< Luka 20 >

1 Tsiku lina pamene Iye ankaphunzitsa anthu mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu ndi kuphunzitsa Uthenga Wabwino, akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, pamodzi ndi akuluakulu anabwera kwa Iye.
And it came to pass, that on one of those days, as he taught the people in the temple, and preached the gospel, the chief priests and the scribes came upon him with the elders,
2 Iwo anati, “Mutiwuze mukuchita izi ndi ulamuliro wayani? Ndani anakupatsani ulamuliro uwu?”
And spoke to him, saying, Tell us, by what authority doest thou these things? or who is he that gave thee this authority?
3 Iye anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani, mundiyankhe,
And he answered and said to them, I will also ask you one thing; and answer me:
4 ‘Kodi ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena wochokera kwa anthu?’”
The baptism of John, was it from heaven, or from men?
5 Iwo anakambirana pakati pawo ndikuti, “Ngati ife tinena kuti, ‘Kuchokera kumwamba’ Iye akatifunsa kuti, ‘chifukwa chiyani simunamukhulupirire iye?’
And they reasoned with themselves, saying, If we shall say, From heaven; he will say, Why then believed ye him not?
6 Koma ngati ife tinena kuti, ‘kuchokera kwa anthu,’ anthu onse atigenda miyala, chifukwa amatsimikiza kuti Yohane anali mneneri.”
But if we say, From men; all the people will stone us: for they are persuaded that John was a prophet.
7 Pamenepo iwo anayankha kuti, “Ife sitidziwa kumene unachokera.”
And they answered, that they could not tell where it was from.
8 Yesu anati, “Ngakhale Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira zimenezi.”
And Jesus said to them, Neither do I tell you by what authority I do these things.
9 Iye anapitirira kuwawuza anthu fanizo ili: “Munthu wina analima munda wamphesa, nabwereketsa kwa alimi ena ndipo anachoka kwa nthawi yayitali.
Then he began to speak to the people this parable; A certain man planted a vineyard, and let it out to vinedressers, and went into a far country for a long time.
10 Pa nthawi yokolola, iye anatumiza wantchito wake kwa alimi aja kuti amupatseko zina mwa zipatso za munda wamphesawo. Koma alimi aja anamumenya namubweza wopanda kanthu.
And at the season he sent a servant to the vinedressers, that they should give him of the fruit of the vineyard: but the vinedressers beat him, and sent him away empty.
11 Iye anatumiza wantchito wina, koma uyunso anamumenya namuchita zachipongwe ndi kumubweza wopanda kanthu.
And again he sent another servant: and they beat him also, and treated him shamefully, and sent him away empty.
12 Iye anatumizanso wina wachitatu ndipo iwo anamuvulaza namuponya kunja.
And again he sent the third: and they wounded him also, and cast him out.
13 “Kenaka mwini mundawo anati, ‘Kodi ndichite chiyani? Ndidzatumiza mwana wanga wamwamuna, amene ndimukonda; mwina iwo adzamuchitira ulemu.’
Then said the lord of the vineyard, What shall I do? I will send my beloved son: it may be when they see him they will reverence him.
14 “Koma alimiwo ataona mwanayo, anakambirananso. Iwo anati, ‘Uyu ndiye wodzamusiyira chumachi. Tiyeni timuphe ndipo chumachi chikhala chathu.’
But when the vinedressers saw him, they reasoned among themselves, saying, This is the heir: come, let us kill him, that the inheritance may be ours.
15 Ndipo anamuponya kunja kwa mundawo ndi kumupha. “Nanga tsono mwini munda wamphesayo adzawatani anthuwa?
So they cast him out of the vineyard, and killed him. What therefore shall the lord of the vineyard do to them?
16 Iye adzabwera ndi kupha alimi aja ndi kupereka mundawo kwa ena.” Pamene anthu anamva izi, anati, “Musatero ayi.”
He shall come and destroy these vinedressers, and shall give the vineyard to others. And when they heard it, they said, may that never be.
17 Yesu anawayangʼanitsitsa ndipo anafunsa kuti, “Kodi tanthauzo lake ndi chiyani la zimene zinalembedwa kuti, “‘Mwala umene omanga nyumba anawukana wasanduka mwala wa pa ngodya.
And he beheld them, and said, What is this then that is written, The stone which the builders rejected, the same is become the head of the corner?
18 Aliyense amene agwa pa mwalawu adzapweteka, koma iye amene udzamugwera udzamuphwanya.’”
Whoever shall fall upon that stone shall be broken; but on whomever it shall fall, it will grind him to powder.
19 Aphunzitsi amalamulo ndi akulu a ansembe amafuna njira yoti amuphe nthawi yomweyo, chifukwa anadziwa kuti ananena fanizo ili powatsutsa iwo. Koma iwo anali ndi mantha chifukwa cha anthu.
And the chief priests and the scribes the same hour sought to lay hands on him; and they feared the people: for they perceived that he had spoken this parable against them.
20 Pamene ankamulondalonda Iye, iwo anatumiza akazitape amene amaoneka ngati achilungamo. Iwo ankafuna kumutapa mʼkamwa Yesu mu china chilichonse chimene Iye ananena kuti amupereke Iye kwa amene anali ndi mphamvu ndi ulamuliro oweruza.
And they watched him, and sent forth spies, who pretended to be righteous men, that they might take hold of his words, that so they might deliver him to the power and authority of the governor.
21 Potero akazitapewo anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi, tidziwa kuti mumayankhula ndi kuphunzitsa zimene zili zoonadi, ndi kuti simuonetsa tsankho koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu mwachoonadi.
And they asked him, saying, Master, we know that thou sayest and teachest rightly, neither acceptest thou the person of any, but teachest the way of God truly:
22 Kodi ndi bwino kwa ife kumapereka msonkho kwa Kaisara kapena kusapereka?”
Is it lawful for us to give tribute to Caesar, or not?
23 Iye anaona chinyengo chawo ndipo anawawuza kuti,
But he perceived their craftiness, and said to them, Why tempt ye me?
24 “Onetseni ndalama. Chithunzi ndi malembawa ndi zayani?”
Show me a penny. Whose image and superscription hath it? They answered and said, Caesar’s.
25 Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.” Iye anawawuza kuti, “Ndiye perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zimene ndi za Mulungu.”
And he said to them, Render therefore to Caesar the things which are Caesar’s, and to God the things which are God’s.
26 Iwo analephera kumupeza cholakwa pa zimene ankayankhula pamaso pa anthu. Ndipo pothedwa nzeru ndi yankho lake, iwo anakhala chete.
And they could not take hold of his words before the people: and they marvelled at his answer, and held their peace.
27 Ena mwa Asaduki, amene ankanena kuti kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Yesu ndi funso.
Then came to him certain of the Sadducees, who deny that there is any resurrection; and they asked him,
28 Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
Saying, Master, Moses wrote to us, If any man’s brother should die, having a wife, and he should die without children, that his brother should take his wife, and raise up seed to his brother.
29 Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyambayo anakwatira mkazi ndipo anafa wopanda mwana.
There were therefore seven brothers: and the first took a wife, and died without children.
30 Wachiwiri
And the second took her for a wife, and he died childless.
31 ndipo kenaka wachitatuyo anamukwatira iye, ndipo chimodzimodzi asanu ndi awiri aja anafa osasiya ana.
And the third took her; and in like manner the seven also: and they left no children, and died.
32 Pa mapeto pake mkaziyo anafanso.
Last of all the woman died also.
33 Tsopano, pa nthawi ya kuukanso, kodi mkaziyu adzakhala wayani popeza onse asanu ndi awiri anamukwatirapo?”
Therefore in the resurrection whose wife of them is she? for seven had her for a wife.
34 Yesu anayankha kuti, “Anthu a mʼbado uno amakwatira ndi kukwatiwa. (aiōn g165)
And Jesus answering said to them, The children of this world marry, and are given in marriage: (aiōn g165)
35 Koma mʼmoyo umene ukubwerawo, anthu amene adzaukitsidwe kwa akufa sadzakwatira kapena kukwatiwa. (aiōn g165)
But they who shall be accounted worthy to obtain that world, and the resurrection from the dead, neither marry, nor are given in marriage: (aiōn g165)
36 Ndipo sadzafanso, pakuti adzakhala ngati angelo. Iwo ndi ana a Mulungu, chifukwa adzakhala ataukitsidwa kwa akufa.
Neither can they die any more: for they are equal to the angels; and are the children of God, being the children of the resurrection.
37 Ngakhale pa nkhani yachitsamba choyaka moto, Mose anaonetsa kuti akufa amauka, pakuti anatcha Ambuye ‘Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo.’
Now that the dead are raised, even Moses showed at the bush, when he calleth the Lord the God of Abraham, and the God of Isaac, and the God of Jacob.
38 Mulungu si Mulungu wa akufa, koma wa amoyo, pakuti kwa Iye onse ali ndi moyo.”
For he is not a God of the dead, but of the living: for all live to him.
39 Ena mwa aphunzitsi amalamulo anayankha kuti, “Mwanena bwino mphunzitsi!”
Then certain of the scribes answering said, Master, thou hast well said.
40 Ndipo panalibe wina amene akanalimba mtima kumufunsa Iye mafunso ena.
And after that they dared not ask him any question at all.
41 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Zikutheka bwanji kuti aziti Khristu ndi mwana wa Davide?
And he said to them, How say they that Christ is David’s son?
42 Davide mwini wake akunenetsa mʼbuku la Masalimo kuti, “Ambuye anati kwa Ambuye anga: ‘Khalani ku dzanja langa lamanja,
And David himself saith in the book of Psalms, The LORD said to my Lord, Sit thou on my right hand,
43 mpaka Ine nditasandutsa adani anu chopondapo mapazi anu?’
Till I make thy enemies thy footstool.
44 Davide akumutcha Iye ‘Ambuye.’ Nanga zingatheke bwanji kuti Iye akhale mwana wake?”
David therefore calleth him Lord, how is he then his son?
45 Pamene anthu onse ankamvetsera, Yesu anati kwa ophunzira ake,
Then in the hearing of all the people he said to his disciples,
46 “Chenjerani ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo amakonda kuyenda atavala mikanjo ndipo amakonda kulonjeredwa mʼmisika ndipo amakhala mʼmipando yofunika mʼmasunagoge ndi mʼmalo aulemu mʼmaphwando.
Beware of the scribes, who desire to walk in long robes, and love greetings in the markets, and the highest seats in the synagogues, and the best places at feasts;
47 Amawadyera akazi amasiye chuma chawo ndi kuchita mapemphero aatali kuti awaone. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”
Who devour widows’ houses, and for a show make long prayers: the same shall receive greater condemnation.

< Luka 20 >