< Luka 21 >

1 Yesu atayangʼana, anaona olemera akuyika mphatso zawo mu chosungira ndalama za mʼNyumba ya Mulungu.
A pohleděv, uzřel bohaté, kteříž metali dary své do pokladnice.
2 Iye anaonanso mkazi wamasiye wosauka akuyikamo timakopala tiwiri.
Uzřel pak i jednu vdovu chudičkou, ana uvrhla tam dva šarty.
3 Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mkazi wamasiye wosaukayu wapereka zambiri kuposa ena onsewa.
I řekl: V pravdě pravím vám, že vdova tato chudá více než všickni uvrhla.
4 Anthu onsewa atapa mphatso zawo kuchokera pa zochuluka zimene ali nazo; koma uyu, mwa umphawi wake, wapereka zonse zimene ali nazo.”
Nebo všickni tito z toho, což jim zbývalo, dali dary Bohu, tato pak z své chudoby všecku živnost svou, kterouž měla, uvrhla.
5 Ena mwa ophunzira ake ankachita ndemanga za mmene Nyumba ya Mulungu anayikongoletsera ndi miyala yokongola ndiponso zinthu zina zomwe anthu anapereka kwa Mulungu. Koma Yesu anati,
A když někteří pravili o chrámu, kterak by kamením pěkným i okrasami ozdoben byl, řekl:
6 “Koma zimene mukuziona panozi, nthawi idzafika pamene ngakhale mwala umodzi omwe sudzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
Nač se to díváte? Přijdouť dnové, v nichž nebude zůstaven kámen na kameni, kterýž by nebyl zbořen.
7 Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, kodi zonsezi zidzachitika liti? Ndipo tidzaonera chiyani kuti zili pafupi kuchitika?”
I otázali se ho, řkouce: Mistře, kdy to bude? A které znamení, když se to bude míti státi?
8 Iye anayankha kuti, “Chenjerani kuti musanyengedwe. Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati ‘Ine ndine Iye’ ndi kuti ‘Nthawi yayandikira.’ Musadzawatsate iwo.
On pak řekl: Vizte, abyste nebyli svedeni. Nebo mnozí přijdou ve jménu mém, řkouce: Já jsem, a čas se blíží. Protož nepostupujte po nich.
9 Mukadzamva zankhondo ndi zipolowe, musadzachite mantha. Zinthu izi ziyenera kuchitika poyamba, koma chimaliziro sichidzafika nthawi yomweyo.”
Když pak uslyšíte o válkách a různicech, nestrachujte se; neboť musí to prvé býti, ale ne i hned konec.
10 Kenaka anawawuza kuti, “Mtundu wa anthu udzawukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu kuwukira ufumu wina.
Tehdy pravil jim: Povstaneť národ proti národu, a království proti království.
11 Kudzakhala zivomerezi zazikulu, njala ndi miliri mʼmalo osiyanasiyana, ndi zinthu zoopsa ndi zizindikiro zamphamvu kuchokera kumwamba.
A země třesení veliká budou po místech, a hladové, a morové, hrůzy i zázrakové s nebe velicí.
12 “Koma zonsezi zisanachitike, adzakugwirani ndi kukuzunzani. Adzakuperekani ku masunagoge ndi ku ndende, ndipo adzakutengerani pamaso pa mafumu ndi olamulira, ndipo zonsezi zidzachitika chifukwa cha dzina langa.
Ale před tím přede vším vztáhnou ruce své na vás, a protiviti se budou, vydávajíce vás do škol a žalářů, vodíce k králům a k vládařům pro jméno mé.
13 Umenewu udzakhala mwayi wanu ochitira umboni.
A toť se vám díti bude na svědectví.
14 Koma tsimikizani mtima kuti musadzade nkhawa za momwe mudzadzitchinjirizire.
Protož složtež to v srdcích svých, abyste se nestarali, kterak byste odpovídati měli.
15 Pakuti Ine ndidzakupatsani mawu ndi nzeru kotero kuti palibe mmodzi wa adani anu adzathe kuwakana kapena kuwatsutsa.
Jáť zajisté dám vám ústa a moudrost, kteréž nebudou moci odolati, ani proti ní ostáti všickni protivníci vaši.
16 Inu mudzaperekedwa ndi makolo anu, abale, anansi ndi abwenzi anu ndipo ena mwa inu adzakuphani.
Budete pak zrazováni i od rodičů a od bratří, od příbuzných i od přátel, a zmordují některé z vás.
17 Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine.
A budete v nenávisti u všech pro jméno mé.
18 Koma palibe tsitsi limodzi la mʼmutu mwanu lidzawonongeke.
Ale ani vlas s hlavy vaší nikoli nezahyne.
19 Mukadzalimbikira ndiye mudzapeze moyo.
V trpělivosti své vládněte dušemi svými.
20 “Mukadzaona Yerusalemu atazingidwa ndi magulu ankhondo, inu mudzadziwe kuti kuwonongeka kwake kuli pafupi.
Když pak uzříte obležený od vojska Jeruzalém, tehdy vězte, žeť se přiblížilo zkažení jeho.
21 Pamenepo amene ali ku Yudeya adzathawire ku mapiri, amene ali mu mzinda adzatulukemo, ndi amene ali ku midzi asadzalowe mu mzinda.
Tehdy ti, kdož jsou v Judstvu, utíkejte k horám, a kdo u prostřed něho, vyjděte, a kteří v končinách, nevcházejte do něho.
22 Pakuti iyi ndi nthawi yachilango pokwaniritsa zonse zimene zinalembedwa.
Neboť budou dnové pomsty, aby se naplnilo všecko, což psáno jest.
23 Zidzakhala zoopsa nthawi imenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa! Kudzakhala masautso aakulu mʼdziko ndipo anthu onse adzawakwiyira.
Ale běda těhotným a těm, kteréž kojí v těch dnech. Neboť bude dav veliký v této zemi, a hněv nad lidem tímto.
24 Iwo adzaphedwa ndi lupanga ndi kutengedwa ukapolo kupita ku mayiko wonse. Yerusalemu adzaponderezedwa ndi anthu a mitundu ina mpaka nthawi ya a mitundu ina itakwaniritsidwa.
I padati budou ostrostí meče, a zjímaní vedeni budou mezi všecky národy, a Jeruzalém tlačen bude od pohanů, dokudž se nenaplní časové pohanů.
25 “Padzakhala zizindikiro zodabwitsa pa dzuwa, mwezi ndi nyenyezi. Pa dziko lapansi, mitundu ya anthu idzakhala mʼmasautso ndipo idzathedwa nzeru pakumva mkokomo ndi mafunde a mʼnyanja.
I budouť znamení na slunci a na měsíci i na hvězdách, a na zemi ssoužení národů, nevědoucích se kam díti, když zvuk vydá moře a vlnobití,
26 Anthu adzakomoka chifukwa cha mantha, akadzamva za zimene zikubwera pa dziko lapansi, pakuti zinthu zamlengalenga zidzagwedezeka.
Tak že zmrtvějí lidé pro strach a pro očekávání těch věcí, kteréž přijdou na všecken svět. Nebo moci nebeské pohybovati se budou.
27 Nthawi imeneyo adzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
A tehdyť uzří Syna člověka, an se béře v oblace s mocí a slavou velikou.
28 Zinthu izi zikadzayamba kuchitika, mudzayimirire ndi kutukula mitu yanu, chifukwa chipulumutso chanu chayandikira.”
A když se toto počne díti, pohleďtež a pozdvihnětež hlav svých, proto že se přibližuje vykoupení vaše.
29 Iye anawawuza fanizo ili, “Taonani mtengo wamkuyu ndi mitengo ina yonse.
I pověděl jim podobenství: Patřte na fíkový strom i na všecka stromoví.
30 Ikamatulutsa masamba, mumakhoza kudzionera nokha ndi kudziwa kuti dzinja lili pafupi.
Když se již pučí, vidouce to, sami to znáte, že blízko jest již léto.
31 Chimodzimodzinso, mukadzaona zinthu zonsezi, dziwani kuti ufumu wa Mulungu uli pafupi.
Takž i vy, když uzříte, ano se tyto věci dějí, vězte, že blízko jest království Boží.
32 “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika.
Amen pravím vám, že nepomine věk tento, až se všecko stane.
33 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
Nebe a země pominou, ale slova má nepominou.
34 “Samalani, kuti mitima yanu ingalemetsedwe ndi maphwando, kuledzera ndi kudera nkhawa za moyo uno, ndi kuti tsiku ilo lingadzakupezeni modzidzimutsa ngati msampha.
Pilně se pak varujte, aby snad nebyla obtížená srdce vaše obžerstvím a opilstvím a pečováním o tento život, a v náhle přikvačil by vás ten den.
35 Pakuti lidzafika pa onse okhala pa dziko lonse lapansi.
Nebo jako osídlo přijde na všecky, kteříž přebývají na tváři vší země.
36 Khalani tcheru nthawi zonse ndi kupemphera kuti inu mudzathe kuthawa zonse zimene zili pafupi kuchitika, ndi kuti mudzathe kuyima pamaso pa Mwana wa Munthu.”
Protož bděte, všelikého času modléce se, abyste hodni byli ujíti všech těch věcí, kteréž se budou díti, a postaviti se před Synem člověka.
37 Tsiku lililonse Yesu amaphunzitsa ku Nyumba ya Mulungu, ndi madzulo ali wonse Iye amachoka kukakhala pa phiri la Olivi usiku wonse.
I býval ve dne v chrámě, uče, ale v noci vycházeje, přebýval na hoře, kteráž slove Olivetská.
38 Ndipo anthu onse amabwera mmamawa kudzamumva Iye ku Nyumba ya Mulungu.
A všecken lid na úsvitě přicházel k němu do chrámu, aby ho poslouchal.

< Luka 21 >