumba ya mkulu wa ansembe. Petro anamutsatira patali.
I dolinde e Isuse hem adathar legarde le ko čher e bare sveštenikosoro. A o Petar odural džala ine palo lende.
55 Koma pamene anasonkha moto pakati pa bwalo la milandu, anakhala onse pansi ndipo Petro anakhalanso pansi.
Kad resle, tharde jag ko maškar e borosoro hem bešle uzalo late. O Petar bešlo olencar.
56 Mtsikana wantchito anamuona atakhala nawo pafupi ndi moto. Iye anamuyangʼanitsitsa ndipo anati, “Munthu uyu anali ndi Yesu.”
I nesavi sluškinja dikhlja le sar bešela uzali jag, i po šukar dikhlja ano leste hem phenđa: “I akava inele e dolime manušeja!”
57 Koma Petro anakana nati, “Mtsikana, ine sindimudziwa ameneyu.”
A o Petar hovavđa vaćerindoj: “Đuvlije, na pendžarava le!”
58 Patatha kanthawi pangʼono, wina wake anamuona ndipo anati, “Iwenso ndiwe mmodzi mwa iwo.” Petro anayankha kuti, “Munthu iwe, ayi sindine.”
Na nakhlo but palo adava, dikhlja le nesavo aver manuš hem phenđa: “I tu injan jekh okolendar kola inele e dolime manušeja!” A o Petar phenđa: “Manušeja, na injum!”
59 Patatha pafupifupi ora limodzi, munthu winanso anati, “Zoonadi, munthu uyu anali ndi Iye, pakuti ndi mu Galileya.”
I kad nakhlo đi ko jekh sati, aver nesavo odlučime phenđa: “Čače akava inele e dolime manušeja, adalese soi hem ov Galilejco!”
60 Petro anayankha kuti, “Munthu iwe, sindikudziwa zimene ukunena apa.” Pamene iye ankayankhula, tambala analira.
A o Petar phenđa: “Manušeja, na džanav sostar vaćereja!” I ko adava momenti, sar pana vaćeri ine, o bašno đilabđa.
61 Ambuye anachewuka namuyangʼanitsitsa Petro. Pamenepo Petro anakumbukira mawu amene Ambuye anayankhula kwa iye kuti, “Asanalire tambala lero lino, udzandikana Ine katatu.”
Tegani o Gospod o Isus irinđa pe hem dikhlja ano Petar, a o Petar setinđa pe lesere lafendar: “Vaćerava će, Petre, angleder so o bašno avdive ka đilabi, trin puti ka hovave da na pendžareja man.”
62 Ndipo iye anapita panja nakalira kwambiri.
I iklilo taro boro hem zorale runđa.
63 Anthu amene ankalonda Yesu anayamba kumuchita chipongwe ndi kumumenya.
O čuvarija lelje te maren muj e Isuseja hem te maren le.
64 Anamumanga mʼmaso ndi kumufunsa kuti, “Tanenera! Wakumenya iwe ndi ndani?”
Učharde lesere jaćha hem phende lese: “Prorokujin ko khuvđa tut!”
65 Ndipo iwo anamunena zachipongwe zambiri.
I bute avere lafencar vređinena ine e Isuse.
66 Kutacha, bungwe la akuluakulu, pamodzi ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, anakumana pamodzi, ndipo anamuyika Yesu patsogolo pawo.
Kad dislilo, čedinde pe o starešine e jevrejengere, o šerutne sveštenici hem o učitelja e Zakonestar, ande e Isuse pumenđe ko sabor
67 Iwo anati, “Tiwuze, ngati ndiwe Khristu.” Yesu anayankha kuti, “Ine nditakuwuzani simungandikhulupirire.
hem phende lese: “Te injan tu o Hrist, phen amenđe!” A ov phenđa lenđe: “Te phenđum tumenđe, naka verujinen;
68 Ine nditakufunsani inu, simungandiyankhe.
a te pučljum tumen e Hristestar, naka odgovorinen.
69 Koma kuyambira tsopano, Mwana wa Munthu adzakhala ku dzanja lamanja la Mulungu wamphamvu.”
Ali od akana me, o Čhavo e manušesoro, ka bešav ko počasno than uzalo zoralipe e Devlesoro.”
70 Onse anafunsa kuti, “Ndiye kuti ndiwe Mwana wa Mulungu?” Iye anayankha kuti, “Mwanena ndinu kuti Ndine.”
A on sare pučle e Isuse: “Znači tu injan o Čhavo e Devlesoro?” A ov phenđa lenđe: “Korkore šukar phenđen da injum.”
71 Pamenepo iwo anati, “Nanga tikufuniranjinso umboni wina? Ife tamva kuchokera pa milomo yake.”
Tegani on phende: “Na valjani amenđe više dokazija dai krivo. Sare amen šunđam da korkoro pes osudinđa!”

< Luka 22 >