< Luka 19 >

1 Yesu analowa mu Yeriko napitirira.
A Jezus wszedłszy, szedł przez Jerycho.
2 Kunali munthu kumeneko dzina lake Zakeyu; iye anali mkulu wa wolandira msonkho ndipo anali wolemera.
A oto mąż, którego zwano imieniem Zacheusz, który był przełożony nad celnikami, a ten był bogaty.
3 Iye ankafuna kuona Yesu kuti ndani, koma pokhala wamfupi sanathe chifukwa cha gulu la anthu.
I żądał widzieć Jezusa, co by zacz był; lecz nie mógł przed ludem, bo był małego wzrostu.
4 Choncho iye anathamangira patsogolo ndipo anakwera mu mtengo wamkuyu kuti amuone Iye, pakuti Yesu ankadutsa njira imeneyo.
A bieżawszy naprzód, wstąpił na drzewo leśnej figi, aby go ujrzał; bo tamtędy iść miał.
5 Yesu atafika pa malopo, anayangʼana mmwamba ndipo anati kwa iye, “Zakeyu, tsika msangamsanga. Ine ndiyenera kukhala mʼnyumba mwako lero.”
A gdy przyszedł na ono miejsce, spojrzawszy Jezus w górę, ujrzał go, i rzekł do niego: Zacheuszu! zstąp prędko na dół, albowiem dziś muszę zostać w domu twoim.
6 Ndipo nthawi yomweyo anatsika ndipo anamulandira mosangalala.
I zstąpił prędko i przyjął go z radością.
7 Anthu onse ataona zimenezi anayamba kungʼungʼudza, nati, “Iye akupita kuti akakhale mlendo wa wochimwa.”
A widząc to wszyscy, szemrali, mówiąc: U człowieka grzesznego gospodą stanął.
8 Koma Zakeyu anayimirira ndipo anati kwa Ambuye, “Taonani Ambuye! Theka la chuma changa ndipereka kwa osauka ndipo ngati ndinamubera wina aliyense pa chilichonse, ndidzamubwezera mochulukitsa kanayi.”
A stanąwszy Zacheusz, rzekł do Pana: Oto połowę majętności moich dam ubogim, Panie! a jeźliżem kogo w czem podszedł, oddam w czwórnasób.
9 Yesu anati kwa iye, “Lero chipulumutso chafika mʼnyumba ino, chifukwa munthu uyu nayenso ndi mwana wa Abrahamu.
I rzekł mu Jezus: Dziś się stało zbawienie domowi temu, dlatego że i on jest synem Abrahamowym.
10 Pajatu Mwana wa Munthu anabwera kudzafunafuna ndi kupulumutsa chotayikacho.”
Bo przyszedł Syn człowieczy, aby szukał i zachował, co było zginęło.
11 Pamene iwo ankamvera izi, Iye anapitiriza kuwawuza fanizo, chifukwa Iye anali kufupi ndi Yerusalemu ndipo anthu ankaganiza kuti ufumu wa Mulungu ukanaoneka nthawi yomweyo.
Tedy gdy oni słuchali, mówiąc dalej powiedział im podobieństwo, dlatego że był blisko od Jeruzalemu, a iż oni mniemali, że się wnet królestwo Boże objawić miało.
12 Iye anati, “Munthu wa banja laufumu anapita ku dziko lakutali kukadzozedwa ufumu ndipo kenaka abwerenso kwawo.
Rzekł tedy: Niektóry człowiek rodu zacnego jechał w daleką krainę, aby sobie wziął królestwo, i zasię się wrócił.
13 Tsono iye anayitana antchito ake khumi ndi kuwapatsa ndalama khumi. Iye anati, ‘Gwiritsani ntchito ndalama izi mpaka nditabwerera.’
A zawoławszy dziesięciu sług swoich, dał im dziesięć grzywien i rzekł do nich: Handlujcie, aż przyjadę.
14 “Koma anthu ake anamuda ndipo anatuma nthumwi pambuyo pake kukanena kuti, ‘Sitikufuna munthuyu kuti akhale mfumu yathu.’
Lecz mieszczanie jego mieli go w nienawiści, i wyprawili za nim poselstwo, mówiąc: Nie chcemy, aby ten królował nad nami.
15 “Iye analandira ufumuwo ngakhale zinali zotero, ndipo anabwerera kwawo. Kenaka iye anatumiza uthenga kwa antchito ake amene anawapatsa ndalama aja, ndi cholinga chakuti adziwe chimene anapindula nazo.
I stało się, gdy się wrócił wziąwszy królestwo, że rozkazał do siebie zawołać sług onych, którym był dał pieniądze, aby się dowiedział, co który handlując zyskał.
16 “Woyamba anabwera ndipo anati, ‘Bwana ndalama zanu zapindula khumi zina.’
Tedy przyszedł pierwszy, mówiąc: Panie! grzywna twoja dziesięć grzywien urobiła.
17 “Bwana wakeyo anayankha kuti, Wachita bwino wantchito wabwino. ‘Chifukwa wakhulupirika pa zinthu zazingʼono, lamulira mizinda khumi.’
I rzekł mu: Dobrze, sługo dobry! iżeś był nad małem wiernym, miejże władzę nad dziesięcioma miastami.
18 “Wachiwiri anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama zanu zapindula zisanu zina.’
Przyszedł i drugi, mówiąc: Panie! grzywna twoja pięć grzywien urobiła.
19 “Bwana anayankha kuti, ‘Iwe lamulira mizinda isanu.’
Rzekł i temu: I ty bądź nad pięcioma miastami.
20 “Kenaka wantchito wina anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama yanu nayi; ine ndinayibisa ndi kuyisunga mʼkansalu.
A inszy przyszedł, mówiąc: Panie! oto grzywna twoja, którąm miał schowaną w chustce;
21 Ine ndimakuopani, chifukwa ndinu munthu wowuma mtima. Inu mumatenga chimene simunachiyike ndi kukolola chimene simunadzale.’
Bom się ciebie bał, żeś jest człowiek srogi; bierzesz, czegoś nie położył, a żniesz, czegoś nie siał.
22 “Bwana wake anayankha kuti, ‘Ine ndikukuweruza iwe ndi mawu ako omwewo. Ndiwe wantchito woyipa. Kani umadziwa kuti ndine munthu wowuma mtima ndi wotenga chimene sindinasungitse, ndi kukolola chimene sindinadzale?
Tedy mu rzekł: Z ust twoich sądzę cię, zły sługo! Wiedziałeś, żem ja jest człowiek srogi, który biorę, czegom nie położył, a żnę, czegom nie siał.
23 Nanga nʼchifukwa chiyani sunasungitse ndalama yanga, kuti ine pobwera, ndidzayitenge ndi chiwongoladzanja?’
Przeczżeś tedy nie dał srebra mego do lichwiarzy? a ja przyszedłszy, wziąłbym je był z lichwą.
24 “Ndipo iye anawuza amene anayimirira pafupi kuti, ‘Tengani ndalama yake ndi kumupatsa amene ali ndi ndalama khumiyo!’”
I rzekł tym, którzy tuż stali: Weźmijcie od niego tę grzywnę, a dajcie temu, który ma dziesięć grzywien.
25 Iwo anati, “Bwana iyeyu ali nazo kale khumi!”
I rzekli mu: Panie! mać dziesięć grzywien.
26 Iye anayankha kuti, “Ndikukuwuzani kuti, aliyense amene ali nazo, adzapatsidwa zambiri, koma amene alibe, adzalandidwa ngakhale chimene ali nacho.
Zaprawdę powiadam wam, iż wszelkiemu, który ma, będzie dane, a od tego, który nie ma, i to, co ma, będzie od niego odjęte.
27 Tsono adani anga aja amene sankafuna kuti ndikhale mfumu yawo, abweretseni pano ndi kuwapha ine ndikuona.”
Ale i nieprzyjacioły moje, którzy nie chcieli, abym królował nad nimi, przywiedźcie tu, a pobijcie przede mną.
28 Yesu atatha kunena izi, anayendabe kupita ku Yerusalemu.
A to powiedziawszy, szedł wprzód, wstępując do Jeruzalemu.
29 Iye atayandikira ku Betifage ndi Betaniya pa phiri lotchedwa Olivi, Iye anatuma awiri a ophunzira nati kwa iwo,
I stało się, gdy się przybliżył do Betfagie i Betanii, ku górze, którą zowią oliwną, posłał dwóch z uczniów swoich,
30 “Pitani mʼmudzi uli patsogolo panu, mukakalowa mʼmudzimo, mukapeza mwana wabulu womangiriridwa amene wina aliyense sanakwerepo. Mukamumasule ndi kubwera naye kuno.
Mówiąc: Idźcie do miasteczka, które jest przeciwko wam, do którego wszedłszy, znajdziecie oślę uwiązane, na którem żaden człowiek nigdy nie siedział; odwiązawszy je, przywiedźcie:
31 Ngati wina aliyense akakufunsani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mukumumasula mwana buluyo?’ Mukamuwuze kuti, ‘Ambuye akumufuna.’”
A jeźliby was kto spytał, przecz je odwiązujecie? tak mu powiecie: Przeto, że go Pan potrzebuje.
32 Otumidwawo anapita nakamupeza mwana wabulu monga momwe Yesu anawawuzira.
Odszedłszy tedy ci, którzy byli posłani, znaleźli, jako im był powiedział.
33 Pamene ankamasula mwana wabuluyo, eni ake anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukumasula mwana wabuluyo?”
A gdy oni odwiązywali ono oślę, rzekli panowie jego do nich: Przecz odwiązujecie oślę?
34 Iwo anayankha kuti, “Ambuye akumufuna.”
A oni powiedzieli: Pan go potrzebuje.
35 Iwo anabweretsa buluyo kwa Yesu, naponya zovala zawo pa bulupo ndi kumukwezapo Yesu.
I przywiedli je do Jezusa, a włożywszy szaty swoje na ono oślę, wsadzili Jezusa na nie.
36 Pamene ankapita, anthu anayala zovala zawo mu msewu.
A gdy on jechał, słali szaty swoje na drodze.
37 Iye atafika pafupi ndi pamene msewu umatsikira ku phiri la Olivi, gulu lonse la ophunzira linayamba kuyamika Mulungu mwachimwemwe ndi mawu ofuwula chifukwa cha zodabwitsa zonse anaziona.
A gdy się już przybliżał tam, gdzie się spuszczają z góry oliwnej, poczęło wszystko mnóstwo uczniów radując się chwalić Boga głosem wielkim ze wszystkich cudów, które widzieli,
38 “Yodala mfumu imene ikubwera mʼdzina la Ambuye!” “Mtendere kumwamba ndi ulemerero mmwambamwamba!”
Mówiąc: Błogosławiony król, który idzie w imieniu Pańskiem; pokój na niebie, a chwała na wysokościach.
39 Ena mwa Afarisi mʼgulumo anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, adzudzuleni ophunzira anu!”
Ale niektórzy z Faryzeuszów z onego ludu rzekli do niego: Nauczycielu! zgrom ucznie twoje.
40 Iye anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani kuti, ngati atakhala chete, miyala idzafuwula.”
A on odpowiadając, rzekł im: Powiadam wam, jeźliby ci milczeli, wnet kamienie wołać będą.
41 Iye atayandikira ku Yerusalemu ndi kuona mzindawo, anawulirira
A gdy się przybliżył, ujrzawszy miasto, płakał nad niem, mówiąc:
42 nati, “Iwe ukanadziwa lero lino zinthu zokubweretsera mtendere, koma tsopano zabisikira maso ako.
O gdybyś poznało i ty, a zwłaszcza w ten to dzień twój, co jest ku pokojowi twemu! lecz to teraz zakryte od oczów twoich.
43 Pakuti masiku adzabwera pamene adani ako adzamanga mitumbira yankhondo nakuzungulira, nadzakutsekereza mbali zonse.
Albowiem przyjdą na cię dni, gdy cię otoczą nieprzyjaciele twoi wałem, i oblęgą cię, i ścisną cię zewsząd;
44 Iwo adzakugwetsera pansi, iwe, ana ako onse a mʼkati mwako. Iwo sadzasiya mwa iwe mwala wina pa unzake, chifukwa sunazindikire nthawi ya kubwera kwa Mulungu.”
I zrównają cię z ziemią, i dzieci twoje w tobie, a nie zostawią w tobie kamienia na kamieniu, dlatego żeś nie poznało czasu nawiedzenia twego.
45 Kenaka Iye analowa mʼdera la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kutulutsa kunja amene amachita malonda.
A wszedłszy do kościoła, począł wyganiać te, którzy w nim sprzedawali i kupowali.
46 Iye anawawuza kuti, “Zinalembedwa kuti Nyumba yanga idzakhala nyumba ya mapemphero, koma inu mwayisadutsa phanga la achifwamba.”
Mówiąc im: Napisano: Dom mój dom modlitwy jest, a wyście go uczynili jaskinią zbójców.
47 Tsiku lililonse amaphunzitsa mʼNyumba ya Mulungu. Koma akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi atsogoleri pakati pa anthu amayesetsa kuti amuphe.
I uczył na każdy dzień w kościele; lecz przedniejsi kapłani i nauczeni w Piśmie, i przedniejsi z ludu szukali go stracić;
48 Komabe iwo sanathe kupeza njira ina iliyonse kuti achite izi, chifukwa anthu onse anakhulupirira mawu ake.
Ale nie znaleźli, co by mu uczynili; albowiem wszystek lud zawieszał się na nim, słuchając go.

< Luka 19 >