< Luka 2 >

1 Mʼmasiku amenewo Kaisara Augusto anapereka lamulo kuti kalembera achitike mʼdziko lonse la Aroma.
U one dane izađe naredba cara Augusta da se provede popis svega svijeta.
2 (Uyu ndi kalembera woyamba amene anachitika pamene Kureniyo anali bwanamkubwa wa Siriya).
Bijaše to prvi popis izvršen za Kvirinijeva upravljanja Sirijom.
3 Ndipo aliyense anapita ku mzinda wa kwawo kukalembetsa.
Svi su išli na popis, svaki u svoj grad.
4 Choncho Yosefe anachoka ku Nazareti ku Galileya kupita ku Yudeya, ku Betelehemu ku mudzi wa Davide, chifukwa anali wa banja ndi fuko la Davide.
Tako i Josip, budući da je bio iz doma i loze Davidove, uziđe iz Galileje, iz grada Nazareta, u Judeju - u grad Davidov, koji se zove Betlehem -
5 Iye anapita kumeneko kukalembetsa pamodzi ndi Mariya, amene anapalana naye ubwenzi kuti akwatirane ndipo anali woyembekezera.
da se podvrgne popisu zajedno sa svojom zaručnicom Marijom koja bijaše trudna.
6 Ali kumeneko, nthawi inakwana yakuti mwana abadwe,
I dok se bili ondje, navršilo joj se vrijeme da rodi.
7 ndipo anabereka mwana wake woyamba, wamwamuna. Iye anamukulunga mʼnsalu ndi kumuyika modyera ngʼombe, chifukwa kunalibe malo mʼnyumba ya alendo.
I porodi sina svoga, prvorođenca, povi ga i položi u jasle jer za njih nije bilo mjesta u svratištu.
8 Ndipo kunali abusa amene amakhala ku dera lomwelo, kuyangʼanira ziweto zawo usiku.
A u tom kraju bijahu pastiri: pod vedrim su nebom čuvali noćnu stražu kod svojih stada.
9 Mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iwo ndipo ulemerero wa Ambuye unawala mowazungulira. Iwo anachita mantha.
Anđeo im Gospodnji pristupi i slava ih Gospodnja obasja! Silno se prestrašiše.
10 Koma mngeloyo anawawuza kuti, “Musachite mantha. Ine ndakubweretserani Uthenga Wabwino wachimwemwe chachikulu umene udzakhala wa anthu onse.
No anđeo im reče: “Ne bojte se! Evo javljam vam blagovijest, veliku radost za sav narod!
11 Lero mʼmudzi wa Davide wakubwadwirani Mpulumutsi; Iye ndi Khristu Ambuye.
Danas vam se u gradu Davidovu rodio Spasitelj - Krist, Gospodin.
12 Ichi chidzakhala chizindikiro kwa inu: mukapeza mwana wakhanda wokutidwa ndi nsalu atagona modyera ngʼombe.”
I evo vam znaka: naći ćete novorođenče povijeno gdje leži u jaslama.”
13 Mwadzidzidzi gulu lalikulu la angelo linaonekera pamodzi ndi mngeloyo, kuyamika Mulungu ndi kumati,
I odjednom se anđelu pridruži silna nebeska vojska hvaleći Boga i govoreći:
14 “Ulemerero kwa Mulungu mmwambamwamba, ndi mtendere kwa anthu pa dziko lapansi amene Iye akondwera nawo.”
“Slava na visinama Bogu, a na zemlji mir ljudima, miljenicima njegovim!”
15 Angelowo atabwerera kumwamba, abusawo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni ku Betelehemu tikaone zinthu zomwe zachitika, zimene Ambuye atiwuza ife.”
Čim anđeli otiđoše od njih na nebo, pastiri stanu poticati jedni druge: “Hajdemo dakle do Betlehema. Pogledajmo što se to dogodilo, događaj koji nam obznani Gospodin.”
16 Ndipo iwo anafulumira nyamuka nakapeza Mariya ndi Yosefe ndi mwana wakhanda, amene anagona modyera ngʼombe.
I pohite te pronađu Mariju, Josipa i novorođenče gdje leži u jaslama.
17 Pamene anamuona Iye, iwo anafotokoza zomwe anawuzidwa za mwanayo,
Pošto sve pogledaše, ispripovijediše što im bijaše rečeno o tom djetetu.
18 ndipo onse amene anamva zimene abusawa ananena anadabwa.
A svi koji su to čuli divili se tome što su im pripovijedali pastiri.
19 Koma Mariya anasunga zonsezi mu mtima mwake ndi kumazilingalira.
Marija u sebi pohranjivaše sve te događaje i prebiraše ih u svome srcu.
20 Abusa anabwerera, akulemekeza ndi kuyamika Mulungu chifukwa cha zonse anazimva ndi kuziona, zomwe zinali monga anawuzidwira ndi angelo aja.
Pastiri se zatim vratiše slaveći i hvaleći Boga za sve što su čuli i vidjeli kako im je bilo rečeno.
21 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, tsiku loti amuchite mdulidwe anamutcha Yesu, dzina limene mngelo anamupatsa asanabadwe.
Kad se navršilo osam dana da bude obrezan, nadjenuše mu ime Isus, kako ga je bio prozvao anđeo prije njegova začeća.
22 Nthawi yoyeretsedwa kwawo itatha, monga mwa lamulo la Mose, Yosefe ndi Mariya anapita naye ku Yerusalemu kukamupereka kwa Ambuye.
Kad se zatim po Mojsijevu Zakonu navršiše dani njihova čišćenja, poniješe ga u Jeruzalem da ga prikažu Gospodinu -
23 (Monga mmene zinalembedwera mu lamulo la Ambuye kuti, “Muzikapereka kwa Ambuye mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa”),
kao što piše u Zakonu Gospodnjem: Svako muško prvorođenče neka se posveti Gospodinu! -
24 ndi kupereka nsembe posunga zimene zinanenedwa mulamulo la Ambuye: “Njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri.”
i da prinesu žrtvu kako je rečeno u Zakonu Gospodnjem: dvije grlice ili dva golubića.
25 Ndipo taonani, mu Yerusalemu munali munthu wotchedwa Simeoni, amene anali wolungama ndi wodzipereka. Iye ankadikira chitonthozo cha Israeli, ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.
Živio tada u Jeruzalemu čovjek po imenu Šimun. Taj čovjek, pravedan i bogobojazan, iščekivaše Utjehu Izraelovu i Duh Sveti bijaše na njemu.
26 Mzimu Woyera anamuwululira kuti sadzafa asanaone Khristu wa Ambuye.
Objavio mu Duh Sveti da neće vidjeti smrti dok ne vidi Pomazanika Gospodnjega.
27 Motsogozedwa ndi Mzimu Woyera, iye anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Makolo ake a Yesu atabwera naye kuti achite naye mwambo malingana ndi malamulo,
Ponukan od Duha, dođe u Hram. I kad roditelji uniješe dijete Isusa da obave što o njemu propisuje Zakon,
28 Simeoni anamunyamula mʼmanja mwake nayamika Mulungu, nati:
primi ga on u naručje, blagoslovi Boga i reče:
29 “Ambuye waulamuliro, monga munalonjeza, tsopano lolani kuti mtumiki wanu apite mu mtendere.
“Sad otpuštaš slugu svojega, Gospodaru, po riječi svojoj, u miru!
30 Pakuti maso anga aona chipulumutso chanu,
Ta vidješe oči moje spasenje tvoje,
31 chimene Inu munakonza pamaso pa anthu onse,
koje si pripravio pred licem svih naroda:
32 kuwala kowunikira anthu a mitundu ina ndi kwa ulemerero kwa anthu anu Aisraeli.”
svjetlost na prosvjetljenje naroda, slavu puka svoga izraelskoga.”
33 Abambo ndi amayi a Mwanayo anadabwa chifukwa cha zimene zinanenedwa za Iye.
Otac njegov i majka divili se što se to o njemu govori.
34 Kenaka Simeoni anawadalitsa ndipo anati kwa Mariya amayi ake: “Mwana uyu wakonzedwa kukhala kugwa ndi kudzuka kwa ambiri mu Israeli, ndi kukhala chizindikiro chimene adzayankhula motsutsana nacho,
Šimun ih blagoslovi i reče Mariji, majci njegovoj: “Ovaj je evo postavljen na propast i uzdignuće mnogima u Izraelu i za znak osporavan -
35 kotero kuti malingaliro a mitima ya ambiri adzawululidwa. Ndipo lupanga lidzabaya moyo wakonso.”
a i tebi će samoj mač probosti dušu - da se razotkriju namisli mnogih srdaca!”
36 Panalinso mneneri wamkazi, dzina lake Ana, mwana wa Fanuelo, wa fuko la Aseri. Anali wokalamba kwambiri; anakhala ndi mwamuna wake zaka zisanu ndi ziwiri atakwatiwa,
A bijaše neka proročica Ana, kći Penuelova, iz plemena Ašerova, žena veoma odmakla u godinama. Nakon djevojaštva živjela je s mužem sedam godina,
37 ndipo kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera.
a sama kao udovica do osamdeset i četvrte. Nije napuštala Hrama, nego je postovima i molitvama danju i noću služila Bogu.
38 Pa nthawiyo pamene ankapita kwa iwo, iye anayamika Mulungu ndi kuyankhula za Mwanayo kwa onse amene ankayembekezera chipulumutso cha Yerusalemu.
Upravo u taj čas nadođe. Hvalila je Boga i svima koji iščekivahu otkupljenje Jeruzalema pripovijedala o djetetu.
39 Yosefe ndi Mariya atachita zonse zimene zinkafunikira ndi lamulo la Ambuye, anabwerera ku Galileya ku mudzi wa Nazareti.
Kad obaviše sve po Zakonu Gospodnjem, vratiše se u Galileju, u svoj grad Nazaret.
40 Ndipo Mwanayo anakula nakhala wamphamvu; Iye anadzazidwa ndi nzeru, ndipo chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.
A dijete je raslo, jačalo i napunjalo se mudrosti i milost je Božja bila na njemu.
41 Chaka chilichonse makolo ake ankapita ku Yerusalemu ku phwando la Paska.
Njegovi su roditelji svake godine o blagdanu Pashe išli u Jeruzalem.
42 Iye ali ndi zaka khumi ndi ziwiri, anapita ku phwando, monga mwa mwambo.
Kad mu bijaše dvanaest godina, uziđoše po običaju blagdanskom.
43 Phwando litatha, pamene makolo ake ankabwerera kwawo, mnyamata Yesu anatsalira ku Yerusalemu, koma iwo sanadziwe zimenezi.
Kad su minuli ti dani, vraćahu se oni, a dječak Isus osta u Jeruzalemu, a da nisu znali njegovi roditelji.
44 Poganiza kuti anali nawo mʼgulu lawo, anayenda tsiku limodzi. Kenaka anayamba kumufunafuna pakati pa abale awo ndi anzawo.
Uvjereni da je među suputnicima, odoše dan hoda, a onda ga stanu tražiti među rodbinom i znancima.
45 Atalephera kumupeza, anabwerera ku Yerusalemu kukamufuna.
I kad ga ne nađu, vrate se u Jeruzalem tražeći ga.
46 Patatha masiku atatu anamupeza ali mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, atakhala pakati pa aphunzitsi, akumvetsera ndi kuwafunsa mafunso.
Nakon tri dana nađoše ga u Hramu gdje sjedi posred učitelja, sluša ih i pita.
47 Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake.
Svi koji ga slušahu bijahu zaneseni razumnošću i odgovorima njegovim.
48 Makolo ake atamuona, anadabwa. Amayi ake anati kwa Iye, “Mwanawe, watichitira zimenezi chifukwa chiyani? Abambo ako ndi ine takhala tili ndi nkhawa kukufunafuna Iwe.”
Kad ga ugledaše, zapanjiše se, a majka mu njegova reče: “Sinko, zašto si nam to učinio? Gle, otac tvoj i ja žalosni smo te tražili.”
49 Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumandifunafuna? Kodi simukudziwa kuti ndikuyenera kukhala mʼnyumba ya Atate anga?”
A on im reče: “Zašto ste me tražili? Niste li znali da mi je biti u onome što je Oca mojega?”
50 Koma iwo sanazindikire chomwe Iye amatanthauza.
Oni ne razumješe riječi koju im reče.
51 Kenaka anapita nawo ku Nazareti ndipo anawamvera iwo. Koma amayi ake anasunga zinthu zonsezi mu mtima mwawo.
I siđe s njima, dođe u Nazaret i bijaše im poslušan. A majka je njegova brižno čuvala sve ove uspomene u svom srcu.
52 Ndipo Yesu anakula mu nzeru, msinkhu ndi chisomo cha Mulungu ndi anthu.
A Isus napredovaše u mudrosti, dobi i milosti kod Boga i ljudi.

< Luka 2 >