< Luka 20 >

1 Tsiku lina pamene Iye ankaphunzitsa anthu mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu ndi kuphunzitsa Uthenga Wabwino, akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, pamodzi ndi akuluakulu anabwera kwa Iye.
О И във време на беритбата прати един слуга при земеделците, за да му дадат от плода на лозето; но земеделците го биха и отпратиха го празен.
2 Iwo anati, “Mutiwuze mukuchita izi ndi ulamuliro wayani? Ndani anakupatsani ulamuliro uwu?”
Кажи ни с каква власт правиш това? Или, кой е онзи, който Ти е дал тази власт.
3 Iye anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani, mundiyankhe,
И в отговор им рече: Ще ви задам и Аз един въпрос, и отговорете Ми:
4 ‘Kodi ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena wochokera kwa anthu?’”
Иоановото кръщение от небето ли беше, или от човеците?
5 Iwo anakambirana pakati pawo ndikuti, “Ngati ife tinena kuti, ‘Kuchokera kumwamba’ Iye akatifunsa kuti, ‘chifukwa chiyani simunamukhulupirire iye?’
А те разискваха помежду си, думайки: Ако речем: От небето, ще каже: Защо го не повярвахте?
6 Koma ngati ife tinena kuti, ‘kuchokera kwa anthu,’ anthu onse atigenda miyala, chifukwa amatsimikiza kuti Yohane anali mneneri.”
Но ако речем: От човеците, всичките люде ще ни убият с камъни, защото са убедени, че Иоан беше пророк.
7 Pamenepo iwo anayankha kuti, “Ife sitidziwa kumene unachokera.”
И отговориха, че не знаят от къде беше.
8 Yesu anati, “Ngakhale Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira zimenezi.”
Тогава Исус им рече: Нито Аз ви казвам с каква власт правя това.
9 Iye anapitirira kuwawuza anthu fanizo ili: “Munthu wina analima munda wamphesa, nabwereketsa kwa alimi ena ndipo anachoka kwa nthawi yayitali.
И почна да говори на людете тая притча: Един човек насади лозе, даде го под наем на земеделци, и отиде в чужбина за дълго време.
10 Pa nthawi yokolola, iye anatumiza wantchito wake kwa alimi aja kuti amupatseko zina mwa zipatso za munda wamphesawo. Koma alimi aja anamumenya namubweza wopanda kanthu.
И във време [на беритбата] прати един слуга при земеделците за да му дадат от плода на лозето; но земеделците го биха и отпратиха го празен.
11 Iye anatumiza wantchito wina, koma uyunso anamumenya namuchita zachipongwe ndi kumubweza wopanda kanthu.
И изпрати друг слуга; а те и него биха, срамно го оскърбиха, и го отпратиха празен.
12 Iye anatumizanso wina wachitatu ndipo iwo anamuvulaza namuponya kunja.
Изпрати и трети; но те и него нараниха и изхвърлиха.
13 “Kenaka mwini mundawo anati, ‘Kodi ndichite chiyani? Ndidzatumiza mwana wanga wamwamuna, amene ndimukonda; mwina iwo adzamuchitira ulemu.’
Тогава стопанинът на лозето рече: Що да сторя? Ще изпратя любезния си син; може него да почетат.
14 “Koma alimiwo ataona mwanayo, anakambirananso. Iwo anati, ‘Uyu ndiye wodzamusiyira chumachi. Tiyeni timuphe ndipo chumachi chikhala chathu.’
Но земеделците, като го видяха, разискваха по между си, като думаха: Това е наследникът; нека го убием, за да стане наследството наше.
15 Ndipo anamuponya kunja kwa mundawo ndi kumupha. “Nanga tsono mwini munda wamphesayo adzawatani anthuwa?
Изхвърлиха го вън от лозето и го убиха. И тъй, какво ще им стори стопанинът на лозето?
16 Iye adzabwera ndi kupha alimi aja ndi kupereka mundawo kwa ena.” Pamene anthu anamva izi, anati, “Musatero ayi.”
Ще дойде и ще погуби тия земеделци, и ще даде лозето на други. А като чуха това рекоха: Дано не бъде!
17 Yesu anawayangʼanitsitsa ndipo anafunsa kuti, “Kodi tanthauzo lake ndi chiyani la zimene zinalembedwa kuti, “‘Mwala umene omanga nyumba anawukana wasanduka mwala wa pa ngodya.
А тоя ги погледна и рече: Тогава що значи това, което е писано: "Камъкът, който отхвърлиха зидарите, той стана глава на ъгъла"?
18 Aliyense amene agwa pa mwalawu adzapweteka, koma iye amene udzamugwera udzamuphwanya.’”
Всеки, който падне върху този камък, ще се смаже, а върху когото падне, ще го пръсне.
19 Aphunzitsi amalamulo ndi akulu a ansembe amafuna njira yoti amuphe nthawi yomweyo, chifukwa anadziwa kuti ananena fanizo ili powatsutsa iwo. Koma iwo anali ndi mantha chifukwa cha anthu.
И в същия час книжниците и главните свещеници се стараеха да турят ръце на Него, защото разбраха, че Той каза тая притча против тях, но се бояха от народа.
20 Pamene ankamulondalonda Iye, iwo anatumiza akazitape amene amaoneka ngati achilungamo. Iwo ankafuna kumutapa mʼkamwa Yesu mu china chilichonse chimene Iye ananena kuti amupereke Iye kwa amene anali ndi mphamvu ndi ulamuliro oweruza.
И като Го наблюдаваха, пратиха издебници, които се преструваха, че са праведни, за да уловят някоя Негова дума, тъй щото да Го предадат на началството и на властта на управителя.
21 Potero akazitapewo anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi, tidziwa kuti mumayankhula ndi kuphunzitsa zimene zili zoonadi, ndi kuti simuonetsa tsankho koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu mwachoonadi.
И те Го попитаха, казвайки: Учителю, знаем, че право говориш и учиш, и у Тебе няма лицеприятие, но учиш Божия път според истината;
22 Kodi ndi bwino kwa ife kumapereka msonkho kwa Kaisara kapena kusapereka?”
право ли е за нас да даваме данък на Кесаря, или не?
23 Iye anaona chinyengo chawo ndipo anawawuza kuti,
А Той разбра лукавството им, и рече им:
24 “Onetseni ndalama. Chithunzi ndi malembawa ndi zayani?”
Покажете ми един динарий. Чий образ и надпис има? И [в отговор] казаха: Кесарев.
25 Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.” Iye anawawuza kuti, “Ndiye perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zimene ndi za Mulungu.”
А Той рече: Тогава отдавайте Кесаревото на Кесаря, а Божието на Бога.
26 Iwo analephera kumupeza cholakwa pa zimene ankayankhula pamaso pa anthu. Ndipo pothedwa nzeru ndi yankho lake, iwo anakhala chete.
И не можаха да уловят нещо в думата пред народа; и, зачудени на отговора Му, млъкнаха.
27 Ena mwa Asaduki, amene ankanena kuti kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Yesu ndi funso.
Тогава се приближиха някои от садукеите, които твърдят, че няма възкресение, и Го попитаха, казвайки:
28 Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
Учителю, Моисей ни е писал: "Ако умре на някого брат му, който е женен, но е бездетен, брат му да вземе жената и да въздигне потомък на брата си".
29 Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyambayo anakwatira mkazi ndipo anafa wopanda mwana.
А имаше седмина братя; и първия взе жена и умря бездетен.
30 Wachiwiri
И вторият и третият я взеха;
31 ndipo kenaka wachitatuyo anamukwatira iye, ndipo chimodzimodzi asanu ndi awiri aja anafa osasiya ana.
така също и седмината я взеха и умряха без да оставят деца.
32 Pa mapeto pake mkaziyo anafanso.
А после умря и жената.
33 Tsopano, pa nthawi ya kuukanso, kodi mkaziyu adzakhala wayani popeza onse asanu ndi awiri anamukwatirapo?”
И тъй, във възкресението, на кого от тях ще бъде жена? Защото и седмината я имаха за жена.
34 Yesu anayankha kuti, “Anthu a mʼbado uno amakwatira ndi kukwatiwa. (aiōn g165)
А Исус им рече: Човеците на този свят се женят и се омъжват; (aiōn g165)
35 Koma mʼmoyo umene ukubwerawo, anthu amene adzaukitsidwe kwa akufa sadzakwatira kapena kukwatiwa. (aiōn g165)
а ония, които се удостоят да достигнат онзи свят и възкресението от мъртвите, нито се женят, нито се омъжват. (aiōn g165)
36 Ndipo sadzafanso, pakuti adzakhala ngati angelo. Iwo ndi ana a Mulungu, chifukwa adzakhala ataukitsidwa kwa akufa.
И не могат вече да умрат, понеже са равни на ангелите; и, като участници на възкресението, са чада на Бога.
37 Ngakhale pa nkhani yachitsamba choyaka moto, Mose anaonetsa kuti akufa amauka, pakuti anatcha Ambuye ‘Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo.’
А че мъртвите биват възкресени, това и Моисей показа в мястото, дето писа за къпината, когато нарече Господа "Бог Авраамов, Бог Исааков и Бог Яковов".
38 Mulungu si Mulungu wa akufa, koma wa amoyo, pakuti kwa Iye onse ali ndi moyo.”
Но Той не е Бог на мъртвите, а на живите; защото за Него всички са живи.
39 Ena mwa aphunzitsi amalamulo anayankha kuti, “Mwanena bwino mphunzitsi!”
А някои от книжниците в отговор рекоха: Учителю, Ти добре каза.
40 Ndipo panalibe wina amene akanalimba mtima kumufunsa Iye mafunso ena.
Защото не смееха вече за нищо да Го попитат.
41 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Zikutheka bwanji kuti aziti Khristu ndi mwana wa Davide?
И рече им: Как казват, че Христос е Давидов син?
42 Davide mwini wake akunenetsa mʼbuku la Masalimo kuti, “Ambuye anati kwa Ambuye anga: ‘Khalani ku dzanja langa lamanja,
Защото сам Давид казва в книгата на псалмите: - Рече Господ на моя Господ: Седи отдясно Ми.
43 mpaka Ine nditasandutsa adani anu chopondapo mapazi anu?’
докле положа враговете Ти за Твое подножие.
44 Davide akumutcha Iye ‘Ambuye.’ Nanga zingatheke bwanji kuti Iye akhale mwana wake?”
И тъй, Давид Го нарича Господ, тогава как е негов син?
45 Pamene anthu onse ankamvetsera, Yesu anati kwa ophunzira ake,
И когато слушаха всичките люде, Той рече на учениците Си:
46 “Chenjerani ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo amakonda kuyenda atavala mikanjo ndipo amakonda kulonjeredwa mʼmisika ndipo amakhala mʼmipando yofunika mʼmasunagoge ndi mʼmalo aulemu mʼmaphwando.
Пазете се от книжниците, които обичат да ходят пременени, и обичат поздрави по пазарите, първите столове в синагогите, и първите места по угощенията;
47 Amawadyera akazi amasiye chuma chawo ndi kuchita mapemphero aatali kuti awaone. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”
които изпояждат домовете на вдовиците, и за показ принасят дълги молитви. Те ще получат по-голямо осъждане.

< Luka 20 >