< Luka 22 >

1 Phwando la buledi wopanda yisiti lotchedwa Paska litayandikira,
La fête des Azymes, qu'on appelle la Pâque, approchait;
2 akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo amafunafuna mpata woti amuphere Yesu, pakuti ankachita mantha ndi anthu.
et les Princes des prêtres et les Scribes cherchaient comment ils feraient mourir Jésus; car ils craignaient le peuple.
3 Kenaka Satana analowa mwa Yudasi, wotchedwa Isikarioti, mmodzi wa khumi ndi a iwiriwo.
Or, Satan entra dans Judas, surnommé Iscariote, du nombre des Douze;
4 Ndipo Yudasi anapita kwa akulu a ansembe ndi akulu oyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndi kukambirana nawo za mmene iye angaperekere Yesu.
et celui-ci alla s'entendre avec les Princes des prêtres et les magistrats, sur la manière de le leur livrer.
5 Iwo anakondwa ndipo anagwirizana zomupatsa ndalama.
Eux, pleins de joie, promirent de lui donner de l'argent.
6 Iye anavomera, ndipo anayamba kufunafuna mpata wabwino wakuti amupereke Yesu kwa iwo pamene panalibe gulu la anthu pafupi.
Il s'engagea de son côté, et il cherchait une occasion favorable de leur livrer Jésus à l'insu de la foule.
7 Kenaka linafika tsiku la buledi wopanda yisiti pamene mwana wankhosa wa Paska amaperekedwa nsembe.
Arriva le jour des Azymes, où l'on devait immoler la Pâque.
8 Yesu anatuma Petro ndi Yohane nati, “Pitani kukatikonzera Paska kuti tikadye.”
Jésus envoya Pierre et Jean: " Allez, leur dit-il, nous préparer le repas pascal. "
9 Iwo anafunsa kuti, “Kodi mukufuna tikakonzere kuti?”
Ils lui dirent: " Où voulez-vous que nous le préparions? "
10 Iye anayankha kuti, “Taonani, mukamalowa mu mzinda, mudzakumana ndi mwamuna atanyamula mtsuko wamadzi. Mulondoleni ku nyumba imene akalowe,
Il leur répondit: " En entrant dans la ville, vous rencontrerez un homme portant une cruche d'eau; suivez-le dans la maison où il entrera,
11 ndipo mukamuwuze mwini nyumbayo kuti, ‘Aphunzitsi kufunsa kuti, chili kuti chipinda cha alendo, kumene Ine ndi ophunzira anga tikadyere Paska?’
et vous direz au maître de cette maison: Le Maître te fait dire: Où est la salle où je mangerai la Pâque avec mes disciples?
12 Iyeyo adzakuonetsani chipinda chachikulu chapamwamba, chokhala ndi zonse. Kachiteni zokonzekera mʼmenemo.”
Et il vous montrera un grand cénacle meublé: préparez-y ce qu'il faut. "
13 Iwo anapita nakapeza zinthu monga mmene Yesu anawawuzira. Tsono anakonza Paska.
Ils partirent, et trouvèrent les choses comme il le leur avait dit; et ils préparèrent la Pâque.
14 Ora litakwana, Yesu ndi ophunzira ake anakhala pa tebulo.
L'heure étant venue, Jésus se mit à table, et les douze Apôtres avec lui;
15 Ndipo Iye anawawuza kuti, “Ine ndakhala ndikuyembekezera kudya Paska uyu ndi inu ndisanamve zowawa.
et il leur dit: " J'ai désiré d'un grand désir de manger cette Pâque avec vous avant de souffrir.
16 Pakuti Ine ndikukuwuzani kuti sindidzadyanso Paska wina mpaka Paskayi itakwaniritsidwa mu ufumu wa Mulungu.”
Car, je vous le dis, je ne la mangerai plus jusqu'à la Pâque parfaite, célébrée dans le royaume de Dieu. "
17 Atanyamula chikho, Iye anayamika ndipo anati, “Tengani ndipo patsiranani pakati panu.
Et prenant une coupe, il rendit grâces et dit: " Prenez et partagez entre vous.
18 Pakuti ndikukuwuzani kuti, Ine sindidzamwanso zochokera ku chipatso cha mphesa mpaka ufumu wa Mulungu utabwera.”
Car, je vous le dis, je ne boirai plus du fruit de la vigne, jusqu'à ce que le royaume de Dieu soit venu. "
19 Ndipo Iye anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema, nagawira iwo nati, “Ili ndi thupi langa lomwe laperekedwa kwa inu; muzichita zimenezi pokumbukira Ine.”
Puis il prit du pain, et ayant rendu grâces, il le rompit et le leur donna, en disant: " Ceci est mon corps, qui est donné pour vous: faites ceci en mémoire de moi. "
20 Chimodzimodzinso, utatha mgonero, anatenga chikho nati, “Chikho ichi ndi pangano latsopano la magazi anga, amene akhetsedwa chifukwa cha inu.
Il fit de même pour la coupe, après le souper, disant: " Cette coupe est la nouvelle alliance en mon sang, lequel est versé pour vous.
21 Koma dzanja la amene akundipereka Ine lili pamodzi ndi langa pa chakudya pano.
Cependant voici que la main de celui qui me trahit est avec moi à cette table.
22 Mwana wa Munthu apita monga mmene zinalembedwera, koma tsoka kwa munthu amene amupereka Iye.”
Quant au Fils de l'homme, il va selon ce qui a été décrété; mais malheur à l'homme par qui il est trahi! "
23 Iwo anayamba kufunsana pakati pawo kuti ndi ndani wa iwo amene akanachita ichi.
Et les disciples se mirent à se demander les uns aux autres quel était celui d'entre eux qui devait faire cela.
24 Komanso mkangano unabuka pakati pawo kuti ndani mwa iwo amene amaganiziridwa kukhala wamkulu.
Il s'éleva aussi parmi eux une dispute, pour savoir lequel d'entre eux devait être estimé le plus grand.
25 Yesu anawawuza kuti, “Mafumu a anthu a mitundu ina amaonetsa mphamvu za ufumu wawo pa anthuwo; ndipo amene ali ndi ulamuliro, amapatsidwa dzina la kuti ‘Opindula.’
Jésus leur dit: " Les rois des nations dominent sur elles, et ceux qui leur commandent sont appelés Bienfaiteurs.
26 Koma inu simuyenera kukhala choncho. Mʼmalo mwake, wamkulu pakati panu akhale ngati wamngʼono pa onse, ndipo iye amene alamulira akhale ngati wotumikira.
Pour vous, ne faites pas ainsi; mais que le plus grand parmi vous soit comme le dernier, et celui qui gouverne comme celui qui sert.
27 Pakuti wamkulu ndani, iye amene ali pa tebulo kapena iye amene akutumikira? Kodi si iye amene ali pa tebulo? Koma ndili pakati panu ngati mmodzi wokutumikirani.
Car quel est le plus grand, de celui qui est à table, ou de celui qui sert? N'est-ce pas celui qui est à table? Et moi, cependant, je suis au milieu de vous comme celui qui sert.
28 Inu ndinu amene mwayima nane mʼmayesero.
Vous, vous êtes demeurés avec moi dans mes épreuves;
29 Ndipo Ine ndikupatsani inu ufumu, monga momwe Atate anga anandipatsiranso Ine,
et moi, je vous prépare un royaume, comme mon Père me l'a préparé,
30 kuti inu muthe kudya ndi kumwa pa tebulo langa mu ufumu wanga ndi kukhala pa mipando yaufumu kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israeli.”
afin que vous mangiez et buviez à ma table dans mon royaume, et que vous soyez assis sur des trônes, pour juger les douze tribus d'Israël. "
31 “Simoni, Simoni, Satana wapempha kuti akupete ngati tirigu.
Et le Seigneur dit: " Simon, Simon, voici que Satan vous a réclamés pour vous cribler comme le froment;
32 Koma Ine ndakupempherera Simoni, kuti chikhulupiriro chako chisafowoke ndipo pamene udzabwerera kwa Ine, udzalimbikitse abale ako.”
mais j'ai prié pour toi, afin que ta foi ne défaille point; et toi, quand tu seras converti, affermis tes frères. —
33 Koma iye anayankha kuti, “Ambuye, ndine wokonzeka kupita nanu ku ndende ndi kufa komwe.”
Seigneur, lui dit Pierre, je suis prêt à aller avec vous et en prison et à la mort. "
34 Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuza Petro, tambala asanalire lero lino, udzandikana katatu kuti sukundidziwa Ine.”
Jésus lui répondit: " Je te le dis, Pierre, le coq ne chantera pas aujourd'hui, que tu n'aies nié trois fois de me connaître. "
35 Kenaka Yesu anawafunsa iwo kuti, “Ine nditakutumizani wopanda chikwama cha ndalama, thumba kapena nsapato, kodi inu munasowa kanthu?” Iwo anayankha kuti, “Palibe chimene tinasowa.”
Il dit encore à ses disciples: " Quand je vous ai envoyés sans bourse, ni sac, ni chaussures, avez-vous manqué de quelque chose? —
36 Iye anawawuza kuti, “Koma tsopano ngati muli ndi chikwama cha ndalama, chitengeni, ndiponso thumba. Ndipo ngati mulibe lupanga, gulitsani mkanjo wanu ndi kugula.
De rien, " lui dirent-ils. Il ajouta: " Mais maintenant, que celui qui a une bourse la prenne, et de même celui qui a un sac; et que celui qui n'a point d'épée vende son manteau, et en achète une.
37 Zalembedwa kuti, ‘Ndipo Iye anawerengedwa pamodzi ndi anthu ochimwa,’ ndipo Ine ndikuwuzani kuti izi ziyenera kukwaniritsidwa mwa Ine. Inde, zimene zinalembedwa za Ine, zikukwaniritsidwa.”
Car, je vous le dis, il faut encore que cette parole de l'Écriture s'accomplisse en moi: Il a été mis au rang des malfaiteurs. En effet, ce qui me concerne touche à sa fin. "
38 Ophunzira anati, “Taonani Ambuye, awa malupanga awiri.” Iye anayankha kuti, “Amenewa akwanira.”
Ils lui dirent: " Seigneur, il y a ici deux épées. " Il leur répondit: " C'est assez. "
39 Yesu anapitanso monga mwa masiku onse ku Phiri la Olivi, ndipo ophunzira ake anamutsatira Iye.
Etant sorti, il s'en alla, selon sa coutume, vers le mont des Oliviers, et ses disciples le suivirent.
40 Atafika pamalopo, Iye anawawuza kuti, “Pempherani kuti musagwe mʼmayesero.”
Lorsqu'il fut arrivé dans ce lieu, il leur dit: " Priez, afin de ne point tomber en tentation. "
41 Iye anapita patsogolo pangʼono patali ngati kuponya mwala, anagwada napephera kuti,
Puis il s'éloigna d'eux à la distance d'un jet de pierre; et s'étant mis à genoux, il priait,
42 “Atate ngati mukufuna chotsereni chikho ichi. Komatu muchite zimene mukufuna osati zimene ndikufuna ine.”
disant: " Père, si vous voulez, éloignez de moi ce calice! Cependant que ce ne soit pas ma volonté, mais la vôtre qui se fasse. "
43 Mngelo wochokera kumwamba anafika namulimbikitsa.
Alors lui apparut du ciel un ange qui le fortifiait.
44 Ndipo mopsinjika mtima, anapemphera moona mtima, ndipo thukuta lake linali ngati madontho a magazi akugwera pansi.
Et se trouvant en agonie, il priait plus instamment, et sa sueur devint comme des gouttes de sang découlant jusqu'à terre.
45 Iye atamaliza kupemphera, ndi kubwerera kwa ophunzira ake, anawapeza atagona atafowoka ndi chisoni.
Après avoir prié, il se leva et vint vers les disciples, qu'il trouva endormis de tristesse.
46 Iye anafunsa kuti, Nʼchifukwa chiyani mukugona? “Dzukani ndipo pempherani kuti inu musagwe mʼmayesero.”
Et il leur dit: " Pourquoi dormez-vous? Levez-vous et priez, afin de ne point entrer en tentation. "
47 Pamene Iye ankayankhulabe, gulu la anthu linabwera, ndipo munthu wotchedwa Yudasi, mmodzi wa khumi ndi awiriwo analitsogolera. Iye anamuyandikira Yesu kuti amupsompsone.
Comme il parlait encore, voici qu'une troupe de gens parut; celui qu'on appelait Judas, l'un des Douze, marchait en tête. Il s'approcha de Jésus pour le baiser.
48 Koma Yesu anamufunsa kuti, “Yudasi, kodi ukupereka Mwana wa Munthu ndi mpsopsono?”
Et Jésus lui dit: " Judas, tu livres le Fils de l'homme par un baiser! "
49 Otsatira Yesu ataona zimene zimati zichitike, anati, “Ambuye, kodi timenyane ndi malupanga athu?”
Ceux qui étaient avec Jésus, voyant ce qui allait arriver, lui dirent: " Seigneur, si nous frappions de l'épée? "
50 Ndipo mmodzi wa iwo anatema wantchito wamkulu wa ansembe, nadula khutu lake lamanja.
Et l'un d'eux frappa le serviteur du grand prêtre, et lui emporta l'oreille droite.
51 Koma Yesu anayankha kuti, “Zisachitikenso zimenezi!” Ndipo Iye anakhudza khutu la munthuyo ndi kumuchiritsa.
Mais Jésus dit: " Restez-en là. " Et, ayant touché l'oreille de cet homme, il le guérit.
52 Kenaka Yesu anafunsa akulu a ansembe, akuluakulu oyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndi akuluakulu ena amene anabwerawo kuti, “Kodi Ine ndikutsogolera gulu lowukira kuti mubwere ndi malupanga ndi zibonga?
Puis, s'adressant aux Princes des prêtres, aux officiers du temple et aux Anciens qui étaient venus pour le prendre, il leur dit: " Vous êtes venus comme après un brigand, avec des épées et des bâtons.
53 Tsiku lililonse ndinali nanu mʼmabwalo a mʼNyumba ya Mulungu ndipo inu simunandigwire. Koma iyi ndi nthawi yanu pamene mdima ukulamulira.”
J'étais tous les jours avec vous dans le temple, et vous n'avez mis pas la main sur moi. Mais voici votre heure et la puissance des ténèbres. "
54 Pamenepo anamugwira Iye, napita naye ndipo anamutengera ku nyumba ya mkulu wa ansembe. Petro anamutsatira patali.
S'étant saisis de lui, ils l'emmenèrent et le conduisirent dans la maison du grand prêtre; Pierre suivait de loin.
55 Koma pamene anasonkha moto pakati pa bwalo la milandu, anakhala onse pansi ndipo Petro anakhalanso pansi.
Ayant allumé du feu au milieu de la cour, ils s'assirent autour, et Pierre s'assit parmi eux.
56 Mtsikana wantchito anamuona atakhala nawo pafupi ndi moto. Iye anamuyangʼanitsitsa ndipo anati, “Munthu uyu anali ndi Yesu.”
Une servante, qui le vit assis devant le feu, l'ayant regardé fixement, dit: " Cet homme était aussi avec lui. "
57 Koma Petro anakana nati, “Mtsikana, ine sindimudziwa ameneyu.”
Mais Pierre renia Jésus, en disant: " Femme, je ne le connais point. "
58 Patatha kanthawi pangʼono, wina wake anamuona ndipo anati, “Iwenso ndiwe mmodzi mwa iwo.” Petro anayankha kuti, “Munthu iwe, ayi sindine.”
Peu après, un autre l'ayant vu, dit: " Tu es aussi de ces gens-là. " Pierre répondit: " Mon ami, je n'en suis point. "
59 Patatha pafupifupi ora limodzi, munthu winanso anati, “Zoonadi, munthu uyu anali ndi Iye, pakuti ndi mu Galileya.”
Une heure s'était écoulée, lorsqu'un autre se mit à dire avec assurance: " Certainement cet homme était aussi avec lui, car il est de la Galilée. "
60 Petro anayankha kuti, “Munthu iwe, sindikudziwa zimene ukunena apa.” Pamene iye ankayankhula, tambala analira.
Pierre répondit: " Mon ami, je ne sais ce que tu veux dire. " Et aussitôt, comme il parlait encore, le coq chanta.
61 Ambuye anachewuka namuyangʼanitsitsa Petro. Pamenepo Petro anakumbukira mawu amene Ambuye anayankhula kwa iye kuti, “Asanalire tambala lero lino, udzandikana Ine katatu.”
Et le Seigneur, s'étant retourné, regarda Pierre, et Pierre se souvint de la parole que le Seigneur lui avait dite: " Avant que le coq chante, tu me renieras trois fois. "
62 Ndipo iye anapita panja nakalira kwambiri.
Et étant sorti de la maison, Pierre pleura amèrement.
63 Anthu amene ankalonda Yesu anayamba kumuchita chipongwe ndi kumumenya.
Or, ceux qui tenaient Jésus se moquaient de lui et le frappaient.
64 Anamumanga mʼmaso ndi kumufunsa kuti, “Tanenera! Wakumenya iwe ndi ndani?”
Ils lui bandèrent les yeux, et, le frappant au visage, ils l'interrogeaient, disant: " Devine qui t'a frappé. "
65 Ndipo iwo anamunena zachipongwe zambiri.
Et ils proféraient contre lui beaucoup d'autres injures.
66 Kutacha, bungwe la akuluakulu, pamodzi ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, anakumana pamodzi, ndipo anamuyika Yesu patsogolo pawo.
Dès qu'il fit jour, les Anciens du peuple, les Princes des prêtres et les Scribes se réunirent, et amenèrent Jésus dans leur assemblée. Ils dirent: " Si tu es le Christ, dis-le-nous. "
67 Iwo anati, “Tiwuze, ngati ndiwe Khristu.” Yesu anayankha kuti, “Ine nditakuwuzani simungandikhulupirire.
Il leur répondit: " Si je vous le dis, vous ne le croirez pas;
68 Ine nditakufunsani inu, simungandiyankhe.
et si je vous interroge, vous ne me répondrez pas et ne me relâcherez pas.
69 Koma kuyambira tsopano, Mwana wa Munthu adzakhala ku dzanja lamanja la Mulungu wamphamvu.”
Désormais le Fils de l'homme sera assis à la droite de la puissance de Dieu. "
70 Onse anafunsa kuti, “Ndiye kuti ndiwe Mwana wa Mulungu?” Iye anayankha kuti, “Mwanena ndinu kuti Ndine.”
Alors ils dirent tous: " Tu es donc le Fils de Dieu? " Il leur répondit: " Vous le dites, je le suis. "
71 Pamenepo iwo anati, “Nanga tikufuniranjinso umboni wina? Ife tamva kuchokera pa milomo yake.”
Et ils dirent: " Qu'avons-nous encore besoin de témoignage? Nous l'avons nous-mêmes entendu de sa bouche. "

< Luka 22 >