< Luka 21 >

1 Yesu atayangʼana, anaona olemera akuyika mphatso zawo mu chosungira ndalama za mʼNyumba ya Mulungu.
Jésus, levant les yeux, vit les riches qui mettaient leurs offrandes dans le tronc.
2 Iye anaonanso mkazi wamasiye wosauka akuyikamo timakopala tiwiri.
Il vit aussi une pauvre veuve qui y mettait deux pites.
3 Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mkazi wamasiye wosaukayu wapereka zambiri kuposa ena onsewa.
Et il dit: En vérité, je vous le déclare, cette pauvre veuve a mis plus que tous les autres.
4 Anthu onsewa atapa mphatso zawo kuchokera pa zochuluka zimene ali nazo; koma uyu, mwa umphawi wake, wapereka zonse zimene ali nazo.”
Car tous ceux-là, pour leurs offrandes, ont donné de leur superflu; mais celle-ci a donné de son indigence, tout ce qu'elle avait pour vivre.
5 Ena mwa ophunzira ake ankachita ndemanga za mmene Nyumba ya Mulungu anayikongoletsera ndi miyala yokongola ndiponso zinthu zina zomwe anthu anapereka kwa Mulungu. Koma Yesu anati,
Quelques-uns parlaient du temple, des belles pierres et des dons qui l'ornaient. Jésus dit:
6 “Koma zimene mukuziona panozi, nthawi idzafika pamene ngakhale mwala umodzi omwe sudzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
Les jours viendront où, de ce que vous regardez, il ne restera pas ici une pierre sur une autre pierre qui ne soit renversée.
7 Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, kodi zonsezi zidzachitika liti? Ndipo tidzaonera chiyani kuti zili pafupi kuchitika?”
Alors ils lui demandèrent: Maître, quand donc ces choses arriveront-elles, et à quel signe connaîtra-t-on qu'elles sont sur le point d'arriver?
8 Iye anayankha kuti, “Chenjerani kuti musanyengedwe. Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati ‘Ine ndine Iye’ ndi kuti ‘Nthawi yayandikira.’ Musadzawatsate iwo.
Il répondit: Prenez garde de ne pas vous laisser séduire; car plusieurs viendront en mon nom, disant: C'est moi qui suis le Christ. Le moment approche! Ne les suivez pas!
9 Mukadzamva zankhondo ndi zipolowe, musadzachite mantha. Zinthu izi ziyenera kuchitika poyamba, koma chimaliziro sichidzafika nthawi yomweyo.”
Et quand vous entendrez parler de guerres et de séditions, ne vous effrayez pas, car il faut que ces choses arrivent d'abord; mais ce ne sera pas de sitôt la fin.
10 Kenaka anawawuza kuti, “Mtundu wa anthu udzawukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu kuwukira ufumu wina.
Il leur dit aussi: Une nation s'élèvera contre une autre nation, et un royaume contre un autre royaume.
11 Kudzakhala zivomerezi zazikulu, njala ndi miliri mʼmalo osiyanasiyana, ndi zinthu zoopsa ndi zizindikiro zamphamvu kuchokera kumwamba.
Il y aura de grands tremblements de terre, des famines et des pestes en divers lieux, des phénomènes effrayants et de grands signes dans le ciel.
12 “Koma zonsezi zisanachitike, adzakugwirani ndi kukuzunzani. Adzakuperekani ku masunagoge ndi ku ndende, ndipo adzakutengerani pamaso pa mafumu ndi olamulira, ndipo zonsezi zidzachitika chifukwa cha dzina langa.
Mais avant tout cela, on mettra la main sur vous, on vous persécutera, on vous livrera aux synagogues, on vous mettra en prison; et vous serez traînés devant les rois et devant les gouverneurs, à cause de mon nom.
13 Umenewu udzakhala mwayi wanu ochitira umboni.
Cela vous arrivera pour que vous rendiez témoignage.
14 Koma tsimikizani mtima kuti musadzade nkhawa za momwe mudzadzitchinjirizire.
Mettez-vous donc bien dans l'esprit de ne pas vous préoccuper de votre défense.
15 Pakuti Ine ndidzakupatsani mawu ndi nzeru kotero kuti palibe mmodzi wa adani anu adzathe kuwakana kapena kuwatsutsa.
En effet, je vous donnerai une parole pleine de sagesse, à laquelle tous vos adversaires ne pourront résister ni contredire.
16 Inu mudzaperekedwa ndi makolo anu, abale, anansi ndi abwenzi anu ndipo ena mwa inu adzakuphani.
Vous serez livrés même par vos pères et vos mères, par vos frères, vos parents et vos amis; et ils feront mourir plusieurs d'entre vous.
17 Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine.
Vous serez haïs de tous, à cause de mon nom.
18 Koma palibe tsitsi limodzi la mʼmutu mwanu lidzawonongeke.
Mais il ne se perdra pas un cheveu de votre tête.
19 Mukadzalimbikira ndiye mudzapeze moyo.
C'est par votre patience que vous sauverez vos âmes.
20 “Mukadzaona Yerusalemu atazingidwa ndi magulu ankhondo, inu mudzadziwe kuti kuwonongeka kwake kuli pafupi.
Or, quand vous verrez Jérusalem investie par des armées, sachez, à ce moment-là, que sa ruine approche.
21 Pamenepo amene ali ku Yudeya adzathawire ku mapiri, amene ali mu mzinda adzatulukemo, ndi amene ali ku midzi asadzalowe mu mzinda.
Que ceux qui seront alors dans la Judée s'enfuient dans les montagnes; que ceux qui seront dans l'intérieur de la ville en sortent, et que ceux qui seront dans les champs, ne se retirent pas dans la ville.
22 Pakuti iyi ndi nthawi yachilango pokwaniritsa zonse zimene zinalembedwa.
Car ce sont là les jours de la vengeance, afin que s'accomplisse tout ce qui est écrit.
23 Zidzakhala zoopsa nthawi imenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa! Kudzakhala masautso aakulu mʼdziko ndipo anthu onse adzawakwiyira.
Malheur aux femmes qui seront enceintes, et à celles qui allaiteront en ces jours-là! Car il y aura une grande détresse dans le pays et une grande colère contre ce peuple.
24 Iwo adzaphedwa ndi lupanga ndi kutengedwa ukapolo kupita ku mayiko wonse. Yerusalemu adzaponderezedwa ndi anthu a mitundu ina mpaka nthawi ya a mitundu ina itakwaniritsidwa.
Ils tomberont sous le tranchant de l'épée, ils seront emmenés captifs parmi toutes les nations; et Jérusalem sera foulée aux pieds par les Païens, jusqu'à ce que les temps des nations païennes soient accomplis.
25 “Padzakhala zizindikiro zodabwitsa pa dzuwa, mwezi ndi nyenyezi. Pa dziko lapansi, mitundu ya anthu idzakhala mʼmasautso ndipo idzathedwa nzeru pakumva mkokomo ndi mafunde a mʼnyanja.
Il y aura des signes dans le soleil, dans la lune et dans les étoiles; et, sur la terre, l'angoisse s'emparera des nations troublées par le fracas de la mer et des flots.
26 Anthu adzakomoka chifukwa cha mantha, akadzamva za zimene zikubwera pa dziko lapansi, pakuti zinthu zamlengalenga zidzagwedezeka.
Les hommes rendront l'âme de frayeur, dans l'attente des maux qui viendront sur le monde; car les puissances des cieux seront ébranlées.
27 Nthawi imeneyo adzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
Alors on verra le Fils de l'homme venant sur une nuée, avec une grande puissance et une grande gloire.
28 Zinthu izi zikadzayamba kuchitika, mudzayimirire ndi kutukula mitu yanu, chifukwa chipulumutso chanu chayandikira.”
Lorsque ces choses commenceront à arriver, redressez-vous et levez vos têtes, parce que votre délivrance est proche.
29 Iye anawawuza fanizo ili, “Taonani mtengo wamkuyu ndi mitengo ina yonse.
Puis il leur dit une parabole: Voyez le figuier et tous les autres arbres;
30 Ikamatulutsa masamba, mumakhoza kudzionera nokha ndi kudziwa kuti dzinja lili pafupi.
quand ils commencent à pousser, vous savez de vous-mêmes, en les voyant, que l'été est déjà proche.
31 Chimodzimodzinso, mukadzaona zinthu zonsezi, dziwani kuti ufumu wa Mulungu uli pafupi.
De même, lorsque vous verrez ces choses arriver, sachez que le royaume de Dieu est proche.
32 “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika.
En vérité, je vous le dis, cette génération ne passera pas, que toutes ces choses n'arrivent.
33 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
Le ciel et la terre passeront; mais mes paroles ne passeront point.
34 “Samalani, kuti mitima yanu ingalemetsedwe ndi maphwando, kuledzera ndi kudera nkhawa za moyo uno, ndi kuti tsiku ilo lingadzakupezeni modzidzimutsa ngati msampha.
Prenez donc garde à vous-mêmes, de peur que vos coeurs ne soient appesantis par les excès de la bonne chère, par l'ivresse et par les inquiétudes, de cette vie, et que ce jour-là ne vienne subitement sur vous,
35 Pakuti lidzafika pa onse okhala pa dziko lonse lapansi.
comme un filet; car il surprendra tous ceux qui habitent la surface de la terre entière.
36 Khalani tcheru nthawi zonse ndi kupemphera kuti inu mudzathe kuthawa zonse zimene zili pafupi kuchitika, ndi kuti mudzathe kuyima pamaso pa Mwana wa Munthu.”
Veillez donc en tout temps et priez, afin que vous puissiez échapper à tous ces maux qui doivent arriver, et subsister devant le Fils de l'homme.
37 Tsiku lililonse Yesu amaphunzitsa ku Nyumba ya Mulungu, ndi madzulo ali wonse Iye amachoka kukakhala pa phiri la Olivi usiku wonse.
Or, Jésus enseignait dans le temple pendant le jour; mais le soir, il sortait et passait les nuits sur la montagne appelée montagne des Oliviers.
38 Ndipo anthu onse amabwera mmamawa kudzamumva Iye ku Nyumba ya Mulungu.
Et, dès le point du jour, tout le peuple venait à lui dans le temple pour l'écouter.

< Luka 21 >