< Luka 20 >

1 Tsiku lina pamene Iye ankaphunzitsa anthu mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu ndi kuphunzitsa Uthenga Wabwino, akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, pamodzi ndi akuluakulu anabwera kwa Iye.
And it came to passe, that on one of those dayes, as he taught the people in the Temple, and preached the Gospel, the hie Priests and the Scribes came vpon him with the Elders,
2 Iwo anati, “Mutiwuze mukuchita izi ndi ulamuliro wayani? Ndani anakupatsani ulamuliro uwu?”
And spake vnto him, saying, Tell vs by what authoritie thou doest these things, or who is hee that hath giuen thee this authoritie?
3 Iye anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani, mundiyankhe,
And he answered, and sayde vnto them, I also will aske you one thing: tell me therefore:
4 ‘Kodi ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena wochokera kwa anthu?’”
The baptisme of Iohn, was it from heauen, or of men?
5 Iwo anakambirana pakati pawo ndikuti, “Ngati ife tinena kuti, ‘Kuchokera kumwamba’ Iye akatifunsa kuti, ‘chifukwa chiyani simunamukhulupirire iye?’
And they reasoned within themselues, saying, If we shall say, From heauen, he will say, Why then beleeued ye him not?
6 Koma ngati ife tinena kuti, ‘kuchokera kwa anthu,’ anthu onse atigenda miyala, chifukwa amatsimikiza kuti Yohane anali mneneri.”
But if we shall say, Of men, all the people will stone vs: for they be perswaded that Iohn was a Prophet.
7 Pamenepo iwo anayankha kuti, “Ife sitidziwa kumene unachokera.”
Therefore they answered, that they could not tell whence it was.
8 Yesu anati, “Ngakhale Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira zimenezi.”
Then Iesus sayd vnto them, Neither tell I you, by what authoritie I doe these things.
9 Iye anapitirira kuwawuza anthu fanizo ili: “Munthu wina analima munda wamphesa, nabwereketsa kwa alimi ena ndipo anachoka kwa nthawi yayitali.
Then began he to speake to ye people this parable, A certaine man planted a vineyarde, and let it forth to husbandmen: and went into a strange countrey, for a great time.
10 Pa nthawi yokolola, iye anatumiza wantchito wake kwa alimi aja kuti amupatseko zina mwa zipatso za munda wamphesawo. Koma alimi aja anamumenya namubweza wopanda kanthu.
And at the time conuenient he sent a seruant to the husbandmen, that they should giue him of the fruite of the vineyard: but the husbandmen did beate him, and sent him away emptie.
11 Iye anatumiza wantchito wina, koma uyunso anamumenya namuchita zachipongwe ndi kumubweza wopanda kanthu.
Againe he sent yet another seruant: and they did beate him, and foule entreated him, and sent him away emptie.
12 Iye anatumizanso wina wachitatu ndipo iwo anamuvulaza namuponya kunja.
Moreouer he sent the third, and him they wounded, and cast out.
13 “Kenaka mwini mundawo anati, ‘Kodi ndichite chiyani? Ndidzatumiza mwana wanga wamwamuna, amene ndimukonda; mwina iwo adzamuchitira ulemu.’
Then sayd the Lord of the vineyard, What shall I doe? I will send my beloued sonne: it may be that they will doe reuerence, when they see him.
14 “Koma alimiwo ataona mwanayo, anakambirananso. Iwo anati, ‘Uyu ndiye wodzamusiyira chumachi. Tiyeni timuphe ndipo chumachi chikhala chathu.’
But when the husbandmen sawe him, they reasoned with themselues, saying, This is the heire: come, let vs kill him, that the inheritance may be ours.
15 Ndipo anamuponya kunja kwa mundawo ndi kumupha. “Nanga tsono mwini munda wamphesayo adzawatani anthuwa?
So they cast him out of the vineyarde, and killed him. What shall the Lord of the vineyarde therefore doe vnto them?
16 Iye adzabwera ndi kupha alimi aja ndi kupereka mundawo kwa ena.” Pamene anthu anamva izi, anati, “Musatero ayi.”
He will come and destroy these husbandmen, and wil giue out his vineyard to others. But when they heard it, they sayd, God forbid.
17 Yesu anawayangʼanitsitsa ndipo anafunsa kuti, “Kodi tanthauzo lake ndi chiyani la zimene zinalembedwa kuti, “‘Mwala umene omanga nyumba anawukana wasanduka mwala wa pa ngodya.
And he beheld them, and said, What meaneth this then that is written, The stone that the builders refused, that is made the head of the corner?
18 Aliyense amene agwa pa mwalawu adzapweteka, koma iye amene udzamugwera udzamuphwanya.’”
Whosoeuer shall fall vpon that stone, shall be broken: and on whomsoeuer it shall fall, it will grinde him to pouder.
19 Aphunzitsi amalamulo ndi akulu a ansembe amafuna njira yoti amuphe nthawi yomweyo, chifukwa anadziwa kuti ananena fanizo ili powatsutsa iwo. Koma iwo anali ndi mantha chifukwa cha anthu.
Then the hie Priests, and the Scribes the same houre went about to lay hands on him: (but they feared the people) for they perceiued that he had spoken this parable against them.
20 Pamene ankamulondalonda Iye, iwo anatumiza akazitape amene amaoneka ngati achilungamo. Iwo ankafuna kumutapa mʼkamwa Yesu mu china chilichonse chimene Iye ananena kuti amupereke Iye kwa amene anali ndi mphamvu ndi ulamuliro oweruza.
And they watched him, and sent forth spies, which should faine themselues iust men, to take him in his talke, and to deliuer him vnto the power and authoritie of the gouernour.
21 Potero akazitapewo anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi, tidziwa kuti mumayankhula ndi kuphunzitsa zimene zili zoonadi, ndi kuti simuonetsa tsankho koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu mwachoonadi.
And they asked him, saying, Master, we know that thou sayest, and teachest right, neither doest thou accept mans person, but teachest the way of God truely.
22 Kodi ndi bwino kwa ife kumapereka msonkho kwa Kaisara kapena kusapereka?”
Is it lawfull for vs to giue Cesar tribute or no?
23 Iye anaona chinyengo chawo ndipo anawawuza kuti,
But he perceiued their craftines, and sayd vnto them, Why tempt ye me?
24 “Onetseni ndalama. Chithunzi ndi malembawa ndi zayani?”
Shew me a penie. Whose image and superscription hath it? They answered, and sayd, Cesars.
25 Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.” Iye anawawuza kuti, “Ndiye perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zimene ndi za Mulungu.”
Then he sayd vnto them, Giue then vnto Cesar the things which are Cesars, and to God those which are Gods.
26 Iwo analephera kumupeza cholakwa pa zimene ankayankhula pamaso pa anthu. Ndipo pothedwa nzeru ndi yankho lake, iwo anakhala chete.
And they could not reproue his saying before the people: but they marueiled at his answere, and helde their peace.
27 Ena mwa Asaduki, amene ankanena kuti kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Yesu ndi funso.
Then came to him certaine of the Sadduces (which denie that there is any resurrection) and they asked him,
28 Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
Saying, Master, Moses wrote vnto vs, If any mans brother die hauing a wife, and hee die without children, that his brother should take his wife, and raise vp seede vnto his brother.
29 Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyambayo anakwatira mkazi ndipo anafa wopanda mwana.
Now there were seuen brethren, and the first tooke a wife, and he dyed without children.
30 Wachiwiri
And the second tooke the wife, and he dyed childelesse.
31 ndipo kenaka wachitatuyo anamukwatira iye, ndipo chimodzimodzi asanu ndi awiri aja anafa osasiya ana.
Then the third tooke her: and so likewise the seuen dyed, and left no children.
32 Pa mapeto pake mkaziyo anafanso.
And last of all the woman dyed also.
33 Tsopano, pa nthawi ya kuukanso, kodi mkaziyu adzakhala wayani popeza onse asanu ndi awiri anamukwatirapo?”
Therefore at the resurrection, whose wife of them shall she be? for seuen had her to wife.
34 Yesu anayankha kuti, “Anthu a mʼbado uno amakwatira ndi kukwatiwa. (aiōn g165)
Then Iesus answered, and sayd vnto them, The children of this world marry wiues, and are married. (aiōn g165)
35 Koma mʼmoyo umene ukubwerawo, anthu amene adzaukitsidwe kwa akufa sadzakwatira kapena kukwatiwa. (aiōn g165)
But they which shalbe counted worthy to enioy that world, and the resurrection from the dead, neither marry wiues, neither are married. (aiōn g165)
36 Ndipo sadzafanso, pakuti adzakhala ngati angelo. Iwo ndi ana a Mulungu, chifukwa adzakhala ataukitsidwa kwa akufa.
For they can die no more, forasmuch as they are equall vnto the Angels, and are the sonnes of God, since they are the children of the resurrection.
37 Ngakhale pa nkhani yachitsamba choyaka moto, Mose anaonetsa kuti akufa amauka, pakuti anatcha Ambuye ‘Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo.’
And that the dead shall rise againe, euen Moses shewed it besides the bush, when he said, The Lord is the God of Abraham, and the God of Isaac, and the God of Iacob.
38 Mulungu si Mulungu wa akufa, koma wa amoyo, pakuti kwa Iye onse ali ndi moyo.”
For he is not the God of the dead, but of them which liue: for all liue vnto him.
39 Ena mwa aphunzitsi amalamulo anayankha kuti, “Mwanena bwino mphunzitsi!”
Then certaine of the Scribes answered, and sayd, Master, thou hast well sayd.
40 Ndipo panalibe wina amene akanalimba mtima kumufunsa Iye mafunso ena.
And after that, durst they not aske him any thing at all.
41 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Zikutheka bwanji kuti aziti Khristu ndi mwana wa Davide?
Then sayd he vnto them, Howe say they that Christ is Dauids sonne?
42 Davide mwini wake akunenetsa mʼbuku la Masalimo kuti, “Ambuye anati kwa Ambuye anga: ‘Khalani ku dzanja langa lamanja,
And Dauid himselfe sayth in the booke of the Psalmes, The Lord sayd vnto my Lord, Sit at my right hand,
43 mpaka Ine nditasandutsa adani anu chopondapo mapazi anu?’
Till I shall make thine enemies thy footestoole.
44 Davide akumutcha Iye ‘Ambuye.’ Nanga zingatheke bwanji kuti Iye akhale mwana wake?”
Seeing Dauid called him Lord, howe is he then his sonne?
45 Pamene anthu onse ankamvetsera, Yesu anati kwa ophunzira ake,
Then in the audience of all the people he sayd vnto his disciples,
46 “Chenjerani ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo amakonda kuyenda atavala mikanjo ndipo amakonda kulonjeredwa mʼmisika ndipo amakhala mʼmipando yofunika mʼmasunagoge ndi mʼmalo aulemu mʼmaphwando.
Beware of the Scribes, which willingly go in long robes, and loue salutations in the markets, and the highest seates in the assemblies, and the chiefe roomes at feastes:
47 Amawadyera akazi amasiye chuma chawo ndi kuchita mapemphero aatali kuti awaone. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”
Which deuoure widowes houses, and in shewe make long prayers: These shall receiue greater damnation.

< Luka 20 >