< Luka 18 >

1 Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke.
Sade han ock en liknelse till dem derom, att man skall alltid bedja, och icke förtröttas;
2 Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu.
Sägandes: En domare var uti en stad, den icke fruktade Gud, och ej heller hade försyn för några mennisko;
3 Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’
Så var i samma stad en enka; hon kom till honom, och sade: Hjelp mig ifrå min trätobroder.
4 “Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu,
Och han ville icke till någon tid. Sedan sade han vid sig: Ändock jag icke fruktar Gud, ej heller hafver försyn för någon mennisko;
5 koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’”
Dock, fördenskull att denna enkan öfverfaller mig så svåra, måste jag fly henne rätt, att hon icke skall komma på det sista, och ropa på mig.
6 Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena.
Och sade Herren: Hörer här, hvad den orätta domaren säger.
7 Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira?
Skulle ock icke Gud hämnas sina utkorade, som ropa till honom dag och natt; skulle han hafva tålamod dermed?
8 Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”
Jag säger eder, att han skall hämnas dem snarliga. Dock likväl, då menniskones Son kommer, månn han skall finna tro på jordene?
9 Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse.
Sade han ock till somliga, som tröste på sig sjelfva, att de voro rättfärdige, och försmådde andra, denna liknelsen:
10 “Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho.
Två män gingo upp i templet till att bedja; den ene en Pharisee, och den andre en Publican.
11 Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu.
Phariseen stod och bad så vid sig sjelf: Jag tackar dig Gud, att jag är icke såsom andra menniskor, röfvare, orättfärdige, horkarlar, eller ock såsom denne Publicanen.
12 Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’
Jag fastar två resor i veckone, och gifver tiond af allt det jag äger.
13 “Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’
Och Publicanen stod långt ifrån, och ville icke lyfta sin ögon upp till himmelen; utan slog sig för sitt bröst, och sade: Gud, miskunda dig öfver mig syndare.
14 “Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”
Jag säger eder: Denne gick dädan hem igen rättfärdigad, mer än den andre; ty den sig upphöjer, han varder förnedrad; och den sig förnedrar, han varder upphöjd.
15 Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula.
Så båro de ock barn till honom, att han skulle taga på dem; då hans Lärjungar det sågo, näpste de dem.
16 Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere.
Men Jesus kallade dem till sig, och sade: Låter barnen komma till mig, och förmener dem icke; ty sådana hörer Guds rike till.
17 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
Sannerliga säger jag eder: Hvilken som icke tager Guds rike som ett barn, han skall icke komma derin.
18 Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios g166)
Och frågade honom en öfverste, sägandes: Gode Mästar, hvad skall jag göra, att jag må få evinnerligit lif? (aiōnios g166)
19 Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha.
Sade Jesus till honom: Hvi kallar du mig godan? Ingen är god, utan allena Gud.
20 Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
Budorden vetst du: Du skall icke bedrifva hor; du skall icke dräpa; du skall icke stjäla; du skall icke säga falskt vittnesbörd; du skall ära din fader och dina moder.
21 Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”
Då sade han: Allt detta hafver jag hållit af min ungdom.
22 Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”
Då Jesus det hörde, sade han till honom: Än fattas dig ett; sälj bort allt det du hafver, och skift emellan de fattiga, och du skall få en skatt i himmelen; och kom, och följ mig.
23 Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri.
Då han det hörde, vardt han storliga bedröfvad; ty han var ganska rik.
24 Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!
Då Jesus såg honom vara mägta bedröfvad, sade han: O! med huru stor plats komma de i Guds rike, som penningar hafva;
25 Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”
Ty snarare kan en camel gå igenom ett nålsöga, än en riker komma in i Guds rike.
26 Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
Då sade de som det hörde: Ho kan då varda salig?
27 Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”
Men han sade: Det omöjeligit är för menniskom, det är möjeligit för Gud.
28 Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”
Då sade Petrus: Si, vi hafve all ting öfvergifvit, och följt dig.
29 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu
Sade han till dem: Sannerliga säger jag eder; ingen är den som hafver öfvergifvit hus, eller föräldrar, eller bröder, eller hustru, eller barn, för Guds rikes skull;
30 adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
Den icke skall igenfå mycket mer i denna tiden, och i tillkommande verld evinnerligit lif. (aiōn g165, aiōnios g166)
31 Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa.
Då tog Jesus till sig de tolf, och sade till dem: Si, vi gåm upp till Jerusalem, och all ting skola fullbordad varda, som skrifven äro af Propheterna om menniskones Son.
32 Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira,
Ty han skall öfverantvardas Hedningom, och begabbas, och försmädas, och bespottas.
33 adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”
Och sedan de hafva hudflängt honom, skola de döda honom; och tredje dagen skall han uppstå igen.
34 Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.
Men de förstodo der intet af, och talet var dem så fördoldt, att de icke förstodo hvad som sades.
35 Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha,
Så hände sig, att när han kom in mot Jericho, satt en blinder vid vägen, och tiggde.
36 anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika.
Och när han hörde folket framgå, frågade han hvad det var?
37 Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”
Då sade de till honom, att Jesus af Nazareth gick der fram.
38 Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
Då ropade han, och sade: Jesu, Davids Son, varkunna dig öfver mig.
39 Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”
Men de, som föregingo, näpste honom, att han skulle tiga; men han ropade dessmer: Davids Son, varkunna dig öfver mig.
40 Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti,
Då stadnade Jesus, och böd leda honom till sig. Då han kom fram, frågade han honom,
41 “Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?” Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”
Sägandes: Hvad vill du, att jag skall göra dig? Då sade han: Herre, att jag måtte få min syn.
42 Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.”
Och Jesus sade till honom: Haf din syn; din tro hafver frälst dig.
43 Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.
Och straxt fick han sin syn igen, och följde honom, prisandes Gud. Och allt folket, som detta sågo, lofvade Gud.

< Luka 18 >